< 1 Samueli 30 >

1 Pa tsiku lachitatu, Davide ndi anthu ake anakafika ku Zikilagi. Tsono anapeza Aamaleki atawononga kale dera la Negevi ndi Zikilagi. Anathira nkhondo mzinda wa Zikilagi ndi kuwutentha ndi moto.
UDavida labantu bakhe bafika eZikhilagi ngelanga lesithathu. Ama-Amaleki ayehlasele iNegebi leZikhilagi. Ayehlasele iZikhilagi ayitshisa,
2 Anatenga akazi ndi onse amene anali mʼmenemo akuluakulu ndi angʼono omwe kuti akakhale akapolo. Sanaphe aliyense koma anawatenga amoyo napita nawo.
njalo ayethumbe abesifazane labo bonke ababekuyo, abatsha labadala. Kawabulalanga lamunye wabo, kodwa ahamba labo ekuhambeni kwawo.
3 Davide ndi anthu ake atafika ku Zikilagi anapeza kuti mzindawo watenthedwa ndi moto ndipo akazi awo, ana awo, amuna ndi akazi atengedwa ukapolo.
Kwathi uDavida labantu bakhe befika eZikhilagi, bayifica iqothulwe ngomlilo njalo omkabo lamadodana kanye lamadodakazi abo bethunjiwe.
4 Kotero Davide ndi anthu ake analira mofuwula mpaka analibenso mphamvu zolirira.
Ngakho uDavida labantu bakhe bakhala kakhulu baze baphela amandla okukhala.
5 Akazi awiri a Davide, Ahinoamu wa ku Yezireeli ndi Abigayeli mkazi wa Nabala wa ku Karimeli anatengedwanso.
Abafazi bakaDavida bobabili babethunjiwe, u-Ahinowama waseJezerili lo-Abhigeli, umfelokazi kaNabhali waseKhameli.
6 Davide anavutika kwambiri mu mtima mwake chifukwa anthu amakamba zoti amuponye miyala popeza aliyense anali ndi chisoni pokumbukira ana ake aamuna ndi aakazi. Koma Davide anapeza mphamvu mwa Yehova Mulungu wake.
UDavida wayesekhathazeke kakhulu ngoba abantu babekhuluma ngokumkhanda ngamatshe, lowo lalowo efuthelene emoyeni ngenxa yamadodana akhe lamadodakazi. Kodwa uDavida wathola amandla kuThixo uNkulunkulu wakhe.
7 Kenaka Davide anawuza wansembe Abiatara, mwana wa Ahimeleki kuti, “Ndipatse efodi ija.” Abiatara anabwera nayo efodiyo.
UDavida wasesithi ku-Abhiyatha umphristi, indodana ka-Ahimeleki, “Ngilethela isembatho samahlombe.” U-Abhiyathari wasiletha kuye,
8 Tsono Davide anapempha nzeru kwa Yehova nati, “Kodi ndilitsatire gulu lankhondoli? Kodi ndidzawapambana?” Yehova anayankha kuti, “Litsatire, iwe udzawapambana ndithu ndipo udzapulumutsa anthu ako.”
uDavida wasebuza kuThixo esithi, “Ngililandele yini lelixuku elihlaselayo? Ngizalifica na?” Waphendula wathi, “Lilandele. Uzalifica impela njalo uzaphumelela ekuhlengeni.”
9 Davide pamodzi ndi anthu ake 600 aja ananyamuka nafika ku mtsinje wa Besori. Kumeneko anasiyako anthu ena.
UDavida labantu abangamakhulu ayisithupha ababelaye bafika eDongeni lwaseBhesori, lapho abanye abasala khona,
10 Davide ndi anthu ake 400 anapitirira kuwalondola Aamaleki aja. Koma anthu ena 200 anatsala popeza anatopa moti sakanatha kuwoloka mtsinje wa Besori uja.
ngoba abangamakhulu amabili basebedinwe kakhulu ukuba bachaphe udonga. Kodwa uDavida labantu abangamakhulu amane baqhubeka belandela.
