< 1 Samueli 6 >

1 Bokosi la Yehova linakhala mʼdziko la Afilisti kwa miyezi isanu ndi iwiri.
L’Arche du Seigneur était depuis sept mois dans le territoire des Philistins,
2 Tsono Afilisti anayitana ansembe ndi amawula ndipo anati, “Tichite nalo chiyani Bokosi la Yehova? Tiwuzeni momwe tidzalitumizira ku malo ake.”
lorsqu’ils mandèrent prêtres et devins et leur dirent: "Comment procéderons-nous pour l’arche de l’Eternel? Apprenez-nous la façon de la renvoyer au lieu de sa résidence."
3 Iwo anayankha kuti, “Ngati mufuna kubweza Bokosi la Mulungu wa Israeli, musalitumize wopanda kanthu, koma muyesetse kulitumiza pamodzi ndi nsembe yopepesera machimo. Mukatero mudzachiritsidwa, ndipo mudzadziwa chifukwa chiyani chilango cha Yehova sichikukuchokani.”
Ceux-là répondirent: "Si vous renvoyez l’arche du Dieu d’Israël, ne la renvoyez point à vide, il faut aussi lui offrir un expiatoire; alors vous serez guéris, et vous saurez pourquoi sa main ne cesse de vous frapper.
4 Afilisti anafunsanso kuti “Kodi ife tipereke nsembe yanji yopepesera machimo?” Iwo anayankha kuti, “Mupereke zifanizo zagolide za zithupsa zisanu ndi zamakoswe asanu malingana ndi chiwerengero cha akalonga a Afilisti popeza mliri womwewo wagwera inu ndi akalonga anu.
Quel expiatoire, dirent-ils, devons-nous lui offrir? Autant, répondit-on, que les Philistins ont de princes: cinq images d’hémorroïdes en or et cinq mulots en or; car vous souffrez d’une même plaie, vous tous et vos princes.
5 Mupange zifanizo za zithupsa zisanu ndi za makoswe asanu amene akuwononga dziko lanu ndipo mupereke ulemu kwa Israeli. Mwina adzaleka kuzunza inu, milungu yanu ndi dziko lanu.
Faites donc des simulacres de vos hémorroïdes et des mulots qui ravagent le pays, et offrez-les en hommage au Dieu d’Israël; peut-être cessera-t-il de faire peser sa main sur vous, sur votre dieu et votre pays.
6 Nʼchifukwa chiyani mukuwumitsa mitima monga anachita Aigupto ndi Farao? Mulungu atawalanga anthu a ku Igupto aja kodi suja anawalola Aisraeli kuti azipita ndipo anapitadi?
Et pourquoi endurcir votre cœur comme l’ont fait les Egyptiens et Pharaon? Assurément, quand il les eut accablés de sa puissance, ils ont dû renvoyer ce peuple et il est parti!
7 “Tsopano konzani galeta latsopano limodzi ndiponso ngʼombe ziwiri zazikazi zamkaka zimene sizinavalepo goli. Muzimangirire ngʼombezo ku ngoloyo, koma ana awo muwachotse ndi kuwasiya kwanu.
Donc, faites fabriquer un chariot neuf, et prenez deux vaches laitières qui n’aient pas encore porté le joug; attelez ces vaches au chariot, et faites ramener leurs petits, séparés d’elles, à l’étable.
8 Mutenge Bokosi la Yehova ndi kuliyika pa galetapo ndipo pambali pake pakhale Bokosi, mʼmene muyikemonso zinthu zagolide zomwe mukutumiza kwa Iye monga nsembe yopepesera machimo. Kenaka, mulisiye lizipita.
Prenez alors l’arche de l’Eternel, placez-la sur le chariot, et, à côté d’elle, posez dans un coffret les simulacres d’or que vous lui aurez destinés comme offrande d’expiation; puis vous la laisserez partir,
9 Koma muziliyangʼana. Ngati lilondola njira yopita kwawo kwa Bokosilo mpaka ku Beti-Semesi ndiye kuti amene watichita zoyipa zazikulu zoterezi ndi Mulungu wa Israeli. Koma ngati silitero, ife tidzadziwa kuti sanali Mulungu wa Israeli amene watizunza koma kuti zinangochitika mwatsoka.”
et vous la suivrez des yeux: si elle s’achemine vers son territoire, à Beth-Chémech, c’est elle qui nous a infligé cette grande calamité; sinon, nous en conclurons que ce n’est pas sa main, mais le hasard seul, qui nous a frappés."
10 Anthu aja anachitadi zimenezi. Anatenga ngʼombe zamkaka ziwiri nazimanga ku galeta lija. Koma ana awo anawatsekera mʼkhola.
Ainsi fit-on. L’On prit deux vaches laitières, qu’on attela à un chariot, en retenant les veaux à l’étable;
11 Tsono anayika Bokosi la Yehova pa galeta pamodzi ndi bokosi limene munali makoswe agolide ndi zifanizo zawo za zithupsa.
et l’on mit l’arche du Seigneur sur le chariot, ainsi que le coffret contenant les mulots d’or et les simulacres d’hémorroïdes.
