< 1 Samueli 27 >

1 Davide anaganiza mu mtima mwake nati, “Tsiku lina ine ndidzaphedwa ndi Sauli. Palibe chabwino ndingachite, koma kuthawira ku dziko la Afilisti. Kotero Sauli adzasiya kundifunafuna mʼdziko lonse la Israeli, ndipo ndidzapulumuka.”
Tedy rzekł Dawid w sercu swojem: Zginę ja kiedyżkolwiek od ręki Saulowej. Azaż mnie nie lepiej, abym co prędzej uszedł do ziemi Filistyńskiej, aby zwątpił o mnie Saul, i nie szukał mię więcej po wszystkich granicach Izraelskich, i tak abym uszedł rąk jego?
2 Choncho Davide ndi anthu 600 amene anali nawo anachoka napita kwa Akisi mwana wa Maoki mfumu ya ku Gati.
Wstawszy tedy Dawid, poszedł sam i onych sześć set mężów, którzy byli z nim, do Achisa, syna Maocha, króla Get.
3 Davide anakhala ndi Akisi ku Gati pamodzi ndi ankhondo ake, aliyense ndi banja lake. Davide ali ndi akazi ake awiri, Ahinoamu wa ku Yezireeli ndi Abigayeli wa ku Karimeli, mkazi wamasiye wa Nabala.
I mnieszkał Dawid przy Achisie w Get, sam i mężowie jego, każdy z czeladzią swoją, Dawid i dwie żony jego, Achinoam Jezreelitka, i Abigail, żona przedtem Nabalowa z Karmelu.
4 Sauli anamva kuti Davide wathawira ku Gati, ndipo sanamufunefunenso.
A gdy powiedziano Saulowi, że uciekł Dawid do Get, przestał go więcej szukać.
5 Kenaka Davide anawuza Akisi kuti, “Ngati ndapeza kuyanja pamaso panu mundipatse malo dera limodzi la dziko lanu kuti ndizikhala kumeneko. Mtumiki wanu adzakhala mu mzinda waufumu chifukwa chiyani?”
I rzekł Dawid do Achisa: Jeźlim proszę znalazł łaskę w oczach twoich, niech mi dadzą miejsce w jednem z miast tego kraju, abym tam mieszkał; bo czemużby miał mieszkać sługa twój w mieście królewskiem z tobą?
6 Choncho tsiku limenelo Akisi anamupatsa Zikilagi ndipo mzindawo wakhala wa mafumu a Yuda mpaka lero.
I dał mu Achis dnia onego Syceleg; dla tego Syceleg było królów Judzkich aż do dnia tego.
7 Davide anakhala mʼdziko la Afilisti kwa chaka chimodzi ndi miyezi inayi.
A była liczba dni, których mieszkał Dawid w krainie Filistyńskiej, rok i cztery miesiące.
8 Tsono Davide ndi anthu ake ankapita kukathira nkhondo Agesuri, Agirizi ndi Aamaleki. (Mitundu ya anthu imeneyi kuyambira kale inkakhala mʼdziko la pakati pa Suri ndi Igupto).
I wypadał Dawid i mężowie jego, a wtargiwali do Giessurytów, i do Gierzytów, i do Amalekitów; bo ci mieszkali w onej ziemi zdawna; którędy chodzą przez Sur aż do ziemi Egipskiej.
9 Davide ankati akathira nkhondo dera lina, sankasiya munthu wamoyo, mwamuna kapena mkazi, koma ankatenga nkhosa, ngʼombe, abulu, ngamira ndi zovala, pambuyo pake nʼkubwerera kwa Akisi.
I pustoszył Dawid ziemię onę, a nie zostawiał żywego męża i niewiasty; a zabrawszy owce, i woły, i osły i wielbłądy, i szaty, wracał się zasię, i przychadzał do Achisa.
10 Akisi akafunsa kuti, “Kodi lero unapita kukathira nkhondo kuti?” Davide ankayankha kuti, “Ndinapita kukathira nkhondo kummwera kwa Yuda,” mwinanso ankanena kuti, “Ndinapita ku dziko la Ayerahimeeli” kapenanso ankanena kuti, “Ndinapita ku dziko la Akeni.”
A gdy się pytał Achis: Gdzieżeście byli dziś wpadli? odpowiadał Dawid: Ku południu Judy, i ku południu w Jerameel, i ku południu Ceni.
11 Davide sankasiya mwamuna kapena mkazi wamoyo kuti akafotokozere anthu a ku Gati zochitikazo kuopa kuti opulumukawo akhoza kudzanena kuti “Davide watichita zakutizakuti.” Tsono izi ndi zimene Davide ankachita pamene ankakhala mʼdziko la Afilisti.
Ale Dawid nie żywił męża, ani niewiasty, ani ich przywodził do Get, mówiąc: By snać nie skarżyli na nas, mówiąc: Tak uczynił Dawid. I był to jego zwyczaj po wszystkie dni, póki mieszkał w ziemi Filistyńskiej.
12 Akisi ankamukhulupirira Davide ndipo ankati mu mtima mwake, “Davide wadzisandutsa munthu woyipa kwambiri pakati pa anthu ake omwe, Aisraeli. Tsono adzakhala mtumiki wanga mpaka kalekale.”
Wierzył tedy Achis Dawidowi i mówił: Prawie się już stał obrzydłym ludowi swemu Izraelskiemu, a tak będzie mi sługą wiecznym.

< 1 Samueli 27 >