< 1 Samueli 28 >
1 Mʼmasiku amenewo Afilisti anasonkhanitsa ankhondo awo kuti akamenyane ndi Aisraeli. Akisi anawuza Davide kuti, “Udziwe kuti iwe pamodzi ndi anthu ako mudzapita nane ku nkhondo.”
And it came to pass in those days, that the Philistines gathered their camps together for warfare, to fight with Israel; and Achish said unto David, Thou must know that thou shalt go out with me into the camp, thou and thy men.
2 Davide anayankha kuti, “Tsono inu mudzaona zimene mtumiki wanune ndingachite.” Akisi anayankha kuti, “Chabwino ine ndidzakuyika iwe kukhala mlonda wanga moyo wako wonse.”
And David said to Achish, By reason of this wilt thou thyself ascertain what thy servant will do. And Achish said to David, Therefore will I make thee the guard of my head for all times.
3 Nthawi imeneyi nʼkuti Samueli atamwalira, ndipo Aisraeli onse anamulira namuyika mʼmanda ku mzinda wake wa Rama. Sauli anali atachotsa mʼdzikomo anthu owombeza mawula ndi woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa.
Now Samuel was dead, and all Israel had lamented him, and buried him in Ramah, even in his own city; and Saul had removed those that had familiar spirits, and the wizards, out of the land.
4 Tsono Afilisti anasonkhana nabwera kudzamanga misasa yawo ku Sunemu. Nayenso Sauli anasonkhanitsa Aisraeli onse ndi kumanga misasa yawo ku Gilibowa.
And the Philistines assembled themselves together, and came and encamped at Shunem: and Saul assembled together all Israel, and they encamped at Gilboa'.
5 Sauli ataona gulu lankhondo la Afilisti anaopa ndipo ananjenjemera kwambiri.
And when Saul saw the camp of the Philistines, he was afraid, and his heart trembled greatly.
6 Choncho Sauli anafunsa nzeru kwa Yehova koma Yehova sanamuyankhe ngakhale kudzera mʼmaloto, kapena mwa Urimu ngakhalenso kudzera mwa aneneri.
And Saul asked counsel of the Lord; but the Lord answered him not, either by means of dreams, or by means of the Urim, or by means of the prophets.
7 Kenaka Sauli anawuza nduna zake kuti, “Mundipezere mkazi amene amawombeza mawula kuti ndipite ndikafunse kwa iye.” Nduna zakezo zinamuyankha kuti, “Alipo mkazi woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa ku Endori.”
Then said Saul unto his servants, Seek out for me a woman that hath a familiar spirit, that I may go to her and inquire of her. And his servants said to him, Behold, there is a woman that hath a familiar spirit at 'En-dor.
8 Kotero Sauli anadzizimbayitsa navala zovala zachilendo. Tsono iye pamodzi ndi anthu awiri anapita nakafika kwa mkazi uja usiku, ndipo anamupempha kuti, “Chonde ndifunsireni nzeru kwa mizimu ya anthu akufa. Koma makamaka munditulutsire mzimu wa amene ndimutchule.”
And Saul disguised himself, and put on other garments, and he went, he and two men with him, and they came to the woman by night: and he said, Divine, I pray thee, unto me by the familiar spirit, and bring up for me the one whom I shall say unto thee.
9 Koma mkaziyo anayankha kuti, “Ndithu inu mukudziwa chimene Sauli anachita. Paja iye anachotsa mʼdziko muno anthu onse owombeza ndi woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa. Chifukwa chiyani mukutchera moyo wanga msampha kuti ndiphedwe?”
And the woman said unto him, Behold, thou well knowest that which Saul hath done, that he hath cut off those that have familiar spirits, and the wizards, out of the land; wherefore then layest thou a snare for my life, to cause me to die?
10 Koma Sauli analonjeza mkaziyo molumbira nati, “Pali Yehova wamoyo, iweyo sudzalangidwa chifukwa cha zimenezi.”
And Saul swore to her by the Lord, saying, As the Lord liveth, there shall no guilt attach to thee for this thing.
11 Kenaka mkaziyo anafunsa, “Ndikuyitanireni yani?” Iye anati, “Undiyitanire Samueli.”
Then said the woman, Whom shall I bring up for thee? And he said, Samuel thou must bring up for me.
12 Pamene mkaziyo anaona Samueli anakuwa kwambiri, nawuza Sauli kuti, “Nʼchifukwa chiyani inu mwandipusitsa? Inu ndinu Sauli!”
And when the woman saw Samuel, she cried with a loud voice: and the woman said to Saul thus, Why hast thou deceived me? since thou art Saul.
13 Mfumuyo inamuwuza kuti, “Usaope. Kodi ukuona chiyani?” Mkaziyo anayankha kuti, “Ndikuona mzimu ukutuluka pansi.”
And the king said unto her, Be not afraid; however, what hast thou seen? And the woman said unto Saul, A divine being have I seen ascending out of the earth.
