< 1 Samueli 26 >

1 Anthu a ku Zifi anapita kwa Sauli ku Gibeya nati, “Davide akubisala ku phiri la Hakila, limene limayangʼanana ndi Yesimoni.”
And they went the Ziphites to Saul Gibeah towards saying ¿ not [is] David hiding himself on [the] hill of Hakilah on [the] face of Jeshimon.
2 Choncho Sauli ananyamuka pamodzi ndi ankhondo ake 3,000 napita ku chipululu cha Zifi kukafunafuna Davide ku chipululuko.
And he arose Saul and he went down to [the] wilderness of Ziph and [were] with him three thousand man [the] chosen [men] of Israel to seek David in [the] wilderness of Ziph.
3 Sauli anamanga msasa wake mʼmbali mwa njira yopita ku phiri la Hakila moyangʼanana ndi Yesimoni. Koma Davide anali mʼchipululumo. Davide ataona kuti Sauli amamulondola mpaka kumeneko,
And he encamped Saul on [the] hill of Hakilah which [was] on [the] face of Jeshimon on the way and David [was] dwelling in the wilderness and he saw that he had come Saul after him the wilderness towards.
4 iye anatumiza anthu okazonda ndipo anapeza kuti Sauli wafikadi ndithu.
And he sent David spies and he knew that he had come Saul to a certain [thing].
5 Tsono Davide ananyamuka napita kumalo kumene Sauli anamanga misasa. Iye anaona pamene Sauli ndi Abineri mwana wa Neri mkulu wa ankhondo anagona. Sauli anagona mʼkati mwa tenti ndipo asilikali anagona momuzungulira.
And he arose David and he went to the place where he had encamped there Saul and he saw David the place where he lay there Saul and Abner [the] son of Ner [the] commander of army his and Saul [was] lying in the camp and the people [was] encamped (around him. *Q(K)*)
6 Ndipo Davide anafunsa Ahimeleki Mhiti ndi Abisai mwana wa Zeruya, mʼbale wa Yowabu kuti, “Ndani adzapita nane ku msasa kwa Sauli?” Abisai anayankha kuti, “Ine ndidzapita nanu.”
And he answered David and he said - to Ahimelech the Hittite and to Abishai [the] son of Zeruiah [the] brother of Joab saying who? will he go down with me to Saul into the camp and he said Abishai I I will go down with you.
7 Choncho Davide ndi Abisai anapita ku misasa ya ankhondowo usiku. Atafika anangopeza Sauli ali gone mu msasa wake mkondo wake atawuzika pansi pafupi ndi mutu wake, Abineri ndi ankhondo onse anali atagona momuzungulira.
And he went David and Abishai - to the people night and there! Saul [was] lying sleeping in the camp and spear his [was] thrust in the ground ([the] place of head his *Q(K)*) and Abner and the people [were] lying (around him. *Q(K)*)
8 Abisai anawuza Davide kuti, “Lero Mulungu wapereka mdani wanu mʼmanja mwanu. Tsopano ndiloleni ndimukhomere pansi ndi mkondo wangawu kamodzinʼkamodzi. Sindimulasa kawiri.”
And he said Abishai to David he has delivered up God this day enemy your in hand your and therefore let me strike him please with the spear and in the ground a time one and not I will repeat to him.
9 Koma Davide anamuyankha Abisai kuti, “Usamuphe! Ndani adzapha wodzozedwa wa Yehova ndi kupezeka wosalakwa?
And he said David to Abishai may not you destroy him for who? has he stretched out hand his on [the] [one] anointed of Yahweh and will he be free from guilt?
10 Davide anati, Pali Yehova wamoyo, Yehova mwini ndiye adzamukanthe, mwina tsiku lake lomwalira lidzafika, kapena adzapita ku nkhondo nakaphedwa komweko.
And he said David [by] [the] life of Yahweh that except Yahweh he will strike him or day his it will come and he will die or in battle he will go down and he will be carried away.
11 Koma Yehova andiletse kuti ndisapweteke wodzozedwa wa Yehova. Tsopano tingotenga mkondo umene uli ku mutu kwakewo ndi botolo la madzilo ndipo tizipita.”
Far be it to me from Yahweh from stretching out hand my on [the] [one] anointed of Yahweh and now take please the spear which ([is the] place of head his *Q(K)*) and [the] jug of water and let us go for ourselves.
12 Motero Davide anatenga mkondo ndi botolo lamadzi zimene zinali ku mutu kwa Sauli ndipo anachoka. Palibe amene anaona zimenezi kapena kudziwa, ndipo palibenso amene anadzuka. Onse anali mʼtulo, chifukwa Yehova anawagonetsa tulo tofa nato.
And he took David the spear and [the] jug of water [at the] head of Saul and they went for themselves and there not [was one who] saw and there not [was one who] knew and there not [was one who] awoke for all of them [were] sleeping for deep sleep of Yahweh it had fallen on them.
13 Pambuyo pake Davide anadutsa nakakwerera mbali ina ya phiri, ndi kuyimirira pamwamba pa phiri patali. Pakati pawo panali mpata waukulu.
