< 1 Samueli 4 >
1 Ndipo mawu a Samueli anafika kwa Aisraeli onse. Aisraeli anapita kukamenya nkhondo ndi Afilisti. Aisraeli anamanga misasa yawo ku Ebenezeri, ndipo Afilisti anamanga ku Afeki.
Nakadanon ti sao ni Samuel iti entero nga Israel. Ita, mapan makigubat ti Israel kadagiti Filisteo. Nagkampoda idiay Ebenezer, ket nagkampo dagiti Filisteo idiay Afek.
2 Afilisti anandanda kuyangʼana Aisraeli nayamba kumenyana. Nkhondo inakula ndipo Afilisti anagonjetsa Aisraeli napha anthu 4,000 pa malo a nkhondopo.
Naglilinya dagiti Filisteo a makigubat iti Israel. Idi nagtultuloy ti gubat, inabak dagiti Filisteo ti Israel, a nakatayan ti agarup uppat a ribu a tattao iti paggugubatan.
3 Asilikali atabwerera ku misasa, akuluakulu a Israeli anafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani Yehova walola kuti tigonjetsedwe lero pamaso pa Afilisti? Tiyeni tikatenge Bokosi la Chipangano cha Yehova ku Silo kuti Yehovayo abwere kukhala pakati pathu ndi kutipulumutsa mʼmanja mwa adani athu.”
Idi napan dagiti tattao iti kampo, kinuna dagiti panglakayen ti Israel, “Apay nga impaabaknatayo ni Yahweh kadagiti Filisteo ita nga aldaw? Iyegtayo ditoy ti lakasa ti tulag ni Yahweh manipud Silo, tapno adda koma ditoy a kaduatayo, tapno pagtalinaidennatayo a natalged manipud iti kinapigsa dagiti kabusortayo.”
4 Choncho anatuma anthu ku Silo ndipo anakatenga Bokosi la Chipangano cha Yehova Wamphamvuzonse amene amakhala pa akerubi. Ndipo ana awiri a Eli, Hofini ndi Finehasi anatsagana nalo Bokosi la Chipangano cha Mulungu.
Isu a nangibaon dagiti tattao kadagiti lallaki idiay Silo; manipud sadiay, binaklayda ti lakasa ti tulag ni Yahweh a mannakabalin-amin, a nakatugaw iti ngatoen dagiti kerubim. Adda sadiay dagiti dua nga annak ni Eli, da Ofni ken Finees, agraman ti lakasa ti tulag ti Dios.
5 Bokosi la Chipangano cha Yehova litafika ku msasa, Aisraeli onse anafuwula kwambiri mpaka nthaka inagwedezeka.
Idi naisangpet iti kampo ti lakasa ti tulag ni Yahweh, nagpukkaw iti napigsa dagiti amin a tattao ti Israel, ket nagungor ti daga.
6 Atamva kufuwulaku, Afilisti anafunsa, “Kodi kufuwula kwakukulu kumeneku ku misasa ya Ahebri ndi kwachiyani?” Atamva kuti Bokosi la Yehova lafika ku msasako,
Idi nangngeg dagiti Filisteo ti ariwawa dagiti agpupukkaw, kinunada, “Ania ti kayat a sawen daytoy a napigsa a panagpupukkaw iti kampo dagiti Hebreo?” Ket naamirisda nga adda iti kampo ti lakasa ti tulag ni Yahweh.
7 Afilisti anachita mantha pakuti iwo ankanena kuti, “Milungu yafika ku msasa. Iwo anati, ‘Tili pamavuto. Chinthu choterechi sichinachitikepo nʼkale lomwe.
Nagbuteng dagiti Filisteo; kinunada, “Immay ti Dios iti kampo.” Kinunada, “Asitayo pay! Awan pay ti kastoy a napasamak idi!
8 Atsoka ife! Adzatipulumutsa ndani mʼmanja mwa milungu yamphamvuyi? Iyi ndi milungu imene inakantha Aigupto ndi miliri yosiyanasiyana mʼchipululu.
Asitayo pay! Siasino ti mangsalaknib kadatayo manipud iti pigsa daytoy a mannakabalin a Dios? Daytoy ti Dios a nangdarup kadagiti taga-Egipto idiay let-ang babaen iti agduduma a kita ti angol.
9 Limbani mtima Afilisti! Chitani chamuna, kuti mungakhale akapolo a Ahebri monga iwowa alili akapolo anu. Chitani chamuna ndipo menyani nkhondo!’”
Tumured ken agpakalalakikayo, dakayo a Filisteo, ta no saan agbalinkayo a tagabu dagiti Hebreo, a kas panagbalinda a tagabuyo. Agpakalalaki ken makirangetkayo.”
10 Choncho Afilisti anamenya nkhondo, ndipo anagonjetsa Aisraeli. Iwo anathawa aliyense kwawo. Ankhondo a Aisraeli oyenda pansi okwanira 30,000 anaphedwa.
Nakiranget dagiti Filisteo, ket naabak ti Israel. Tunggal maysa a lalaki ket timmaray iti kampona, ket adu unay dagiti napapatay; ta tallopulo a soldado manipud iti Israel ti naidasay.
11 Ndipo Bokosi la Chipangano la Yehova linalandidwa, ndiponso ana awiri Eli, Hofini ndi Finehasi anaphedwa.
Naalada ti lakasa ti tulag ti Dios, ket natay dagiti dua nga anak ni Eli, a da Ofni ken Finees.
