< 1 Samueli 24 >
1 Sauli atabwera kuchokera kumene amathamangitsa Afilisti anamva kuti, “Davide ali mʼchipululu cha Eni Gedi.”
Pripetilo se je, ko se je Savel vrnil iz zasledovanja Filistejcev, da mu je bilo povedano, rekoč: »Glej, David je v divjini En Gedi.«
2 Tsono Sauli anatenga asilikali 3,000 odziwa kumenya bwino nkhondo kuchokera pakati pa Aisraeli onse ndipo anapita kukafunafuna Davide ndi anthu ake ku Matanthwe a Mbalale.
Potem je Savel vzel tri tisoč izbranih mož iz vsega Izraela in odšel, da poišče Davida in njegove ljudi na skalah divjih koz.
3 Iye anafika ku makola a nkhosa amene anali mʼmbali mwa njira. Kumeneko kunali phanga, ndipo Sauli analowa mʼphangamo kuti akadzithandize. Davide ndi anthu ake ankabisala mʼkati mwenimweni mwa phangalo.
Ob poti je prišel k stajam za ovce, kjer je bila votlina in Savel je šel noter, da pokrije svoja stopala. David in njegovi možje pa so ostajali ob straneh votline.
4 Tsono anthu a Davide anamuwuza kuti, “Tsiku lija lafika limene Yehova anakuwuzani kuti, ‘Ndidzapereka mdani wanu mʼmanja mwanu, ndi kumuchita chimene chidzakukomereni.’” Koma Davide anapita mwakachetechete ndi kukadula msonga ya mkanjo wa Sauli.
Davidovi možje so mu rekli: »Glej, dan, o katerem ti je rekel Gospod: ›Glej, tvojega sovražnika bom izročil v tvojo roko, da mu boš lahko storil, kakor se ti zdi dobro.‹« Potem je David vstal in na skrivnem odsekal krajec Savlovega svečanega oblačila.
5 Atachita izi, Davide anatsutsika mu mtima chifukwa anadula msonga ya mkanjo wa Sauli.
Pripetilo se je potem, da ga je Davidovo srce udarilo, ker je odsekal krajec Savlovega oblačila.
6 Tsono anawuza anthu ake kuti, “Yehova asalole kuti ndimuchite choyipa mbuye wanga, wodzozedwa wa Yehova. Ndisamupweteke pakuti ndi wodzozedwa wa Yehova.”
Svojim možem je rekel: » Gospod ne daj, da bi storil tako stvar svojemu gospodarju, Gospodovemu maziljencu, da iztegnem svojo roko zoper njega, ker je maziljen od Gospoda.«
7 Choncho Davide anabweza mitima ya anthu ake ndi mawu amenewa, ndipo sanawalole kuti aphe Sauli. Pambuyo pake Sauli anatuluka mʼphangamo ndipo anachoka.
Tako je David s temi besedami zadržal svoje služabnike in jim ni pustil, da vstanejo zoper Savla. Toda Savel je vstal iz votline in odšel na svojo pot.
8 Kenaka Davide anatuluka mʼphanga muja ndipo anayitana Sauli, “Mbuye wanga!” Sauli atayangʼana mʼmbuyo, Davide anawerama ndi kugunditsa nkhope yake pansi.
Potem je tudi David vstal in šel ven iz votline in zaklical za Savlom, rekoč: »Moj gospod kralj.« Ko je Savel pogledal za seboj, se je David sklonil s svojim obrazom k zemlji in se priklonil.
9 Anafunsa Sauli kuti, “Nʼchifukwa chiyani mumamvera mawu a anthu kuti, ‘Davide wakukonzerani chiwembu?’
David je rekel Savlu: »Zakaj poslušaš besede ljudi, govoreč: ›Glej, David išče tvoje zlo?‹
10 Lero lino inu mwadzionera nokha kuti Yehova anakuperekani mʼmanja mwanga mʼphanga muja. Ena anandiwuza kuti ndikupheni, koma ndakusiyani. Ndinati, ‘Sindidzapha mbuye wanga pakuti ndiye wodzozedwa wa Yehova.’
