< 1 Samueli 7 >

1 Choncho anthu a ku Kiriati-Yearimu anabwera ndi kudzatenga Bokosi la Yehova. Iwo anapita nalo ku nyumba ya Abinadabu ya ku phiri ndipo anapatula Eliezara mwana wake kuti aziyangʼanira Bokosi la Yehovalo.
The men of Kiriath Jearim came and took up the ark of YHWH and brought it into the house of Abinadab, which was on the hill, and sanctified Eleazar his son to keep the ark of YHWH.
2 Zaka makumi awiri zinapita kuyambira pamene Bokosi la Yehova linakhala ku Kiriati-Yearimu, ndipo anthu a Israeli onse analira kupempha Yehova kuti awathandize.
It happened, from the day that the ark stayed in Kiriath Jearim, that the time was long; for it was twenty years: and all the house of Israel lamented after YHWH.
3 Ndipo Samueli anati kwa nyumba yonse ya Israeli, “Ngati mukubwerera kwa Yehova ndi mtima wanu wonse, muchotse milungu yachilendo ndi Asiteroti pakati panu ndipo mitima yanu ikhazikike pa Yehova ndi kutumikira Iye yekha. Mukatero Iye adzakupulumutsani mʼmanja mwa Afilisti.”
Samuel spoke to all the house of Israel, saying, "If you do return to YHWH with all your heart, then put away the foreign gods and the Ashtaroth from among you, and direct your hearts to YHWH, and serve him only; and he will deliver you out of the hand of the Philistines."
4 Choncho Aisraeli anachotsa milungu yawo ya Baala ndi Asitoreti ndi kutumikira Yehova yekha.
Then the children of Israel removed the Baals and the Ashtaroth, and served YHWH only.
5 Kenaka Samueli anati, “Sonkhanitsani Aisraeli onse ku Mizipa ndipo ine ndidzakupemphererani kwa Yehova.”
Samuel said, "Gather all Israel to Mizpah, and I will pray for you to YHWH."
6 Choncho anasonkhana ku Mizipa, ndipo anatunga madzi ndi kuwathira pansi pamaso pa Yehova. Pa tsiku limenelo anasala kudya namanena kuti, “Ife tachimwira Yehova.” Ndipo Samueli anali mtsogoleri wa Israeli ku Mizipa.
They gathered together to Mizpah, and drew water, and poured it out before YHWH, and fasted on that day, and said, "We have sinned against YHWH." Samuel judged the children of Israel in Mizpah.
7 Afilisti anamva kuti Aisraeli asonkhana ku Mizipa, choncho akalonga awo anabwera kudzawathira nkhondo. Ndipo Aisraeli atamva anachita mantha chifukwa cha Afilisti.
When the Philistines heard that the children of Israel were gathered together at Mizpah, the lords of the Philistines went up against Israel. When the children of Israel heard it, they were afraid of the Philistines.
8 Choncho anati kwa Samueli, “Musasiye kutipempherera kwa Yehova Mulungu wathu, kuti atipulumutse mʼdzanja la Afilistiwa.”
The children of Israel said to Samuel, "Do not cease to cry to YHWH our God for us, that he will save us out of the hand of the Philistines."
9 Ndipo Samueli anatenga mwana wankhosa wamkazi woyamwa ndi kumupereka monga nsembe yopsereza kwa Yehova. Iye anapemphera kwa Yehova mʼmalo mwa Aisraeli, ndipo Yehova anamuyankha.
Samuel took a suckling lamb, and offered it for a whole burnt offering to YHWH: and Samuel cried to YHWH for Israel; and YHWH answered him.
10 Samueli akupereka nsembe yopsereza, Afilisti anayandikira kuti ayambe kuwathira nkhondo Aisraeli. Koma tsiku limenelo Yehova anawaopseza Afilisti aja ndi mawu aakulu ngati bingu. Choncho anasokonezeka motero kuti Aisraeli anawagonjetsa.
As Samuel was offering up the burnt offering, the Philistines drew near to battle against Israel; but YHWH thundered with a great thunder on that day on the Philistines, and confused them; and they were struck down before Israel.
11 Aisraeli anatuluka ku Mizipa kuthamangitsa Afilisti aja nʼkumawapha mʼnjira yonse mpaka kumunsi kwa Beti-Kari.
The men of Israel went out of Mizpah, and pursued the Philistines, and struck them, as far as below Beth Kar.
12 Kenaka Samueli anatenga mwala nawuyika pakati pa Mizipa ndi Seni. Iye anawutcha Ebenezeri, popeza anati, “Yehova watithandiza mpaka pano.”
Then Samuel took a stone, and set it between Mizpah and Jashan, and called its name Ebenezer, saying, "YHWH helped us until now."
13 Kotero Afilisti anagonjetsedwa ndipo sanadzalowenso mʼdziko la Israeli. Yehova analimbana ndi Afilisti masiku onse a Samueli.
So the Philistines were subdued, and they came no more within the territory of Israel. The hand of YHWH was against the Philistines all the days of Samuel.
14 Mizinda yonse imene Afilisti analanda kuchokera ku Ekroni mpaka ku Gati inabwezedwa kwa Aisraeli. Choncho Aisraeli anapulumutsa dziko lawo. Ndipo panalinso mtendere pakati pa Aisraeli ndi Aamori.
The cities which the Philistines had taken from Israel were restored to Israel, from Ekron even to Gath; and Israel recovered its territory out of the hand of the Philistines. There was peace between Israel and the Amorites.
15 Samueli anatsogolera Aisraeli moyo wake wonse.
Samuel judged Israel all the days of his life.
16 Chaka ndi chaka Samueli ankakonza ulendo wozungulira kuchokera ku Beteli mpaka ku Giligala ndi Mizipa, kuweruza milandu ya Aisraeli mʼmadera onsewa.
He went from year to year in circuit to Bethel and Gilgal, and Mizpah; and he judged Israel in all those places.
17 Koma pambuyo pake ankabwerera ku Rama, kumene kunali nyumba yake. Ankaweruza Aisraeli kumeneko. Ndipo iye anamanga guwa lansembe la Yehova kumeneko.
His return was to Ramah, for there was his house; and there he judged Israel: and he built there an altar to YHWH.

< 1 Samueli 7 >