< 1 Samueli 4 >

1 Ndipo mawu a Samueli anafika kwa Aisraeli onse. Aisraeli anapita kukamenya nkhondo ndi Afilisti. Aisraeli anamanga misasa yawo ku Ebenezeri, ndipo Afilisti anamanga ku Afeki.
La parole de Samuel fut adressée à tout Israël. Israël sortit contre les Philistins pour combattre, et il campa près d'Ébénézer; les Philistins campèrent à Aphek.
2 Afilisti anandanda kuyangʼana Aisraeli nayamba kumenyana. Nkhondo inakula ndipo Afilisti anagonjetsa Aisraeli napha anthu 4,000 pa malo a nkhondopo.
Les Philistins se rangèrent en bataille contre Israël. Lorsqu'ils se battirent, Israël fut vaincu par les Philistins, qui tuèrent en campagne environ quatre mille hommes de l'armée.
3 Asilikali atabwerera ku misasa, akuluakulu a Israeli anafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani Yehova walola kuti tigonjetsedwe lero pamaso pa Afilisti? Tiyeni tikatenge Bokosi la Chipangano cha Yehova ku Silo kuti Yehovayo abwere kukhala pakati pathu ndi kutipulumutsa mʼmanja mwa adani athu.”
Lorsque le peuple fut rentré dans le camp, les anciens d'Israël dirent: « Pourquoi Yahvé nous a-t-il vaincus aujourd'hui devant les Philistins? Allons chercher l'arche de l'alliance de Yahvé à Silo et apportons-la à nous, afin qu'elle vienne au milieu de nous et nous sauve de la main de nos ennemis. »
4 Choncho anatuma anthu ku Silo ndipo anakatenga Bokosi la Chipangano cha Yehova Wamphamvuzonse amene amakhala pa akerubi. Ndipo ana awiri a Eli, Hofini ndi Finehasi anatsagana nalo Bokosi la Chipangano cha Mulungu.
Et le peuple envoya à Silo, et l'on apporta de là l'arche de l'alliance de Yahvé des armées, qui est assis au-dessus des chérubins; et les deux fils d'Eli, Hophni et Phinées, étaient là avec l'arche de l'alliance de Dieu.
5 Bokosi la Chipangano cha Yehova litafika ku msasa, Aisraeli onse anafuwula kwambiri mpaka nthaka inagwedezeka.
Lorsque l'arche de l'alliance de Yahvé entra dans le camp, tout Israël poussa de grands cris, au point que la terre en résonna.
6 Atamva kufuwulaku, Afilisti anafunsa, “Kodi kufuwula kwakukulu kumeneku ku misasa ya Ahebri ndi kwachiyani?” Atamva kuti Bokosi la Yehova lafika ku msasako,
Lorsque les Philistins entendirent le bruit de ce cri, ils dirent: « Que signifie le bruit de ce grand cri dans le camp des Hébreux? ». Ils comprirent que l'arche de Yahvé était entrée dans le camp.
7 Afilisti anachita mantha pakuti iwo ankanena kuti, “Milungu yafika ku msasa. Iwo anati, ‘Tili pamavuto. Chinthu choterechi sichinachitikepo nʼkale lomwe.
Les Philistins eurent peur, car ils disaient: « Dieu est entré dans le camp. » Ils dirent: « Malheur à nous! Car il n'y a jamais eu de chose semblable auparavant.
8 Atsoka ife! Adzatipulumutsa ndani mʼmanja mwa milungu yamphamvuyi? Iyi ndi milungu imene inakantha Aigupto ndi miliri yosiyanasiyana mʼchipululu.
Malheur à nous! Qui nous délivrera de la main de ces dieux puissants? Ce sont ces dieux qui ont frappé les Égyptiens de toutes sortes de plaies dans le désert.
9 Limbani mtima Afilisti! Chitani chamuna, kuti mungakhale akapolo a Ahebri monga iwowa alili akapolo anu. Chitani chamuna ndipo menyani nkhondo!’”
Fortifiez-vous et comportez-vous comme des hommes, Philistins, pour ne pas être les esclaves des Hébreux, comme ils l'ont été pour vous. Fortifiez-vous comme des hommes, et combattez! »
10 Choncho Afilisti anamenya nkhondo, ndipo anagonjetsa Aisraeli. Iwo anathawa aliyense kwawo. Ankhondo a Aisraeli oyenda pansi okwanira 30,000 anaphedwa.
Les Philistins combattirent, Israël fut vaincu, et chacun s'enfuit dans sa tente. Il y eut un très grand carnage, car trente mille fantassins d'Israël tombèrent.
11 Ndipo Bokosi la Chipangano la Yehova linalandidwa, ndiponso ana awiri Eli, Hofini ndi Finehasi anaphedwa.
L'arche de Dieu fut prise, et les deux fils d'Eli, Hophni et Phinées, furent tués.
