< 1 Samueli 30 >
1 Pa tsiku lachitatu, Davide ndi anthu ake anakafika ku Zikilagi. Tsono anapeza Aamaleki atawononga kale dera la Negevi ndi Zikilagi. Anathira nkhondo mzinda wa Zikilagi ndi kuwutentha ndi moto.
Lorsque David arriva avec ses hommes le troisième jour à Siceleg, les Amalécites avaient fait une invasion dans le Négéb et à Siceleg; ils avaient frappé Siceleg et l’avaient brûlée;
2 Anatenga akazi ndi onse amene anali mʼmenemo akuluakulu ndi angʼono omwe kuti akakhale akapolo. Sanaphe aliyense koma anawatenga amoyo napita nawo.
et ils avaient fait prisonniers les femmes et tous ceux qui s’y trouvaient, petits et grands, sans tuer personne, et ils les avaient emmenés, et s’étaient remis en route.
3 Davide ndi anthu ake atafika ku Zikilagi anapeza kuti mzindawo watenthedwa ndi moto ndipo akazi awo, ana awo, amuna ndi akazi atengedwa ukapolo.
Lors donc que David et ses gens arrivèrent à la ville, ils virent qu’elle était brûlée, et que leurs femmes, leurs fils et leurs filles avaient été emmenés captifs.
4 Kotero Davide ndi anthu ake analira mofuwula mpaka analibenso mphamvu zolirira.
Et David et le peuple qui était avec lui élevèrent la voix et pleurèrent jusqu’à ce qu’ils n’eussent plus la force de pleurer.
5 Akazi awiri a Davide, Ahinoamu wa ku Yezireeli ndi Abigayeli mkazi wa Nabala wa ku Karimeli anatengedwanso.
Les deux femmes de David avaient été aussi emmenées captives, Achinoam de Jezraël, et Abigaïl de Carmel, femme de Nabal.
6 Davide anavutika kwambiri mu mtima mwake chifukwa anthu amakamba zoti amuponye miyala popeza aliyense anali ndi chisoni pokumbukira ana ake aamuna ndi aakazi. Koma Davide anapeza mphamvu mwa Yehova Mulungu wake.
David fut dans une grande angoisse, car la troupe parlait de le lapider, parce que tout le peuple avait de l’amertume dans l’âme, chacun au sujet de ses fils et de ses filles. Mais David reprit courage en Yahweh, son Dieu.
7 Kenaka Davide anawuza wansembe Abiatara, mwana wa Ahimeleki kuti, “Ndipatse efodi ija.” Abiatara anabwera nayo efodiyo.
David dit au prêtre Abiathar, fils d’Achimélech: « Apporte-moi l’éphod. » Abiathar apporta l’éphod à David.
8 Tsono Davide anapempha nzeru kwa Yehova nati, “Kodi ndilitsatire gulu lankhondoli? Kodi ndidzawapambana?” Yehova anayankha kuti, “Litsatire, iwe udzawapambana ndithu ndipo udzapulumutsa anthu ako.”
Et David consulta Yahweh en disant: « Poursuivrai-je cette bande? L’atteindrai-je? » Yahweh lui répondit: « Poursuis, car certainement tu atteindras et tu délivreras. »
9 Davide pamodzi ndi anthu ake 600 aja ananyamuka nafika ku mtsinje wa Besori. Kumeneko anasiyako anthu ena.
Et David se mit en marche, lui et les six cents hommes qui étaient avec lui. Lorsqu’ils furent arrivés au torrent de Bésor, les traînards s’arrêtèrent.
10 Davide ndi anthu ake 400 anapitirira kuwalondola Aamaleki aja. Koma anthu ena 200 anatsala popeza anatopa moti sakanatha kuwoloka mtsinje wa Besori uja.
Et David continua la poursuite avec quatre cents hommes; deux cents hommes s’étaient arrêtés, trop fatigués pour passer le torrent de Bésor.