14 Sauli anafunsa, “Kodi mzimuwo ukuoneka motani?” Mkaziyo anayankha kuti, “Amene akutuluka ndi munthu wokalamba ndipo wavala mkanjo.” Apo Sauli anadziwa kuti anali Samueli ndipo anawerama nagunditsa nkhope yake pansi.
And he said unto her, What is his form? And she said, An old man is coming up; and he is wrapt in a mantle. And so Saul perceived that it was Samuel, and he bowed with his face to the ground, and prostrated himself.
15 Samueli anafunsa Sauli kuti, “Nʼchifukwa chiyani wandivutitsa pondiyitana kuti ndibwere kuno?” Sauli anayankha kuti, “Ine ndavutika kwambiri mʼmaloto. Afilisti akumenyana nane, ndipo Mulungu wandifulatira. Iye sakundiyankhulanso, ngakhale kudzera mwa aneneri kapena maloto. Choncho ndakuyitanani kuti mundiwuze zoti ndichite.”
And Samuel said to Saul, Why hast thou disquieted me, to bring me up? And Saul answered, I am greatly distressed, and the Philistines make war against me, and God is departed from me, and hath not answered me any more, either by the agency of the prophets, or by means of dreams; wherefore I have called thee, to make known unto me what I shall do.
16 Samueli anati, “Nʼchifukwa chiyani ukundifunsa ine, pakuti tsopano Yehova wakufulatira ndipo wasanduka mdani wako?
Then said Samuel, And why wilt thou ask me, seeing the Lord is departed from thee, and is become thy enemy?
17 Yehova wakuchita zimene ananeneratu kudzera mwa ine. Yehova wachotsa ufumu mʼmanja mwako ndipo waupereka kwa mnansi wako, kwa Davide.
And the Lord hath done for himself as he hath spoken through my agency; and the Lord hath rent the government out of thy hand, and hath given it to thy associate, to David;
18 Yehova wachita zimenezi lero chifukwa sunamvere mawu ake ndipo sunawawonongeretu Aamaleki.
As thou didst not obey the voice of the Lord, and didst not execute his fierce wrath upon 'Amalek; therefore hath the Lord done this thing unto thee this day.
19 Yehova adzapereka ndithu iweyo pamodzi ndi Aisraeli kwa Afilisti. Ndipo mmawa iweyo ndi ana ako mudzakhala ndi ine kuno. Ndithu Yehova adzapereka gulu lankhondo la Aisraeli kwa Afilisti.”
And the Lord will deliver also Israel with thee into the hand of the Philistines; and tomorrow shalt thou and thy sons be with me: also the camp of Israel will the Lord deliver into the hand of the Philistines.
20 Nthawi yomweyo Sauli anagwa pansi atadzazidwa ndi mantha chifukwa cha mawu a Samueli. Analibenso mphamvu, pakuti sanadye tsiku lonse.
Then fell Saul hastily with his full length to the earth, and was greatly afraid, because of the words of Samuel: there was also no strength in him; for he had not eaten any food all that day, and all that night.
21 Mkazi uja tsono anasendera kufupi ndi Sauli, ndipo ataona kuti Sauli akuchita mantha, anamuwuza kuti, “Taonani, mdzakazi wanune ndakumverani. Ndayika moyo wanga pa chiswe ndipo ndamvera zimene munandiwuza.
And the woman came unto Saul, and saw that he was greatly terrified; and she said unto him, Behold, thy hand-maid hath obeyed thy voice; and I put my life in my hand, and hearkened unto thy words which thou spokest unto me.
22 Tsono inunso mumvere mawu a mdzakazi wanune. Mundilole kuti ndikupatseni ka buledi pangʼono kuti mukhale ndi mphamvu zoyendera pa ulendo wanu.”
And now, hearken thou also, I pray thee, unto the voice of thy hand-maid, and let me set before thee a morsel of bread, and eat; that thou mayest have strength when thou goest on the way.
23 Iye anakana ndipo anati, “Ayi, ine sindidya.” Koma nduna zake pamodzi ndi mkaziyo anamuwumiriza, ndipo anawamvera. Choncho anadzuka pansi nakhala pa bedi.
But he refused, and said, I will not eat. But his servants urged him much, as also the woman; and he hearkened unto their voice. So he arose from the earth, and sat upon the bed.
24 Mkaziyo anali ndi mwana wangʼombe wonenepa ndipo anamupha mwachangu. Anatenga ufa nawukanyanga ndipo anaphika buledi wopanda yisiti.
And the woman had a fatted calf in the house; and she hastened, and slaughtered it, and took flour, and kneaded it, and baked unleavened bread thereof:
25 Tsono anapereka bulediyo kwa Sauli ndi nduna zake ndipo anadya. Pambuyo pake ananyamuka kupita kwawo usiku womwewo.
And she brought it near before Saul, and before his servants; and they ate. Then they rose up, and went away that night.