< 1 Samueli 5 >
1 Afilisti atalanda Bokosi la Mulungu lija, analitenga kuchoka ku Ebenezeri kupita ku Asidodi.
Les Philistins s’étaient donc emparés de l’arche du Seigneur, et ils la transportèrent d’Eben-Haézer à Asdod.
2 Kenaka anatenga Bokosi la Chipanganolo nabwera nalo ku nyumba ya Dagoni ndi kuliyika pambali pa Dagoni.
Là ils prirent l’arche du Seigneur, l’amenèrent dans le temple de Dagon et la placèrent à côté de cette idole.
3 Anthu a ku Asidodi atadzuka mmawa mwake, anangoona Dagoni atagwa pansi chafufumimba pamaso pa Bokosi la Yehova! Iwo anatenga Dagoni ndi kumuyimika pamalo pake.
Mais le lendemain, lorsque les gens d’Asdod se levèrent, ils virent Dagon étendu sur la face, à terre, devant l’arche de l’Eternel; ils le relevèrent et le remirent à sa place.
4 Koma mmawa mwakenso atadzuka, anaona Dagoni atagwa chafufumimba pamaso pa Bokosi la Yehova. Mutu wake ndi manja ake zinali zitaduka ndi kugwera pa khonde polowera, thunthu lake lokha ndilo linatsala.
Le matin du jour suivant, voilà que Dagon gisait encore à terre devant l’arche de l’Eternel; on voyait sur le seuil sa tête et ses deux mains coupées, le tronc seul était resté intact.
5 Nʼchifukwa chake mpaka lero ansembe a Dagoni kapena wina aliyense amene amalowa mʼkachisi wa Dagoni ku Asidodi saponda pa khonde.
C’Est pourquoi les prêtres de Dagon ni aucun de ceux qui entrent dans le temple de ce dieu, à Asdod, n’en foulent le seuil, aujourd’hui encore.
6 Yehova analanga koopsa anthu a ku Asidodi. Yehova anawawononga ndi kuwazunza ndi zithupsa Asidoniwa pamodzi ndi anthu a madera ozungulira.
Puis la main de l’Eternel s’appesantit sur les gens d’Asdod et il sévit contre eux, et il les affligea d’hémorroïdes, tant Asdod que le territoire voisin.
7 Anthu a ku Asidodi ataona zimene zimachitika anati, “Bokosi la Mulungu wa Israeli lisakhale kuno chifukwa akutizunza ife pamodzi ndi mulungu wathu Dagoni.”
Ce que voyant, les gens d’Asdod dirent: "L’Arche du Dieu d’Israël ne peut rester au milieu de nous, car il nous fait sentir trop durement sa puissance, à nous et à notre dieu Dagon."
8 Choncho anayitana atsogoleri onse a Afilisti kuti asonkhane ndipo anawafunsa kuti, “Kodi Bokosi la Mulungu wa Israeli tichite nalo chiyani?” Iwo anayankha kuti, “Bokosi la Mulungu wa Israeli lipite ku Gati.” Kotero analichotsa Bokosi la Mulungu wa Israelilo.
Ils mandèrent alors et convoquèrent chez eux tous les princes des Philistins, et leur dirent: "Que ferons-nous de l’arche du Dieu d’Israël?" Ceux-ci répondirent: "Que l’arche du Dieu d’Israël soit transportée à Gath!" Et l’on y transporta l’arche sainte.
9 Koma atafika nalo ku Gati, Yehova analanga mzindawo, ndipo anthu anachita mantha aakulu. Iye anazunza anthu a mu mzindawo, ana ndi akulu omwe, ndi zithupsa.
Mais, après sa translation, la main de l’Eternel sévit sur la ville, y produisant un très grand trouble: il en frappa tous les habitants, du plus petit au plus grand, par une éruption secrète d’hémorroïdes.
10 Choncho anatumiza Bokosi la Mulungu ku Ekroni. Koma Bokosi la Mulungu lija litangofika ku Ekroni, anthu a ku Ekroni analira kuti, “Abwera nalo Bokosi la Mulungu wa Israeli kwa ife kuti atiphe pamodzi ndi anthu athu.”
Ils envoyèrent l’arche divine à Ekron; mais quand elle y fut arrivée, les habitants jetèrent des cris et dirent: "On a transporté chez nous l’arche du Dieu d’Israël, pour nous faire périr, nous et les nôtres!"
11 Kotero iwo anayitana atsogoleri onse a Afilisti kuti asonkhane ndipo anati, “Chotsani Bokosi la Mulungu wa Israeli, libwerere ku malo ake. Tikapanda kutero lidzatipha ife ndi anthu athu.” Pakuti mu mzinda monse munali mantha aakulu kwambiri ndipo Mulungu ankawalanga kwambiri anthu a kumeneko.
Et ils envoyèrent convoquer tous les princes des Philistins et leur dirent: "Renvoyez l’arche du Dieu d’Israël, qu’elle retourne au lieu de sa résidence et ne nous fasse pas mourir, nous et les nôtres!" Car un désarroi mortel régnait dans toute la ville, la main de Dieu s’y faisait sentir lourdement.
12 Anthu amene sanafe anavutika ndi zithupsa, ndipo kulira kwa anthu a mu mzindamo kunamveka kumwamba.
Ceux qui ne mouraient pas étaient atteints d’hémorroïdes, et tes gémissements de la ville s’élevaient jusqu’aux cieux.