And he passed over David the other side and he stood on [the] top of the hill from a distance great place [was] between them.
14 Davide anayitana gulu lankhondo ndi Abineri mwana wa Neri nawafunsa kuti, “Kodi sundiyankha ine Abineri?” Abineri anayankha kuti, “Ndiwe yani amene ukuyitana mfumu?”
And he called out David to the people and to Abner [the] son of Ner saying ¿ not will you answer O Abner and he answered Abner and he said who? [are] you [who] you have called out to the king.
15 Davide anamufunsa Abineri kuti, “Kodi sindiwe mwamuna? Ndipo wofanana nawe ndani mu Israeli? Nʼchifukwa chiyani sunateteze mbuye wako mfumu? Munthu wina anabwera kumeneko.
And he said David to Abner ¿ not a man [are] you and who? [is] like you in Israel and why? not did you guard master your the king if he came one of the people to destroy the king master your.
16 Chimene wachita iwe si chabwino. Pali Yehova wamoyo iwe ndi asilikali ako muyenera kufa chifukwa simunateteze mbuye wanu, wodzozedwa wa Yehova. Tayangʼanayangʼana. Uli kuti mkondo wa mfumu ndi botolo lamadzi zimene zinali kumutu kwa mfumu?”
Not [is] good the thing this which you have done [by] [the] life of Yahweh for [are] sons of death you who not you watched over master your over [the] [one] anointed of Yahweh and now - see where? [is] [the] spear of the king and [the] jug of water which ([was the] place of head his. *Q(K)*)
17 Sauli anazindikira mawu a Davide ndipo anafunsa kuti, “Kodi amenewa ndi mawu ako Davide mwana wanga?” Davide anayankha, “Inde ndi anga, mbuye wanga mfumu.
And he recognized Saul [the] voice of David and he said ¿ voice your [is] this O son my David and he said David voice my O lord my the king.
18 Nʼchifukwa chiyani mbuye wanga mukundilonda ine mtumiki wanu? Kodi ine ndachita chiyani ndipo ndapezeka ndi cholakwa chotani?
And he said why? this [is] lord my pursuing after servant his for what? have I done and what? [is] in hand my evil.
19 Tsopano mbuye wanga mfumu tamverani mawu a mtumiki wanu. Ngati ndi Yehova wautsa mtima wanu kuti mundiwukire, ndiye alandire chipepeso. Koma ngati ndi anthu amene achita zimene, ndiye Yehova awatemberere popeza andipirikitsa lero kundichotsa mʼdziko la Yehova, namati, ‘Pita kapembedze milungu ina.’
And now let him hear please lord my the king [the] words of servant his if Yahweh he has incited you against me may he smell an offering and if - [the] sons of humankind [be] cursed they before Yahweh for they have driven out me this day from having a share in [the] inheritance of Yahweh saying go serve gods other.
20 Tsopano musalole kuti magazi anga akhetsedwe kutali ndi Yehova pakuti mfumu ya Israeli yatuluka kudzafunafuna ine nsabwe, monga mmene munthu asakira nkhwali ku mapiri.”
And now may not it fall blood my [the] ground towards from before [the] presence of Yahweh for he has come out [the] king of Israel to seek a flea one just as someone pursues the partridge in the mountains.
21 Ndipo Sauli anati, “Ine ndachimwa. Bwerera mwana wanga Davide. Sindidzakuchitanso choyipa popeza lero wauwona moyo wanga ngati wamtengowapatali. Taona, ndachita zauchitsiru ndipo ndachimwa kwambiri.”
And he said Saul I have sinned return O son my David for not I will do harm to you again because that it was precious life my in view your the day this here! I have behaved foolishly and I have gone astray greatly very.
22 Davide anayankha kuti, “Nawu mkondo wanu, mfumu. Tumani mmodzi wa anyamata anu abwere adzatenge.
And he answered David and he said here! ([the] spear of *Q(K)*) the king and let him pass over one from the young men and let him take it.
23 Yehova amadalitsa munthu aliyense wolungama ndi wokhulupirika. Yehova anakuperekani lero mʼmanja mwanga, koma ine sindinakhudze wodzozedwa wa Yehova.
And Yahweh he will return to everyone righteousness his and faithfulness his that he gave you Yahweh - this day in a hand and not I was willing to stretch out hand my on [the] [one] anointed of Yahweh.
24 Monga momwe ine lero ndachitira kuwuyesa moyo wanu ngati wamtengowapatali, momwemonso Yehova awuyese moyo wanga wamtengowapatali ndipo andipulumutse mʼmavuto anga onse.”
And here! just as it was great life your the day this in view my so may it be great life my in [the] eyes of Yahweh and may he deliver me from every trouble.
25 Ndipo Sauli anawuza Davide kuti, “Yehova akudalitse iwe Davide mwana wanga. Udzachita zinthu zazikulu ndipo udzapambana.” Choncho Davide anayenda njira yake ndipo Sauli anabwerera kwawo.
And he said Saul to David [be] blessed you O son my David both certainly you will do as well as certainly you will prevail and he went David to way his and Saul he returned to place his.

< 1 Samueli 26 >