< 1 Samueli 4 >
1 Ndipo mawu a Samueli anafika kwa Aisraeli onse. Aisraeli anapita kukamenya nkhondo ndi Afilisti. Aisraeli anamanga misasa yawo ku Ebenezeri, ndipo Afilisti anamanga ku Afeki.
Or la parole de Samuel était pour tout Israël. Et Israël sortit en guerre à la rencontre des Philistins, et campa près d'Ében-Ézer; et les Philistins campèrent à Aphek.
2 Afilisti anandanda kuyangʼana Aisraeli nayamba kumenyana. Nkhondo inakula ndipo Afilisti anagonjetsa Aisraeli napha anthu 4,000 pa malo a nkhondopo.
Et les Philistins se rangèrent en bataille contre Israël; et le combat s'engagea, et Israël fut battu par les Philistins, qui tuèrent en bataille rangée dans la campagne, environ quatre mille hommes.
3 Asilikali atabwerera ku misasa, akuluakulu a Israeli anafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani Yehova walola kuti tigonjetsedwe lero pamaso pa Afilisti? Tiyeni tikatenge Bokosi la Chipangano cha Yehova ku Silo kuti Yehovayo abwere kukhala pakati pathu ndi kutipulumutsa mʼmanja mwa adani athu.”
Et le peuple étant rentré au camp, les anciens d'Israël dirent: Pourquoi l'Éternel nous a-t-il laissé battre aujourd'hui par les Philistins? Faisons venir de Silo l'arche de l'alliance de l'Éternel, et qu'il vienne au milieu de nous, et nous délivre de la main de nos ennemis.
4 Choncho anatuma anthu ku Silo ndipo anakatenga Bokosi la Chipangano cha Yehova Wamphamvuzonse amene amakhala pa akerubi. Ndipo ana awiri a Eli, Hofini ndi Finehasi anatsagana nalo Bokosi la Chipangano cha Mulungu.
Le peuple envoya donc à Silo, d'où l'on apporta l'arche de l'alliance de l'Éternel des armées, qui habite entre les chérubins; et les deux fils d'Héli, Hophni et Phinées, y étaient avec l'arche de l'alliance de Dieu.
5 Bokosi la Chipangano cha Yehova litafika ku msasa, Aisraeli onse anafuwula kwambiri mpaka nthaka inagwedezeka.
Et comme l'arche de l'Éternel entrait au camp, tout Israël jeta de si grands cris de joie, que la terre en retentit.
6 Atamva kufuwulaku, Afilisti anafunsa, “Kodi kufuwula kwakukulu kumeneku ku misasa ya Ahebri ndi kwachiyani?” Atamva kuti Bokosi la Yehova lafika ku msasako,
Et les Philistins, entendant le bruit des cris de joie, dirent: Que veulent dire ces grands cris de joie au camp des Hébreux? Et ils surent que l'arche de l'Éternel était venue au camp.
7 Afilisti anachita mantha pakuti iwo ankanena kuti, “Milungu yafika ku msasa. Iwo anati, ‘Tili pamavuto. Chinthu choterechi sichinachitikepo nʼkale lomwe.
Et les Philistins eurent peur, car ils disaient: Dieu est venu au camp; et ils dirent: Malheur à nous! car il n'en était pas ainsi ces jours passés;
8 Atsoka ife! Adzatipulumutsa ndani mʼmanja mwa milungu yamphamvuyi? Iyi ndi milungu imene inakantha Aigupto ndi miliri yosiyanasiyana mʼchipululu.
Malheur à nous! qui nous délivrera de la main de ces Dieux puissants? Ce sont ces Dieux qui ont frappé les Égyptiens de toute sorte de plaies au désert.
9 Limbani mtima Afilisti! Chitani chamuna, kuti mungakhale akapolo a Ahebri monga iwowa alili akapolo anu. Chitani chamuna ndipo menyani nkhondo!’”
Philistins, renforcez-vous, et agissez en hommes, de peur que vous ne soyez esclaves des Hébreux, comme ils ont été les vôtres; soyez donc hommes, et combattez.
10 Choncho Afilisti anamenya nkhondo, ndipo anagonjetsa Aisraeli. Iwo anathawa aliyense kwawo. Ankhondo a Aisraeli oyenda pansi okwanira 30,000 anaphedwa.
Les Philistins combattirent donc, et Israël fut battu, et chacun s'enfuit en sa tente; la défaite fut très grande, et trente mille hommes de pied d'Israël y périrent.
11 Ndipo Bokosi la Chipangano la Yehova linalandidwa, ndiponso ana awiri Eli, Hofini ndi Finehasi anaphedwa.
Et l'arche de Dieu fut prise; et les deux fils d'Héli, Hophni et Phinées, moururent.