12 Tsiku lomwelo munthu wina wa fuko la Benjamini anathawa ku nkhondo ndipo anafika ku Silo. Iyeyu zovala zake zinali zongʼamba ndipo anadzithira dothi kumutu kuonetsa chisoni.
Iti dayta met laeng nga aldaw, maysa a lalaki a nagtaud iti tribu ni Benjamin ti timmaray manipud iti paggugubatan ket napan idiay Silo, simmangpet a naray-ab ti kawesna ken kataptapok ti ulona.
13 Atafika, anapeza Eli atakhala pa mpando wake mʼmbali mwa msewu, akungoyangʼana, pakuti ankadera nkhawa Bokosi la Mulungu. Munthuyo atalowa mu mzindamo ndi kufotokoza zimene zinachitika ku nkhondo, anthu onse a mu mzindamo anayamba kulira.
Idi simmangpet isuna, nakatugaw ni Eli iti tugawna iti igid ti dalan nga agpadpadaan gapu ta agkebba-kebba ti pusona ta maseknan isuna iti lakasa ti tulag ti Dios. Idi simrek ti lalaki iti siudad ken imbagana ti damag, nagsangit iti napigsa ti entero a siudad.
14 Eli atamva kulirako anafunsa kuti, “Kodi phokosoli likutanthauza chiyani?” Tsono munthu wa fuko la Benjamini uja anapita msanga kwa Eli kukamufotokozera.
Idi nangngeg ni Eli ti ariwawa ti napigsa a panagsasangit, kinunana, “Ania ti kayat a sawen daytoy nga ariwawa?” Dagus nga immay ti lalaki ket imbagana kenni Eli ti makagapu.
15 Nthawiyo nʼkuti Eli ali wa zaka 98 ndipo maso ake anali atachita khungu kotero kuti samatha kuona.
Ita, siyam a pulo ket walo ti tawen ni Eli; nakapsuten ti panagkitana, ket saanen a makakita.
16 Munthuyo anamuwuza Eli kuti, “Ine ndabwera kuchokera ku nkhondo, ndathawako lero lomwe lino.” Eli anafunsa, “Nanga nkhondo yayenda bwanji mwana wanga?”
Kinuna ti lalaki kenni Eli, “Siak ti naggapu iti paggugubatan. Naglibasak manipud iti paggugubatan ita nga aldaw.” Ket kinunana, “Ania ti napasamak anakko?”
17 Iye anayankha kuti, “Aisraeli athawa pamaso pa Afilisti. Anthu ambirimbiri aphedwa. Ana anunso Hofini ndi Finehasi aphedwa. Bokosi la Mulungu nalonso lalandidwa.”
Simmungbat ti lalaki a nangiyeg iti damag ket kinunana, “Intarayan ti Israel dagiti Filisteo. Nakaro met ti pannakaabak dagiti tattao. Dagiti dua nga annakmo, a da Ofni ken Finees, ket natayen ken naipanaw ti lakasa ti tulag ti Dios.”
18 Atangotchula Bokosi la Yehova, Eli anagwa chagada, kuchoka pa mpando wake umene unali mʼmbali mwa chitseko cha mpanda. Khosi lake linathyoka ndipo anafa, pakuti anali okalamba ndi onenepa kwambiri. Iye anatsogolera Israeli zaka makumi anayi.
Idi nadakamatna ti lakasa ti tulag ti Dios, naliad ni Eli iti tugawna iti igid ti ruangan. Narung-o ti tengngedna, ket natay, gapu ta lakayen ken nadagsen isuna. Nagbalin isuna a kas ukom iti Israel iti las-ud ti uppat a pulo a tawen.
19 Nthawiyo, mpongozi wa Eli, mkazi wa Finehasi anali woyembekezera ndipo anali pafupi kuchira. Atamva kuti Bokosi la Mulungu lalandidwa ndi kuti mpongozi wake Eli ndi mwamuna wake amwalira, ululu wa pobereka mwana unamufikira modzidzimutsa ndipo anabereka mwana.
Ita, ti manugangna nga asawa ni Finees ket masikog ken dandanin ti panaganakna. Idi nadamagna a naipanaw ti lakasa ti tulag ti Dios ken natay ti katugangan ken asawana, nagparintumeng isuna ket naganak, ngem nakaro unay ti ut-ot a sinagabana gapu iti panaganakna.
20 Popeza mkaziyo anali pafupi kumwalira, akazi amene amamuthandiza anati, “Usaope, wabereka mwana wamwamuna” Koma iye sanayankhe kapena kulabadirako.
Idi matmatayen isuna, kinuna dagiti babbai a nangpaanak kenkuana, “Saanka a mawanan iti namnanama, ta nangipasngayka iti maysa a lalaki.” Ngem saan isuna a simmungbat wenno saanna ida nga impangag.
21 Tsono iye anatcha mwanayo dzina loti Ikabodi kutanthauza kuti, “Ulemerero wachoka mu Israeli,” chifukwa cha kulandidwa Bokosi la Mulungu ndi imfa ya mpongozi wake Eli ndi mwamuna wake.
Pinanagananna ti ubing iti Icabod, a kinunana, “Pimmanaw ti dayag manipud iti Israel!” ta naagawda ti lakasa ti tulag ti Dios, ken gapu iti katugangan ken asawana. Ket kinunana,
22 Ananena momwemo kuti, “Ulemerero wachoka mu Israeli, pakuti Bokosi la Mulungu lalandidwa.”
“Pimmanaw ti dayag manipud iti Israel, gapu ta naagaw ti lakasa ti tulag ti Dios.”