Glej, ta dan so tvoje oči videle, kako te je Gospod v votlini izročil v mojo roko. Nekateri so mi zaukazali, naj te usmrtim, toda moje oko ti je prizaneslo. Rekel sem: ›Ne bom iztegnil svoje roke zoper svojega gospoda, kajti on je Gospodov maziljenec.‹
11 Tsono abambo anga, onanitu kansalu ka mkanjo wanu kali mʼdzanja langali! Popeza kuti ndinatha kudula msonga ya mkanjo wanu koma osakuphani, pamenepo mudziwe kuti ine ndilibe maganizo woti ndikuchiteni choyipa kapena kukuwukirani. Sindinakulakwireni ngakhale kuti inu mukufuna moyo wanga kuti mundiphe.
Poleg tega, moj oče, glej, da, poglej krajec svojega svečanega oblačila v moji roki, kajti v tem, da sem odsekal krajec tvojega svečanega oblačila in te nisem usmrtil, vedi in vidi, da v moji roki ni niti zla niti prestopka in nisem grešil zoper tebe, vendar ti loviš mojo dušo, da jo vzameš.
12 Yehova aweruze pakati pa inu ndi ine, akulangeni chifukwa cha zoyipa zimene mukundichitazi, koma dzanja langa silidzakukhudzani.
Gospod sodi med menoj in teboj in Gospod naj me maščuje nad teboj, toda moja roka ne bo nad teboj.
13 Paja anthu akale anati, ‘Munthu woyipa, ntchito zakenso ndi zoyipa.’ Kotero dzanja langa silidzakukhudzani.
Kakor pravi pregovor starcev: ›Zlobnost izvira od zlobnih, ‹ toda moja roka ne bo nad teboj.
14 “Kodi mfumu ya Israeli yadzalondola yani. Inu mukuthamangitsa yani? Galu wakufa kodi? Nsabwe kodi?
Za kom je Izraelov kralj prišel ven? Za kom tečeš? Za mrtvim psom, za bolho.
15 Nʼchifukwa chake Yehova agamule, inde aweruze pakati pa inu ndi ine ndi kupeza wolakwa. Yehova anditeteze ndi kundipulumutsa mʼdzanja lanu.”
Gospod naj bo torej sodnik in sodi med menoj in teboj in gleda in zagovarja mojo pravdo in me osvobodi iz tvoje roke.«
16 Davide atatsiriza kuyankhula mawu awa, Sauli anafunsa kuti, “Kodi mawu amenewa ndi akodi mwana wanga Davide?” Sauli anayamba kulira mokweza.
Pripetilo se je, ko je David Savlu prenehal govoriti te besede, da je Savel rekel: » Ali je to tvoj glas, moj sin David?« Savel je povzdignil svoj glas in zajokal.
17 Anawuza Davide kuti, “Ndiwe wolungama kuposa ine. Iwe wandikomera mtima pamene ine ndakuchitira zoyipa.
Davidu je rekel: »Pravičnejši si kakor jaz, kajti nagradil si mi dobro, medtem ko sem ti jaz nagradil zlo.
18 Iweyo lero lino wandifotokozera zabwino zimene wandichitira. Yehova anandipereka mʼdzanja lako koma iwe sunandiphe.
Danes si pokazal, kako dobro si ravnal z menoj, ker ko me je Gospod izročil v tvojo roko, me nisi ubil.
19 Kodi munthu atapeza mdani wake angamulole kuti apite wosamuvulaza? Motero Yehova akuchitire iwe zabwino chifukwa cha zimene wandichitira lerozi.
Kajti če človek najde svojega sovražnika ali ga bo pustil sproščeno oditi? Zato [naj] te Gospod dobro nagradi za to, kar si mi ta dan storil.
20 Ona tsono, Ine ndikudziwa kuti udzakhala mfumu ndithu ndipo ufumu wa Israeli udzakhazikika mʼmanja mwako.
Sedaj glej, dobro vem, da boš zagotovo postal kralj in da bo Izraelovo kraljestvo utrjeno v tvoji roki.
21 Tsopano undilonjeze molumbira lero mʼdzina la Yehova kuti sudzapha zidzukulu zanga ine nditamwalira kapena kufuta dzina langa pa banja la makolo anga.”
Prisezi mi torej sedaj pri Gospodu, da ne boš iztrebil mojega semena za menoj in da ne boš uničil mojega imena iz hiše mojega očeta.«
22 Choncho Davide analumbira pamaso pa Sauli. Pambuyo pake Sauli anabwerera kwawo, koma Davide ndi anthu ake anapitanso ku phanga kuja.
David je prisegel Savlu. Savel je odšel domov, toda David in njegovi možje so se povzpeli na utrjen kraj.