< 1 Samueli 6 >
1 Bokosi la Yehova linakhala mʼdziko la Afilisti kwa miyezi isanu ndi iwiri.
Rəbbina q'utye Filiştinaaşine cigabışee yighıble vazna avxu.
2 Tsono Afilisti anayitana ansembe ndi amawula ndipo anati, “Tichite nalo chiyani Bokosi la Yehova? Tiwuzeni momwe tidzalitumizira ku malo ake.”
Filiştinaaşe kaahinariy falika ilyaakanbı qopt'ul eyhen: – İne Rəbbine q'utyeyk hucoona ha'as? Şak'le eyhe, şi nəxübiy mana çine cigeeqa savaak'al haa'as?
3 Iwo anayankha kuti, “Ngati mufuna kubweza Bokosi la Mulungu wa Israeli, musalitumize wopanda kanthu, koma muyesetse kulitumiza pamodzi ndi nsembe yopepesera machimo. Mukatero mudzachiritsidwa, ndipo mudzadziwa chifukwa chiyani chilango cha Yehova sichikukuchokani.”
Manbışe eyhen: – İzrailyne Allahna q'utye yı'q'əlqa savaak'al haa'as vukkanxhee, mana q'ərab savaak'al hımaa'a. Şu mançinemee, taxsir şolyva Rəbbis pay haa'as vukkan. Mane gahıl şunab yug qeepxhesınbı, Mang'vee şoke nya'asiy xıl ts'ıts'dyaa'avad, ats'axhxhesın.
4 Afilisti anafunsanso kuti “Kodi ife tipereke nsembe yanji yopepesera machimo?” Iwo anayankha kuti, “Mupereke zifanizo zagolide za zithupsa zisanu ndi zamakoswe asanu malingana ndi chiwerengero cha akalonga a Afilisti popeza mliri womwewo wagwera inu ndi akalonga anu.
Filiştinaaşe qiyghanan: – Şal taxsirva nena payne Rəbbis haa'as vukkan? Kaahinaaşeyiy falika ilyaakanbışe eyhen: – Filiştinaaşika xhuleyre xərnayiy, hamanimen k'ınəəğəykena fıriy q'öv hav'u g'axuvle. Mana ver vuşdecab deş, vuşde ç'ak'ınbışdeb vuk'lelqa qabına.
5 Mupange zifanizo za zithupsa zisanu ndi za makoswe asanu amene akuwononga dziko lanu ndipo mupereke ulemu kwa Israeli. Mwina adzaleka kuzunza inu, milungu yanu ndi dziko lanu.
Mançil-alla fıraaşinıd, vuşda ölka q'əra qaa'ane q'övəəşinıd k'opyebı he'e, İzrailyne Allahısıb hı'rmat givxhe. Sayid manke, Mang'vee şokeb, vuşde allahaaşileb, vuşde cigabışileb xıl ts'ıts'aa'a.
6 Nʼchifukwa chiyani mukuwumitsa mitima monga anachita Aigupto ndi Farao? Mulungu atawalanga anthu a ku Igupto aja kodi suja anawalola Aisraeli kuti azipita ndipo anapitadi?
Misirbışeyiy fironee q'ı't'y k'eççuyn xhinne, şunad hıma'a. Allah manbışilqa rəhı'm dena qıxhamee, manbışe İzrailybı g'avkkuynbı.
7 “Tsopano konzani galeta latsopano limodzi ndiponso ngʼombe ziwiri zazikazi zamkaka zimene sizinavalepo goli. Muzimangirire ngʼombezo ku ngoloyo, koma ana awo muwachotse ndi kuwasiya kwanu.
Həşdemee sa ts'edın daşk'a hı'ı, mançik mısacab xamut qidyav'una q'ıkar gyooqa'ana q'öble zer avt'le. Q'ıkarmee mançike curu'u xaaqa qıkkee.
8 Mutenge Bokosi la Yehova ndi kuliyika pa galetapo ndipo pambali pake pakhale Bokosi, mʼmene muyikemonso zinthu zagolide zomwe mukutumiza kwa Iye monga nsembe yopepesera machimo. Kenaka, mulisiye lizipita.
Rəbbina q'utyeb alyapt'ı daşk'eeqa gyuvxhe, taxsir şolyva Mang'us allesın k'ınəəğəyken karbıd mançine k'anene yeşuk'eeqa gixhxhe. Qiyğaled daşk'a yəqqı'l hee'e hooracen.
9 Koma muziliyangʼana. Ngati lilondola njira yopita kwawo kwa Bokosilo mpaka ku Beti-Semesi ndiye kuti amene watichita zoyipa zazikulu zoterezi ndi Mulungu wa Israeli. Koma ngati silitero, ife tidzadziwa kuti sanali Mulungu wa Israeli amene watizunza koma kuti zinangochitika mwatsoka.”
Yı'q'əle saccu ilyaake. Man çine cigeeqa, Bet-Şemeşne suralqa atk'ınee, mana ver şalqa ooxuna Rəbb vornava eyhen vodun. Maqa idyapk'ıneeme, şak'le ats'axhxhesın, şas ı'xı'yn xıl Mang'un deşud. Man çiled-alqa ıxhayn kar vodun.
10 Anthu aja anachitadi zimenezi. Anatenga ngʼombe zamkaka ziwiri nazimanga ku galeta lija. Koma ana awo anawatsekera mʼkhola.
Nəxüdiy uvhu, insanaaşe məxüdud ha'an. Q'öble zer qabı daşk'ayk iviyt'al, mançin q'ıkarıd xaa g'alya'a.
11 Tsono anayika Bokosi la Yehova pa galeta pamodzi ndi bokosi limene munali makoswe agolide ndi zifanizo zawo za zithupsa.
