< 1 Samueli 24 >

1 Sauli atabwera kuchokera kumene amathamangitsa Afilisti anamva kuti, “Davide ali mʼchipululu cha Eni Gedi.”
И бысть егда возвратися Саул вспять от иноплеменник, и возвестиша ему, глаголюще: се, Давид в пустыни Енгадстей.
2 Tsono Sauli anatenga asilikali 3,000 odziwa kumenya bwino nkhondo kuchokera pakati pa Aisraeli onse ndipo anapita kukafunafuna Davide ndi anthu ake ku Matanthwe a Mbalale.
И взя Саул с собою три тысящы мужей избранных от всего Израиля и иде искати Давида и мужей его прямо лицу саддеем:
3 Iye anafika ku makola a nkhosa amene anali mʼmbali mwa njira. Kumeneko kunali phanga, ndipo Sauli analowa mʼphangamo kuti akadzithandize. Davide ndi anthu ake ankabisala mʼkati mwenimweni mwa phangalo.
и прииде до стад пасомых на пути, и бе тамо вертеп: и Саул вниде испразднитися, Давид же и мужие его во внутренних вертепа седяху.
4 Tsono anthu a Davide anamuwuza kuti, “Tsiku lija lafika limene Yehova anakuwuzani kuti, ‘Ndidzapereka mdani wanu mʼmanja mwanu, ndi kumuchita chimene chidzakukomereni.’” Koma Davide anapita mwakachetechete ndi kukadula msonga ya mkanjo wa Sauli.
И реша мужие Давидовы к нему: се, день сей, о немже рече Господь тебе предати врага твоего в руце твои, и сотвориши ему якоже угодно пред очима твоима. И воста Давид, и отреза воскрилие одежды Саули отай.
5 Atachita izi, Davide anatsutsika mu mtima chifukwa anadula msonga ya mkanjo wa Sauli.
И бысть по сих, и вострепета Давиду сердце его, яко отреза воскрилие одежды Саули:
6 Tsono anawuza anthu ake kuti, “Yehova asalole kuti ndimuchite choyipa mbuye wanga, wodzozedwa wa Yehova. Ndisamupweteke pakuti ndi wodzozedwa wa Yehova.”
и рече Давид к мужем своим: никакоже ми от Господа, аще сотворю глагол сей господину моему христу Господню, еже нанести руку мою нань, яко христос Господень есть сей.
7 Choncho Davide anabweza mitima ya anthu ake ndi mawu amenewa, ndipo sanawalole kuti aphe Sauli. Pambuyo pake Sauli anatuluka mʼphangamo ndipo anachoka.
И увеща Давид мужы своя словесы и не даде им воставшым убити Саула. И воста Саул, и сниде на путь.
8 Kenaka Davide anatuluka mʼphanga muja ndipo anayitana Sauli, “Mbuye wanga!” Sauli atayangʼana mʼmbuyo, Davide anawerama ndi kugunditsa nkhope yake pansi.
И изыде Давид вслед его из вертепа: и возопи Давид вслед Саула, глаголя: господине царю. И озреся Саул вслед себе, и преклонися Давид лицем своим до земли, и поклонися ему.
9 Anafunsa Sauli kuti, “Nʼchifukwa chiyani mumamvera mawu a anthu kuti, ‘Davide wakukonzerani chiwembu?’
И рече Давид к Саулу: почто слушаеши словес людий глаголющих: се, Давид ищет души твоея?
10 Lero lino inu mwadzionera nokha kuti Yehova anakuperekani mʼmanja mwanga mʼphanga muja. Ena anandiwuza kuti ndikupheni, koma ndakusiyani. Ndinati, ‘Sindidzapha mbuye wanga pakuti ndiye wodzozedwa wa Yehova.’
