< 1 Samueli 6 >
1 Bokosi la Yehova linakhala mʼdziko la Afilisti kwa miyezi isanu ndi iwiri.
L'arche de l'Éternel resta sept mois dans le pays des Philistins.
2 Tsono Afilisti anayitana ansembe ndi amawula ndipo anati, “Tichite nalo chiyani Bokosi la Yehova? Tiwuzeni momwe tidzalitumizira ku malo ake.”
Les Philistins appelèrent les prêtres et les devins et dirent: « Que ferons-nous de l'arche de l'Éternel? Montre-nous comment nous devons l'envoyer à sa place. »
3 Iwo anayankha kuti, “Ngati mufuna kubweza Bokosi la Mulungu wa Israeli, musalitumize wopanda kanthu, koma muyesetse kulitumiza pamodzi ndi nsembe yopepesera machimo. Mukatero mudzachiritsidwa, ndipo mudzadziwa chifukwa chiyani chilango cha Yehova sichikukuchokani.”
Ils dirent: « Si tu renvoies l'arche du Dieu d'Israël, ne la renvoie pas à vide, mais renvoie-lui une offrande. Alors tu seras guéri, et tu sauras pourquoi sa main ne s'est pas retirée de toi. »
4 Afilisti anafunsanso kuti “Kodi ife tipereke nsembe yanji yopepesera machimo?” Iwo anayankha kuti, “Mupereke zifanizo zagolide za zithupsa zisanu ndi zamakoswe asanu malingana ndi chiwerengero cha akalonga a Afilisti popeza mliri womwewo wagwera inu ndi akalonga anu.
Et ils dirent: « Quelle sera l'offrande d'expiation que nous lui rendrons? » Ils dirent: « Cinq tumeurs d'or et cinq souris d'or, pour le nombre des princes des Philistins; car une seule plaie vous a frappés tous, vous et vos princes.
5 Mupange zifanizo za zithupsa zisanu ndi za makoswe asanu amene akuwononga dziko lanu ndipo mupereke ulemu kwa Israeli. Mwina adzaleka kuzunza inu, milungu yanu ndi dziko lanu.
C'est pourquoi vous ferez des images de vos tumeurs et des images de vos souris qui souillent le pays, et vous rendrez gloire au Dieu d'Israël. Peut-être relâchera-t-il sa main de vous, de vos dieux et de votre pays.
6 Nʼchifukwa chiyani mukuwumitsa mitima monga anachita Aigupto ndi Farao? Mulungu atawalanga anthu a ku Igupto aja kodi suja anawalola Aisraeli kuti azipita ndipo anapitadi?
Pourquoi donc endurcissez-vous votre cœur comme les Égyptiens et Pharaon ont endurci leur cœur? Quand il avait fait des merveilles au milieu d'eux, n'ont-ils pas laissé aller le peuple, qui s'en est allé?
7 “Tsopano konzani galeta latsopano limodzi ndiponso ngʼombe ziwiri zazikazi zamkaka zimene sizinavalepo goli. Muzimangirire ngʼombezo ku ngoloyo, koma ana awo muwachotse ndi kuwasiya kwanu.
« Maintenant, prenez et préparez vous-mêmes un chariot neuf et deux vaches à lait sur lesquelles il n'y a pas de joug; attachez les vaches au chariot, et ramenez leurs veaux à la maison;
8 Mutenge Bokosi la Yehova ndi kuliyika pa galetapo ndipo pambali pake pakhale Bokosi, mʼmene muyikemonso zinthu zagolide zomwe mukutumiza kwa Iye monga nsembe yopepesera machimo. Kenaka, mulisiye lizipita.
prenez l'arche de Yahvé et posez-la sur le chariot. Mets dans un coffret, à côté d'elle, les bijoux d'or que tu lui rends comme offrande de culpabilité, et envoie-la, pour qu'elle monte.
9 Koma muziliyangʼana. Ngati lilondola njira yopita kwawo kwa Bokosilo mpaka ku Beti-Semesi ndiye kuti amene watichita zoyipa zazikulu zoterezi ndi Mulungu wa Israeli. Koma ngati silitero, ife tidzadziwa kuti sanali Mulungu wa Israeli amene watizunza koma kuti zinangochitika mwatsoka.”
Voici, s'il monte par le chemin de sa frontière jusqu'à Beth Shemesh, il nous a fait ce grand mal; sinon, nous saurons que ce n'est pas sa main qui nous a frappés. C'est un hasard qui nous a frappés. »
10 Anthu aja anachitadi zimenezi. Anatenga ngʼombe zamkaka ziwiri nazimanga ku galeta lija. Koma ana awo anawatsekera mʼkhola.
Les hommes firent ainsi, prirent deux vaches laitières et les attachèrent au chariot, et enfermèrent leurs veaux à la maison.
11 Tsono anayika Bokosi la Yehova pa galeta pamodzi ndi bokosi limene munali makoswe agolide ndi zifanizo zawo za zithupsa.
