< 1 Samueli 29 >

1 Afilisti anasonkhanitsa asilikali awo onse ku Afeki, ndipo Israeli anamanga misasa yawo pa chitsime cha Yezireeli.
و فلسطینیان همه لشکرهای خود را درافیق جمع کردند، و اسرائیلیان نزدچشمه‌ای که در یزرعیل است، فرود آمدند.۱
2 Pamene atsogoleri a Afilisti ankatsogolera magulu awo ankhondo a miyandamiyanda, Davide ndi ankhondo ake ankayenda pambuyo pamodzi ndi Akisi.
وسرداران فلسطینیان صدها و هزارها می‌گذشتند، و داود و مردانش با اخیش در دنباله ایشان می‌گذشتند.۲
3 Tsono atsogoleri a Afilisti aja anafunsa kuti, “Kodi Ahebri awa akufuna chiyani?” Akisi anayankha kuti, “Uyu ndi Davide, mtumiki wa Sauli mfumu ya Israeli. Iye wakhala ndi ine kwa masiku ndithu, kapena titi zaka ndipo kuyambira tsiku limene anachoka kwa Sauli mpaka lero, ine sindinapeze cholakwa mwa iye.”
و سرداران فلسطینیان گفتند که «این عبرانیان کیستند؟» و اخیش به جواب سرداران فلسطینیان گفت: «مگر این داود، بنده شاول، پادشاه اسرائیل نیست که نزد من این‌روزهایا این سالها بوده است و از روزی که نزد من آمد تاامروز در او عیبی نیافتم.»۳
4 Koma atsogoleri a ankhondo a Afilisti anamukwiyira Akisi kwambiri ndipo anati, “Mubweze munthuyu kuti abwerere ku malo amene unamupatsa. Iye asapite nafe ku nkhondo kuopa kuti angadzasanduke mdani wathu. Kodi iyeyu adzadziyanjanitsa bwanji ndi mbuye wake? Iyeyutu adzadziyanjanitsa ndi mbuye wake pakupha anthu ali panowa?
اما سرداران فلسطینیان بر وی غضبناک شدند، و سرداران فلسطینیان او را گفتند: «این مردرا باز گردان تا به‌جایی که برایش تعیین کرده‌ای برگردد، و با ما به جنگ نیاید، مبادا در جنگ دشمن ما بشود، زیرا این کس با چه چیز با آقای خود صلح کند آیا نه با سرهای این مردمان؟۴
5 Paja ameneyu ndi Davide yemwe ankamuvinira namuyimbira kuti, “‘Sauli wapha anthu 1,000 koma Davide wapha miyandamiyanda?’”
آیااین داود نیست که درباره او با یکدیگر رقص کرده، می‌سراییدند و می‌گفتند: «شاول هزارهای خود و داود ده هزارهای خویش را کشته است.»۵
6 Kotero Akisi anayitana Davide ndipo anamuwuza kuti, “Pali Yehova wamoyo, iwe wakhala wodalirika ndipo chikanakhala chinthu chabwino kuti uzimenya nkhondo pamodzi nane popeza chibwerere iwe kuno ine sindinapeze cholakwa chilichonse ndi iwe. Koma atsogoleri enawa ndiwo sakukufuna.
آنگاه اخیش داود را خوانده، او را گفت: «به حیات یهوه قسم که تو مرد راست هستی و خروج و دخول تو با من در اردو به نظر من پسند آمد، زیرا از روز آمدنت نزد من تا امروز از تو بدی ندیده‌ام لیکن در نظر سرداران پسند نیستی.۶
7 Tsono bwerera. Upite mu mtendere kuopa kuti ungachite kanthu kena koyipira atsogoleri a Afilistiwa.”
پس الان برگشته، به سلامتی برو مبادا مرتکب عملی شوی که در نظر سرداران فلسطینیان ناپسند آید.»۷
8 Davide anafunsa Akisi kuti, “Kodi ndachita chiyani? Kodi mwapeza cholakwa chotani mwa ine mtumiki wanu chiyambire kukutumikirani mpaka lero? Tsono chifukwa chiyani sindingapite kukamenya nkhondo ndi adani a mbuye wanga mfumu?”
و داود به اخیش گفت: «چه کرده‌ام و از روزی که به حضور تو بوده‌ام تا امروز در بنده ات چه یافته‌ای تا آنکه به جنگ نیایم و با دشمنان آقایم پادشاه جنگ ننمایم؟»۸
9 Akisi anayankha kuti, “Ine ndikudziwa kuti ndiwe wangwiro ngati mngelo wa Mulungu. Komabe atsogoleri a ankhondo a Afilisti akuti, ‘Davide asapite nafe ku nkhondo.’
اخیش در جواب داود گفت: «می‌دانم که تودر نظر من مثل فرشته خدا نیکو هستی لیکن سرداران فلسطینیان گفتند که با ما به جنگ نیاید.۹
10 Tsono udzuke mmamawa, pamodzi ndi ankhondo ako amene unabwera nawo, ndipo unyamuke kukangocha.”
پس الحال بامدادان با بندگان آقایت که همراه تو آمده‌اند، برخیز و چون بامدادان برخاسته باشید و روشنایی برای شما بشود، روانه شوید.»۱۰
11 Choncho Davide ndi anthu ake anadzuka mmamawa kubwerera ku dziko la Afilisti. Koma Afilistiwo anapita ku Yezireeli.
پس داود با کسان خود صبح زود برخاستند تا روانه شده، به زمین فلسطینیان برگردند وفلسطینیان به یزرعیل برآمدند.۱۱

< 1 Samueli 29 >