< 1 Samueli 25 >

1 Samueli anamwalira, ndipo Aisraeli onse anasonkhana kudzalira maliro ake ndipo anamuyika mʼmanda ku mudzi kwawo ku Rama. Ndipo Davide anapita ku chipululu cha Parani.
Uto umrije Samuel. Sav se Izrael skupi i oplaka ga naričući za njim; i pokopaše ga u njegovu zavičaju u Rami. A David usta i siđe u pustinju Paran.
2 Kunali munthu wina wolemera kwambiri ku Maoni amene malo ake a ntchito anali ku Karimeli. Iyeyu anali ndi mbuzi 1,000 ndi nkhosa 3,000.
U Maonu živio čovjek koji je imao svoje gospodarstvo u Karmelu; bio je to vrlo bogat čovjek, imao je tri tisuće ovaca i tisuću koza. Upravo je tada strigao svoje ovce u Karmelu.
3 Dzina lake linali Nabala ndipo anali wa fuko la Kalebe. Dzina la mkazi wake linali Abigayeli. Anali mkazi wanzeru ndi wokongola, koma mwamuna wake, wa banja la Kalebe, anali wowuma mtima ndi wamwano pa zochita zake.
Taj se čovjek zvao Nabal, a njegova žena Abigajila. Žena je bila mudra i vrlo lijepa, a čovjek surov i opak: bio je Kalebovac.
4 Davide anamva akanali ku chipululu kuti Nabala akumeta nkhosa.
David je u pustinji čuo da Nabal striže svoje ovce.
5 Choncho anatuma anyamata khumi nawawuza kuti, “Pitani kwa Nabala ku Karimeli ndipo mukamulonjere mʼdzina langa.
Stoga posla deset momaka naloživši im: “Idite gore u Karmel, otiđite k Nabalu i pozdravite ga u moje ime.
6 Mukamuwuze kuti, ‘Mtendere ukhale ndi inu, banja lanu pamodzi ndi zonse zimene muli nazo.
I recite ovako mome bratu: 'Mir tebi, mir tvome domu, mir svemu što imaš!
7 “‘Tsono ndamva kuti muli ndi anthu ometa nkhosa. Pamene abusa anu anali nafe kuno, sitinawachite china chilichonse choyipa, ndipo sanasowe kanthu pa nthawi yonse imene anali ku Karimeli.
Sada, čujem, strižeš ovce. A tvoji su pastiri bili kod nas, nismo ih dirali, ništa im nije nestalo dokle god su bili u Karmelu.
8 Muwafunse antchito anu ndipo akuwuzani. Kotero akomereni mtima anyamata anga, pakuti tabwera pa nthawi yachikondwerero. Chonde apatseniko antchito anuwo ndi mwana wanu Davide chilichonse chimene mungakhale nacho.’”
Pitaj svoje sluge i kazat će ti. Zato neka ovi momci nađu milost pred tobom, jer smo došli u svečan dan. Podaj svojim slugama i svome sinu Davidu što ti se nađe pri ruci.'”
9 Anyamata a Davide aja atafika, anamuwuza Nabala zonse zimene Davide anayankhula. Ndipo anadikira yankho.
Dođoše momci Davidovi i ponoviše Nabalu u Davidovo ime sve ove riječi, a onda pričekaše.
10 Nabala anayankha anyamata a Davide kuti, “Kodi Davide ndi ndani? Mwana wa Yese ndi ndani? Masiku ano pali antchito ambiri amene akuthawa kwa mabwana awo.
Ali Nabal odgovori Davidovim slugama ovako: “Tko je David, tko je Jišajev sin? Danas ima mnogo slugu koji su pobjegli od svojih gospodara.
11 Nditengerenji buledi, madzi ndi nyama zimene ndaphera anthu anga ometa nkhosa ndi kuzipereka kwa anthu amene sindikudziwa kumene achokera?”
Zar da uzmem svoj kruh, svoju vodu, svoju stoku koju sam poklao za svoje strigače pa da to poklonim ljudima o kojima ne znam ni odakle su?”
12 Choncho anyamata a Davide aja anatembenuka nabwerera. Atafika anafotokozera Davide mawu onse a Nabala.
Davidovi se momci okrenuše i vratiše se svojim putem. Kad su se vratili, javiše sve ove riječi Davidu.
