< 1 Samueli 31 >
1 Tsono Afilisti anachitanso nkhondo ndi Aisraeli ndipo Aisraeli anathawa Afilistiwo, kotero kuti ambiri anaphedwa pa phiri la Gilibowa.
Og Filisterne strede imod Israel, og Israels Mænd flyede for Filisternes Ansigt, og de faldt ihjelslagne paa Gilboas Bjerg.
2 Afilisti anapanikiza kwambiri Sauli ndi ana ake, ndipo anapha Yonatani, Abinadabu ndi Maliki-Suwa.
Og Filisterne forfulgte Saul og hans Sønner, og Filisterne sloge Jonathan og Abinadab og Malkisua, Sauls Sønner.
3 Nkhondo inakula kwambiri mozungulira Sauli ndipo pamene anthu amauta anamupeza, anamuvulaza kwambiri.
Og Kampen blev svar imod Saul, og Skytterne, som førte Bue, naaede ham, og han blev saare angest for Skytterne.
4 Tsono Sauli anawuza mnyamata wake wonyamula zida zake kuti, “Solola lupanga lako undiphe kuopa kuti anthu osachita mdulidwewa angabwere kudzandizunza ine.” Koma mnyamata wonyamula zida uja anachita mantha kwambiri ndipo sanathe kutero. Choncho Sauli anatenga lupanga lake lomwe nagwerapo.
Da sagde Saul til sin Vaabendrager: Drag dit Sværd ud og stik mig igennem dermed, at ikke disse uomskaarne skulle komme og gennemstikke mig og handle ilde med mig; men hans Vaabendrager vilde ikke, thi han frygtede saare; da tog Saul Sværdet og styrtede sig deri.
5 Mnyamata wonyamula zida zake uja ataona kuti Sauli wafa, nayenso anadzigwetsera pa lupanga lake nafa naye limodzi.
Der hans Vaabendrager saa, at Saul var død, da styrtede ogsaa han sig i sit Sværd og døde med ham.
6 Motero Sauli ndi ana ake atatu, wonyamula zida zake pamodzi ndi anthu ake onse anafera limodzi pa tsikulo.
Saa døde Saul og hans tre Sønner og hans Vaabendrager, ogsaa alle hans Mænd til Hobe paa den samme Dag.
7 Pamene Aisraeli amene anali tsidya lina la chigwa ndi amene anali tsidya la chigwa cha Yorodani anaona kuti gulu la ankhondo la Aisraeli lathawa komanso kuti Sauli ndi ana ake aphedwa, nawonso anathawa kusiya mizinda yawo. Ndipo Afilisti anabwera kudzakhalamo.
Og der Israels Mænd, som vare paa hin Side Dalen, og som vare paa hin Side Jordanen, saa, at Israels Mænd vare flygtede, og at Saul og hans Sønner vare døde, da forlode de Stæderne og flyede; og Filisterne kom og boede i dem.
8 Mmawa mwake, Afilisti atabwera kudzatenga zinthu za anthu ophedwa anapeza Sauli ndi ana ake atatu atafa pa phiri la Gilibowa.
Og det skete den anden Dag, da Filisterne kom for at plyndre de ihjelslagne, at de fandt Saul og hans tre Sønner faldne paa Gilboas Bjerg.
9 Iwo anadula mutu wake ndi kumuvula zida zake zankhondo. Ndipo anatumiza amithenga mʼdziko lonse la Afilisti kukafalitsa nkhani yabwinoyi kwa mafano awo ndi kwa anthu awo.
Da afhuggede de hans Hoved og afførte ham hans Vaaben, og de sendte hen i Filisternes Land trindt omkring for at bringe Budskab derom i deres Afguders Hus og iblandt Folket.
10 Iwo anayika zida zake zankhondo mʼnyumba yopembedzera Asitoreti, ndipo thupi lake analikhomera pa khoma la mzinda wa Beti-Sani.
Og de lagde hans Vaaben i Astarte-Billedernes Hus og hængte hans Krop ud paa Muren i Bethsan.
11 Pamene anthu a ku Yabesi Giliyadi anamva zimene Afilisti anachitira Sauli,
Der Indbyggerne i Jabes udi Gilead hørte om ham, hvad Filisterne havde gjort mod Saul,
12 anthu awo onse olimba mtima anayenda usiku wonse kupita ku Beti-Sani. Anakachotsa mtembo wa Sauli ndi mitembo ya ana ake pa khoma la mzinda wa Beti-Sani, ndipo anabwera nayo ku Yabesi kumene anayitentha ndi moto.
da gjorde de sig rede, hver stridbar Mand, og de gik den ganske Nat, og de toge Sauls Legeme og hans Sønners Legemer ned af Muren i Bethsan, og de kom til Jabes og brændte dem der.
13 Pambuyo pake anatenga mafupa awo ndi kuwakwirira pansi pa mtengo wabwemba ku Yabesi, ndipo anasala kudya masiku asanu ndi awiri.
Og de toge deres Ben og begrove dem under Tamariske-Træet i Jabes, og de fastede syv Dage.