< 1 Samueli 29 >
1 Afilisti anasonkhanitsa asilikali awo onse ku Afeki, ndipo Israeli anamanga misasa yawo pa chitsime cha Yezireeli.
Les Philistins concentrèrent toutes leurs troupes à Aphek, tandis que les Israélites étaient campés près de la source qui est à Jezreël.
2 Pamene atsogoleri a Afilisti ankatsogolera magulu awo ankhondo a miyandamiyanda, Davide ndi ankhondo ake ankayenda pambuyo pamodzi ndi Akisi.
Les princes des Philistins s’avancèrent avec leurs troupes de cent et de mille; David et ses hommes formaient l’arrière-garde avec Akhich.
3 Tsono atsogoleri a Afilisti aja anafunsa kuti, “Kodi Ahebri awa akufuna chiyani?” Akisi anayankha kuti, “Uyu ndi Davide, mtumiki wa Sauli mfumu ya Israeli. Iye wakhala ndi ine kwa masiku ndithu, kapena titi zaka ndipo kuyambira tsiku limene anachoka kwa Sauli mpaka lero, ine sindinapeze cholakwa mwa iye.”
Les chefs des Philistins dirent: "Qu’est-ce que ces Hébreux?" Akhich leur répondit: "Mais c’est David, le serviteur de Saül, roi d’Israël, qui a été auprès de moi bien des jours et même des années, et chez qui je n’ai rien trouvé à reprendre depuis son arrivée jusqu’à ce jour."
4 Koma atsogoleri a ankhondo a Afilisti anamukwiyira Akisi kwambiri ndipo anati, “Mubweze munthuyu kuti abwerere ku malo amene unamupatsa. Iye asapite nafe ku nkhondo kuopa kuti angadzasanduke mdani wathu. Kodi iyeyu adzadziyanjanitsa bwanji ndi mbuye wake? Iyeyutu adzadziyanjanitsa ndi mbuye wake pakupha anthu ali panowa?
Les chefs des Philistins se mirent en colère contre lui et lui dirent: "Fais repartir cet homme; qu’il retourne à l’endroit que tu lui as assigné, mais qu’il ne nous accompagne pas à la guerre et ne devienne pas un obstacle contre nous dans le combat; car, comment cet homme se ferait-il bien venir de son maître, si ce n’est avec les têtes de nos soldats?
5 Paja ameneyu ndi Davide yemwe ankamuvinira namuyimbira kuti, “‘Sauli wapha anthu 1,000 koma Davide wapha miyandamiyanda?’”
N’Est-ce pas ce même David que les chœurs acclamaient en disant: "Saül a battu ses mille, Et David ses myriades?"
6 Kotero Akisi anayitana Davide ndipo anamuwuza kuti, “Pali Yehova wamoyo, iwe wakhala wodalirika ndipo chikanakhala chinthu chabwino kuti uzimenya nkhondo pamodzi nane popeza chibwerere iwe kuno ine sindinapeze cholakwa chilichonse ndi iwe. Koma atsogoleri enawa ndiwo sakukufuna.
Akhich appela David et lui dit: "Par le Dieu vivant! Tu es honnête, ta conduite auprès de moi dans l’armée me plaît, et je n’ai rien trouvé à te reprocher depuis le jour de ton arrivée chez moi jusqu’à ce jour; mais tu n’es pas agréable aux princes.
7 Tsono bwerera. Upite mu mtendere kuopa kuti ungachite kanthu kena koyipira atsogoleri a Afilistiwa.”
Repars donc et va en paix, pour ne pas mécontenter les princes des Philistins.
8 Davide anafunsa Akisi kuti, “Kodi ndachita chiyani? Kodi mwapeza cholakwa chotani mwa ine mtumiki wanu chiyambire kukutumikirani mpaka lero? Tsono chifukwa chiyani sindingapite kukamenya nkhondo ndi adani a mbuye wanga mfumu?”
Mais, dit David à Akhich, qu’ai-je fait et qu’as-tu trouvé en ton serviteur, du jour où j’ai paru devant toi jusqu’à présent, pour que je ne puisse aller me battre contre les ennemis de mon seigneur le roi?"
9 Akisi anayankha kuti, “Ine ndikudziwa kuti ndiwe wangwiro ngati mngelo wa Mulungu. Komabe atsogoleri a ankhondo a Afilisti akuti, ‘Davide asapite nafe ku nkhondo.’
Akhich, reprenant la parole, dit à David: "Je le sais, tu me plais autant que le ferait un ange de Dieu; mais les chefs des Philistins ont dit: Il ne doit pas aller en guerre avec nous.
10 Tsono udzuke mmamawa, pamodzi ndi ankhondo ako amene unabwera nawo, ndipo unyamuke kukangocha.”
Donc, lève-toi demain de bonne heure avec les serviteurs de ton maître, venus avec toi; vous vous lèverez matin, et, le jour venu, vous partirez."
11 Choncho Davide ndi anthu ake anadzuka mmamawa kubwerera ku dziko la Afilisti. Koma Afilistiwo anapita ku Yezireeli.
Et David se leva de bonne heure ainsi que ses hommes pour se mettre en route le matin et retourner au pays des Philistins, tandis que ceux-ci montaient vers Jezreël.