13 Davide anawuza anthu ake kuti, “Aliyense amangirire lupanga lake!” Choncho aliyense anamangirira lupanga lake. Davidenso anamangirira lupanga lake. Anthu pafupifupi 400 ndiwo anapita ndi Davide, pamene anthu 200 anatsala ndi katundu.
A David reče svojim ljudima: “Pripašite svaki svoj mač!” I pripasaše svaki svoj mač, i David pripasa svoj, i oko četiri stotine ljudi krenu za Davidom, dok ih dvije stotine osta kod tovara.
14 Tsono mmodzi mwa antchito anawuza Abigayeli mkazi wa Nabala kuti, “Davide anatumiza amithenga kuchokera ku chipululu kudzalonjera mbuye wathu, koma iye anawalalatira.
A ženi Nabalovoj, Abigajili, javio jedan od Nabalovih slugu ovo: “Eto, David je poslao iz pustinje glasnike da pozdrave našega gospodara, a on ih potjerao.
15 Komatu anthuwa anatichitira zabwino kwambiri. Sanatizunze, ndipo nthawi yonse imene tinali nawo ku busa sitinasowe kanthu.
A ti su ljudi bili vrlo dobri prema nama: nisu nas dirali, ništa nismo izgubili dokle god smo bili u njihovoj blizini kad smo bili u polju.
16 Ankatitchinjiriza ngati mpanda usiku ndi usana nthawi yonse tinkaweta nkhosa.
Noću i danju bili su nam kao bedem u sve vrijeme dok smo bili s njima pasući stada.
17 Tsono onani chimene mungachite, chifukwa zimenezi zingadzetse tsoka pa mbuye wathu pamodzi ndi nyumba yake. Paja mbuye athu aja ndi munthu wa khalidwe loyipa moti palibe amene angathe kuyankhula naye.”
Razmisli sada i vidi što ćeš učiniti, jer je gotova pogibija našem gospodaru i svemu njegovu domu; a on je opak čovjek komu se ne može ništa kazati.”
18 Ndipo Abigayeli sanataye nthawi. Iye anatenga malofu a buledi 200, matumba a chikopa awiri a vinyo, nkhosa zisanu zowotcheratu, makilogalamu 17 a tirigu wokazinga, makeke a mphesa zowuma 100, ndiponso makeke a nkhuyu 200, ndipo anazisenzetsa abulu.
Abigajila brzo uze dvije stotine hljebova, dva mijeha vina, pet zgotovljenih ovaca, pet mjera pržena žita, sto grozdova suhoga grožđa, dvije stotine smokovih kolača i sve to natovari na magarce.
19 Kenaka anawuza antchito ake kuti, “Tsogolani, ine ndikutsatirani.” Koma sanawuze mwamuna wake Nabala.
I zapovjedi svojim slugama: “Idite preda mnom, a ja ću za vama.” Svome mužu Nabalu nije kazala ništa.
20 Mayi uja atakwera pa bulu wake ndi kufika pa tsinde la phiri, anangoona Davide ndi ankhondo ake akubwera kunali iye. Choncho anakumana nawo.
Dok je, jašući na magarcu, silazila iza gorskog zavoja, David je sa svojim ljudima silazio nasuprot njoj, tako da se ona susrela s njima.
21 Nthawiyi nʼkuti Davide atanena kuti, “Kani ndinalondera pachabe katundu wa munthu uyu mʼchipululu muja! Ndipotu palibe kanthu nʼkamodzi komwe kake kamene kanasowa. Tsono wandibwezera zoyipa mʼmalo mwa zabwino.
A David je upravo mislio: “Uzalud sam, dakle, zaštićivao u pustinji sve što je taj čovjek imao i ništa mu nije nestalo od svega što je posjedovao! Sada mi vraća zlo za dobro!
22 Mulungu andilange kwambiri ngati pofika mmawa nditakhale nditasiyako ngakhale munthu mmodzi mwa onse amene ali nawo.”
Neka Bog učini Davidu ovo zlo i neka mu doda drugo ako Nabalu do zore od svega što ima ostavim i ono što mokri uza zid!”
23 Abigayeli ataona Davide, anatsika pa bulu wake mofulumira ndipo anadzigwetsa pansi pamaso pa Davide.
Kad je Abigajila ugledala Davida, brzo sjaha s magarca i pade pred Davida ničice, poklonivši se do zemlje.
24 Ali chigonere choncho pa mapazi a Davide anati, “Mbuye wanga, kulakwa kukhale pa ine ndekha. Chonde lolani kuti mdzakazi wanune ndiyankhule nanu, ndipo mumve mawu a ine mdzakazi wanu.