Ils mirent l'arche de Yahvé sur le chariot, et la boîte avec les souris d'or et les images de leurs tumeurs.
12 Ngʼombe zija zinapita molunjika kutsata msewu wopita ku Beti Semesi zikulira njira yonse. Sizinakhotere kumanja kapena kumanzere. Akalonga a Afilisti anazitsatira mpaka mʼmalire a Beti-Semesi.
Les vaches prirent le chemin droit par le chemin de Beth Shemesh. Elles suivirent la route, en mugissant, sans se détourner ni à droite ni à gauche, et les princes des Philistins les poursuivirent jusqu'à la frontière de Beth Shemesh.
13 Nthawi imeneyi anthu a ku Beti-Semesi amakolola tirigu mʼchigwa ndipo pamene anayangʼana ndi kuona Bokosi la Chipangano likubwera anakondwa.
Les habitants de Beth Shemesh moissonnaient leur blé dans la vallée; ils levèrent les yeux et virent l'arche, et ils se réjouirent de la voir.
14 Galeta lija linafika ku munda wa Yoswa ku Beti-Semesi ndipo linayima. Kumeneko kunali mwala waukulu. Tsono anthu anawaza nkhuni galetalo, ndipo anapha ngʼombe zija ndi kuzipereka ngati nsembe zopsereza kwa Yehova.
Le chariot entra dans le champ de Josué de Beth Shemesh, et s'arrêta là où il y avait une grande pierre. Ils fendirent le bois du char et offrirent les vaches en holocauste à Yahvé.
15 Alevi nʼkuti atatsitsa Bokosi la Yehova, pamodzi ndi bokosi mmene munali zinthu zagolide, ndipo anawayika pa mwala uja waukulu. Tsiku limenelo anthu a ku Beti-Semesi anapereka nsembe yopsereza ndi nsembe zina kwa Yehova.
Les Lévites descendirent l'arche de l'Éternel et le coffret qui l'accompagnait, dans lequel se trouvaient les bijoux d'or, et ils les posèrent sur la grande pierre; et les hommes de Beth Shemesh offrirent des holocaustes et des sacrifices à l'Éternel le même jour.
16 Atsogoleri asanu a Afilisti ataona izi anabwerera ku Ekroni tsiku lomwelo.
Lorsque les cinq princes des Philistins l'eurent vu, ils retournèrent à Ekron le même jour.
17 Zifanizo zagolide za zithupsa zimene Afilisti anatumiza ngati nsembe zopepesera machimo kwa Yehova zinkayimirira mizinda isanu iyi motere: chimodzi cha ku Asidodi, china cha ku Gaza ndi zina za ku Asikeloni, Gati ndi Ekroni.
Voici les tumeurs d'or que les Philistins offrirent en sacrifice de culpabilité à Yahvé: une pour Asdod, une pour Gaza, une pour Askalon, une pour Gath, une pour Ekron,
18 Ndipo chiwerengero cha zifanizo za makoswe chinali chofanana ndi chiwerengero cha mizinda ya akalonga asanu a Afilisti. Mizindayi inali yotetezedwa bwino ndi ina yapamtetete. Mwala waukulu umene anayikapo Bokosi la Chipangano la Yehova mʼmunda mwa Yoswa ku Beti-Semesi uli ngati mboni mpaka lero.
et les souris d'or, selon le nombre de toutes les villes des Philistins appartenant aux cinq seigneurs, villes fortes et villages, jusqu'à la grande pierre sur laquelle ils posèrent l'arche de Yahvé. Cette pierre est restée jusqu'à ce jour dans le champ de Josué de Beth Shemesh.
19 Yehova anakantha amuna a ku Beti-Semesi 70 chifukwa anasuzumira mʼBokosi la Chipangano cha Yehova. Ndipo anzawo analira chifukwa Yehova anawalanga kwambiri.
Il frappa les hommes de Beth Shemesh, parce qu'ils avaient regardé dans l'arche de Yahvé, il frappa cinquante mille soixante-dix hommes. Et le peuple se lamenta, car l'Éternel avait frappé le peuple d'une grande défaite.
20 Tsono anthu a ku Beti-Semesi anafunsa, “Ndani angathe kuyima pamaso pa Yehova Mulungu Woyera? Bokosi la Chipanganoli lipita kuti likachoka pano?”
Les hommes de Beth Shemesh dirent: « Qui peut tenir devant l'Éternel, ce Dieu saint? Vers qui montera-t-il de notre part? »
21 Tsono iwo anatumiza a mithenga kwa anthu a ku Kiriati-Yearimu kuti, “Afilisti atibwezera Bokosi la Yehova. Bwerani kuno mudzalitenge, mupite nalo kwanuko.”
Ils envoyèrent des messagers aux habitants de Kiriath Jearim, en disant: « Les Philistins ont ramené l'arche de Yahvé. Descendez et faites-la monter jusqu'à vous. »