< 1 Samueli 6 >
1 Bokosi la Yehova linakhala mʼdziko la Afilisti kwa miyezi isanu ndi iwiri.
And it was [the] ark of Yahweh in [the] region of [the] Philistines seven months.
2 Tsono Afilisti anayitana ansembe ndi amawula ndipo anati, “Tichite nalo chiyani Bokosi la Yehova? Tiwuzeni momwe tidzalitumizira ku malo ake.”
And they summoned [the] Philistines the priests and the diviners saying what? will we do to [the] ark of Yahweh make known to us how? will we send it to own place its.
3 Iwo anayankha kuti, “Ngati mufuna kubweza Bokosi la Mulungu wa Israeli, musalitumize wopanda kanthu, koma muyesetse kulitumiza pamodzi ndi nsembe yopepesera machimo. Mukatero mudzachiritsidwa, ndipo mudzadziwa chifukwa chiyani chilango cha Yehova sichikukuchokani.”
And they said if [you are] about to send away [the] ark of [the] God of Israel may not you send away it empty for certainly you will send back to him a guilt offering then you will be healed and it will be known by you why? not does it turn aside hand his from you.
4 Afilisti anafunsanso kuti “Kodi ife tipereke nsembe yanji yopepesera machimo?” Iwo anayankha kuti, “Mupereke zifanizo zagolide za zithupsa zisanu ndi zamakoswe asanu malingana ndi chiwerengero cha akalonga a Afilisti popeza mliri womwewo wagwera inu ndi akalonga anu.
And they said what? [is] the guilt offering which we will send back to him and they said [the] number of [the] rulers of [the] Philistines five (tumors of *Q(K)*) gold and five mice of gold for a plague one [belongs] to all of them and to rulers your.
5 Mupange zifanizo za zithupsa zisanu ndi za makoswe asanu amene akuwononga dziko lanu ndipo mupereke ulemu kwa Israeli. Mwina adzaleka kuzunza inu, milungu yanu ndi dziko lanu.
And you will make images of (tumors your *Q(K)*) and images of mice your which are ruining the land and you will give to [the] God of Israel honor perhaps he will lighten hand his from with you and from on gods your and from on land your.
6 Nʼchifukwa chiyani mukuwumitsa mitima monga anachita Aigupto ndi Farao? Mulungu atawalanga anthu a ku Igupto aja kodi suja anawalola Aisraeli kuti azipita ndipo anapitadi?
And why? will you harden heart your just as they hardened Egypt and Pharaoh heart their ¿ not just when he dealt wantonly with them and they sent away them and they went.
7 “Tsopano konzani galeta latsopano limodzi ndiponso ngʼombe ziwiri zazikazi zamkaka zimene sizinavalepo goli. Muzimangirire ngʼombezo ku ngoloyo, koma ana awo muwachotse ndi kuwasiya kwanu.
And therefore take and make a cart new one and two cows nursing which not it has gone up on them a yoke and you will harness the cows on the cart and you will take back young ones their from after them the house towards.
8 Mutenge Bokosi la Yehova ndi kuliyika pa galetapo ndipo pambali pake pakhale Bokosi, mʼmene muyikemonso zinthu zagolide zomwe mukutumiza kwa Iye monga nsembe yopepesera machimo. Kenaka, mulisiye lizipita.
And you will take [the] ark of Yahweh and you will put it into the cart and - [the] articles of gold which you have sent back to him a guilt offering you will put in the box from side its and you will send away it and it will go.
9 Koma muziliyangʼana. Ngati lilondola njira yopita kwawo kwa Bokosilo mpaka ku Beti-Semesi ndiye kuti amene watichita zoyipa zazikulu zoterezi ndi Mulungu wa Israeli. Koma ngati silitero, ife tidzadziwa kuti sanali Mulungu wa Israeli amene watizunza koma kuti zinangochitika mwatsoka.”
And you will see if [the] way of own territory its it will go up Beth Shemesh he he has done to us the harm great this and if not and we will know that not hand his it touched us chance it it happened to us.
10 Anthu aja anachitadi zimenezi. Anatenga ngʼombe zamkaka ziwiri nazimanga ku galeta lija. Koma ana awo anawatsekera mʼkhola.
And they did the men thus and they took two cows nursing and they harnessed them on the cart and young ones their they shut up in the house.
11 Tsono anayika Bokosi la Yehova pa galeta pamodzi ndi bokosi limene munali makoswe agolide ndi zifanizo zawo za zithupsa.
And they put [the] ark of Yahweh into the cart and the box and [the] mice of gold and [the] images of tumors their.
