< 1 Samueli 31 >

1 Tsono Afilisti anachitanso nkhondo ndi Aisraeli ndipo Aisraeli anathawa Afilistiwo, kotero kuti ambiri anaphedwa pa phiri la Gilibowa.
Los filisteos atacaron a Israel, y los hombres de Israel huyeron en fuga ante los filisteos, cayendo muertos en el monte Gilboa.
2 Afilisti anapanikiza kwambiri Sauli ndi ana ake, ndipo anapha Yonatani, Abinadabu ndi Maliki-Suwa.
Y los filisteos tomaron a Saúl y sus hijos; y mataron a Jonatán, a Abinadab y a Malquisua, los hijos de Saúl.
3 Nkhondo inakula kwambiri mozungulira Sauli ndipo pamene anthu amauta anamupeza, anamuvulaza kwambiri.
Y la lucha iba mal para Saúl, y los arqueros se cruzaron con él y fue herido por los arqueros.
4 Tsono Sauli anawuza mnyamata wake wonyamula zida zake kuti, “Solola lupanga lako undiphe kuopa kuti anthu osachita mdulidwewa angabwere kudzandizunza ine.” Koma mnyamata wonyamula zida uja anachita mantha kwambiri ndipo sanathe kutero. Choncho Sauli anatenga lupanga lake lomwe nagwerapo.
Entonces Saúl dijo al siervo su escudero: Saca tu espada y pásala a través de mí, antes de que estos hombres sin circuncisión vengan y se burlen de mí. Pero su sirviente, lleno de miedo, no lo hizo. Entonces Saúl sacó su espada y cayendo sobre ella, se puso fin a sí mismo.
5 Mnyamata wonyamula zida zake uja ataona kuti Sauli wafa, nayenso anadzigwetsera pa lupanga lake nafa naye limodzi.
Y cuando su criado vio que Saúl estaba muerto, él hizo lo mismo, y se unió a él en la muerte.
6 Motero Sauli ndi ana ake atatu, wonyamula zida zake pamodzi ndi anthu ake onse anafera limodzi pa tsikulo.
Entonces la muerte alcanzó a Saúl y sus tres hijos y su siervo el mismo día.
7 Pamene Aisraeli amene anali tsidya lina la chigwa ndi amene anali tsidya la chigwa cha Yorodani anaona kuti gulu la ankhondo la Aisraeli lathawa komanso kuti Sauli ndi ana ake aphedwa, nawonso anathawa kusiya mizinda yawo. Ndipo Afilisti anabwera kudzakhalamo.
Y cuando los hombres de Israel cruzaron el valle y al otro lado del Jordán vieron que el ejército de Israel estaba huyendo y que Saúl y sus hijos estaban muertos, salieron de sus ciudades y huyeron; Y vinieron los filisteos y los tomaron para sí mismos.
8 Mmawa mwake, Afilisti atabwera kudzatenga zinthu za anthu ophedwa anapeza Sauli ndi ana ake atatu atafa pa phiri la Gilibowa.
Al día siguiente, cuando los filisteos vinieron a sacar sus bienes de los muertos, vieron a Saúl y sus tres hijos muertos en la tierra en el monte Gilboa.
9 Iwo anadula mutu wake ndi kumuvula zida zake zankhondo. Ndipo anatumiza amithenga mʼdziko lonse la Afilisti kukafalitsa nkhani yabwinoyi kwa mafano awo ndi kwa anthu awo.
Y cortándole la cabeza y quitándole el traje de guerra, enviaron un mensaje a la tierra de los filisteos por todas partes, para llevar las noticias a sus dioses y al pueblo.
10 Iwo anayika zida zake zankhondo mʼnyumba yopembedzera Asitoreti, ndipo thupi lake analikhomera pa khoma la mzinda wa Beti-Sani.
Se pusieron sus ropas de guerra en la casa de Astarté. y su cuerpo fue fijado en la pared de Beth-san.
11 Pamene anthu a ku Yabesi Giliyadi anamva zimene Afilisti anachitira Sauli,
Y cuando los habitantes de Jabes-galaad tuvieron noticias de lo que los filisteos habían hecho a Saúl,
12 anthu awo onse olimba mtima anayenda usiku wonse kupita ku Beti-Sani. Anakachotsa mtembo wa Sauli ndi mitembo ya ana ake pa khoma la mzinda wa Beti-Sani, ndipo anabwera nayo ku Yabesi kumene anayitentha ndi moto.
Se levantaron todos los fuertes y valientes, viajando toda la noche, tomaron el cuerpo de Saúl y los cuerpos de sus hijos del muro de Bet-sán; y viniendo a Jabes y los quemaron allí.
13 Pambuyo pake anatenga mafupa awo ndi kuwakwirira pansi pa mtengo wabwemba ku Yabesi, ndipo anasala kudya masiku asanu ndi awiri.
Y tomando los huesos lo enterraron debajo del árbol tamarisco en Jabes; Y por siete días guardaron ayuno.

< 1 Samueli 31 >