Bacivši mu se tako pred noge, reče: “Gospodaru, neka na mene padne krivica! Dopusti da službenica tvoja progovori tvojim ušima i udostoj se poslušati riječi službenice svoje!
25 Mbuye wanga musasamale za mwamuna wanga Nabala, munthu wa khalidwe loyipa. Iyeyu ali monga dzina lake liliri. Monga dzina lake litanthauza kuti chitsiru, ndiye kuti zake zonse ndi zauchitsiru basi. Koma ine mdzakazi wanu, sindinawaone anthu amene mbuye wanga munawatuma.
Neka moj gospodar ne gleda na toga opakog čovjeka, na Nabala, jer on s pravom nosi svoje ime: zove se Luda i ludost je s njim. A ja, službenica tvoja, nisam vidjela momaka koje je poslao moj gospodar.
26 Tsono mbuye wanga muli apa, ndikulumbira pali Yehova wamoyo amene wakuletsani kuti musakhetse magazi a munthu ndi kulipsira nokha, kuti adani anu amene afuna kukuchitani zoyipa adzakhale ngati Nabala.
Zato sada, gospodaru, živoga mi Jahve, i tako živ bio ti, i tako ti Jahve koji te očuvao da ne svališ na se krvnu krivicu i da ne pribaviš sebi pravdu svojom rukom: neka prođu kao Nabal tvoji neprijatelji i oni koji snuju zlo mome gospodaru!
27 Choncho, nazi mphatso zimene mdzakazi wanu ndabwera nazo kwa mbuye wanga kuti zipatsidwe kwa anyamata amene muli nawo.
A ovaj dar, što ga evo tvoja službenica nosi svome gospodaru, neka se dade momcima koji idu za mojim gospodarom na njegovim putovima.
28 Chonde khululukani zolakwa za ine mdzakazi wanu. Ndithu Yehova adzakhazikitsa banja la mbuye wanga mu ufumu, popeza mukumenya nkhondo ya Yehova. Choncho choyipa sichidzapezeka mwa inu masiku onse a moyo wanu.
Oprosti službenici svojoj njezinu krivnju! Zacijelo će Jahve osnovati trajan dom mome gospodaru, jer moj gospodar bije Jahvine bojeve i za svega tvoga života neće se naći zlo na tebi.
29 Ngati munthu wina akuwukirani ndi kukulondani, Yehova Mulungu wanu adzateteza moyo wa mbuye wanga monga mmene munthu asungira chuma mʼphukusi, koma moyo wa adani anu adzawutaya kutali monga momwe munthu amaponyera mwala ndi legeni.
Ako se tko digne da te progoni i da ti radi o glavi, neka život moga gospodara bude pohranjen u škrinji života kod Jahve, tvoga Boga, a život tvojih neprijatelja neka on baci kao iz praćke.
30 Yehova adzakuchitirani mbuye wanga zabwino zonse zimene anakulonjezani. Adzakuyikani kukhala wolamulira Aisraeli.
I kad Jahve učini mome gospodaru svako dobro koje ti je obećao i kad te odredi da budeš knezom nad Izraelom,
31 Zikadzatero, inu mbuye wanga simudzakhala ndi chikumbumtima choti munakhetsa magazi kapena kulipsira popanda chifukwa. Koma Yehova akadzakuchitirani zabwino zonsezi musadzandiyiwale ine mdzakazi wanu.”
onda neka ne bude na smutnju ni na grižnju savjesti mome gospodaru da je ni za što prolio krv i da je sebi pribavio pravdu svojoj rukom. I kad Jahve učini dobro mome gospodaru, sjeti se tada službenice svoje!”
32 Tsono Davide anawuza Abigayeli kuti, “Alemekezeke Yehova Mulungu wa Israeli, amene wakutuma iwe lero kuti ukumane nane.
David odgovori Abigajili: “Neka je blagoslovljen Jahve, Bog Izraelov, koji te danas poslao meni u susret!
33 Yehova akudalitseni chifukwa cha nzeru zanu pondiletsa lero kuti ndisakhetse magazi ndi kubwezera adani anga ndi manja anga.
Neka je blagoslovljena tvoja mudrost i blagoslovljena bila ti što si me danas zadržala da ne svalim na se krvnu krivicu i da ne pribavim sebi pravdu svojom rukom.
