< 1 Samueli 29 >
1 Afilisti anasonkhanitsa asilikali awo onse ku Afeki, ndipo Israeli anamanga misasa yawo pa chitsime cha Yezireeli.
Filistliler bütün ordularını Afek'te topladılar. İsrailliler ise Yizreel'deki pınarın yanına kurdukları ordugahta kalıyorlardı.
2 Pamene atsogoleri a Afilisti ankatsogolera magulu awo ankhondo a miyandamiyanda, Davide ndi ankhondo ake ankayenda pambuyo pamodzi ndi Akisi.
Filist beyleri yüzer ve biner kişilik birliklerle ilerliyordu. Davut'la adamlarıysa Akiş'le birlikte geriden geliyorlardı.
3 Tsono atsogoleri a Afilisti aja anafunsa kuti, “Kodi Ahebri awa akufuna chiyani?” Akisi anayankha kuti, “Uyu ndi Davide, mtumiki wa Sauli mfumu ya Israeli. Iye wakhala ndi ine kwa masiku ndithu, kapena titi zaka ndipo kuyambira tsiku limene anachoka kwa Sauli mpaka lero, ine sindinapeze cholakwa mwa iye.”
Filistli komutanlar, “Bu İbraniler'in burada ne işi var?” diye sorunca, Akiş şu karşılığı verdi: “Bu, İsrail Kralı Saul'un görevlisi Davut'tur. Bir yıldan uzun süredir yanımda kalıyor. Bana geldiğinden beri kendisinde hiçbir kötülük bulamadım.”
4 Koma atsogoleri a ankhondo a Afilisti anamukwiyira Akisi kwambiri ndipo anati, “Mubweze munthuyu kuti abwerere ku malo amene unamupatsa. Iye asapite nafe ku nkhondo kuopa kuti angadzasanduke mdani wathu. Kodi iyeyu adzadziyanjanitsa bwanji ndi mbuye wake? Iyeyutu adzadziyanjanitsa ndi mbuye wake pakupha anthu ali panowa?
Ama Filistli komutanlar Akiş'e öfkelendiler. “Adamı geri gönder, kendisine verdiğin yere dönsün” dediler, “Bizimle birlikte savaşa gelmesin; yoksa savaş sırasında bize karşı çıkar. Efendisinin beğenisini nasıl kazanabilir? Adamlarımızın başını ona vermekten daha iyi bir yol bulabilir mi?
5 Paja ameneyu ndi Davide yemwe ankamuvinira namuyimbira kuti, “‘Sauli wapha anthu 1,000 koma Davide wapha miyandamiyanda?’”
Çalıp oynarken, ‘Saul binlercesini öldürdü, Davut'sa on binlercesini’ diye hakkında ezgiler okudukları Davut değil mi bu?”
6 Kotero Akisi anayitana Davide ndipo anamuwuza kuti, “Pali Yehova wamoyo, iwe wakhala wodalirika ndipo chikanakhala chinthu chabwino kuti uzimenya nkhondo pamodzi nane popeza chibwerere iwe kuno ine sindinapeze cholakwa chilichonse ndi iwe. Koma atsogoleri enawa ndiwo sakukufuna.
Bunun üzerine Akiş, Davut'u çağırıp, “Yaşayan RAB'bin adıyla derim ki, sen dürüst bir kişisin” dedi, “Benimle birlikte savaşa katılmanı isterdim. Yanıma geldiğin günden bu yana ters bir davranışını görmedim. Ama Filist beyleri seni uygun görmedi.
7 Tsono bwerera. Upite mu mtendere kuopa kuti ungachite kanthu kena koyipira atsogoleri a Afilistiwa.”
Şimdi geri dön ve esenlikle git. Filist beylerinin gözünde ters bir davranışta bulunma.”
8 Davide anafunsa Akisi kuti, “Kodi ndachita chiyani? Kodi mwapeza cholakwa chotani mwa ine mtumiki wanu chiyambire kukutumikirani mpaka lero? Tsono chifukwa chiyani sindingapite kukamenya nkhondo ndi adani a mbuye wanga mfumu?”
Davut, “Ama ben ne yaptım?” diye sordu, “Yanına geldiğimden bu yana bende ne buldun ki, gidip efendim kralın düşmanlarına karşı savaşmayayım?”
9 Akisi anayankha kuti, “Ine ndikudziwa kuti ndiwe wangwiro ngati mngelo wa Mulungu. Komabe atsogoleri a ankhondo a Afilisti akuti, ‘Davide asapite nafe ku nkhondo.’
Akiş, “Biliyorum, sen benim gözümde Tanrı'nın bir meleği gibi iyisin” diye yanıtladı, “Ne var ki Filistli komutanlar, ‘Bizimle savaşa gelmesin’ diyorlar.
10 Tsono udzuke mmamawa, pamodzi ndi ankhondo ako amene unabwera nawo, ndipo unyamuke kukangocha.”
Seninle gelmiş olan efendin Saul'un kullarıyla birlikte sabah erkenden kalkın ve tan ağarır ağarmaz gidin.”
11 Choncho Davide ndi anthu ake anadzuka mmamawa kubwerera ku dziko la Afilisti. Koma Afilistiwo anapita ku Yezireeli.
Böylece Davut'la adamları Filist ülkesine dönmek üzere sabah erkenden kalktılar. Filistliler ise Yizreel'e gittiler.