< 1 Samueli 4 >

1 Ndipo mawu a Samueli anafika kwa Aisraeli onse. Aisraeli anapita kukamenya nkhondo ndi Afilisti. Aisraeli anamanga misasa yawo ku Ebenezeri, ndipo Afilisti anamanga ku Afeki.
And the word of Samuel became known to all Israel. Now Israel went out against the Philistines to battle, and encamped beside Eben-ha'ezer; and the Philistines encamped in Aphek.
2 Afilisti anandanda kuyangʼana Aisraeli nayamba kumenyana. Nkhondo inakula ndipo Afilisti anagonjetsa Aisraeli napha anthu 4,000 pa malo a nkhondopo.
And the Philistines put themselves in battle-array against Israel; and the battle became general, and Israel was smitten before the Philistines: and they slew on the battle-ground, in the field, about four thousand men.
3 Asilikali atabwerera ku misasa, akuluakulu a Israeli anafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani Yehova walola kuti tigonjetsedwe lero pamaso pa Afilisti? Tiyeni tikatenge Bokosi la Chipangano cha Yehova ku Silo kuti Yehovayo abwere kukhala pakati pathu ndi kutipulumutsa mʼmanja mwa adani athu.”
And when the people were come back into the camp, the elders of Israel said, Wherefore hath the Lord smitten us this day before the Philistines? Let us bring over to us out of Shiloh the ark of the covenant of the Lord, that it may come in the midst of us, and deliver us out of the hand of our enemies.
4 Choncho anatuma anthu ku Silo ndipo anakatenga Bokosi la Chipangano cha Yehova Wamphamvuzonse amene amakhala pa akerubi. Ndipo ana awiri a Eli, Hofini ndi Finehasi anatsagana nalo Bokosi la Chipangano cha Mulungu.
So the people sent to Shiloh, and they brought away from there the ark of the covenant of the Lord of hosts, who dwelleth over the cherubim: and the two sons of 'Eli, Chophni and Phinehas, were there with the ark of the covenant of God.
5 Bokosi la Chipangano cha Yehova litafika ku msasa, Aisraeli onse anafuwula kwambiri mpaka nthaka inagwedezeka.
And it happened when the ark of the covenant of the Lord came into the camp, that all Israel set up a great shout, so that the earth trembled.
6 Atamva kufuwulaku, Afilisti anafunsa, “Kodi kufuwula kwakukulu kumeneku ku misasa ya Ahebri ndi kwachiyani?” Atamva kuti Bokosi la Yehova lafika ku msasako,
And when the Philistines heard the noise of the shouting, they said, What meaneth the noise of this great shouting in the camp of the Hebrews? And they understood that the ark of the Lord was come into the camp.
7 Afilisti anachita mantha pakuti iwo ankanena kuti, “Milungu yafika ku msasa. Iwo anati, ‘Tili pamavuto. Chinthu choterechi sichinachitikepo nʼkale lomwe.
And the Philistines were afraid; for they said, God is come into the camp. And they said, Woe unto us! for the like of this hath not been, yesterday or the day before.
8 Atsoka ife! Adzatipulumutsa ndani mʼmanja mwa milungu yamphamvuyi? Iyi ndi milungu imene inakantha Aigupto ndi miliri yosiyanasiyana mʼchipululu.
Woe unto us! who shall deliver us out of the hand of these mighty Gods? these are the Gods that smote the Egyptians with every plague in the wilderness.
9 Limbani mtima Afilisti! Chitani chamuna, kuti mungakhale akapolo a Ahebri monga iwowa alili akapolo anu. Chitani chamuna ndipo menyani nkhondo!’”
Be strong, and act like men, O Philistines, so that ye become not servants unto the Hebrews, as they have been servants to you: therefore act like men, and fight.
10 Choncho Afilisti anamenya nkhondo, ndipo anagonjetsa Aisraeli. Iwo anathawa aliyense kwawo. Ankhondo a Aisraeli oyenda pansi okwanira 30,000 anaphedwa.
And the Philistines fought, and the Israelites were smitten, and they fled every man unto his tent: and the defeat was very great; and there fell of Israel thirty thousand men on foot.
11 Ndipo Bokosi la Chipangano la Yehova linalandidwa, ndiponso ana awiri Eli, Hofini ndi Finehasi anaphedwa.
And the ark of God was taken; and the two sons of 'Eli, Chophni and Phinehas, died also.