11 Anthu amene anali ndi Davide anapeza Mwigupto mʼmunda wina ndipo anabwera naye kwa Davide. Iwo anamupatsa madzi kuti amwe ndi chakudya kuti adye.
Ils trouvèrent dans les champs un Egyptien, qu’ils amenèrent à David. Ils lui donnèrent du pain qu’il mangea, et ils lui firent boire de l’eau;
12 Anamupatsanso chidutswa cha keke yankhuyu ndi makeke awiri a mphesa zowumika kuti adye. Atadya anapezanso mphamvu popeza anakhala masiku atatu wosadya kapena kumwa kanthu kalikonse.
ils lui donnèrent une tranche d’un gâteau de figues sèches et deux gâteaux de raisins secs. Dès qu’il eut pris de la nourriture, ses esprits lui revinrent, car il n’avait mangé de nourriture ni bu d’eau depuis trois jours et trois nuits.
13 Davide anafunsa kuti, “Kodi ndiwe yani, ndipo ukuchokera kuti?” Iye anayankha kuti, “Ine ndine Mwigupto, kapolo wa Mwamaleki. Mbuye wanga anandisiya nditayamba kudwala masiku atatu apitawo.
David lui dit: « A qui es-tu et d’où es-tu? » Il répondit: « Je suis un esclave égyptien, au service d’un Amalécite, et voilà trois jours que mon maître m’a abandonné, parce que j’étais malade.
14 Ife tinathira nkhondo dera la kummwera kwa mayiko a Akereti, dera la Yuda, ndi dera la kummwera kwa mayiko a Kalebe. Mzinda wa Zikilagi tinawutentha ndi moto.”
Nous avons fait une incursion dans le Négéb des Céréthiens, et sur le territoire de Juda, et dans le Négéb de Caleb, et nous avons brûlé Siceleg. »
15 Davide anamupempha kuti, “Kodi unganditsogolere kumene kuli gulu lankhondoli?” Iye anayankha kuti, “Mukandilonjeza molumbira kuti simudzandipha kapena kundipereka kwa mbuye wanga, ine ndikulondolerani kumene kuli gululo.”
David lui dit: « Veux-tu me conduire vers cette bande? » Il répondit: « Jure-moi par le nom de Dieu que tu ne me tueras pas et que tu ne me livreras pas aux mains de mon maître, et je te conduirai vers cette bande. »
16 Mwigupto uja anaperekeza Davide. Tsono Aamaleki anali atamwazikana ponseponse. Iwo ankadya, kumwa ndi kuvina chifukwa cha zofunkha zambiri zimene anatenga ku dziko la Afilisti ndi ku dziko la Ayuda.
Lorsqu’il l’eut conduit, voici que les Amalécites étaient répandus sur toute la contrée, mangeant, buvant et dansant, à cause de tout le grand butin qu’ils avaient enlevé du pays des Philistins et du pays de Juda.
17 Tsono Davide anawakantha kuyambira madzulo atsikulo mpaka madzulo a tsiku linalo. Palibe anapulumuka kupatula anyamata 400 amene anakwera pa ngamira nʼkuthawa.
David les battit depuis le crépuscule du soir jusqu’au soir du lendemain, et aucun d’eux n’échappa, excepté quatre cents jeunes hommes, qui s’enfuirent, montés sur des chameaux.
18 Choncho Davide analanditsa zinthu zonse zimene Aamaleki aja anatenga. Anapulumutsanso akazi ake awiri aja.
David sauva tout ce que les Amalécites avaient pris, et David sauva ses deux femmes.
19 Palibe chimene chinasowa anthu onse, kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu, mnyamata mpaka mtsikana anapulumutsidwa. Davide anapulumutsa chilichonse chimene anafunkha Aamaleki aja.
Il ne leur manqua personne, ni petit ni grand, ni fils ni fille, ni aucune partie du butin, ni rien de ce qu’on leur avait enlevé: David ramena tout.
