< 1 Samueli 24 >

1 Sauli atabwera kuchokera kumene amathamangitsa Afilisti anamva kuti, “Davide ali mʼchipululu cha Eni Gedi.”
And it came to pass when Saul returned from pursuing after the Philistines, that it was reported to him, saying, David [is] in the wilderness of Engaddi.
2 Tsono Sauli anatenga asilikali 3,000 odziwa kumenya bwino nkhondo kuchokera pakati pa Aisraeli onse ndipo anapita kukafunafuna Davide ndi anthu ake ku Matanthwe a Mbalale.
And he took with him three thousand men, chosen out of all Israel, and went to seek David and his men in front of Saddaeem.
3 Iye anafika ku makola a nkhosa amene anali mʼmbali mwa njira. Kumeneko kunali phanga, ndipo Sauli analowa mʼphangamo kuti akadzithandize. Davide ndi anthu ake ankabisala mʼkati mwenimweni mwa phangalo.
And he came to the flocks of sheep that were by the way, and there was a cave there; and Saul went in to make preparation, and David and his men were sitting in the inner part of the cave.
4 Tsono anthu a Davide anamuwuza kuti, “Tsiku lija lafika limene Yehova anakuwuzani kuti, ‘Ndidzapereka mdani wanu mʼmanja mwanu, ndi kumuchita chimene chidzakukomereni.’” Koma Davide anapita mwakachetechete ndi kukadula msonga ya mkanjo wa Sauli.
And the men of David said to him, Behold, this [is] the day of which the Lord spoke to thee, that he would deliver thine enemy into thy hands; and thou shalt do to him as [it is] good in thy sight. So David arose and cut off the skirt of Saul's garment secretly.
5 Atachita izi, Davide anatsutsika mu mtima chifukwa anadula msonga ya mkanjo wa Sauli.
And it came to pass after this that David's heart smote him, because he had cut off the skirt of his garment.
6 Tsono anawuza anthu ake kuti, “Yehova asalole kuti ndimuchite choyipa mbuye wanga, wodzozedwa wa Yehova. Ndisamupweteke pakuti ndi wodzozedwa wa Yehova.”
And David said to his men, The Lord forbid it me, that I should do this ting to my lord the anointed of the Lord, to lift my hand against him; for he is the anointed of the Lord.
7 Choncho Davide anabweza mitima ya anthu ake ndi mawu amenewa, ndipo sanawalole kuti aphe Sauli. Pambuyo pake Sauli anatuluka mʼphangamo ndipo anachoka.
So David persuaded his men by [his] words, and did not suffer them to arise and slay Saul: and Saul arose and went his way.
8 Kenaka Davide anatuluka mʼphanga muja ndipo anayitana Sauli, “Mbuye wanga!” Sauli atayangʼana mʼmbuyo, Davide anawerama ndi kugunditsa nkhope yake pansi.
And David rose up [and went] after him out of the cave: and David cried after Saul, saying, [My] lord, [O] king! and Saul looked behind him, and David bowed with his face to the ground, and did obeisance to him.
9 Anafunsa Sauli kuti, “Nʼchifukwa chiyani mumamvera mawu a anthu kuti, ‘Davide wakukonzerani chiwembu?’
And David said to Saul, Why dost thou hearken to the words of the people, saying, Behold, David seeks thy life?
10 Lero lino inu mwadzionera nokha kuti Yehova anakuperekani mʼmanja mwanga mʼphanga muja. Ena anandiwuza kuti ndikupheni, koma ndakusiyani. Ndinati, ‘Sindidzapha mbuye wanga pakuti ndiye wodzozedwa wa Yehova.’
Behold, thine eyes have seen this day how that the Lord has delivered thee this day into my hands in the cave; and I would not slay thee, but spared thee, and said, I will not lift up my hand against my lord, for he is the Lord's anointed.
