< 1 Samueli 7 >

1 Choncho anthu a ku Kiriati-Yearimu anabwera ndi kudzatenga Bokosi la Yehova. Iwo anapita nalo ku nyumba ya Abinadabu ya ku phiri ndipo anapatula Eliezara mwana wake kuti aziyangʼanira Bokosi la Yehovalo.
And then men of Cariathiarim came and fetched up the ark of the Lord and carried it into the house of Abinadab in Gabaa: and they sanctified Eleazar his son, to keep the ark of the Lord.
2 Zaka makumi awiri zinapita kuyambira pamene Bokosi la Yehova linakhala ku Kiriati-Yearimu, ndipo anthu a Israeli onse analira kupempha Yehova kuti awathandize.
And it came to pass, that from the day the ark of the Lord abode in Cariathiarim days were multiplied, (for it was now the twentieth year, ) and all the house of Israel rested following the Lord.
3 Ndipo Samueli anati kwa nyumba yonse ya Israeli, “Ngati mukubwerera kwa Yehova ndi mtima wanu wonse, muchotse milungu yachilendo ndi Asiteroti pakati panu ndipo mitima yanu ikhazikike pa Yehova ndi kutumikira Iye yekha. Mukatero Iye adzakupulumutsani mʼmanja mwa Afilisti.”
And Samuel spoke to all the house of Israel, saying: If you turn to the Lord with all your heart, put away the strange gods from among you, Baalim and Astaroth: and prepare your hearts unto the Lord, and serve him only, and he will deliver you out of the hand of the Philistines.
4 Choncho Aisraeli anachotsa milungu yawo ya Baala ndi Asitoreti ndi kutumikira Yehova yekha.
Then the children of Israel put away Baalim and Astaroth, and served the Lord only.
5 Kenaka Samueli anati, “Sonkhanitsani Aisraeli onse ku Mizipa ndipo ine ndidzakupemphererani kwa Yehova.”
And Samuel said: Gather all Israel to Masphath, that I may pray to the Lord for you.
6 Choncho anasonkhana ku Mizipa, ndipo anatunga madzi ndi kuwathira pansi pamaso pa Yehova. Pa tsiku limenelo anasala kudya namanena kuti, “Ife tachimwira Yehova.” Ndipo Samueli anali mtsogoleri wa Israeli ku Mizipa.
And they gathered together to Masphath: and they drew water, and poured it out before the Lord, and they fasted on that day, and they said there: We have sinned against the Lord. And Samuel judged the children of Israel in Masphath.
7 Afilisti anamva kuti Aisraeli asonkhana ku Mizipa, choncho akalonga awo anabwera kudzawathira nkhondo. Ndipo Aisraeli atamva anachita mantha chifukwa cha Afilisti.
And the Philistines heard that the children of Israel were gathered together to Masphath, and the lords of the Philistines went up against Israel. And when the children of Israel heard this, they were afraid of the Philistines.
8 Choncho anati kwa Samueli, “Musasiye kutipempherera kwa Yehova Mulungu wathu, kuti atipulumutse mʼdzanja la Afilistiwa.”
And they said to Samuel: Cease not to cry to the Lord our God for us, that he may save us out of the hand of the Philistines.
9 Ndipo Samueli anatenga mwana wankhosa wamkazi woyamwa ndi kumupereka monga nsembe yopsereza kwa Yehova. Iye anapemphera kwa Yehova mʼmalo mwa Aisraeli, ndipo Yehova anamuyankha.
And Samuel took a sucking lamb, and offered it whole for a holocaust to the Lord: and Samuel cried to the Lord for Israel, and the Lord heard him.
10 Samueli akupereka nsembe yopsereza, Afilisti anayandikira kuti ayambe kuwathira nkhondo Aisraeli. Koma tsiku limenelo Yehova anawaopseza Afilisti aja ndi mawu aakulu ngati bingu. Choncho anasokonezeka motero kuti Aisraeli anawagonjetsa.
And it came to pass, when Samuel was offering the holocaust, the Philistines began the battle against Israel: but the Lord thundered with a great thunder on that day upon the Philistines, and terrified them, and they were overthrown before the face of Israel.
11 Aisraeli anatuluka ku Mizipa kuthamangitsa Afilisti aja nʼkumawapha mʼnjira yonse mpaka kumunsi kwa Beti-Kari.
And the men of Israel going out of Masphath pursued after the Philistines, and made slaughter of them till they came under Bethchar.
12 Kenaka Samueli anatenga mwala nawuyika pakati pa Mizipa ndi Seni. Iye anawutcha Ebenezeri, popeza anati, “Yehova watithandiza mpaka pano.”
And Samuel took a stone, and laid it between Masphath and Sen: and he called the place, the Stone of help. And he said: Thus far the Lord hath helped us.
13 Kotero Afilisti anagonjetsedwa ndipo sanadzalowenso mʼdziko la Israeli. Yehova analimbana ndi Afilisti masiku onse a Samueli.
And the Philistines were humbled, and they did not come any more into the borders of Israel. And the hand of the Lord was against the Philistines, all the days of Samuel.
14 Mizinda yonse imene Afilisti analanda kuchokera ku Ekroni mpaka ku Gati inabwezedwa kwa Aisraeli. Choncho Aisraeli anapulumutsa dziko lawo. Ndipo panalinso mtendere pakati pa Aisraeli ndi Aamori.
And the cities, which the Philistines had taken from Israel, were restored to Israel, from Accaron to Geth, and their borders: and he delivered Israel from the hand of the Philistines, and there was peace between Israel and the Amorrhites.
15 Samueli anatsogolera Aisraeli moyo wake wonse.
And Samuel judged Israel all the days of his life:
16 Chaka ndi chaka Samueli ankakonza ulendo wozungulira kuchokera ku Beteli mpaka ku Giligala ndi Mizipa, kuweruza milandu ya Aisraeli mʼmadera onsewa.
And he went every year about to Bethel and to Galgal and to Masphath, and he judged Israel in the aforesaid places.
17 Koma pambuyo pake ankabwerera ku Rama, kumene kunali nyumba yake. Ankaweruza Aisraeli kumeneko. Ndipo iye anamanga guwa lansembe la Yehova kumeneko.
And he returned to Ramatha, for there was his house, and there he judged Israel: he built also there an altar to the Lord.

< 1 Samueli 7 >