20 Anapulumutsanso nkhosa ndi ngʼombe zonse. Tsono anthu ankakusa ziwetozo namati, “Izi ndizo zofunkha za Davide.”
Et David prit tout le menu et le gros bétail, et ils se mirent en marche devant ce troupeau, en disant: « C’est le butin de David. »
21 Davide anafika ku malo kumene kunali anthu 200 otopa kwambiri aja amene sanathe kutsagana naye koma anangokhala ku mtsinje wa Besori. Tsono ananyamuka kuti akumane ndi Davide pamodzi ndi anthu amene anali naye. Davide anawayandikira nawalonjera.
David revint vers les deux cents hommes qui avaient été trop fatigués pour suivre David, et qu’on avait laissés au torrent de Bésor; ils s’avancèrent au-devant de David et au-devant du peuple qui était avec lui. S’approchant d’eux, David les salua amicalement.
22 Tsono anthu ena oyipa mtima achabechabe mwa amene anatsagana ndi Davide aja anati, “Popeza awa sanapite nafe, sitiwapatsako zofunkha zimene tapulumutsazi, kupatula kuti aliyense atenge mkazi wake ndi ana ake azipita.”
Tout ce qu’il y avait d’hommes méchants et vils parmi les gens qui étaient allés avec David prirent la parole et dirent: « Puisqu’ils ne sont pas venus avec nous, nous ne leur donnerons rien du butin que nous avons sauvé, sinon à chacun sa femme et ses enfants; qu’ils les emmènent et s’en aillent. »
23 Koma Davide anawayankha kuti, “Ayi, abale anga, musachite zimenezi ndi zinthu zimene Yehova watipatsa. Iye watisunga ndi kupereka mʼmanja mwathu gulu la ankhondo limene linabwera kudzalimbana nafe.
Mais David dit: « N’agissez pas ainsi, mes frères, avec ce que Yahweh nous a donné; car il nous a gardés, et il a livré entre nos mains la bande qui était venue contre nous.
24 Ndani angakumvereni zimene mukunenazi? Gawo la munthu amene anapita kukamenya nkhondo likhale lofanana ndi la munthu amene anatsala pano kuyangʼanira katundu wathu. Pasakhale kusiyana kulikonse.”
Et qui vous écouterait dans cette affaire? La part doit être la même pour celui qui est descendu au combat et pour celui qui est resté près des bagages: ils partageront ensemble. »
25 Choncho Davide anakhazikitsa ngati lamulo mʼchitidwe woterewu pakati pa Aisraeli kuyambira tsiku limenelo mpaka lero.
Il en fut ainsi dès ce jour et dans la suite, et David a fait de cela une loi et une règle qui subsiste jusqu’à ce jour.
26 Davide atafika ku Zikilagi, anatumiza zina mwa zofunkhazo kwa akuluakulu a Yuda, amene anali abwenzi ake. Anati, “Nayi mphatso yanu yochokera pa zofunkha za adani a Yehova.”
De retour à Siceleg, David envoya une partie du butin aux anciens de Juda, ses amis, en disant: « Voici un présent pour vous sur le butin des ennemis de Yahweh. »
27 Iye anatumiza mphatsozo kwa anthu a ku Beteli, Ramoti-Negavi, Yatiri,
Il fit ces envois à ceux de Béthel, à ceux de Ramoth du Négéb, à ceux de Jéther,
28 Aroeri, Sifimoti, Esitemowa
à ceux d’Aroër, à ceux de Séphamoth, à ceux d’Estamo,
29 Rakala, mizinda ya fuko la Ayerahimeeli, mizinda ya fuko la Akeni,
à ceux de Rachal, à ceux des villes de Jéraméélites, à ceux des villes des Cinéens,
30 a ku Horima, Borasani, Ataki,
à ceux d’Arama, à ceux de Cor-Asan, à ceux d’Athach,
31 Hebroni pamodzi ndi onse a kumalo kumene Davide ndi anthu ake anakhala akuyendayendako.
à ceux d’Hébron et dans tous les lieux où David et ses gens avaient passé.