< 1 Samueli 29 >

1 Afilisti anasonkhanitsa asilikali awo onse ku Afeki, ndipo Israeli anamanga misasa yawo pa chitsime cha Yezireeli.
A tak shromáždili Filistinští všecka vojska svá u Afeku, Izrael pak položil se u studnice, kteráž byla v Jezreel.
2 Pamene atsogoleri a Afilisti ankatsogolera magulu awo ankhondo a miyandamiyanda, Davide ndi ankhondo ake ankayenda pambuyo pamodzi ndi Akisi.
I táhla knížata Filistinská po stu a po tisících, David pak a muži jeho táhli nazad s Achisem.
3 Tsono atsogoleri a Afilisti aja anafunsa kuti, “Kodi Ahebri awa akufuna chiyani?” Akisi anayankha kuti, “Uyu ndi Davide, mtumiki wa Sauli mfumu ya Israeli. Iye wakhala ndi ine kwa masiku ndithu, kapena titi zaka ndipo kuyambira tsiku limene anachoka kwa Sauli mpaka lero, ine sindinapeze cholakwa mwa iye.”
Tedy řekla knížata Filistinská: K čemu jsou Židé tito? Odpověděl Achis knížatům Filistinským: Zdaliž toto není David služebník Saule, krále Izraelského, kterýž byl při mně dnů těchto, nýbrž těchto let, a neshledal jsem na něm ničeho ode dne, jakž odpadl od Saule, až do tohoto dne?
4 Koma atsogoleri a ankhondo a Afilisti anamukwiyira Akisi kwambiri ndipo anati, “Mubweze munthuyu kuti abwerere ku malo amene unamupatsa. Iye asapite nafe ku nkhondo kuopa kuti angadzasanduke mdani wathu. Kodi iyeyu adzadziyanjanitsa bwanji ndi mbuye wake? Iyeyutu adzadziyanjanitsa ndi mbuye wake pakupha anthu ali panowa?
I rozhněvala se na něj knížata Filistinská, a řekli jemu ta knížata Filistinská: Odešli zase muže toho, ať se navrátí k místu svému, kteréž jsi mu ukázal, a nechť netáhne s námi k boji, aby se nám nepostavil za nepřítele v bitvě. Nebo čím se zalíbiti může pánu svému tento? Zdali ne hlavami mužů těchto?
5 Paja ameneyu ndi Davide yemwe ankamuvinira namuyimbira kuti, “‘Sauli wapha anthu 1,000 koma Davide wapha miyandamiyanda?’”
Zdaliž tento není ten David, o kterémž zpívali v houfích plésajících, říkajíce: Porazil Saul svůj tisíc, ale David svých deset tisíců?
6 Kotero Akisi anayitana Davide ndipo anamuwuza kuti, “Pali Yehova wamoyo, iwe wakhala wodalirika ndipo chikanakhala chinthu chabwino kuti uzimenya nkhondo pamodzi nane popeza chibwerere iwe kuno ine sindinapeze cholakwa chilichonse ndi iwe. Koma atsogoleri enawa ndiwo sakukufuna.
I povolal Achis Davida, a řekl jemu: Živť jest Hospodin, že jsi upřímý, a líbí mi se vycházení tvé i vcházení tvé se mnou do vojska. Nebo neshledal jsem na tobě nic zlého ode dne, v kterýž jsi přišel ke mně, až do dne tohoto, ale před očima knížat nejsi vzácný.
7 Tsono bwerera. Upite mu mtendere kuopa kuti ungachite kanthu kena koyipira atsogoleri a Afilistiwa.”
Protož nyní navrať se a jdi v pokoji, a nebudeš těžký v očích knížat Filistinských.
8 Davide anafunsa Akisi kuti, “Kodi ndachita chiyani? Kodi mwapeza cholakwa chotani mwa ine mtumiki wanu chiyambire kukutumikirani mpaka lero? Tsono chifukwa chiyani sindingapite kukamenya nkhondo ndi adani a mbuye wanga mfumu?”
I řekl David Achisovi: Co jsem pak učinil, a co jsi shledal na služebníku svém ode dne, v kterýž jsem počal býti u tebe, až do tohoto dne, abych nešel a nebojoval proti nepřátelům pána svého krále?
9 Akisi anayankha kuti, “Ine ndikudziwa kuti ndiwe wangwiro ngati mngelo wa Mulungu. Komabe atsogoleri a ankhondo a Afilisti akuti, ‘Davide asapite nafe ku nkhondo.’
A odpovídaje Achis, řekl Davidovi: Vímť, že jsi vzácný před očima mýma jako anděl Boží, ale knížata Filistinská řekla: Nechť netáhne s námi k boji.
10 Tsono udzuke mmamawa, pamodzi ndi ankhondo ako amene unabwera nawo, ndipo unyamuke kukangocha.”
Nyní tedy vstaň tím raněji a služebníci pána tvého, kteříž přišli s tebou, a vstanouce tím spíše ráno, hned jakž by zasvitávalo, odejděte.
11 Choncho Davide ndi anthu ake anadzuka mmamawa kubwerera ku dziko la Afilisti. Koma Afilistiwo anapita ku Yezireeli.
I vstal David, on i muži jeho, aby odšel tím raněji, a navrátil se do země Filistinské. Filistinští pak táhli do Jezreel.

< 1 Samueli 29 >