< 1 Samueli 5 >

1 Afilisti atalanda Bokosi la Mulungu lija, analitenga kuchoka ku Ebenezeri kupita ku Asidodi.
Les Philistins avaient pris l'arche de Dieu, et ils l'avaient transportée d'Ébenezer à Asdod.
2 Kenaka anatenga Bokosi la Chipanganolo nabwera nalo ku nyumba ya Dagoni ndi kuliyika pambali pa Dagoni.
Les Philistins prirent l'arche de Dieu, l'apportèrent dans la maison de Dagon et la placèrent près de Dagon.
3 Anthu a ku Asidodi atadzuka mmawa mwake, anangoona Dagoni atagwa pansi chafufumimba pamaso pa Bokosi la Yehova! Iwo anatenga Dagoni ndi kumuyimika pamalo pake.
Le lendemain, lorsque les habitants d'Asdod se levèrent de bonne heure, voici que Dagon était tombé à terre, la face contre terre, devant l'arche de Yahvé. Ils prirent Dagon et le remirent à sa place.
4 Koma mmawa mwakenso atadzuka, anaona Dagoni atagwa chafufumimba pamaso pa Bokosi la Yehova. Mutu wake ndi manja ake zinali zitaduka ndi kugwera pa khonde polowera, thunthu lake lokha ndilo linatsala.
Le lendemain matin, ils se levèrent de bonne heure, et voici que Dagon était tombé à terre devant l'arche de Yahvé; la tête de Dagon et les deux paumes de ses mains furent coupées sur le seuil. Seul le torse de Dagon était intact.
5 Nʼchifukwa chake mpaka lero ansembe a Dagoni kapena wina aliyense amene amalowa mʼkachisi wa Dagoni ku Asidodi saponda pa khonde.
C'est pourquoi, jusqu'à ce jour, ni les prêtres de Dagon ni ceux qui entrent dans la maison de Dagon ne marchent sur le seuil de Dagon à Asdod.
6 Yehova analanga koopsa anthu a ku Asidodi. Yehova anawawononga ndi kuwazunza ndi zithupsa Asidoniwa pamodzi ndi anthu a madera ozungulira.
Mais la main de Yahvé s'appesantit sur le peuple d'Asdod, il le détruisit et le frappa de tumeurs, Asdod et son territoire.
7 Anthu a ku Asidodi ataona zimene zimachitika anati, “Bokosi la Mulungu wa Israeli lisakhale kuno chifukwa akutizunza ife pamodzi ndi mulungu wathu Dagoni.”
Les hommes d'Asdod, voyant qu'il en était ainsi, dirent: « L'arche du Dieu d'Israël ne restera pas chez nous, car sa main est sévère envers nous et envers Dagon, notre dieu. »
8 Choncho anayitana atsogoleri onse a Afilisti kuti asonkhane ndipo anawafunsa kuti, “Kodi Bokosi la Mulungu wa Israeli tichite nalo chiyani?” Iwo anayankha kuti, “Bokosi la Mulungu wa Israeli lipite ku Gati.” Kotero analichotsa Bokosi la Mulungu wa Israelilo.
Ils envoyèrent donc rassembler tous les princes des Philistins, et dirent: « Que ferons-nous de l'arche du Dieu d'Israël? » Ils répondirent: « Que l'arche du Dieu d'Israël soit transportée à Gath. » Ils y portèrent l'arche du Dieu d'Israël.
9 Koma atafika nalo ku Gati, Yehova analanga mzindawo, ndipo anthu anachita mantha aakulu. Iye anazunza anthu a mu mzindawo, ana ndi akulu omwe, ndi zithupsa.
Après qu'ils l'eurent transportée là, la main de Yahvé s'abattit sur la ville avec une très grande violence, et il frappa les habitants de la ville, petits et grands, de sorte que la tumeur éclata sur eux.
10 Choncho anatumiza Bokosi la Mulungu ku Ekroni. Koma Bokosi la Mulungu lija litangofika ku Ekroni, anthu a ku Ekroni analira kuti, “Abwera nalo Bokosi la Mulungu wa Israeli kwa ife kuti atiphe pamodzi ndi anthu athu.”
On envoya donc l'arche de Dieu à Ekron. Comme l'arche de Dieu arrivait à Ékron, les Ékronites poussèrent des cris, en disant: « On a amené chez nous l'arche du Dieu d'Israël, pour nous tuer, nous et notre peuple. »
11 Kotero iwo anayitana atsogoleri onse a Afilisti kuti asonkhane ndipo anati, “Chotsani Bokosi la Mulungu wa Israeli, libwerere ku malo ake. Tikapanda kutero lidzatipha ife ndi anthu athu.” Pakuti mu mzinda monse munali mantha aakulu kwambiri ndipo Mulungu ankawalanga kwambiri anthu a kumeneko.
Ils envoyèrent donc rassembler tous les seigneurs des Philistins et dirent: « Renvoie l'arche du Dieu d'Israël, et qu'elle retourne dans son lieu, afin qu'elle ne nous tue pas, nous et notre peuple. » Car il y eut une panique mortelle dans toute la ville. La main de Dieu y était très lourde.
12 Anthu amene sanafe anavutika ndi zithupsa, ndipo kulira kwa anthu a mu mzindamo kunamveka kumwamba.
Les hommes qui ne mouraient pas étaient frappés de tumeurs, et le cri de la ville montait jusqu'au ciel.

< 1 Samueli 5 >