< 1 Samueli 5 >
1 Afilisti atalanda Bokosi la Mulungu lija, analitenga kuchoka ku Ebenezeri kupita ku Asidodi.
and Philistine to take: take [obj] ark [the] God and to come (in): bring him from Ebenezer [the] Ebenezer Ashdod [to]
2 Kenaka anatenga Bokosi la Chipanganolo nabwera nalo ku nyumba ya Dagoni ndi kuliyika pambali pa Dagoni.
and to take: take Philistine [obj] ark [the] God and to come (in): bring [obj] him house: temple Dagon and to set [obj] him beside Dagon
3 Anthu a ku Asidodi atadzuka mmawa mwake, anangoona Dagoni atagwa pansi chafufumimba pamaso pa Bokosi la Yehova! Iwo anatenga Dagoni ndi kumuyimika pamalo pake.
and to rise Ashdod from morrow and behold Dagon to fall: fall to/for face his land: soil [to] to/for face: before ark LORD and to take: take [obj] Dagon and to return: return [obj] him to/for place his
4 Koma mmawa mwakenso atadzuka, anaona Dagoni atagwa chafufumimba pamaso pa Bokosi la Yehova. Mutu wake ndi manja ake zinali zitaduka ndi kugwera pa khonde polowera, thunthu lake lokha ndilo linatsala.
and to rise in/on/with morning from morrow and behold Dagon to fall: fall to/for face his land: soil [to] to/for face: before ark LORD and head Dagon and two palm hand his to cut: eliminate to(wards) [the] threshold except Dagon to remain upon him
5 Nʼchifukwa chake mpaka lero ansembe a Dagoni kapena wina aliyense amene amalowa mʼkachisi wa Dagoni ku Asidodi saponda pa khonde.
upon so not to tread priest Dagon and all [the] to come (in): come house: temple Dagon upon threshold Dagon in/on/with Ashdod till [the] day [the] this
6 Yehova analanga koopsa anthu a ku Asidodi. Yehova anawawononga ndi kuwazunza ndi zithupsa Asidoniwa pamodzi ndi anthu a madera ozungulira.
and to honor: heavy hand: power LORD to(wards) [the] Ashdod and be desolate: appalled them and to smite [obj] them (in/on/with tumor *Q(K)*) [obj] Ashdod and [obj] border: area her
7 Anthu a ku Asidodi ataona zimene zimachitika anati, “Bokosi la Mulungu wa Israeli lisakhale kuno chifukwa akutizunza ife pamodzi ndi mulungu wathu Dagoni.”
and to see: see human Ashdod for so and to say not to dwell ark God Israel with us for to harden hand: power his upon us and upon Dagon God our
8 Choncho anayitana atsogoleri onse a Afilisti kuti asonkhane ndipo anawafunsa kuti, “Kodi Bokosi la Mulungu wa Israeli tichite nalo chiyani?” Iwo anayankha kuti, “Bokosi la Mulungu wa Israeli lipite ku Gati.” Kotero analichotsa Bokosi la Mulungu wa Israelilo.
and to send: depart and to gather [obj] all lord Philistine to(wards) them and to say what? to make: do to/for ark God Israel and to say Gath to turn: turn ark God Israel and to turn: turn [obj] ark God Israel
9 Koma atafika nalo ku Gati, Yehova analanga mzindawo, ndipo anthu anachita mantha aakulu. Iye anazunza anthu a mu mzindawo, ana ndi akulu omwe, ndi zithupsa.
and to be after to turn: turn [obj] him and to be hand: power LORD in/on/with city tumult great: large much and to smite [obj] human [the] city from small: young and till great: old and to burst to/for them (tumor *Q(K)*)
10 Choncho anatumiza Bokosi la Mulungu ku Ekroni. Koma Bokosi la Mulungu lija litangofika ku Ekroni, anthu a ku Ekroni analira kuti, “Abwera nalo Bokosi la Mulungu wa Israeli kwa ife kuti atiphe pamodzi ndi anthu athu.”
and to send: depart [obj] ark [the] God Ekron and to be like/as to come (in): come ark [the] God Ekron and to cry out [the] Ekron to/for to say to turn: turn to(wards) me [obj] ark God Israel to/for to die me and [obj] people my
11 Kotero iwo anayitana atsogoleri onse a Afilisti kuti asonkhane ndipo anati, “Chotsani Bokosi la Mulungu wa Israeli, libwerere ku malo ake. Tikapanda kutero lidzatipha ife ndi anthu athu.” Pakuti mu mzinda monse munali mantha aakulu kwambiri ndipo Mulungu ankawalanga kwambiri anthu a kumeneko.
and to send: depart and to gather [obj] all lord Philistine and to say to send: depart [obj] ark God Israel and to return: return to/for place his and not to die [obj] me and [obj] people my for to be tumult death in/on/with all [the] city to honor: heavy much hand: power [the] God there
12 Anthu amene sanafe anavutika ndi zithupsa, ndipo kulira kwa anthu a mu mzindamo kunamveka kumwamba.
and [the] human which not to die to smite (in/on/with tumor *Q(K)*) and to ascend: rise cry [the] city [the] heaven