Daşk'eeqa Rəbbine q'utyeyka sacigee, manbışe k'ınəəğəyke hı'iyn q'övərnanayiy fırarnana yeşuk giviyxhe.
12 Ngʼombe zija zinapita molunjika kutsata msewu wopita ku Beti Semesi zikulira njira yonse. Sizinakhotere kumanja kapena kumanzere. Akalonga a Afilisti anazitsatira mpaka mʼmalire a Beti-Semesi.
Mançile qiyğa zerbı qotkuda ayk'ananbı Bet-Şemeşne suralqa. Manbı sağılqa, solulqa siditk'ıl, sa yəq avqu, heğa-heğa ayk'ananbı. Filiştinaaşin ç'ak'ınbı mançiqab qihna Bet-Şemeş giviyğalne cigeeqamee avayk'ananbı.
13 Nthawi imeneyi anthu a ku Beti-Semesi amakolola tirigu mʼchigwa ndipo pamene anayangʼana ndi kuona Bokosi la Chipangano likubwera anakondwa.
Mane gahıl Bet-Şemeşğançenbı suk qiviyşal çolee vooxhe. Manbı q'utye g'avcu şadeebaxhenbı.
14 Galeta lija linafika ku munda wa Yoswa ku Beti-Semesi ndipo linayima. Kumeneko kunali mwala waukulu. Tsono anthu anawaza nkhuni galetalo, ndipo anapha ngʼombe zija ndi kuzipereka ngati nsembe zopsereza kwa Yehova.
Daşk'a Bet-Şemeşğançene Yeşuayne çoleeqa qadı, sa xənne g'ayeyne k'ane ulyoyzaran. İnsanaaşe daşk'a haq'var hı'ı mançike osbı ha'a. Zerbışiked, Rəbbis gyooxhan haa'ana q'urban ablyaa'a.
15 Alevi nʼkuti atatsitsa Bokosi la Yehova, pamodzi ndi bokosi mmene munali zinthu zagolide, ndipo anawayika pa mwala uja waukulu. Tsiku limenelo anthu a ku Beti-Semesi anapereka nsembe yopsereza ndi nsembe zina kwa Yehova.
Leviyne nasıleençene insanaaşe Rəbbina q'utye, k'ınəəğəyke hı'iyn q'övəriy fırar sı'ına yeşuk'ub daşk'eençe gyaqqı, sa xənne g'ayel ooqa giyxhe. Mane yiğıl Bet-Şemeşğançenbışe Rəbbis gyooxhan haa'ane q'urbanıle ğayrı, medın q'urbanbıd gyaat'anbı.
16 Atsogoleri asanu a Afilisti ataona izi anabwerera ku Ekroni tsiku lomwelo.
Filiştinaaşine maqa abıyne xhone xərıng'uk'le man g'acu, mane yiğılycab Ekronqa siviyk'al.
17 Zifanizo zagolide za zithupsa zimene Afilisti anatumiza ngati nsembe zopepesera machimo kwa Yehova zinkayimirira mizinda isanu iyi motere: chimodzi cha ku Asidodi, china cha ku Gaza ndi zina za ku Asikeloni, Gati ndi Ekroni.
Filiştinaaşe taxsir colyva Aşdod eyhene şaharne doyule, Gəzzə eyhene şaharne doyule, Aşkelon eyhene şaharne doyule, Gat eyhene şaharne doyule, Ekron eyhene şaharne doyule Rəbbis k'ınəəğəyke hı'iyn fırar adayle.
18 Ndipo chiwerengero cha zifanizo za makoswe chinali chofanana ndi chiwerengero cha mizinda ya akalonga asanu a Afilisti. Mizindayi inali yotetezedwa bwino ndi ina yapamtetete. Mwala waukulu umene anayikapo Bokosi la Chipangano la Yehova mʼmunda mwa Yoswa ku Beti-Semesi uli ngati mboni mpaka lero.
K'ınəəğəyke hı'iyn q'övərmee, hiqiy-alla cabırbışikane şaharbışisiy çine hiqiy-allane xivaaşis sik'ı adayle. Mane şaharbışiqa xhoyre xərna ıxha. Bet-Şemeşğane Yeşuayne çoleena, Rəbbina q'utye gyuvxhuna xəbna g'aye giyniyne yiğılqamee avxu vob.
19 Yehova anakantha amuna a ku Beti-Semesi 70 chifukwa anasuzumira mʼBokosi la Chipangano cha Yehova. Ndipo anzawo analira chifukwa Yehova anawalanga kwambiri.
Rəbbine q'utyeyne aq'a ilyaakıva, Allahee Bet-Şemeşğançenbışde vuk'lelqa ver ooxa. Rəbbee manbışda yights'al insan gek'a. Milletıd, Rəbbee cone vuk'lelqa ooxune verır-alla geşşe ıxha.
20 Tsono anthu a ku Beti-Semesi anafunsa, “Ndani angathe kuyima pamaso pa Yehova Mulungu Woyera? Bokosi la Chipanganoli lipita kuti likachoka pano?”
Bet-Şemeşğançenbışe eyhen: – İne muq'addasne Allahne, Rəbbine ögil şavusse ulyozaras əxəye? Nyaqane ina q'utye quvkees?
21 Tsono iwo anatumiza a mithenga kwa anthu a ku Kiriati-Yearimu kuti, “Afilisti atibwezera Bokosi la Yehova. Bwerani kuno mudzalitenge, mupite nalo kwanuko.”
Qiyğa manbışe Kiryat-Yearim eyhene şaharne milletısqa xabar ana insanar g'axuvu, eyhen: – Filiştinaaşe Rəbbina q'utye yı'q'əlqa savaak'al hav'u, able mana quvkee.