< 1 Samueli 8 >

1 Samueli atakalamba anasankha ana ake kuti akhale oweruza Aisraeli.
Když se pak zstaral Samuel, ustanovil syny své za soudce v Izraeli.
2 Mwana wake woyamba anali Yoweli, wachiwiri anali Abiya, ndipo ankaweruza ku Beeriseba.
A bylo jméno syna jeho prvorozeného Joel, a jméno druhého Abia; ti byli soudcové v Bersabé.
3 Koma ana akewo sanatengere makhalidwe ake abwino. Iwo ankapotokera ku zoyipa namatsata phindu mwachinyengo. Ankalandira ziphuphu ndi kumaweruza mwachinyengo.
Nechodili pak synové jeho po cestách jeho, ale uchýlili se po lakomství, a berouce dary, převraceli soud.
4 Tsono akuluakulu onse a Israeli anasonkhana pamodzi ndipo anabwera kwa Samueli ku Rama.
Shromáždili se tedy všickni starší Izraelští, a přišli k Samuelovi do Ramata.
5 Iwo anati kwa iye “Taonani, inu mwakula tsopano ndipo ana anu sakutsata makhalidwe anu abwino. Tsono mutipatse mfumu kuti izitilamulira, monga momwe ikuchitira mitundu ina yonseyi.”
A řekli jemu: Aj, tys se již zstaral, a synové tvoji nechodí po cestách tvých; protož nyní ustanov nám krále, aby soudil nás, jakož jest u všech národů.
6 Koma mawu oti, “Mutipatse mfumu kuti izitilamulira,” sanakondweretse Samueli. Choncho anapemphera kwa Yehova.
I nelíbila se ta řeč Samuelovi, že řekli: Dej nám krále, aby nás soudil. Protož modlil se Samuel Hospodinu.
7 Yehova anamuyankha nati, “Mvera zonse zimene anthuwa akukuwuza. Si ndiwe amene akumukana, koma akukana Ine kuti ndikhale mfumu yawo.
Tedy řekl Hospodin Samuelovi: Uposlechni hlasu lidu ve všem, což mluví tobě; nebo ne tebouť jsou pohrdli, ale mnou pohrdli, abych nekraloval nad nimi.
8 Kuyambira tsiku limene ndinawatulutsa mʼdziko la Igupto mpaka lero zochita zawo zakhala zondikana Ine nʼkumatumikira milungu ina. Tsopano akukukananso iwe.
Podlé všech skutků těch, kteréž činili od onoho dne, v němž jsem je vyvedl z Egypta až do tohoto dne, kdyžto opustili mne, a sloužili bohům cizím, takť oni činí i tobě.
9 Tsono amvere zimene akunena, koma uwachenjeze kwambiri ndipo uwawuzitse za khalidwe la mfumu imene idzawalamulire.”
Protož nyní uposlechni hlasu jejich, a však nejprv osvědč pilně před nimi, a oznam jim obyčej krále, kterýž nad nimi kralovati bude.
10 Samueli anawawuza anthu amene amamupempha mfumu aja mawu onse a Yehova.
I mluvil Samuel všecky řeči Hospodinovy k lidu, kteříž krále žádali od něho.
11 Iye anati, “Zimene mfumu imene idzakulamulireniyo idzachite ndi izi: Izidzatenga ana anu aamuna kuti akhale ankhondo ake; ena pa magaleta ake, ena pa akavalo ake ndipo ena othamanga patsogolo pa magaleta akewo.
A řekl: Tento bude obyčej krále, kterýž kralovati bude nad vámi: Bráti bude syny vaše, a dá je k vozům svým, a zdělá sobě z nich jezdce, a běhati budou před vozem jeho.
12 Ena adzawayika kukhala olamulira asilikali 1,000, ena olamulira asilikali makumi asanu, ndi ena otipula minda yake, ndi kukolola ndiponso ena adzakhala osula zida zankhondo ndi zida za magaleta ake.
Také ustanoví je sobě za hejtmany nad tisíci a za padesátníky, a aby jemu orali rolí jeho, a žali obilé jeho, též aby jemu dělali nástroje válečné a přípravy k vozům jeho.
13 Iyo idzatenga ana anu akazi kuti akhale oyenga mafuta onunkhira, ophika chakudya ndi kupanga buledi.
Dcery také vaše bráti bude, aby dělaly masti, a byly kuchařky a pekařky.
14 Idzatenga minda yanu yabwino ya mpesa ndi ya mitengo ya olivi ndipo adzayipereka kwa antchito ake.
Nadto pole vaše a vinice vaše, i olivoví vaše nejvýbornější pobéře a rozdá služebníkům svým.
15 Idzatenga gawo lakhumi la tirigu wanu ndi mphesa zanu ndi kupereka kwa nduna zake ndi akapitawo ake.
Také z toho, což vsejete, a z vinic vašich desátky bráti bude, a dá komorníkům a služebníkům svým.
16 Mfumuyo idzatenga antchito anu aamuna ndi aakazi. Idzatenganso ngʼombe zanu zabwino ndi abulu anu nʼkumazingwiritsa ntchito.
Též služebníky vaše a děvky vaše, a mládence vaše nejzpůsobnější, i osly vaše vezme, aby jimi dělal dílo své.
17 Iyo idzatenga gawo lakhumi la zoweta zanu, ndipo inu eni mudzakhala akapolo ake.
Z stád vašich desátky bráti bude, a vy budete jemu za služebníky.
18 Nthawi imeneyo ikadzafika inu mudzalira momvetsa chisoni chifukwa cha mfumu imene mwadzisankhira, koma Yehova sadzakuyankhani.”
I budete volati v ten den příčinou krále vašeho, kteréhož byste sobě vyvolili, a nevyslyší vás Hospodin dne toho.
19 Koma anthu anakana kumumvera Samueli. Iwo anati, “Ayi! Ife tikufuna mfumu yotilamulira.
Nechtěl však lid uposlechnouti řeči Samuelovy, a řekli: Nikoli, ale král bude nad námi,
20 Kotero ifenso tidzakhala ngati mayiko ena. Mfumu yathu idzatiweruza ndiponso idzatuluka nafe kutitsogolera kukamenya nkhondo.”
Abychom i my také byli, jako všickni jiní národové, a souditi nás bude král náš, a vycházeje před námi, bojovati bude za nás.
21 Samueli atamva zonse zimene anthuwo ananena, iye anakazifotokozanso kwa Yehova.
Vyslyšev tedy Samuel všecka slova lidu, oznámil je Hospodinu.
22 Yehova anamuyankha nati, “Amvere zimene akunena ndipo apatse mfumu.” Ndipo Samueli anati kwa Aisraeli aja, “Bwererani aliyense kwawo.”
I řekl Hospodin Samuelovi: Uposlechni hlasu jejich, a ustanov jim krále. Protož řekl Samuel mužům Izraelským: Jdětež jeden každý do města svého.

< 1 Samueli 8 >