< 1 Samueli 7 >
1 Choncho anthu a ku Kiriati-Yearimu anabwera ndi kudzatenga Bokosi la Yehova. Iwo anapita nalo ku nyumba ya Abinadabu ya ku phiri ndipo anapatula Eliezara mwana wake kuti aziyangʼanira Bokosi la Yehovalo.
And the men of Kiryath-ye'arim came, and fetched up the ark of the Lord, and brought it unto the house of Abinadab on the hill, and Elazar his son they sanctified to guard the ark of the Lord.
2 Zaka makumi awiri zinapita kuyambira pamene Bokosi la Yehova linakhala ku Kiriati-Yearimu, ndipo anthu a Israeli onse analira kupempha Yehova kuti awathandize.
And it came to pass, from the time the ark remained in Kiryath-ye'arim, and the time was long, and it was twenty years: that all the house of Israel followed anxiously after the Lord.
3 Ndipo Samueli anati kwa nyumba yonse ya Israeli, “Ngati mukubwerera kwa Yehova ndi mtima wanu wonse, muchotse milungu yachilendo ndi Asiteroti pakati panu ndipo mitima yanu ikhazikike pa Yehova ndi kutumikira Iye yekha. Mukatero Iye adzakupulumutsani mʼmanja mwa Afilisti.”
And Samuel said unto all the house of Israel, as followeth, If with all your heart ye do return unto the Lord, then put away the gods of the stranger and the 'Ashtaroth from your midst, and direct your heart unto the Lord, and serve him alone: and then will he deliver you out of the hand of the Philistines.
4 Choncho Aisraeli anachotsa milungu yawo ya Baala ndi Asitoreti ndi kutumikira Yehova yekha.
Then did the children of Israel put away the Be'alim and the 'Ashtaroth, and served the Lord alone.
5 Kenaka Samueli anati, “Sonkhanitsani Aisraeli onse ku Mizipa ndipo ine ndidzakupemphererani kwa Yehova.”
And Samuel said, Assemble all Israel together at Mizpah, and I will pray in your behalf unto the Lord.
6 Choncho anasonkhana ku Mizipa, ndipo anatunga madzi ndi kuwathira pansi pamaso pa Yehova. Pa tsiku limenelo anasala kudya namanena kuti, “Ife tachimwira Yehova.” Ndipo Samueli anali mtsogoleri wa Israeli ku Mizipa.
And they assembled themselves together at Mizpah, and drew water, and poured it out before the Lord, and fasted on that day, and said there, We have sinned against the Lord. And Samuel judged the children of Israel in Mizpah.
7 Afilisti anamva kuti Aisraeli asonkhana ku Mizipa, choncho akalonga awo anabwera kudzawathira nkhondo. Ndipo Aisraeli atamva anachita mantha chifukwa cha Afilisti.
And when the Philistines heard that the children of Israel had assembled themselves at Mizpah, the lords of the Philistines went up against Israel. And when the children of Israel heard it, they were afraid of the Philistines.
8 Choncho anati kwa Samueli, “Musasiye kutipempherera kwa Yehova Mulungu wathu, kuti atipulumutse mʼdzanja la Afilistiwa.”
And the children of Israel said to Samuel, Do not abstain, so as not to cry for us unto the Lord our God, that he may help us out of the hand of the Philistines.
9 Ndipo Samueli anatenga mwana wankhosa wamkazi woyamwa ndi kumupereka monga nsembe yopsereza kwa Yehova. Iye anapemphera kwa Yehova mʼmalo mwa Aisraeli, ndipo Yehova anamuyankha.
And Samuel took one sucking lamb, and offered it for an entire burnt-offering unto the Lord: and Samuel cried unto the Lord in behalf of Israel; and the Lord answered him.
10 Samueli akupereka nsembe yopsereza, Afilisti anayandikira kuti ayambe kuwathira nkhondo Aisraeli. Koma tsiku limenelo Yehova anawaopseza Afilisti aja ndi mawu aakulu ngati bingu. Choncho anasokonezeka motero kuti Aisraeli anawagonjetsa.
And as Samuel was offering up the burnt-offering, the Philistines drew near to battle against Israel; but the Lord thundered with a loud noise on that day over the Philistines, and brought them into confusion, and they were smitten before Israel.
11 Aisraeli anatuluka ku Mizipa kuthamangitsa Afilisti aja nʼkumawapha mʼnjira yonse mpaka kumunsi kwa Beti-Kari.
And the men of Israel went out of Mizpah, and pursued the Philistines, and smote them, as far as below Beth-car.
12 Kenaka Samueli anatenga mwala nawuyika pakati pa Mizipa ndi Seni. Iye anawutcha Ebenezeri, popeza anati, “Yehova watithandiza mpaka pano.”
And Samuel took one stone, and set it between Mizpah and Shen, and called its name Eben-ha'ezer, saying, As far as this hath the Lord helped us.
13 Kotero Afilisti anagonjetsedwa ndipo sanadzalowenso mʼdziko la Israeli. Yehova analimbana ndi Afilisti masiku onse a Samueli.
So were the Philistines humbled, and they came no more into the territory of Israel; and the hand of the Lord was against the Philistines all the days of Samuel.
14 Mizinda yonse imene Afilisti analanda kuchokera ku Ekroni mpaka ku Gati inabwezedwa kwa Aisraeli. Choncho Aisraeli anapulumutsa dziko lawo. Ndipo panalinso mtendere pakati pa Aisraeli ndi Aamori.
And the cities which the Philistines had taken from Israel came again to Israel, from 'Ekron even unto Gath, and their territory did Israel deliver out of the hand of the Philistines. And there was peace between Israel and the Emorites.
15 Samueli anatsogolera Aisraeli moyo wake wonse.
And Samuel judged Israel all the days of his life.
16 Chaka ndi chaka Samueli ankakonza ulendo wozungulira kuchokera ku Beteli mpaka ku Giligala ndi Mizipa, kuweruza milandu ya Aisraeli mʼmadera onsewa.
And he went from year to year and traveled in circuit to Beth-el, and Gilgal, and Mizpah, and judged Israel in all these places.
17 Koma pambuyo pake ankabwerera ku Rama, kumene kunali nyumba yake. Ankaweruza Aisraeli kumeneko. Ndipo iye anamanga guwa lansembe la Yehova kumeneko.
And his return was to Ramah; for there was his house; and there he judged Israel: and he built there an altar unto the Lord.