< 1 Samueli 27 >
1 Davide anaganiza mu mtima mwake nati, “Tsiku lina ine ndidzaphedwa ndi Sauli. Palibe chabwino ndingachite, koma kuthawira ku dziko la Afilisti. Kotero Sauli adzasiya kundifunafuna mʼdziko lonse la Israeli, ndipo ndidzapulumuka.”
David disait en son cœur: « Je vais maintenant périr un jour par la main de Saül. Il n'y a rien de mieux pour moi que de m'échapper dans le pays des Philistins; et Saül désespérera de moi, pour me chercher encore dans tout le territoire d'Israël. Je m'échapperai donc de sa main. »
2 Choncho Davide ndi anthu 600 amene anali nawo anachoka napita kwa Akisi mwana wa Maoki mfumu ya ku Gati.
David se leva et passa, lui et les six cents hommes qui étaient avec lui, chez Akish, fils de Maoch, roi de Gath.
3 Davide anakhala ndi Akisi ku Gati pamodzi ndi ankhondo ake, aliyense ndi banja lake. Davide ali ndi akazi ake awiri, Ahinoamu wa ku Yezireeli ndi Abigayeli wa ku Karimeli, mkazi wamasiye wa Nabala.
David habitait avec Akish à Gath, lui et ses hommes, chacun avec sa maison, même David avec ses deux femmes, Ahinoam la Jizreelite et Abigaïl la Carmélite, femme de Nabal.
4 Sauli anamva kuti Davide wathawira ku Gati, ndipo sanamufunefunenso.
Saül apprit que David s'était enfui à Gath, et il cessa de le chercher.
5 Kenaka Davide anawuza Akisi kuti, “Ngati ndapeza kuyanja pamaso panu mundipatse malo dera limodzi la dziko lanu kuti ndizikhala kumeneko. Mtumiki wanu adzakhala mu mzinda waufumu chifukwa chiyani?”
David dit à Akish: « Si maintenant j'ai trouvé grâce à tes yeux, qu'on me donne une place dans une des villes du pays, pour que j'y demeure. Car pourquoi ton serviteur devrait-il habiter avec toi dans la ville royale? »
6 Choncho tsiku limenelo Akisi anamupatsa Zikilagi ndipo mzindawo wakhala wa mafumu a Yuda mpaka lero.
Et Akish lui donna Ziklag ce jour-là: c'est pourquoi Ziklag appartient aux rois de Juda jusqu'à ce jour.
7 Davide anakhala mʼdziko la Afilisti kwa chaka chimodzi ndi miyezi inayi.
Le nombre de jours que David vécut dans le pays des Philistins fut d'une année entière et de quatre mois.
8 Tsono Davide ndi anthu ake ankapita kukathira nkhondo Agesuri, Agirizi ndi Aamaleki. (Mitundu ya anthu imeneyi kuyambira kale inkakhala mʼdziko la pakati pa Suri ndi Igupto).
David et ses hommes montèrent et attaquèrent les Gueshuriens, les Girziens et les Amalécites, car c'étaient les habitants du pays d'autrefois, sur le chemin de Shur, jusqu'au pays d'Égypte.
9 Davide ankati akathira nkhondo dera lina, sankasiya munthu wamoyo, mwamuna kapena mkazi, koma ankatenga nkhosa, ngʼombe, abulu, ngamira ndi zovala, pambuyo pake nʼkubwerera kwa Akisi.
David frappa le pays, ne sauva ni homme ni femme en vie, et prit les brebis, les bœufs, les ânes, les chameaux et les vêtements. Il s'en retourna, et arriva chez Akish.
10 Akisi akafunsa kuti, “Kodi lero unapita kukathira nkhondo kuti?” Davide ankayankha kuti, “Ndinapita kukathira nkhondo kummwera kwa Yuda,” mwinanso ankanena kuti, “Ndinapita ku dziko la Ayerahimeeli” kapenanso ankanena kuti, “Ndinapita ku dziko la Akeni.”
Akish dit: « Contre qui as-tu fait un raid aujourd'hui? » David répondit: « Contre le midi de Juda, contre le midi des Jerahmeelites, et contre le midi des Kenites. »
11 Davide sankasiya mwamuna kapena mkazi wamoyo kuti akafotokozere anthu a ku Gati zochitikazo kuopa kuti opulumukawo akhoza kudzanena kuti “Davide watichita zakutizakuti.” Tsono izi ndi zimene Davide ankachita pamene ankakhala mʼdziko la Afilisti.
David ne sauva ni homme ni femme en vie pour les amener à Gath, en disant: « De peur qu'on ne raconte à notre sujet: « David a fait cela, et c'est ainsi qu'il a agi tout le temps qu'il a vécu au pays des Philistins ». »
12 Akisi ankamukhulupirira Davide ndipo ankati mu mtima mwake, “Davide wadzisandutsa munthu woyipa kwambiri pakati pa anthu ake omwe, Aisraeli. Tsono adzakhala mtumiki wanga mpaka kalekale.”
Akish crut David, en disant: « Il a rendu son peuple d'Israël complètement odieux. C'est pourquoi il sera mon serviteur pour toujours. »