11 Anthu amene anali ndi Davide anapeza Mwigupto mʼmunda wina ndipo anabwera naye kwa Davide. Iwo anamupatsa madzi kuti amwe ndi chakudya kuti adye.
Bafica umGibhithe egangeni bamusa kuDavida. Bamnika amanzi okunatha lokudla ukuba adle,
12 Anamupatsanso chidutswa cha keke yankhuyu ndi makeke awiri a mphesa zowumika kuti adye. Atadya anapezanso mphamvu popeza anakhala masiku atatu wosadya kapena kumwa kanthu kalikonse.
ingxenye yekhekhe lemikhiwa ekhanyiweyo lekhekhe lamavini awonyisiweyo. Wadla wathola amandla, ngoba wayengadlanga lutho njalo enganathanga manzi insuku ezintathu lobusuku obuthathu.
13 Davide anafunsa kuti, “Kodi ndiwe yani, ndipo ukuchokera kuti?” Iye anayankha kuti, “Ine ndine Mwigupto, kapolo wa Mwamaleki. Mbuye wanga anandisiya nditayamba kudwala masiku atatu apitawo.
UDavida wambuza wathi, “Ungokabani wena, njalo uvela ngaphi na?” Yena wathi, “NgingumGibhithe, isigqili somʼAmaleki. Inkosi yami ingitshiyile sengigula ensukwini ezintathu ezedluleyo.
14 Ife tinathira nkhondo dera la kummwera kwa mayiko a Akereti, dera la Yuda, ndi dera la kummwera kwa mayiko a Kalebe. Mzinda wa Zikilagi tinawutentha ndi moto.”
Sihlasele iNegebi yamaKherethi lelizwe likaJuda kanye leNegebi yamaKhalebi. Njalo iZikhilagi siyitshisile.”
15 Davide anamupempha kuti, “Kodi unganditsogolere kumene kuli gulu lankhondoli?” Iye anayankha kuti, “Mukandilonjeza molumbira kuti simudzandipha kapena kundipereka kwa mbuye wanga, ine ndikulondolerani kumene kuli gululo.”
UDavida wambuza wathi, “Ungangisa kulelixuku elihlaselayo na?” Waphendula wathi, “Funga kimi phambi kukaNkulunkulu ukuthi kawuyikungibulala kumbe unginikele enkosini yami, besengikusa-ke kubo.”
16 Mwigupto uja anaperekeza Davide. Tsono Aamaleki anali atamwazikana ponseponse. Iwo ankadya, kumwa ndi kuvina chifukwa cha zofunkha zambiri zimene anatenga ku dziko la Afilisti ndi ku dziko la Ayuda.
Wakhokhela uDavida, bababona begcwele indawana yonke, besidla, benatha njalo bejabula ngenxa yobunengi bempango ababeyithumbile elizweni lamaFilistiya kanye lakoJuda.
17 Tsono Davide anawakantha kuyambira madzulo atsikulo mpaka madzulo a tsiku linalo. Palibe anapulumuka kupatula anyamata 400 amene anakwera pa ngamira nʼkuthawa.
UDavida walwa labo kusukela ekuseni kwaze kwahlwa ngelanga elilandelayo, njalo kakho owabo owaphunyukayo ngaphandle kwamajaha angamakhulu amane agada amakamela abaleka.
18 Choncho Davide analanditsa zinthu zonse zimene Aamaleki aja anatenga. Anapulumutsanso akazi ake awiri aja.
UDavida wakuthatha njalo konke okwakuthunjwe ngama-Amaleki kanye labomkakhe ababili.
19 Palibe chimene chinasowa anthu onse, kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu, mnyamata mpaka mtsikana anapulumutsidwa. Davide anapulumutsa chilichonse chimene anafunkha Aamaleki aja.
Akukho lutho olwaswelakalayo: omutsha kumbe omdala, umfana kumbe inkazana, impango kumbe olunye nje ulutho ababeluthethe. UDavida wabuyisa konke.
20 Anapulumutsanso nkhosa ndi ngʼombe zonse. Tsono anthu ankakusa ziwetozo namati, “Izi ndizo zofunkha za Davide.”
Wathatha izimvu zonke lenkomo, abantu bakhe baziqhuba ziphambi kwezinye izifuyo, besithi, “Le yimpango kaDavida.”
