< 1 Samueli 7 >

1 Choncho anthu a ku Kiriati-Yearimu anabwera ndi kudzatenga Bokosi la Yehova. Iwo anapita nalo ku nyumba ya Abinadabu ya ku phiri ndipo anapatula Eliezara mwana wake kuti aziyangʼanira Bokosi la Yehovalo.
Ngakho abantu baseKhiriyathi-Jeyarimi beza balithatha ibhokisi lesivumelwano sikaThixo. Balisa endlini ka-Abhinadabi eqaqeni bangcwelisa u-Eliyazari indodana yakhe ukuba agcine ibhokisi lesivumelwano sikaThixo.
2 Zaka makumi awiri zinapita kuyambira pamene Bokosi la Yehova linakhala ku Kiriati-Yearimu, ndipo anthu a Israeli onse analira kupempha Yehova kuti awathandize.
Kwakuyisikhathi eside, iminyaka engamatshumi amabili isiyonke, ibhokisi lesivumelwano liseKhiriyathi-Jeyarimi. Njalo bonke abantu bako-Israyeli bakhala befuna uThixo.
3 Ndipo Samueli anati kwa nyumba yonse ya Israeli, “Ngati mukubwerera kwa Yehova ndi mtima wanu wonse, muchotse milungu yachilendo ndi Asiteroti pakati panu ndipo mitima yanu ikhazikike pa Yehova ndi kutumikira Iye yekha. Mukatero Iye adzakupulumutsani mʼmanja mwa Afilisti.”
USamuyeli wasesithi kuyo yonke indlu ka-Israyeli, “Nxa libuyela kuThixo ngezinhliziyo zenu zonke zehlukaniseni labonkulunkulu bezizweni labo-Ashithorethi lizinikele kuThixo njalo likhonze yena kuphela, uzalikhulula esandleni samaFilistiya.”
4 Choncho Aisraeli anachotsa milungu yawo ya Baala ndi Asitoreti ndi kutumikira Yehova yekha.
Ngakho abako-Israyeli babalahla oBhali babo labo-Ashithorethi, bakhonza uThixo kuphela.
5 Kenaka Samueli anati, “Sonkhanitsani Aisraeli onse ku Mizipa ndipo ine ndidzakupemphererani kwa Yehova.”
USamuyeli wasesithi, “Buthanisani u-Israyeli wonke eMizipha mina ngizalikhulekela kuThixo.”
6 Choncho anasonkhana ku Mizipa, ndipo anatunga madzi ndi kuwathira pansi pamaso pa Yehova. Pa tsiku limenelo anasala kudya namanena kuti, “Ife tachimwira Yehova.” Ndipo Samueli anali mtsogoleri wa Israeli ku Mizipa.
Kwathi sebebuthene eMizipha, bakha amanzi bawathela phambi kukaThixo. Ngalolosuku bazila njalo bavuma izono zabo khonapho besithi, “Sonile.” Njalo uSamuyeli wahlulela abantu bako-Israyeli eMizipha.
7 Afilisti anamva kuti Aisraeli asonkhana ku Mizipa, choncho akalonga awo anabwera kudzawathira nkhondo. Ndipo Aisraeli atamva anachita mantha chifukwa cha Afilisti.
Kwathi amaFilistiya esizwa ukuthi u-Israyeli wayebuthene eMizipha, ababusi bamaFilistiya baya khona ukuyabahlasela. Kwathi abako-Israyeli bekuzwa, besaba ngenxa yamaFilistiya.
8 Choncho anati kwa Samueli, “Musasiye kutipempherera kwa Yehova Mulungu wathu, kuti atipulumutse mʼdzanja la Afilistiwa.”
Bathi kuSamuyeli, “Ungayekeli ukusikhalela kuThixo uNkulunkulu wethu ukuba asihlenge esandleni samaFilistiya.”
