< 1 Samueli 27 >
1 Davide anaganiza mu mtima mwake nati, “Tsiku lina ine ndidzaphedwa ndi Sauli. Palibe chabwino ndingachite, koma kuthawira ku dziko la Afilisti. Kotero Sauli adzasiya kundifunafuna mʼdziko lonse la Israeli, ndipo ndidzapulumuka.”
Men David tenkte ved sig selv: Engang kommer jeg nu allikevel til å miste livet for Sauls hånd; jeg har ikke noget godt i vente. Jeg vil undfly til filistrenes land; så vil Saul holde op med å lete efter mig i hele Israels land, og jeg slipper ut av hans hånd.
2 Choncho Davide ndi anthu 600 amene anali nawo anachoka napita kwa Akisi mwana wa Maoki mfumu ya ku Gati.
Så brøt David op og drog med de seks hundre mann som var hos ham, over til Akis, sønn av Maok, kongen i Gat.
3 Davide anakhala ndi Akisi ku Gati pamodzi ndi ankhondo ake, aliyense ndi banja lake. Davide ali ndi akazi ake awiri, Ahinoamu wa ku Yezireeli ndi Abigayeli wa ku Karimeli, mkazi wamasiye wa Nabala.
Og David blev boende hos Akis i Gat, både han og hans menn, hver med sitt hus, David med sine to hustruer, Akinoam fra Jisre'el og Abiga'il fra Karmel, Nabals hustru.
4 Sauli anamva kuti Davide wathawira ku Gati, ndipo sanamufunefunenso.
Og da Saul fikk vite at David var flyktet til Gat, lette han ikke lenger efter ham.
5 Kenaka Davide anawuza Akisi kuti, “Ngati ndapeza kuyanja pamaso panu mundipatse malo dera limodzi la dziko lanu kuti ndizikhala kumeneko. Mtumiki wanu adzakhala mu mzinda waufumu chifukwa chiyani?”
Så sa David til Akis: Har jeg funnet nåde for dine øine, så la mig få et sted å bo på i en av landsbyene. Hvorfor skal din tjener bo hos dig i kongestaden?
6 Choncho tsiku limenelo Akisi anamupatsa Zikilagi ndipo mzindawo wakhala wa mafumu a Yuda mpaka lero.
Da gav Akis ham samme dag Siklag; derfor har Siklag hørt Judas konger til helt til denne dag.
7 Davide anakhala mʼdziko la Afilisti kwa chaka chimodzi ndi miyezi inayi.
Den tid David bodde i filistrenes land, var i alt ett år og fire måneder.
8 Tsono Davide ndi anthu ake ankapita kukathira nkhondo Agesuri, Agirizi ndi Aamaleki. (Mitundu ya anthu imeneyi kuyambira kale inkakhala mʼdziko la pakati pa Suri ndi Igupto).
David og hans menn drog op og overfalt gesurittene og girsittene og amalekittene; det var de folk som fra eldgammel tid hadde bodd i det land som strekker sig bortimot Sur og helt til Egyptens land.
9 Davide ankati akathira nkhondo dera lina, sankasiya munthu wamoyo, mwamuna kapena mkazi, koma ankatenga nkhosa, ngʼombe, abulu, ngamira ndi zovala, pambuyo pake nʼkubwerera kwa Akisi.
Og hver gang David herjet landet, lot han hverken mann eller kvinne bli i live; men han tok både småfe og storfe og asener og kameler og klær og drog så tilbake, og når han så kom til Akis,
10 Akisi akafunsa kuti, “Kodi lero unapita kukathira nkhondo kuti?” Davide ankayankha kuti, “Ndinapita kukathira nkhondo kummwera kwa Yuda,” mwinanso ankanena kuti, “Ndinapita ku dziko la Ayerahimeeli” kapenanso ankanena kuti, “Ndinapita ku dziko la Akeni.”
og Akis spurte: I har vel ikke gjort noget innfall idag? da svarte David: Jo, i sydlandet, både blandt Judas menn og blandt jerahme'elittene og kenittene.
11 Davide sankasiya mwamuna kapena mkazi wamoyo kuti akafotokozere anthu a ku Gati zochitikazo kuopa kuti opulumukawo akhoza kudzanena kuti “Davide watichita zakutizakuti.” Tsono izi ndi zimene Davide ankachita pamene ankakhala mʼdziko la Afilisti.
David lot hverken mann eller kvinne bli i live eller tok dem med sig til Gat; for han tenkte: De kunde fortelle om oss og si: Så og så har David gjort. Således bar han sig at i all den tid han bodde i filistrenes land.
12 Akisi ankamukhulupirira Davide ndipo ankati mu mtima mwake, “Davide wadzisandutsa munthu woyipa kwambiri pakati pa anthu ake omwe, Aisraeli. Tsono adzakhala mtumiki wanga mpaka kalekale.”
Og Akis trodde David og tenkte: Han har gjort sig forhatt blandt Israel, sitt folk, og nu kommer han til å være min tjener for all tid.