< 1 Samueli 5 >

1 Afilisti atalanda Bokosi la Mulungu lija, analitenga kuchoka ku Ebenezeri kupita ku Asidodi.
Now the Philistines had taken the ark of God, and they brought it from Ebenezer to Ashdod.
2 Kenaka anatenga Bokosi la Chipanganolo nabwera nalo ku nyumba ya Dagoni ndi kuliyika pambali pa Dagoni.
The Philistines took it, and brought it into the house of Dagon, and set it by Dagon.
3 Anthu a ku Asidodi atadzuka mmawa mwake, anangoona Dagoni atagwa pansi chafufumimba pamaso pa Bokosi la Yehova! Iwo anatenga Dagoni ndi kumuyimika pamalo pake.
And the Ashdodites rose early on the next day, and look, Dagon had fallen on his face before the ark of YHWH. So they raised up Dagon and set him in his place again.
4 Koma mmawa mwakenso atadzuka, anaona Dagoni atagwa chafufumimba pamaso pa Bokosi la Yehova. Mutu wake ndi manja ake zinali zitaduka ndi kugwera pa khonde polowera, thunthu lake lokha ndilo linatsala.
And it happened when they arose early the next morning, look, Dagon had fallen on his face before the ark of YHWH; and the head of Dagon and both the palms of his hands were cut off on the threshold. Only Dagon's torso was intact.
5 Nʼchifukwa chake mpaka lero ansembe a Dagoni kapena wina aliyense amene amalowa mʼkachisi wa Dagoni ku Asidodi saponda pa khonde.
Therefore neither the priests of Dagon, nor any who come into Dagon's house, step on the threshold of Dagon in Ashdod, to this day.
6 Yehova analanga koopsa anthu a ku Asidodi. Yehova anawawononga ndi kuwazunza ndi zithupsa Asidoniwa pamodzi ndi anthu a madera ozungulira.
But the hand of YHWH was heavy on the Ashdodites, and he ravaged them and afflicted them with tumors, both Ashdod and its territory. And he brought up against them mice, and they burst out in their ships, and mice sprang up in the midst of their land, and there was a great terror of death in the city.
7 Anthu a ku Asidodi ataona zimene zimachitika anati, “Bokosi la Mulungu wa Israeli lisakhale kuno chifukwa akutizunza ife pamodzi ndi mulungu wathu Dagoni.”
When the men of Ashdod saw what was happening, they said, "The ark of God shall not stay with us; for his hand is severe on us, and on Dagon our god."
8 Choncho anayitana atsogoleri onse a Afilisti kuti asonkhane ndipo anawafunsa kuti, “Kodi Bokosi la Mulungu wa Israeli tichite nalo chiyani?” Iwo anayankha kuti, “Bokosi la Mulungu wa Israeli lipite ku Gati.” Kotero analichotsa Bokosi la Mulungu wa Israelilo.
So they sent and gathered all the lords of the Philistines to them, and said, "What shall we do with the ark of God?" Then the Gittites answered, "Let the ark of God be carried over to us." So they brought the ark of God to Gath.
9 Koma atafika nalo ku Gati, Yehova analanga mzindawo, ndipo anthu anachita mantha aakulu. Iye anazunza anthu a mu mzindawo, ana ndi akulu omwe, ndi zithupsa.
And it came about that after they had brought it around, the hand of YHWH was against the city with a very great confusion: and he struck the men of the city, both small and great; and tumors broke out on them.
10 Choncho anatumiza Bokosi la Mulungu ku Ekroni. Koma Bokosi la Mulungu lija litangofika ku Ekroni, anthu a ku Ekroni analira kuti, “Abwera nalo Bokosi la Mulungu wa Israeli kwa ife kuti atiphe pamodzi ndi anthu athu.”
So they sent the ark of God to Ekron. It happened, as the ark of God came to Ekron, that the Ekronites cried out, saying, "Why have you brought about the ark of the God of Israel to us, to kill us and our people?"
11 Kotero iwo anayitana atsogoleri onse a Afilisti kuti asonkhane ndipo anati, “Chotsani Bokosi la Mulungu wa Israeli, libwerere ku malo ake. Tikapanda kutero lidzatipha ife ndi anthu athu.” Pakuti mu mzinda monse munali mantha aakulu kwambiri ndipo Mulungu ankawalanga kwambiri anthu a kumeneko.
And they sent and gathered together all the lords of the Philistines, and they said, "Send away the ark of the God of Israel, and let it go again to its own place, so that it will not kill us and our people." For there was a panic throughout all the city when the ark of God arrived there.
12 Anthu amene sanafe anavutika ndi zithupsa, ndipo kulira kwa anthu a mu mzindamo kunamveka kumwamba.
The men who did not die were struck with the tumors; and the cry of the city went up to heaven.

< 1 Samueli 5 >