< 1 Samueli 31 >

1 Tsono Afilisti anachitanso nkhondo ndi Aisraeli ndipo Aisraeli anathawa Afilistiwo, kotero kuti ambiri anaphedwa pa phiri la Gilibowa.
And the Philistines fought against Israel; and the men of Israel fled from before the Philistines, and fell down slain on mount Gilboa.
2 Afilisti anapanikiza kwambiri Sauli ndi ana ake, ndipo anapha Yonatani, Abinadabu ndi Maliki-Suwa.
And the Philistines followed hard upon Saul and upon his sons; and the Philistines smote Jonathan, and Abinadab, and Malchishua, Saul's sons.
3 Nkhondo inakula kwambiri mozungulira Sauli ndipo pamene anthu amauta anamupeza, anamuvulaza kwambiri.
And the battle went sore against Saul, and the archers came up with him; and he was much terrified by the archers.
4 Tsono Sauli anawuza mnyamata wake wonyamula zida zake kuti, “Solola lupanga lako undiphe kuopa kuti anthu osachita mdulidwewa angabwere kudzandizunza ine.” Koma mnyamata wonyamula zida uja anachita mantha kwambiri ndipo sanathe kutero. Choncho Sauli anatenga lupanga lake lomwe nagwerapo.
Then said Saul to his armour-bearer, Draw thy sword, and thrust me through with it; lest these uncircumcised come and thrust me through, and abuse me. But his armour-bearer would not; for he was much afraid. So Saul took the sword and fell on it.
5 Mnyamata wonyamula zida zake uja ataona kuti Sauli wafa, nayenso anadzigwetsera pa lupanga lake nafa naye limodzi.
And when his armour-bearer saw that Saul was dead, he fell likewise on his sword, and died with him.
6 Motero Sauli ndi ana ake atatu, wonyamula zida zake pamodzi ndi anthu ake onse anafera limodzi pa tsikulo.
So Saul died, and his three sons, and his armour-bearer, and all his men, that same day together.
7 Pamene Aisraeli amene anali tsidya lina la chigwa ndi amene anali tsidya la chigwa cha Yorodani anaona kuti gulu la ankhondo la Aisraeli lathawa komanso kuti Sauli ndi ana ake aphedwa, nawonso anathawa kusiya mizinda yawo. Ndipo Afilisti anabwera kudzakhalamo.
And when the men of Israel that were on this side of the valley, and [they] that were on this side of the Jordan, saw that the men of Israel fled, and that Saul and his sons were dead, they forsook the cities and fled; and the Philistines came and dwelt in them.
8 Mmawa mwake, Afilisti atabwera kudzatenga zinthu za anthu ophedwa anapeza Sauli ndi ana ake atatu atafa pa phiri la Gilibowa.
And it came to pass the next day, that the Philistines came to strip the slain, and they found Saul and his three sons fallen on mount Gilboa.
9 Iwo anadula mutu wake ndi kumuvula zida zake zankhondo. Ndipo anatumiza amithenga mʼdziko lonse la Afilisti kukafalitsa nkhani yabwinoyi kwa mafano awo ndi kwa anthu awo.
And they cut off his head, and stripped off his armour, and sent [them] into the land of the Philistines round about, to announce the glad tidings in the houses of their idols, and to the people.
10 Iwo anayika zida zake zankhondo mʼnyumba yopembedzera Asitoreti, ndipo thupi lake analikhomera pa khoma la mzinda wa Beti-Sani.
And they put his armour in the house of Ashtaroth; and they fastened his body to the wall of Beth-shan.
11 Pamene anthu a ku Yabesi Giliyadi anamva zimene Afilisti anachitira Sauli,
And when the inhabitants of Jabesh-Gilead heard of what the Philistines had done to Saul,
12 anthu awo onse olimba mtima anayenda usiku wonse kupita ku Beti-Sani. Anakachotsa mtembo wa Sauli ndi mitembo ya ana ake pa khoma la mzinda wa Beti-Sani, ndipo anabwera nayo ku Yabesi kumene anayitentha ndi moto.
all the valiant men arose and went all night, and took the body of Saul and the bodies of his sons from the wall of Beth-shan, and came to Jabesh, and burned them there.
13 Pambuyo pake anatenga mafupa awo ndi kuwakwirira pansi pa mtengo wabwemba ku Yabesi, ndipo anasala kudya masiku asanu ndi awiri.
And they took their bones, and buried them under the tamarisk at Jabesh, and fasted seven days.

< 1 Samueli 31 >