12 Ngʼombe zija zinapita molunjika kutsata msewu wopita ku Beti Semesi zikulira njira yonse. Sizinakhotere kumanja kapena kumanzere. Akalonga a Afilisti anazitsatira mpaka mʼmalire a Beti-Semesi.
Les vaches marchèrent droit dans la direction de Beth-Chémech, suivirent toujours une même voie tout en mugissant, et ne s’en écartèrent ni à droite ni à gauche; les princes des Philistins marchèrent derrière elles, jusqu’aux confins de Beth-Chémech.
13 Nthawi imeneyi anthu a ku Beti-Semesi amakolola tirigu mʼchigwa ndipo pamene anayangʼana ndi kuona Bokosi la Chipangano likubwera anakondwa.
Les gens de Beth-Chémech faisaient alors la coupe du froment dans la vallée; en levant les yeux, ils aperçurent l’arche et se réjouirent à cette vue.
14 Galeta lija linafika ku munda wa Yoswa ku Beti-Semesi ndipo linayima. Kumeneko kunali mwala waukulu. Tsono anthu anawaza nkhuni galetalo, ndipo anapha ngʼombe zija ndi kuzipereka ngati nsembe zopsereza kwa Yehova.
Le chariot, arrivé au champ de Josué, de Beth-Chémech, s’y arrêta; là se trouvait une grande pierre. On fendit en morceaux le bois du chariot, et l’on immola les vaches en holocauste à l’Eternel.
15 Alevi nʼkuti atatsitsa Bokosi la Yehova, pamodzi ndi bokosi mmene munali zinthu zagolide, ndipo anawayika pa mwala uja waukulu. Tsiku limenelo anthu a ku Beti-Semesi anapereka nsembe yopsereza ndi nsembe zina kwa Yehova.
Les lévites avaient descendu l’arche du Seigneur et le coffret qui l’accompagnait contenant les objets d’or, et avaient posé le tout sur la grosse pierre; alors les gens de Beth-Chémech offrirent, le même jour, des holocaustes et autres sacrifices à l’Eternel.
16 Atsogoleri asanu a Afilisti ataona izi anabwerera ku Ekroni tsiku lomwelo.
Ce que voyant, les cinq princes des Philistins s’en retournèrent à Ekron ce jour-là.
17 Zifanizo zagolide za zithupsa zimene Afilisti anatumiza ngati nsembe zopepesera machimo kwa Yehova zinkayimirira mizinda isanu iyi motere: chimodzi cha ku Asidodi, china cha ku Gaza ndi zina za ku Asikeloni, Gati ndi Ekroni.
Quant aux hémorroïdes imitées en or, que les Philistins avaient offertes en expiation à l’Eternel, en voici le compte: une pour Asdod, une pour Gaza, une pour Ascalon, une pour Gath, une pour Ekron.
18 Ndipo chiwerengero cha zifanizo za makoswe chinali chofanana ndi chiwerengero cha mizinda ya akalonga asanu a Afilisti. Mizindayi inali yotetezedwa bwino ndi ina yapamtetete. Mwala waukulu umene anayikapo Bokosi la Chipangano la Yehova mʼmunda mwa Yoswa ku Beti-Semesi uli ngati mboni mpaka lero.
Mais le nombre des mulots d’or égalait celui de toutes les villes des Philistins soumises aux cinq princes, depuis la ville forte jusqu’à la place ouverte, et jusqu’à la grosse pierre sur laquelle on posa l’arche du Seigneur et qui subsiste aujourd’hui encore, dans le champ de Josué de Beth-Chémech.
19 Yehova anakantha amuna a ku Beti-Semesi 70 chifukwa anasuzumira mʼBokosi la Chipangano cha Yehova. Ndipo anzawo analira chifukwa Yehova anawalanga kwambiri.
Le Seigneur frappa les habitants de Beth-Chémech, pour avoir regardé dans l’arche; il frappa, dans cette population, soixante-dix hommes sur cinquante mille. Le peuple fut consterné de cette grande mortalité que lui avait infligée le Seigneur;
20 Tsono anthu a ku Beti-Semesi anafunsa, “Ndani angathe kuyima pamaso pa Yehova Mulungu Woyera? Bokosi la Chipanganoli lipita kuti likachoka pano?”
et les gens de Beth-Chémech se dirent: "Qui peut subsister devant l’Eternel, ce Dieu saint? Et où l’arche montera-t-elle de chez nous?"
21 Tsono iwo anatumiza a mithenga kwa anthu a ku Kiriati-Yearimu kuti, “Afilisti atibwezera Bokosi la Yehova. Bwerani kuno mudzalitenge, mupite nalo kwanuko.”
Ils envoyèrent alors des messagers aux habitants de Kiryath-Yearim, pour leur dire: "Les Philistins ont restitué l’arche du Seigneur; venez, faites-la monter chez vous."

< 1 Samueli 6 >