12 Ngʼombe zija zinapita molunjika kutsata msewu wopita ku Beti Semesi zikulira njira yonse. Sizinakhotere kumanja kapena kumanzere. Akalonga a Afilisti anazitsatira mpaka mʼmalire a Beti-Semesi.
And they were straight the cows in the road on [the] road of Beth Shemesh on a highway one they went continuously and lowed and not they turned aside right [hand] and left [hand] and [the] rulers of [the] Philistines [were] going after them to [the] border of Beth Shemesh.
13 Nthawi imeneyi anthu a ku Beti-Semesi amakolola tirigu mʼchigwa ndipo pamene anayangʼana ndi kuona Bokosi la Chipangano likubwera anakondwa.
And Beth Shemesh [were] harvesting [the] harvest of wheat in the valley and they lifted up eyes their and they saw the ark and they rejoiced to see [it].
14 Galeta lija linafika ku munda wa Yoswa ku Beti-Semesi ndipo linayima. Kumeneko kunali mwala waukulu. Tsono anthu anawaza nkhuni galetalo, ndipo anapha ngʼombe zija ndi kuzipereka ngati nsembe zopsereza kwa Yehova.
And the cart it came to [the] field of Joshua [the] Beth Shemeshite and it stopped there and [was] there a stone large and they split [the] wood of the cart and the cows they offered up a burnt offering to Yahweh.
15 Alevi nʼkuti atatsitsa Bokosi la Yehova, pamodzi ndi bokosi mmene munali zinthu zagolide, ndipo anawayika pa mwala uja waukulu. Tsiku limenelo anthu a ku Beti-Semesi anapereka nsembe yopsereza ndi nsembe zina kwa Yehova.
And the Levites they brought down - [the] ark of Yahweh and the box which [was] with it which [were] in it [the] articles of gold and they put [them] to the stone large and [the] people of Beth Shemesh they offered up burnt offerings and they sacrificed sacrifices on the day that to Yahweh.
16 Atsogoleri asanu a Afilisti ataona izi anabwerera ku Ekroni tsiku lomwelo.
And five [the] rulers of [the] Philistines they saw and they went back Ekron on the day that.
17 Zifanizo zagolide za zithupsa zimene Afilisti anatumiza ngati nsembe zopepesera machimo kwa Yehova zinkayimirira mizinda isanu iyi motere: chimodzi cha ku Asidodi, china cha ku Gaza ndi zina za ku Asikeloni, Gati ndi Ekroni.
And these [are] [the] tumors of gold which they sent back [the] Philistines a guilt offering to Yahweh for Ashdod one for Gaza one for Ashkelon one for Gath one for Ekron one.
18 Ndipo chiwerengero cha zifanizo za makoswe chinali chofanana ndi chiwerengero cha mizinda ya akalonga asanu a Afilisti. Mizindayi inali yotetezedwa bwino ndi ina yapamtetete. Mwala waukulu umene anayikapo Bokosi la Chipangano la Yehova mʼmunda mwa Yoswa ku Beti-Semesi uli ngati mboni mpaka lero.
And [the] mice of gold [the] number of all [the] cities of [the] Philistines of [the] five the rulers from a city of fortification and unto village[s] of the hamlet-dweller[s] and to - Abel the great which they set down on it [the] ark of Yahweh until the day this in [the] field of Joshua [the] Beth Shemeshite.
19 Yehova anakantha amuna a ku Beti-Semesi 70 chifukwa anasuzumira mʼBokosi la Chipangano cha Yehova. Ndipo anzawo analira chifukwa Yehova anawalanga kwambiri.
And he struck down among [the] people of Beth Shemesh for they had looked in [the] ark of Yahweh and he struck down among the people seventy man fifty thousand man and they mourned the people for he had struck Yahweh the people a blow (great *LB(ah)*)
20 Tsono anthu a ku Beti-Semesi anafunsa, “Ndani angathe kuyima pamaso pa Yehova Mulungu Woyera? Bokosi la Chipanganoli lipita kuti likachoka pano?”
and they said [the] people of Beth Shemesh who? is he able to stand before Yahweh the God holy this and to whom? will it go up from with us.
21 Tsono iwo anatumiza a mithenga kwa anthu a ku Kiriati-Yearimu kuti, “Afilisti atibwezera Bokosi la Yehova. Bwerani kuno mudzalitenge, mupite nalo kwanuko.”
And they sent messengers to [the] inhabitants of Kiriath Jearim saying they have brought back [the] Philistines [the] ark of Yahweh come down take up it to you.