< 1 Samueli 4 >
1 Ndipo mawu a Samueli anafika kwa Aisraeli onse. Aisraeli anapita kukamenya nkhondo ndi Afilisti. Aisraeli anamanga misasa yawo ku Ebenezeri, ndipo Afilisti anamanga ku Afeki.
I stalo se vedlé řeči Samuelovy všemu lidu Izraelskému. Nebo když vytáhl Izrael proti Filistinským k boji, a položili se při Eben-Ezer, Filistinští pak položili se v Afeku;
2 Afilisti anandanda kuyangʼana Aisraeli nayamba kumenyana. Nkhondo inakula ndipo Afilisti anagonjetsa Aisraeli napha anthu 4,000 pa malo a nkhondopo.
A když se sšikovali Filistinští proti Izraelovi, a již se potýkali: poražen jest Izrael od Filistinských, tak že jich zbito v té bitvě na poli takměř čtyři tisíce mužů.
3 Asilikali atabwerera ku misasa, akuluakulu a Israeli anafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani Yehova walola kuti tigonjetsedwe lero pamaso pa Afilisti? Tiyeni tikatenge Bokosi la Chipangano cha Yehova ku Silo kuti Yehovayo abwere kukhala pakati pathu ndi kutipulumutsa mʼmanja mwa adani athu.”
I navrátil se lid do stanů, a řekli starší Izraelští: Proč nás dnes Hospodin porazil před Filistinskými? Vezměme k sobě z Sílo truhlu smlouvy Hospodinovy, ať přijde mezi nás, a vysvobodí nás z rukou nepřátel našich.
4 Choncho anatuma anthu ku Silo ndipo anakatenga Bokosi la Chipangano cha Yehova Wamphamvuzonse amene amakhala pa akerubi. Ndipo ana awiri a Eli, Hofini ndi Finehasi anatsagana nalo Bokosi la Chipangano cha Mulungu.
Poslal tedy lid do Sílo, a vzali odtud truhlu smlouvy Hospodina zástupů, sedícího na cherubínech. Byli také tam dva synové Elí s truhlou smlouvy Boží, Ofni a Fínes.
5 Bokosi la Chipangano cha Yehova litafika ku msasa, Aisraeli onse anafuwula kwambiri mpaka nthaka inagwedezeka.
Když pak přinesena byla truhla smlouvy Hospodinovy do vojska, zkřikl všecken Izrael s velikým plésáním, až země vzněla.
6 Atamva kufuwulaku, Afilisti anafunsa, “Kodi kufuwula kwakukulu kumeneku ku misasa ya Ahebri ndi kwachiyani?” Atamva kuti Bokosi la Yehova lafika ku msasako,
Uslyševše pak Filistinští hluk plésání, řekli: Jaký jest to hlas výskání velikého tohoto v vojště Hebrejském? I poznali, že truhla Hospodinova přišla do vojska.
7 Afilisti anachita mantha pakuti iwo ankanena kuti, “Milungu yafika ku msasa. Iwo anati, ‘Tili pamavuto. Chinthu choterechi sichinachitikepo nʼkale lomwe.
Protož báli se Filistinští, když praveno bylo: Přišel Bůh do vojska jejich; a řekli: Běda nám, nebo nebylo prvé nic k tomu podobného.
8 Atsoka ife! Adzatipulumutsa ndani mʼmanja mwa milungu yamphamvuyi? Iyi ndi milungu imene inakantha Aigupto ndi miliri yosiyanasiyana mʼchipululu.
Běda nám! Kdo nás vysvobodí z ruky těch bohů silných? Tiť jsou bohové, kteříž zbili Egypt všelikou ranou i na poušti.
9 Limbani mtima Afilisti! Chitani chamuna, kuti mungakhale akapolo a Ahebri monga iwowa alili akapolo anu. Chitani chamuna ndipo menyani nkhondo!’”
Posilňte se a buďte muži, ó Filistinští, abyste nesloužili těm Hebrejským, jako oni sloužili vám; buďtež tedy muži a bojujte.
10 Choncho Afilisti anamenya nkhondo, ndipo anagonjetsa Aisraeli. Iwo anathawa aliyense kwawo. Ankhondo a Aisraeli oyenda pansi okwanira 30,000 anaphedwa.
Bojovali tedy Filistinští, a poražen jest Izrael, a utíkali jeden každý do stanu svého. I byla ta porážka veliká velmi, nebo padlo z Izraele třidceti tisíc pěších;
11 Ndipo Bokosi la Chipangano la Yehova linalandidwa, ndiponso ana awiri Eli, Hofini ndi Finehasi anaphedwa.
Také truhla Boží vzata, a dva synové Elí zabiti, Ofni a Fínes.
