< 1 Samueli 24 >
1 Sauli atabwera kuchokera kumene amathamangitsa Afilisti anamva kuti, “Davide ali mʼchipululu cha Eni Gedi.”
Kad se Šaul vratio iz potjere za Filistejcima, javiše mu ovo: “David je u Engadskoj pustinji!”
2 Tsono Sauli anatenga asilikali 3,000 odziwa kumenya bwino nkhondo kuchokera pakati pa Aisraeli onse ndipo anapita kukafunafuna Davide ndi anthu ake ku Matanthwe a Mbalale.
Tada Šaul uze tri tisuće odabranih ljudi iz svega Izraela i pođe da traži Davida i njegove ljude na istok od Litica divokoza.
3 Iye anafika ku makola a nkhosa amene anali mʼmbali mwa njira. Kumeneko kunali phanga, ndipo Sauli analowa mʼphangamo kuti akadzithandize. Davide ndi anthu ake ankabisala mʼkati mwenimweni mwa phangalo.
Idući dođe k ovčjim torovima pokraj puta; ondje bijaše pećina i Šaul uđe da čučne; a David je sa svojim ljudima sjedio u dnu pećine.
4 Tsono anthu a Davide anamuwuza kuti, “Tsiku lija lafika limene Yehova anakuwuzani kuti, ‘Ndidzapereka mdani wanu mʼmanja mwanu, ndi kumuchita chimene chidzakukomereni.’” Koma Davide anapita mwakachetechete ndi kukadula msonga ya mkanjo wa Sauli.
I rekoše Davidu ljudi njegovi: “Evo dana za koji ti je rekao Jahve: 'Ja ću predati tvoga neprijatelja u tvoje ruke, postupaj s njim kako ti se mili!'” A David ustade i neprimjetno odsiječe skut od Šaulova plašta.
5 Atachita izi, Davide anatsutsika mu mtima chifukwa anadula msonga ya mkanjo wa Sauli.
Ali poslije zapeče Davida savjest što je odsjekao skut od Šaulova plašta,
6 Tsono anawuza anthu ake kuti, “Yehova asalole kuti ndimuchite choyipa mbuye wanga, wodzozedwa wa Yehova. Ndisamupweteke pakuti ndi wodzozedwa wa Yehova.”
pa reče svojim ljudima: “Očuvao me Jahve da takvo što učinim svome gospodaru, da dignem ruku na njega, jer je pomazanik Jahvin.”
7 Choncho Davide anabweza mitima ya anthu ake ndi mawu amenewa, ndipo sanawalole kuti aphe Sauli. Pambuyo pake Sauli anatuluka mʼphangamo ndipo anachoka.
I David oštrim riječima ukori svoje ljude i ne dopusti im da ustanu na Šaula. A Šaul izađe iz pećine i pođe svojim putem.
8 Kenaka Davide anatuluka mʼphanga muja ndipo anayitana Sauli, “Mbuye wanga!” Sauli atayangʼana mʼmbuyo, Davide anawerama ndi kugunditsa nkhope yake pansi.
Zatim ustade David, iziđe iz pećine i vikne za Šaulom: “Gospodaru kralju!” A kad se Šaul obazre, David se baci ničice na zemlju i pokloni mu se.
9 Anafunsa Sauli kuti, “Nʼchifukwa chiyani mumamvera mawu a anthu kuti, ‘Davide wakukonzerani chiwembu?’
Tada David reče Šaulu: “Zašto slušaš ljude koji ti govore da David snuje tebi propast?
10 Lero lino inu mwadzionera nokha kuti Yehova anakuperekani mʼmanja mwanga mʼphanga muja. Ena anandiwuza kuti ndikupheni, koma ndakusiyani. Ndinati, ‘Sindidzapha mbuye wanga pakuti ndiye wodzozedwa wa Yehova.’
Gle, upravo u ovaj dan tvoje su oči mogle vidjeti da te Jahve predao danas u moje ruke u ovoj pećini. Rekoše mi da te ubijem, ali te poštedjeh i rekoh: 'Neću dići svoje ruke na svoga gospodara, jer je Jahvin pomazanik.'