11 Tsono abambo anga, onanitu kansalu ka mkanjo wanu kali mʼdzanja langali! Popeza kuti ndinatha kudula msonga ya mkanjo wanu koma osakuphani, pamenepo mudziwe kuti ine ndilibe maganizo woti ndikuchiteni choyipa kapena kukuwukirani. Sindinakulakwireni ngakhale kuti inu mukufuna moyo wanga kuti mundiphe.
And behold, the skirt of thy mantle [is] in my hand, I cut off the skirt, and did not slay thee: know then and see to-day, there is no evil in my hand, nor impiety, nor rebellion; and I have not sinned against thee, yet thou layest snares for my soul to take it.
12 Yehova aweruze pakati pa inu ndi ine, akulangeni chifukwa cha zoyipa zimene mukundichitazi, koma dzanja langa silidzakukhudzani.
The Lord judge between me and thee, and the Lord requite thee on thyself: but my hand shall not be upon thee.
13 Paja anthu akale anati, ‘Munthu woyipa, ntchito zakenso ndi zoyipa.’ Kotero dzanja langa silidzakukhudzani.
As the old proverb says, Transgression will proceed from the wicked ones: but my hand shall not be upon thee.
14 “Kodi mfumu ya Israeli yadzalondola yani. Inu mukuthamangitsa yani? Galu wakufa kodi? Nsabwe kodi?
And now after whom dost thou come forth, O king of Israel? After whom dost thou pursue? After a dead dog, and after a flea?
15 Nʼchifukwa chake Yehova agamule, inde aweruze pakati pa inu ndi ine ndi kupeza wolakwa. Yehova anditeteze ndi kundipulumutsa mʼdzanja lanu.”
The Lord be judge and umpire between me and thee, the Lord look upon and judge my cause, and rescue me out of thy hand.
16 Davide atatsiriza kuyankhula mawu awa, Sauli anafunsa kuti, “Kodi mawu amenewa ndi akodi mwana wanga Davide?” Sauli anayamba kulira mokweza.
And it came to pass when David had finished speaking these words to Saul, that Saul said, [Is] this thy voice, Son David? And Saul lifted up his voice, and wept.
17 Anawuza Davide kuti, “Ndiwe wolungama kuposa ine. Iwe wandikomera mtima pamene ine ndakuchitira zoyipa.
And Saul said to David, Thou [art] more righteous that I, for thou hast recompensed me good, but I have recompensed thee evil.
18 Iweyo lero lino wandifotokozera zabwino zimene wandichitira. Yehova anandipereka mʼdzanja lako koma iwe sunandiphe.
And thou hast told me to-day what good thou hast done me, how the Lord shut me up into thy hands to-day, and thou didst not slay me.
19 Kodi munthu atapeza mdani wake angamulole kuti apite wosamuvulaza? Motero Yehova akuchitire iwe zabwino chifukwa cha zimene wandichitira lerozi.
And if any one should find his enemy in distress, and should send him forth in a good way, then the Lord will reward him good, as thou has done this day.
20 Ona tsono, Ine ndikudziwa kuti udzakhala mfumu ndithu ndipo ufumu wa Israeli udzakhazikika mʼmanja mwako.
And now, behold, I know that thou shalt surely reign, and the kingdom of Israel shall be established in thy hand.
21 Tsopano undilonjeze molumbira lero mʼdzina la Yehova kuti sudzapha zidzukulu zanga ine nditamwalira kapena kufuta dzina langa pa banja la makolo anga.”
Now then swear to me by the Lord, that thou wilt not destroy my seed after me, that thou wilt not blot out my name from the house of my father.
22 Choncho Davide analumbira pamaso pa Sauli. Pambuyo pake Sauli anabwerera kwawo, koma Davide ndi anthu ake anapitanso ku phanga kuja.
So David swore to Saul: and Saul departed to his place, and David and his men went up to the strong-hold of Messera.

< 1 Samueli 24 >