12 Tsiku lomwelo munthu wina wa fuko la Benjamini anathawa ku nkhondo ndipo anafika ku Silo. Iyeyu zovala zake zinali zongʼamba ndipo anadzithira dothi kumutu kuonetsa chisoni.
Un homme de Benjamin sortit de l'armée et arriva à Silo le même jour, les vêtements déchirés et la tête couverte de terre.
13 Atafika, anapeza Eli atakhala pa mpando wake mʼmbali mwa msewu, akungoyangʼana, pakuti ankadera nkhawa Bokosi la Mulungu. Munthuyo atalowa mu mzindamo ndi kufotokoza zimene zinachitika ku nkhondo, anthu onse a mu mzindamo anayamba kulira.
Lorsqu'il arriva, voici qu'Eli était assis sur son siège, au bord du chemin, à regarder, car son cœur tremblait pour l'arche de Dieu. Lorsque l'homme entra dans la ville et en fit le récit, toute la ville poussa des cris.
14 Eli atamva kulirako anafunsa kuti, “Kodi phokosoli likutanthauza chiyani?” Tsono munthu wa fuko la Benjamini uja anapita msanga kwa Eli kukamufotokozera.
Lorsque Eli entendit le bruit des cris, il dit: « Que signifie le bruit de ce tumulte? » L'homme se hâta, et vint le dire à Eli.
15 Nthawiyo nʼkuti Eli ali wa zaka 98 ndipo maso ake anali atachita khungu kotero kuti samatha kuona.
Or, Eli était âgé de quatre-vingt-dix-huit ans. Ses yeux étaient fixes, de sorte qu'il ne pouvait pas voir.
16 Munthuyo anamuwuza Eli kuti, “Ine ndabwera kuchokera ku nkhondo, ndathawako lero lomwe lino.” Eli anafunsa, “Nanga nkhondo yayenda bwanji mwana wanga?”
L'homme dit à Eli: « Je suis celui qui est sorti de l'armée, et je me suis enfui aujourd'hui de l'armée. » Il a dit: « Comment ça s'est passé, mon fils? »
17 Iye anayankha kuti, “Aisraeli athawa pamaso pa Afilisti. Anthu ambirimbiri aphedwa. Ana anunso Hofini ndi Finehasi aphedwa. Bokosi la Mulungu nalonso lalandidwa.”
Celui qui apportait la nouvelle répondit: « Israël a fui devant les Philistins, et il y a aussi eu un grand massacre parmi le peuple. Tes deux fils aussi, Hophni et Phinées, sont morts, et l'arche de Dieu a été capturée. »
18 Atangotchula Bokosi la Yehova, Eli anagwa chagada, kuchoka pa mpando wake umene unali mʼmbali mwa chitseko cha mpanda. Khosi lake linathyoka ndipo anafa, pakuti anali okalamba ndi onenepa kwambiri. Iye anatsogolera Israeli zaka makumi anayi.
Lorsqu'il parla de l'arche de Dieu, Eli tomba de son siège en arrière, du côté de la porte; son cou se brisa, et il mourut, car il était vieux et pesant. Il avait jugé Israël pendant quarante ans.
19 Nthawiyo, mpongozi wa Eli, mkazi wa Finehasi anali woyembekezera ndipo anali pafupi kuchira. Atamva kuti Bokosi la Mulungu lalandidwa ndi kuti mpongozi wake Eli ndi mwamuna wake amwalira, ululu wa pobereka mwana unamufikira modzidzimutsa ndipo anabereka mwana.
Sa belle-fille, la femme de Phinées, était enceinte, sur le point d'accoucher. Lorsqu'elle apprit la nouvelle de la prise de l'arche de Dieu et de la mort de son beau-père et de son mari, elle se courba et accoucha, car ses douleurs la surprirent.
20 Popeza mkaziyo anali pafupi kumwalira, akazi amene amamuthandiza anati, “Usaope, wabereka mwana wamwamuna” Koma iye sanayankhe kapena kulabadirako.
Vers le moment où elle mourut, les femmes qui se tenaient près d'elle lui dirent: « N'aie pas peur, car tu as donné naissance à un fils. » Mais elle ne répondit pas et n'y fit pas attention.
21 Tsono iye anatcha mwanayo dzina loti Ikabodi kutanthauza kuti, “Ulemerero wachoka mu Israeli,” chifukwa cha kulandidwa Bokosi la Mulungu ndi imfa ya mpongozi wake Eli ndi mwamuna wake.
Elle donna à l'enfant le nom d'Ichabod, en disant: « La gloire s'est retirée d'Israël », parce que l'arche de Dieu avait été prise, et à cause de son beau-père et de son mari.
22 Ananena momwemo kuti, “Ulemerero wachoka mu Israeli, pakuti Bokosi la Mulungu lalandidwa.”
Elle dit: « La gloire a disparu d'Israël, car l'arche de Dieu a été prise. »

< 1 Samueli 4 >