11 Tsono abambo anga, onanitu kansalu ka mkanjo wanu kali mʼdzanja langali! Popeza kuti ndinatha kudula msonga ya mkanjo wanu koma osakuphani, pamenepo mudziwe kuti ine ndilibe maganizo woti ndikuchiteni choyipa kapena kukuwukirani. Sindinakulakwireni ngakhale kuti inu mukufuna moyo wanga kuti mundiphe.
O, moj oče, pogledaj i vidi skut od svoga plašta u mojoj ruci: odsjekao sam skut od tvoga plašta, a tebe nisam ubio; spoznaj i vidi da u mojoj ruci nema ni zlobe ni opačine. Ja nisam zgriješio protiv tebe, a ti vrebaš na moj život da mi ga uzmeš!
12 Yehova aweruze pakati pa inu ndi ine, akulangeni chifukwa cha zoyipa zimene mukundichitazi, koma dzanja langa silidzakukhudzani.
Jahve neka sudi između mene i tebe, Jahve neka me osveti na tebi, ali se moja ruka neće dići na tebe.
13 Paja anthu akale anati, ‘Munthu woyipa, ntchito zakenso ndi zoyipa.’ Kotero dzanja langa silidzakukhudzani.
Kako kaže stara poslovica: od nepravednika dolazi nepravda, i zato se moja ruka neće dići protiv tebe.
14 “Kodi mfumu ya Israeli yadzalondola yani. Inu mukuthamangitsa yani? Galu wakufa kodi? Nsabwe kodi?
Za kim je izišao izraelski kralj? Za kim ideš u potjeru? Za mrtvim psom, za običnom buhom!
15 Nʼchifukwa chake Yehova agamule, inde aweruze pakati pa inu ndi ine ndi kupeza wolakwa. Yehova anditeteze ndi kundipulumutsa mʼdzanja lanu.”
Jahve neka bude sudac, on neka sudi između mene i tebe, neka ispita i brani moju stvar i neka mi pribavi pravdu: neka me izbavi iz tvoje ruke!”
16 Davide atatsiriza kuyankhula mawu awa, Sauli anafunsa kuti, “Kodi mawu amenewa ndi akodi mwana wanga Davide?” Sauli anayamba kulira mokweza.
Kad je David izgovorio te riječi Šaulu, odvrati Šaul: “Je li to tvoj glas, sine Davide?” I Šaul glasno zaplaka.
17 Anawuza Davide kuti, “Ndiwe wolungama kuposa ine. Iwe wandikomera mtima pamene ine ndakuchitira zoyipa.
Zatim reče Davidu: “Pravedniji si od mene jer ti si meni učinio dobro, a ja sam tebi učinio zlo.
18 Iweyo lero lino wandifotokozera zabwino zimene wandichitira. Yehova anandipereka mʼdzanja lako koma iwe sunandiphe.
A danas si okrunio svoju dobrotu prema meni, jer me Jahve predao u tvoje ruke, a ti me nisi ubio.
19 Kodi munthu atapeza mdani wake angamulole kuti apite wosamuvulaza? Motero Yehova akuchitire iwe zabwino chifukwa cha zimene wandichitira lerozi.
Kad se čovjek namjeri na svoga neprijatelja, pušta li ga da ide mirno svojim putem? Neka ti Jahve naplati za ono dobro što si mi danas učinio!
20 Ona tsono, Ine ndikudziwa kuti udzakhala mfumu ndithu ndipo ufumu wa Israeli udzakhazikika mʼmanja mwako.
Sada pouzdano znam da ćeš zacijelo biti kralj i da će se kraljevstvo nad Izraelom trajno održati u tvojoj ruci.
21 Tsopano undilonjeze molumbira lero mʼdzina la Yehova kuti sudzapha zidzukulu zanga ine nditamwalira kapena kufuta dzina langa pa banja la makolo anga.”
Zato mi se sada zakuni Jahvom da nećeš zatrti moga potomstva poslije mene i da nećeš izbrisati moga imena iz moga očinskoga doma!”
22 Choncho Davide analumbira pamaso pa Sauli. Pambuyo pake Sauli anabwerera kwawo, koma Davide ndi anthu ake anapitanso ku phanga kuja.
David se zakle Šaulu, Šaul ode svojoj kući, a David se sa svojim ljudima vrati u gorska skloništa.