34 Kunena zoona, pali Yehova Wamoyo, Mulungu wa Israeli, amene wandiletsa kuti ndisakupwetekeni, mukanapanda kubwera msanga kudzakumana nane, palibe munthu aliyense wamwamuna wa Nabala akanasiyidwa wamoyo pakucha mmawa.”
Ali, tako mi živog Jahve, Boga Izraelova, koji nije dopustio da ti učinim zlo: da mi nisi tako brzo izišla u susret, zaista ne bi Nabalu do jutra ostalo ni ono što uza zid mokri!”
35 Ndipo Davide analandira kwa mayiyo zimene anamutengera ndipo anati, “Pitani kwanu mu mtendere. Ine ndamva mawu anu ndipo ndavomera zimene mwapempha.”
Nato David primi iz njezine ruke što mu bijaše donijela i reče joj: “Vrati se s mirom svojoj kući. Gle, uslišao sam tvoj glas i obazreo se na tebe.”
36 Abigayeli atabwerera kwa Nabala anamupeza ali mʼnyumba akuchita mphwando ngati la mfumu. Iye anali atakondwa kwambiri popeza anali ataledzera kwambiri. Choncho mkazi wakeyo sanamuwuze kalikonse mpaka mmawa kutacha.
Kad se Abigajila vratila k Nabalu, on je upravo imao gozbu u kući, pravu kraljevsku gozbu: Nabal bijaše veseo i sasvim pijan; zato mu ona ne reče ništa dok nije svanulo jutro.
37 Tsono mmawa, mowa utamuchoka Nabala, mkazi wake anamuwuza zonse. Pomwepo mtima wake unaleka kugunda ndipo unawuma gwaa ngati mwala.
A ujutro, kad se Nabal otrijeznio, pripovjedi mu njegova žena sve što se dogodilo, a njemu obamrije srce u grudima i on osta kao da se skamenio.
38 Patapita masiku khumi, Yehova anakantha Nabala ndipo anafa.
A desetak dana poslije toga Jahve udari Nabala te umrije.
39 Pamene Davide anamva kuti Nabala wamwalira, iye anati, “Alemekezeke Yehova, walipsira Nabala chipongwe chimene anandichita ndipo anandiletsa ine mtumiki wake kuti ndisachite choyipa. Yehova wabwezera pamutu pa Nabala choyipa chimene iye anachita.” Kenaka Davide anatumiza mawu kwa Abigayeli, kumupempha kuti akhale mkazi wake.
Kad David ču da je umro Nabal, reče: “Neka je blagoslovljen Jahve, koji mi je ispravio nepravdu što mi je učini Nabal; i Jahve je očuvao svoga slugu da ne učini zla, a svalio je Nabalovu zloću na njegovu glavu!” Potom David posla poruku Abigajili da će je uzeti za ženu.
40 Anyamata a Davide atafika ku Karimeli anawuza Abigayeli kuti, “Davide watituma kwa iwe kuti tikutenge ukhale mkazi wake.”
Davidove sluge dođoše k Abigajili u Karmel i rekoše joj: “David nas je poslao k tebi da te uzme sebi za ženu.”
41 Abigayeli anagwada nagunditsa nkhope yake pansi ndipo anati, “Ine mdzakazi wa mbuye wanga ndakonzeka kutumikira ngakhale kusambitsa mapazi a anyamata ake.”
A ona ustade, pokloni se do zemlje i reče: “Evo službenice tvoje koja je spremna da bude robinja i da pere noge slugama svoga gospodara!”
42 Motero Abigayeli ananyamuka mofulumira nakwera bulu wake. Tsono iye pamodzi ndi anamwali ake asanu amene ankamutumikira, anatsagana ndi amithenga a Davide aja ndipo anakakhala mkazi wake wa Davide.
Potom Abigajila brzo ustade i zajaha na magarca, a za njom pođe pet njezinih dvorkinja. Tako je otišla za Davidovim poslanicima i postala njegovom ženom.
43 Davide nʼkuti atakwatiranso Ahinoamu wa ku Yezireeli ndipo onse awiri anali akazi ake.
I Ahinoamom iz Jizreela bijaše se oženio David i obje mu bjehu žene.
44 Koma Sauli anali atakwatitsa Mikala, mkazi wa Davide kwa Paliti mwana wa Laisi wa ku Galimu.
Jer Šaul bijaše svoju kćer Mikalu, Davidovu ženu, dao Paltiju, sinu Lajiša iz Galima.

< 1 Samueli 25 >