< 1 Samueli 27 >

1 Davide anaganiza mu mtima mwake nati, “Tsiku lina ine ndidzaphedwa ndi Sauli. Palibe chabwino ndingachite, koma kuthawira ku dziko la Afilisti. Kotero Sauli adzasiya kundifunafuna mʼdziko lonse la Israeli, ndipo ndidzapulumuka.”
And Dauid seide in his herte, Sumtyme Y schal falle in o dai in the hond of Saul; whether it is not betere, that Y fle, and be sauyd in the lond of Filisteis, that Saul dispeire, and cesse to seke me in alle the endis of Israel; therfor fle we hise hondis.
2 Choncho Davide ndi anthu 600 amene anali nawo anachoka napita kwa Akisi mwana wa Maoki mfumu ya ku Gati.
And Dauid roos, and yede, he and sixe hundrid men with hym, to Achis, the sone of Maoth, kyng of Geth.
3 Davide anakhala ndi Akisi ku Gati pamodzi ndi ankhondo ake, aliyense ndi banja lake. Davide ali ndi akazi ake awiri, Ahinoamu wa ku Yezireeli ndi Abigayeli wa ku Karimeli, mkazi wamasiye wa Nabala.
And Dauid dwellide with Achis in Geth, he, and hise men, and his hows; Dauid, and hise twei wyues, Achynoem of Jezrael, and Abigail, the wijf of Nabal of Carmele.
4 Sauli anamva kuti Davide wathawira ku Gati, ndipo sanamufunefunenso.
And it was teld to Saul, that Dauid fledde in to Geth; and he addide no more `that he schulde seke Dauid.
5 Kenaka Davide anawuza Akisi kuti, “Ngati ndapeza kuyanja pamaso panu mundipatse malo dera limodzi la dziko lanu kuti ndizikhala kumeneko. Mtumiki wanu adzakhala mu mzinda waufumu chifukwa chiyani?”
Forsothe Dauid seide to Achis, If Y haue founden grace in thin iyen, a place be youun to me in oon of the citees of this cuntrey, that Y dwelle there; for whi dwellith thi seruaunt in the citee of the kyng with thee?
6 Choncho tsiku limenelo Akisi anamupatsa Zikilagi ndipo mzindawo wakhala wa mafumu a Yuda mpaka lero.
Therfor Achis yaf to hym Sichelech in that dai, for which cause Sichelech was maad in to the possessioun of the kyngis of Juda `til in to this dai.
7 Davide anakhala mʼdziko la Afilisti kwa chaka chimodzi ndi miyezi inayi.
Forsothe the noumbre of daies, in whiche Dauid dwellide in the cuntrei of Filisteis, was of foure monethis.
8 Tsono Davide ndi anthu ake ankapita kukathira nkhondo Agesuri, Agirizi ndi Aamaleki. (Mitundu ya anthu imeneyi kuyambira kale inkakhala mʼdziko la pakati pa Suri ndi Igupto).
And Dauid stiede, and hise men, and token preies of Gethsuri, and of Gethri, and of men of Amalech; for these townes weren enhabitid bi eld tyme in the lond, to men goynge to Sur, `til to the lond of Egipt.
9 Davide ankati akathira nkhondo dera lina, sankasiya munthu wamoyo, mwamuna kapena mkazi, koma ankatenga nkhosa, ngʼombe, abulu, ngamira ndi zovala, pambuyo pake nʼkubwerera kwa Akisi.
And Dauid smoot al the lond of hem, and lefte not man `lyuynge and womman; and he took scheep, and oxun, and assis, and camels, and clothis, and turnede ayen, and cam to Achis.
10 Akisi akafunsa kuti, “Kodi lero unapita kukathira nkhondo kuti?” Davide ankayankha kuti, “Ndinapita kukathira nkhondo kummwera kwa Yuda,” mwinanso ankanena kuti, “Ndinapita ku dziko la Ayerahimeeli” kapenanso ankanena kuti, “Ndinapita ku dziko la Akeni.”
Sotheli Achis seide to hym, `In to whom `hurliden ye to dai? Dauid answeride, Ayens the south of Juda, and ayens the south of Hiramel, and ayens the south of Ceney.
11 Davide sankasiya mwamuna kapena mkazi wamoyo kuti akafotokozere anthu a ku Gati zochitikazo kuopa kuti opulumukawo akhoza kudzanena kuti “Davide watichita zakutizakuti.” Tsono izi ndi zimene Davide ankachita pamene ankakhala mʼdziko la Afilisti.
Dauid left not quik man and womman, nether brouyte `in to Geth, and se ide, Lest perauenture thei speken ayens vs. Dauid dide these thingis, and this was his doom, in alle daies in whiche he dwellide in the cuntrei of Filisteis.
12 Akisi ankamukhulupirira Davide ndipo ankati mu mtima mwake, “Davide wadzisandutsa munthu woyipa kwambiri pakati pa anthu ake omwe, Aisraeli. Tsono adzakhala mtumiki wanga mpaka kalekale.”
Therfor Achis bileuyde to Dauid, and seide, Forsothe he wrouyte many yuelis ayens his puple Israel, therfor he schal be euerlastynge seruaunt to me.

< 1 Samueli 27 >