< 1 Samueli 7 >

1 Choncho anthu a ku Kiriati-Yearimu anabwera ndi kudzatenga Bokosi la Yehova. Iwo anapita nalo ku nyumba ya Abinadabu ya ku phiri ndipo anapatula Eliezara mwana wake kuti aziyangʼanira Bokosi la Yehovalo.
Og Mændene af Kirjath-Jearim kom og hentede Herrens Ark op og førte den til Abinadabs Hus paa Højen; og de helligede hans Søn Eleasar til at tage Vare paa Herrens Ark.
2 Zaka makumi awiri zinapita kuyambira pamene Bokosi la Yehova linakhala ku Kiriati-Yearimu, ndipo anthu a Israeli onse analira kupempha Yehova kuti awathandize.
Og fra den Dag, at Arken blev i Kirjath-Jearim, forløb lang Tid, saa at det blev tyve Aar, og hele Israels Hus sukkede efter Herren.
3 Ndipo Samueli anati kwa nyumba yonse ya Israeli, “Ngati mukubwerera kwa Yehova ndi mtima wanu wonse, muchotse milungu yachilendo ndi Asiteroti pakati panu ndipo mitima yanu ikhazikike pa Yehova ndi kutumikira Iye yekha. Mukatero Iye adzakupulumutsani mʼmanja mwa Afilisti.”
Da talede Samuel til al Israels Hus, sigende: Dersom I omvende eder til Herren af eders ganske Hjerte, saa borttager de fremmede Guder og Astartebillederne af eders Midte, og bereder eders Hjerte til Herren og tjener ham alene, og han skal fri eder af Filisternes Haand.
4 Choncho Aisraeli anachotsa milungu yawo ya Baala ndi Asitoreti ndi kutumikira Yehova yekha.
Da borttoge Israels Børn Baal og Astartebillederne, og de tjente Herren alene.
5 Kenaka Samueli anati, “Sonkhanitsani Aisraeli onse ku Mizipa ndipo ine ndidzakupemphererani kwa Yehova.”
Og Samuel sagde: Samler al Israel til Mizpa, og jeg vil ydmygeligen bede for eder til Herren.
6 Choncho anasonkhana ku Mizipa, ndipo anatunga madzi ndi kuwathira pansi pamaso pa Yehova. Pa tsiku limenelo anasala kudya namanena kuti, “Ife tachimwira Yehova.” Ndipo Samueli anali mtsogoleri wa Israeli ku Mizipa.
Og de samledes til Mizpa, og de droge Vand op og udøste det for Herrens Ansigt og fastede paa samme Dag og sagde der: Vi have syndet for Herren; og Samuel dømte Israels Børn i Mizpa.
7 Afilisti anamva kuti Aisraeli asonkhana ku Mizipa, choncho akalonga awo anabwera kudzawathira nkhondo. Ndipo Aisraeli atamva anachita mantha chifukwa cha Afilisti.
Der Filisterne hørte, at Israels Børn havde samlet sig i Mizpa, da droge Filisternes Fyrster op mod Israel; der Israels Børn hørte det, da frygtede de for Filisternes Ansigt.
8 Choncho anati kwa Samueli, “Musasiye kutipempherera kwa Yehova Mulungu wathu, kuti atipulumutse mʼdzanja la Afilistiwa.”
Og Israels Børn sagde til Samuel: Hør ikke op med at raabe for os til Herren vor Gud, at han frelser os fra Filisternes Haand.
9 Ndipo Samueli anatenga mwana wankhosa wamkazi woyamwa ndi kumupereka monga nsembe yopsereza kwa Yehova. Iye anapemphera kwa Yehova mʼmalo mwa Aisraeli, ndipo Yehova anamuyankha.
Saa tog Samuel et diende Lam og ofrede det til et Brændoffer helt for Herren; og Samuel raabte til Herren for Israel, og Herren svarede ham.
10 Samueli akupereka nsembe yopsereza, Afilisti anayandikira kuti ayambe kuwathira nkhondo Aisraeli. Koma tsiku limenelo Yehova anawaopseza Afilisti aja ndi mawu aakulu ngati bingu. Choncho anasokonezeka motero kuti Aisraeli anawagonjetsa.
Og Samuel ofrede Brændofret, og Filisterne kom frem til Krigen imod Israel; men Herren lod tordne med en svar Torden paa den samme Dag over Filisterne og forfærdede dem, og de bleve slagne for Israels Ansigt.
11 Aisraeli anatuluka ku Mizipa kuthamangitsa Afilisti aja nʼkumawapha mʼnjira yonse mpaka kumunsi kwa Beti-Kari.
Og Israels Mænd droge ud af Mizpa og forfulgte Filisterne; og de sloge dem indtil neden for Beth-Kar.
12 Kenaka Samueli anatenga mwala nawuyika pakati pa Mizipa ndi Seni. Iye anawutcha Ebenezeri, popeza anati, “Yehova watithandiza mpaka pano.”
Da tog Samuel en Sten og satte den imellem Mizpa og imellem Sen og kaldte dens Navn Eben-Ezer; og han sagde: Hidindtil har Herren hjulpet os.
13 Kotero Afilisti anagonjetsedwa ndipo sanadzalowenso mʼdziko la Israeli. Yehova analimbana ndi Afilisti masiku onse a Samueli.
Saa bleve Filisterne ydmygede og kom ikke ydermere i Israels Landemærke, og Herrens Haand var imod Filisterne, saa længe Samuel levede.
14 Mizinda yonse imene Afilisti analanda kuchokera ku Ekroni mpaka ku Gati inabwezedwa kwa Aisraeli. Choncho Aisraeli anapulumutsa dziko lawo. Ndipo panalinso mtendere pakati pa Aisraeli ndi Aamori.
Og de Stæder, som Filisterne havde taget fra Israel, kom til Israel igen, fra Ekron og indtil Gath; tilmed udfriede Israel deres Landemærke af Filisternes Haand; men der var Fred imellem Israel og imellem Amoriterne.
15 Samueli anatsogolera Aisraeli moyo wake wonse.
Og Samuel dømte Israel alle sine Livsdage.
16 Chaka ndi chaka Samueli ankakonza ulendo wozungulira kuchokera ku Beteli mpaka ku Giligala ndi Mizipa, kuweruza milandu ya Aisraeli mʼmadera onsewa.
Og han gik hvert Aar og vandrede omkring til Bethel og Gilgal og Mizpa og dømte Israel i alle disse Stæder.
17 Koma pambuyo pake ankabwerera ku Rama, kumene kunali nyumba yake. Ankaweruza Aisraeli kumeneko. Ndipo iye anamanga guwa lansembe la Yehova kumeneko.
Og han kom tilbage til Rama, thi der var hans Hus, og der dømte han Israel; og han byggede der Herren et Alter.

< 1 Samueli 7 >