< 1 Samueli 7 >
1 Choncho anthu a ku Kiriati-Yearimu anabwera ndi kudzatenga Bokosi la Yehova. Iwo anapita nalo ku nyumba ya Abinadabu ya ku phiri ndipo anapatula Eliezara mwana wake kuti aziyangʼanira Bokosi la Yehovalo.
Les hommes de Cariathiarim vinrent donc, ramenèrent l’arche du Seigneur, et la transportèrent dans la maison d’Abinadad à Gabaa: mais ils sanctifièrent Eléazar, son fils, afin qu’il gardât l’arche du Seigneur.
2 Zaka makumi awiri zinapita kuyambira pamene Bokosi la Yehova linakhala ku Kiriati-Yearimu, ndipo anthu a Israeli onse analira kupempha Yehova kuti awathandize.
Et il arriva que depuis le jour où l’arche du Seigneur demeura à Cariathiarim, les jours se multiplièrent (car c’était déjà la vingtième année); et toute la maison d’Israël se reposa à l’abri du Seigneur.
3 Ndipo Samueli anati kwa nyumba yonse ya Israeli, “Ngati mukubwerera kwa Yehova ndi mtima wanu wonse, muchotse milungu yachilendo ndi Asiteroti pakati panu ndipo mitima yanu ikhazikike pa Yehova ndi kutumikira Iye yekha. Mukatero Iye adzakupulumutsani mʼmanja mwa Afilisti.”
Et Samuel s’adressa à toute la maison d’Israël, disant: Si c’est en tout votre cœur que vous revenez au Seigneur, ôtez d’au milieu de vous les dieux étrangers, les Baalim et les Astaroth, et préparez vos cœurs pour le Seigneur, ne servez que lui, et il vous délivrera de la main des Philistins.
4 Choncho Aisraeli anachotsa milungu yawo ya Baala ndi Asitoreti ndi kutumikira Yehova yekha.
Les enfants d’Israël enlevèrent donc les Baalim et les Astaroth, et ne servirent que le Seigneur.
5 Kenaka Samueli anati, “Sonkhanitsani Aisraeli onse ku Mizipa ndipo ine ndidzakupemphererani kwa Yehova.”
Or Samuel dit: Rassemblez tout Israël à Masphath, afin que je prie pour vous le Seigneur.
6 Choncho anasonkhana ku Mizipa, ndipo anatunga madzi ndi kuwathira pansi pamaso pa Yehova. Pa tsiku limenelo anasala kudya namanena kuti, “Ife tachimwira Yehova.” Ndipo Samueli anali mtsogoleri wa Israeli ku Mizipa.
Et ils s’assemblèrent à Masphath; ils puisèrent de l’eau, et la répandirent en la présence du Seigneur; ils jeûnèrent aussi en ce jour, et ils dirent là: Nous avons péché contre le Seigneur. Et Samuel jugea les enfants d’Israël à Masphath.
7 Afilisti anamva kuti Aisraeli asonkhana ku Mizipa, choncho akalonga awo anabwera kudzawathira nkhondo. Ndipo Aisraeli atamva anachita mantha chifukwa cha Afilisti.
Cependant les Philistins apprirent que les enfants d’Israël s’étaient assemblés à Masphath, et les satrapes des Philistins montèrent vers Israël. Ce qu’ayant appris les enfants d’Israël, ils craignirent à l’aspect des Philistins.
8 Choncho anati kwa Samueli, “Musasiye kutipempherera kwa Yehova Mulungu wathu, kuti atipulumutse mʼdzanja la Afilistiwa.”
Et ils dirent à Samuel: Ne cessez point de crier pour nous vers le Seigneur notre Dieu, afin qu’il nous sauve de la main des Philistins.
9 Ndipo Samueli anatenga mwana wankhosa wamkazi woyamwa ndi kumupereka monga nsembe yopsereza kwa Yehova. Iye anapemphera kwa Yehova mʼmalo mwa Aisraeli, ndipo Yehova anamuyankha.
Samuel prit donc un agneau encore à la mamelle, et l’offrit tout entier en holocauste au Seigneur, et Samuel cria vers le Seigneur pour Israël, et le Seigneur l’exauça.
10 Samueli akupereka nsembe yopsereza, Afilisti anayandikira kuti ayambe kuwathira nkhondo Aisraeli. Koma tsiku limenelo Yehova anawaopseza Afilisti aja ndi mawu aakulu ngati bingu. Choncho anasokonezeka motero kuti Aisraeli anawagonjetsa.
Or, il arriva que, tandis que Samuel offrait l’holocauste, les Philistins engagèrent la bataille contre Israël; mais le Seigneur tonna avec un grand éclat ce jour-là sur les Philistins, et les épouvanta, et ils furent taillés en pièces à la face d’Israël.
11 Aisraeli anatuluka ku Mizipa kuthamangitsa Afilisti aja nʼkumawapha mʼnjira yonse mpaka kumunsi kwa Beti-Kari.
Et les hommes d’Israël, étant sortis de Masphath, poursuivirent les Philistins, et ils les battirent jusqu’au lieu qui était au-dessous de Bethchar.
12 Kenaka Samueli anatenga mwala nawuyika pakati pa Mizipa ndi Seni. Iye anawutcha Ebenezeri, popeza anati, “Yehova watithandiza mpaka pano.”
Or, Samuel prit une pierre, et la posa entre Masphath et entre Sen; et il appela ce lieu du nom de Pierre du secours, et il dit: C’est jusqu’ici que le Seigneur nous a secourus.
13 Kotero Afilisti anagonjetsedwa ndipo sanadzalowenso mʼdziko la Israeli. Yehova analimbana ndi Afilisti masiku onse a Samueli.
Ainsi, les Philistins furent humiliés, et ils n’entreprirent plus de venir sur les frontières d’Israël. C’est pourquoi la main du Seigneur fut sur les Philistins, pendant tous les jours de Samuel.
14 Mizinda yonse imene Afilisti analanda kuchokera ku Ekroni mpaka ku Gati inabwezedwa kwa Aisraeli. Choncho Aisraeli anapulumutsa dziko lawo. Ndipo panalinso mtendere pakati pa Aisraeli ndi Aamori.
Et les villes que les Philistins avaient enlevées à Israël, furent rendues à Israël, depuis Accaron jusqu’à Geth, de même que leurs confins: ainsi il délivra Israël de la main des Philistins; et la paix était entre Israël et l’Amorrhéen.
15 Samueli anatsogolera Aisraeli moyo wake wonse.
Samuel jugeait aussi Israël pendant tous les jours de sa vie;
16 Chaka ndi chaka Samueli ankakonza ulendo wozungulira kuchokera ku Beteli mpaka ku Giligala ndi Mizipa, kuweruza milandu ya Aisraeli mʼmadera onsewa.
Et il s’en allait chaque année parcourant Béthel, Galgala et Masphath, et il jugeait Israël dans les susdits lieux.
17 Koma pambuyo pake ankabwerera ku Rama, kumene kunali nyumba yake. Ankaweruza Aisraeli kumeneko. Ndipo iye anamanga guwa lansembe la Yehova kumeneko.
Il retournait ensuite à Ramatha, car là, était sa maison, et là il jugeait Israël; il bâtit là aussi un autel au Seigneur.