12 Tsiku lomwelo munthu wina wa fuko la Benjamini anathawa ku nkhondo ndipo anafika ku Silo. Iyeyu zovala zake zinali zongʼamba ndipo anadzithira dothi kumutu kuonetsa chisoni.
Or, un homme de Benjamin s'enfuit de la bataille, et arriva à Silo ce jour-là, les vêtements déchirés, et de la poussière sur la tête;
13 Atafika, anapeza Eli atakhala pa mpando wake mʼmbali mwa msewu, akungoyangʼana, pakuti ankadera nkhawa Bokosi la Mulungu. Munthuyo atalowa mu mzindamo ndi kufotokoza zimene zinachitika ku nkhondo, anthu onse a mu mzindamo anayamba kulira.
Et comme il arrivait, voici, Héli était assis sur son siège à côté du chemin, en attente; car son cœur tremblait à cause de l'arche de Dieu. Cet homme entra donc dans la ville pour porter ces nouvelles, et toute la ville se mit à crier.
14 Eli atamva kulirako anafunsa kuti, “Kodi phokosoli likutanthauza chiyani?” Tsono munthu wa fuko la Benjamini uja anapita msanga kwa Eli kukamufotokozera.
Et Héli, entendant ces clameurs, dit: Que veut dire ce bruit, ce tumulte? Et cet homme, se hâtant, vint à Héli, et lui raconta tout.
15 Nthawiyo nʼkuti Eli ali wa zaka 98 ndipo maso ake anali atachita khungu kotero kuti samatha kuona.
Or, Héli était âgé de quatre-vingt-dix-huit ans, et ses yeux étaient fixes, et il ne pouvait plus voir.
16 Munthuyo anamuwuza Eli kuti, “Ine ndabwera kuchokera ku nkhondo, ndathawako lero lomwe lino.” Eli anafunsa, “Nanga nkhondo yayenda bwanji mwana wanga?”
L'homme dit donc à Héli: C'est moi qui viens de la bataille; et je me suis échappé de la bataille aujourd'hui. Et Héli dit: Qu'est-il arrivé, mon fils?
17 Iye anayankha kuti, “Aisraeli athawa pamaso pa Afilisti. Anthu ambirimbiri aphedwa. Ana anunso Hofini ndi Finehasi aphedwa. Bokosi la Mulungu nalonso lalandidwa.”
Et celui qui apportait les nouvelles répondit, et dit: Israël a fui devant les Philistins; et même il y a eu une grande défaite parmi le peuple, et tes deux fils, Hophni et Phinées, sont morts aussi, et l'arche de Dieu a été prise.
18 Atangotchula Bokosi la Yehova, Eli anagwa chagada, kuchoka pa mpando wake umene unali mʼmbali mwa chitseko cha mpanda. Khosi lake linathyoka ndipo anafa, pakuti anali okalamba ndi onenepa kwambiri. Iye anatsogolera Israeli zaka makumi anayi.
Et dès qu'il eut fait mention de l'arche de Dieu, Héli tomba à la renverse de dessus son siège, à côté de la porte, et il se rompit le cou, et mourut; car c'était un homme vieux et pesant. Il avait jugé Israël quarante ans.
19 Nthawiyo, mpongozi wa Eli, mkazi wa Finehasi anali woyembekezera ndipo anali pafupi kuchira. Atamva kuti Bokosi la Mulungu lalandidwa ndi kuti mpongozi wake Eli ndi mwamuna wake amwalira, ululu wa pobereka mwana unamufikira modzidzimutsa ndipo anabereka mwana.
Et sa belle-fille, femme de Phinées, qui était enceinte et sur le point d'accoucher, ayant appris la nouvelle que l'arche de Dieu était prise, et que son beau-père et son mari étaient morts, s'affaissa et enfanta; car les douleurs lui survinrent.
20 Popeza mkaziyo anali pafupi kumwalira, akazi amene amamuthandiza anati, “Usaope, wabereka mwana wamwamuna” Koma iye sanayankhe kapena kulabadirako.
Et comme elle se mourait, celles qui étaient près d'elle, lui dirent: Ne crains point; car tu as enfanté un fils. Mais elle ne répondit rien, et n'y fit aucune attention.
21 Tsono iye anatcha mwanayo dzina loti Ikabodi kutanthauza kuti, “Ulemerero wachoka mu Israeli,” chifukwa cha kulandidwa Bokosi la Mulungu ndi imfa ya mpongozi wake Eli ndi mwamuna wake.
Et elle nomma l'enfant Icabod (sans gloire), en disant: La gloire est ôtée d'Israël; parce que l'arche de l'Éternel était prise, et à cause de son beau-père et de son mari.
22 Ananena momwemo kuti, “Ulemerero wachoka mu Israeli, pakuti Bokosi la Mulungu lalandidwa.”
Elle dit donc: La gloire est ôtée d'Israël; car l'arche de Dieu est prise.