21 Davide anafika ku malo kumene kunali anthu 200 otopa kwambiri aja amene sanathe kutsagana naye koma anangokhala ku mtsinje wa Besori. Tsono ananyamuka kuti akumane ndi Davide pamodzi ndi anthu amene anali naye. Davide anawayandikira nawalonjera.
Emva kwalokho uDavida wafika ebantwini abangamakhulu amabili ababedinwe kakhulu baze behluleka ukumlandela ababesele emuva eDongeni lwaseBhesori. Baphuma bahlangabeza uDavida kanye labantu ababelaye. Kwathi uDavida esesondela labantu bakhe, wababingelela.
22 Tsono anthu ena oyipa mtima achabechabe mwa amene anatsagana ndi Davide aja anati, “Popeza awa sanapite nafe, sitiwapatsako zofunkha zimene tapulumutsazi, kupatula kuti aliyense atenge mkazi wake ndi ana ake azipita.”
Kodwa bonke abantu ababi labahlokozi bohlupho abaphakathi kwabalandeli bakaDavida, bathi, “Ngenxa yokuthi kabahambanga lathi kasiyikwabelana labo impango esiyithumbileyo. Kodwa yileyo laleyo indoda ingathatha umkayo labantwabayo ihambe.”
23 Koma Davide anawayankha kuti, “Ayi, abale anga, musachite zimenezi ndi zinthu zimene Yehova watipatsa. Iye watisunga ndi kupereka mʼmanja mwathu gulu la ankhondo limene linabwera kudzalimbana nafe.
UDavida waphendula wathi, “Hatshi, bafowethu, akumelanga lenzenjalo ngalokho uThixo asiphe khona. Usivikele wawanikela kithi amabutho abesihlasela.
24 Ndani angakumvereni zimene mukunenazi? Gawo la munthu amene anapita kukamenya nkhondo likhale lofanana ndi la munthu amene anatsala pano kuyangʼanira katundu wathu. Pasakhale kusiyana kulikonse.”
Pho ngubani ozalalela lokhu elikutshoyo na? Isabelo somuntu osele lempahla sizafana lesalowo ohambileyo ekulweni impi. Bonke bazakwabelwa ngokufanayo.”
25 Choncho Davide anakhazikitsa ngati lamulo mʼchitidwe woterewu pakati pa Aisraeli kuyambira tsiku limenelo mpaka lero.
UDavida wenza lokhu kwaba yisimiso lomthetho ko-Israyeli kusukela ngalelolanga kuze kube yileli.
26 Davide atafika ku Zikilagi, anatumiza zina mwa zofunkhazo kwa akuluakulu a Yuda, amene anali abwenzi ake. Anati, “Nayi mphatso yanu yochokera pa zofunkha za adani a Yehova.”
UDavida esefikile eZikhilagi, wathumela enye impango ebadaleni bakoJuda, ababengabangane bakhe, esithi, “Nansi isipho senu esivela empangweni yezitha zikaThixo.”
27 Iye anatumiza mphatsozo kwa anthu a ku Beteli, Ramoti-Negavi, Yatiri,
Wayithumela kulabo ababeseBhetheli, leRamothi Negebi leJathiri,
28 Aroeri, Sifimoti, Esitemowa
lakulabo abase-Aroweri, eSifimothi, e-Eshithemowa
29 Rakala, mizinda ya fuko la Ayerahimeeli, mizinda ya fuko la Akeni,
leRakhali; kulabo ababesemizini yamaJerameli lamaKheni.
30 a ku Horima, Borasani, Ataki,
Kulabo ababeseHoma, eBhori-Ashani, e-Athakhi
31 Hebroni pamodzi ndi onse a kumalo kumene Davide ndi anthu ake anakhala akuyendayendako.
laseHebhroni; lakubo ababekuzo zonke ezinye izindawo lapho uDavida labantu bakhe ababeke bazulazula kuzo.

< 1 Samueli 30 >