12 Tsiku lomwelo munthu wina wa fuko la Benjamini anathawa ku nkhondo ndipo anafika ku Silo. Iyeyu zovala zake zinali zongʼamba ndipo anadzithira dothi kumutu kuonetsa chisoni.
Běže pak jeden Beniaminský z bitvy, přišel do Sílo téhož dne, maje roucho roztržené a hlavu prstí posypanou.
13 Atafika, anapeza Eli atakhala pa mpando wake mʼmbali mwa msewu, akungoyangʼana, pakuti ankadera nkhawa Bokosi la Mulungu. Munthuyo atalowa mu mzindamo ndi kufotokoza zimene zinachitika ku nkhondo, anthu onse a mu mzindamo anayamba kulira.
Přišel tedy, a aj, Elí seděl na stolici při cestě, hledě, nebo srdce jeho lekalo se za truhlu Boží; a když všel muž ten, a oznámil v městě, kvílilo všecko město.
14 Eli atamva kulirako anafunsa kuti, “Kodi phokosoli likutanthauza chiyani?” Tsono munthu wa fuko la Benjamini uja anapita msanga kwa Eli kukamufotokozera.
A uslyšev Elí hlas křiku toho, řekl: Jaký jest to hlas hřmotu tohoto? Muž pak ten pospíchaje, přiběhl, aby oznámil Elí.
15 Nthawiyo nʼkuti Eli ali wa zaka 98 ndipo maso ake anali atachita khungu kotero kuti samatha kuona.
(A byl Elí v devadesáti a osmi letech; oči také jeho byly již pošly, a nemohl viděti.)
16 Munthuyo anamuwuza Eli kuti, “Ine ndabwera kuchokera ku nkhondo, ndathawako lero lomwe lino.” Eli anafunsa, “Nanga nkhondo yayenda bwanji mwana wanga?”
I řekl muž ten k Elí: Já jdu z bitvy, z bitvy zajisté utekl jsem dnes. I dí jemu on: Co se tam stalo, můj synu?
17 Iye anayankha kuti, “Aisraeli athawa pamaso pa Afilisti. Anthu ambirimbiri aphedwa. Ana anunso Hofini ndi Finehasi aphedwa. Bokosi la Mulungu nalonso lalandidwa.”
Odpověděl ten posel a řekl: Utekl Izrael před Filistinskými, také i porážka veliká stala se v lidu, ano i oba synové tvoji zabiti jsou, Ofni a Fínes, a truhla Boží jest vzata.
18 Atangotchula Bokosi la Yehova, Eli anagwa chagada, kuchoka pa mpando wake umene unali mʼmbali mwa chitseko cha mpanda. Khosi lake linathyoka ndipo anafa, pakuti anali okalamba ndi onenepa kwambiri. Iye anatsogolera Israeli zaka makumi anayi.
I stalo se, že jakž jmenoval truhlu Boží, spadl Elí s stolice nazpět při úhlu brány, a tak zlomiv šíji, umřel; nebo byl muž starý a těžký. On soudil Izraele čtyřidceti let.
19 Nthawiyo, mpongozi wa Eli, mkazi wa Finehasi anali woyembekezera ndipo anali pafupi kuchira. Atamva kuti Bokosi la Mulungu lalandidwa ndi kuti mpongozi wake Eli ndi mwamuna wake amwalira, ululu wa pobereka mwana unamufikira modzidzimutsa ndipo anabereka mwana.
Nevěsta pak jeho, manželka Fínesova, jsuc těhotná a blízká porodu, uslyševši také tu pověst, že by truhla Boží vzata byla, a že umřel tchán její i muž její, sklonila se a porodila; nebo se obořily na ni úzkosti její.
20 Popeza mkaziyo anali pafupi kumwalira, akazi amene amamuthandiza anati, “Usaope, wabereka mwana wamwamuna” Koma iye sanayankhe kapena kulabadirako.
A v ten čas, když ona umírala, řekly, kteréž stály při ní: Neboj se, však jsi porodila syna. Kteráž nic neodpověděla, aniž toho připustila k srdci svému.
21 Tsono iye anatcha mwanayo dzina loti Ikabodi kutanthauza kuti, “Ulemerero wachoka mu Israeli,” chifukwa cha kulandidwa Bokosi la Mulungu ndi imfa ya mpongozi wake Eli ndi mwamuna wake.
I nazvala dítě Ichabod, řkuci: Přestěhovala se sláva z Izraele; proto že vzata byla truhla Boží, a umřel tchán i muž její.
22 Ananena momwemo kuti, “Ulemerero wachoka mu Israeli, pakuti Bokosi la Mulungu lalandidwa.”
Protož řekla: Přestěhovala se sláva z Izraele, nebo vzata jest truhla Boží.