12 Tsiku lomwelo munthu wina wa fuko la Benjamini anathawa ku nkhondo ndipo anafika ku Silo. Iyeyu zovala zake zinali zongʼamba ndipo anadzithira dothi kumutu kuonetsa chisoni.
And there ran a man of Benjamin from the battlefield, and came to Shiloh on the same day, with his clothes rent, and earth upon his head.
13 Atafika, anapeza Eli atakhala pa mpando wake mʼmbali mwa msewu, akungoyangʼana, pakuti ankadera nkhawa Bokosi la Mulungu. Munthuyo atalowa mu mzindamo ndi kufotokoza zimene zinachitika ku nkhondo, anthu onse a mu mzindamo anayamba kulira.
And when he came, lo, 'Eli was sitting upon a chair by the wayside watching; for his heart was anxious for the ark of God. And when the man came to tell it in the city, all the city cried out.
14 Eli atamva kulirako anafunsa kuti, “Kodi phokosoli likutanthauza chiyani?” Tsono munthu wa fuko la Benjamini uja anapita msanga kwa Eli kukamufotokozera.
And when 'Eli heard the noise of the crying, he said, What meaneth the noise of this multitude? And the man came in hastily, and told it to 'Eli.
15 Nthawiyo nʼkuti Eli ali wa zaka 98 ndipo maso ake anali atachita khungu kotero kuti samatha kuona.
Now 'Eli was ninety and eight years old; and his eyes were fixed, so that he could not see.
16 Munthuyo anamuwuza Eli kuti, “Ine ndabwera kuchokera ku nkhondo, ndathawako lero lomwe lino.” Eli anafunsa, “Nanga nkhondo yayenda bwanji mwana wanga?”
And the man said unto 'Eli, I am the person that came from the battlefield, and I myself fled from the battlefield today. And he said, What was it that took place, my son?
17 Iye anayankha kuti, “Aisraeli athawa pamaso pa Afilisti. Anthu ambirimbiri aphedwa. Ana anunso Hofini ndi Finehasi aphedwa. Bokosi la Mulungu nalonso lalandidwa.”
And the messenger answered and said, Israel is fled before the Philistines, and there hath also been a great slaughter among the people, and also thy two sons, Chophni and Phinehas, are dead, and the ark of God hath been taken.
18 Atangotchula Bokosi la Yehova, Eli anagwa chagada, kuchoka pa mpando wake umene unali mʼmbali mwa chitseko cha mpanda. Khosi lake linathyoka ndipo anafa, pakuti anali okalamba ndi onenepa kwambiri. Iye anatsogolera Israeli zaka makumi anayi.
And it came to pass, when he mentioned the ark of God, that he fell from off the chair backward by the side of the gate, and his neck was broken, and he died; for the man was old, and heavy. And he had judged Israel forty years.
19 Nthawiyo, mpongozi wa Eli, mkazi wa Finehasi anali woyembekezera ndipo anali pafupi kuchira. Atamva kuti Bokosi la Mulungu lalandidwa ndi kuti mpongozi wake Eli ndi mwamuna wake amwalira, ululu wa pobereka mwana unamufikira modzidzimutsa ndipo anabereka mwana.
And his daughter-in-law, the wife of Phinehas, was with child, near to be delivered: and when she heard the tidings concerning that the ark of God had been taken, and that her father-in-law and her husband were dead, she sank down and gave birth; for her pains came suddenly upon her.
20 Popeza mkaziyo anali pafupi kumwalira, akazi amene amamuthandiza anati, “Usaope, wabereka mwana wamwamuna” Koma iye sanayankhe kapena kulabadirako.
And at the moment of her dying, the women that stood around her spoke [unto her], Fear not; for a son hast thou born. But she answered not, nor did she take it to heart.
21 Tsono iye anatcha mwanayo dzina loti Ikabodi kutanthauza kuti, “Ulemerero wachoka mu Israeli,” chifukwa cha kulandidwa Bokosi la Mulungu ndi imfa ya mpongozi wake Eli ndi mwamuna wake.
And she named the child I-chabod, saying, Glory is departed from Israel; because of the taking away of the ark of God, and because of her father-in-law and her husband.
22 Ananena momwemo kuti, “Ulemerero wachoka mu Israeli, pakuti Bokosi la Mulungu lalandidwa.”
And she said, Glory is departed from Israel; for the ark of God hath been taken away.

< 1 Samueli 4 >