Се, днесь видеста очи твои, яко предаде тя Господь днесь в руце мои в вертепе, и не восхотех убити тебе, и пощадех тя, и рех: не нанесу руки моея на господа моего, яко помазанник Господень сей есть:
11 Tsono abambo anga, onanitu kansalu ka mkanjo wanu kali mʼdzanja langali! Popeza kuti ndinatha kudula msonga ya mkanjo wanu koma osakuphani, pamenepo mudziwe kuti ine ndilibe maganizo woti ndikuchiteni choyipa kapena kukuwukirani. Sindinakulakwireni ngakhale kuti inu mukufuna moyo wanga kuti mundiphe.
и се, воскрилие одежды твоея в руце моей, аз отях воскрилие одежды твоея, и не убих тебе: и уразумей, и виждь днесь, яко несть злобы в руце моей, ниже нечестия и презорства, ниже согреших к тебе, а ты ищеши души моея изяти ю:
12 Yehova aweruze pakati pa inu ndi ine, akulangeni chifukwa cha zoyipa zimene mukundichitazi, koma dzanja langa silidzakukhudzani.
да судит Господь между мною и тобою, и да защитит мя Господь от тебе: рука же моя не будет на тя,
13 Paja anthu akale anati, ‘Munthu woyipa, ntchito zakenso ndi zoyipa.’ Kotero dzanja langa silidzakukhudzani.
якоже глаголется притча древняя: от беззаконник изыдет преступление: рука же моя не будет на тя:
14 “Kodi mfumu ya Israeli yadzalondola yani. Inu mukuthamangitsa yani? Galu wakufa kodi? Nsabwe kodi?
и ныне ты, царю Израилев, вслед кого исходиши? Кого ты гониши? Вслед ли пса умерша и вслед блохи единыя?
15 Nʼchifukwa chake Yehova agamule, inde aweruze pakati pa inu ndi ine ndi kupeza wolakwa. Yehova anditeteze ndi kundipulumutsa mʼdzanja lanu.”
Да будет Господь судия и отмститель между мною и тобою, да видит Господь и судит суд мой, и осудит мя от руки твоея.
16 Davide atatsiriza kuyankhula mawu awa, Sauli anafunsa kuti, “Kodi mawu amenewa ndi akodi mwana wanga Davide?” Sauli anayamba kulira mokweza.
И бысть, егда сконча Давид глаголы сия, глаголя к Саулу, и рече Саул: твой ли глас сей, чадо Давиде? И воздвиже Саул глас свой и восплакася.
17 Anawuza Davide kuti, “Ndiwe wolungama kuposa ine. Iwe wandikomera mtima pamene ine ndakuchitira zoyipa.
И рече Саул к Давиду: праведен еси ты паче мене, яко ты воздал ми еси благая, аз же тебе воздах злая:
18 Iweyo lero lino wandifotokozera zabwino zimene wandichitira. Yehova anandipereka mʼdzanja lako koma iwe sunandiphe.
и ты возвестил ми еси днесь, яже сотворил ми благая, яко заключи мя Господь в руки твоя днесь, и не убил мя еси:
19 Kodi munthu atapeza mdani wake angamulole kuti apite wosamuvulaza? Motero Yehova akuchitire iwe zabwino chifukwa cha zimene wandichitira lerozi.
и якоже аще кто обрел бы врага своего в печали, и отпустил бы его в путь благ, и Господь воздаст ему благая, якоже ты сотворил еси днесь:
20 Ona tsono, Ine ndikudziwa kuti udzakhala mfumu ndithu ndipo ufumu wa Israeli udzakhazikika mʼmanja mwako.
и ныне се, аз вем, яко царюя царствовати имаши, и стати имать в руце твоей царство Израилево:
21 Tsopano undilonjeze molumbira lero mʼdzina la Yehova kuti sudzapha zidzukulu zanga ine nditamwalira kapena kufuta dzina langa pa banja la makolo anga.”
и ныне кленися ми Господем, яко не искорениши семене моего по мне и не погубиши имене моего от дому отца моего.
22 Choncho Davide analumbira pamaso pa Sauli. Pambuyo pake Sauli anabwerera kwawo, koma Davide ndi anthu ake anapitanso ku phanga kuja.
И клятся Давид Саулу. И отиде Саул на место свое, Давид же и мужие его взыдоша в мессеру тесную.

< 1 Samueli 24 >