9 Ndipo Samueli anatenga mwana wankhosa wamkazi woyamwa ndi kumupereka monga nsembe yopsereza kwa Yehova. Iye anapemphera kwa Yehova mʼmalo mwa Aisraeli, ndipo Yehova anamuyankha.
USamuyeli wathatha iwundlu elimunyayo walinikela kuThixo njengomnikelo opheleleyo wokutshiswa. Wamkhulekela kuThixo u-Israyeli, uThixo wamphendula.
10 Samueli akupereka nsembe yopsereza, Afilisti anayandikira kuti ayambe kuwathira nkhondo Aisraeli. Koma tsiku limenelo Yehova anawaopseza Afilisti aja ndi mawu aakulu ngati bingu. Choncho anasokonezeka motero kuti Aisraeli anawagonjetsa.
Kwathi uSamuyeli enikela umnikelo wokutshiswa, amaFilistiya asondela eduze ukuba alwe lo-Israyeli. Kodwa mhlalokho uThixo waduma ngomdumo omkhulu emelane lamaFilistiya wawenza athuthumela kangangoba aze achithwachithwa phambi kwabako-Israyeli.
11 Aisraeli anatuluka ku Mizipa kuthamangitsa Afilisti aja nʼkumawapha mʼnjira yonse mpaka kumunsi kwa Beti-Kari.
Abantu bako-Israyeli bagijima bephuma eMizipha baxotshana lamaFilistiya bewabulala endleleni baze bayafika endaweni engaphansi kweBhethi-Khari.
12 Kenaka Samueli anatenga mwala nawuyika pakati pa Mizipa ndi Seni. Iye anawutcha Ebenezeri, popeza anati, “Yehova watithandiza mpaka pano.”
USamuyeli wasethatha ilitshe walimisa phakathi kweMizipha leSheni. Walibiza ngokuthi yi-Ebhenezeri, esithi, “Kuze kube khathesi uThixo usisizile.”
13 Kotero Afilisti anagonjetsedwa ndipo sanadzalowenso mʼdziko la Israeli. Yehova analimbana ndi Afilisti masiku onse a Samueli.
Ngakho amaFilistiya anqotshwa njalo kawazange ahlasele ilizwe lako-Israyeli futhi. Kuyo yonke impilo kaSamuyeli, isandla sikaThixo sasimelane lamaFilistiya.
14 Mizinda yonse imene Afilisti analanda kuchokera ku Ekroni mpaka ku Gati inabwezedwa kwa Aisraeli. Choncho Aisraeli anapulumutsa dziko lawo. Ndipo panalinso mtendere pakati pa Aisraeli ndi Aamori.
Amadolobho kusukela e-Ekroni kusiya eGathi ayethunjwe ngamaFilistiya ku-Israyeli abuyiselwa kuye, njalo u-Israyeli wakhulula ilizwe eliseduze emandleni amaFilistiya. Njalo kwaba lokuthula phakathi kuka-Israyeli lama-Amori.
15 Samueli anatsogolera Aisraeli moyo wake wonse.
USamuyeli waqhubeka engumahluleli ka-Israyeli kuzozonke insuku zokuphila kwakhe.
16 Chaka ndi chaka Samueli ankakonza ulendo wozungulira kuchokera ku Beteli mpaka ku Giligala ndi Mizipa, kuweruza milandu ya Aisraeli mʼmadera onsewa.
Iminyaka ngeminyaka wayenquma esuka eBhetheli aye eGiligali leMizipha, esahlulela u-Israyeli kuzozonke lezindawo.
17 Koma pambuyo pake ankabwerera ku Rama, kumene kunali nyumba yake. Ankaweruza Aisraeli kumeneko. Ndipo iye anamanga guwa lansembe la Yehova kumeneko.
Kodwa wayehlezi ebuyela eRama lapho okwakulomuzi wakhe khona, lakhona wahlulela u-Israyeli. Njalo wakhela uThixo i-alithari.

< 1 Samueli 7 >