< 1 Samueli 21 >
1 Davide anapita ku Nobi kwa wansembe Ahimeleki. Ahimelekiyo ankanjenjemera pamene ankamuchingamira, ndipo anafunsa kuti, “Muli nokha chifukwa chiyani? Chifukwa chiyani mulibe wokuperekezani?”
Et David vint à Nob vers Achimélec, le sacrificateur; et Achimélec, tout effrayé, courut au-devant de David, et lui dit: D'où vient que tu es seul, et qu'il n'y a personne avec toi?
2 Davide anayankha Ahimeleki kuti, “Mfumu yandituma zinthu zina ndipo yandiwuza kuti, ‘Munthu aliyense asadziwe za zimene ndakutumazo.’ Kunena za anthu anga, ndawawuza kuti tikakumane pamalo pena pake.
Alors David dit à Achimélec, le sacrificateur: Le roi m'a donné un ordre, et m'a dit: Que personne ne sache rien de l'affaire pour laquelle je t'envoie, et que je t'ai commandée. Et j'ai donné rendez-vous à mes gens à tel endroit.
3 Kodi muli ndi chakudya? Patseniko malofu a buledi asanu, kapena chilichonse muli nacho.”
Maintenant donc qu'as-tu sous la main? Donne-moi cinq pains, ou ce qui se trouvera.
4 Koma wansembeyo anamuyankha Davide kuti, “Ine ndilibe buledi wamba woti ndikupatseni. Koma pali buledi wachipembedzo yekha. Ngati anthu amene muli nawo sanagone ndi akazi awo mukhoza kudya.”
Et le sacrificateur répondit à David, et dit: Je n'ai point de pain commun sous la main, j'ai seulement du pain sacré; mais tes gens se sont-ils au moins gardés des femmes?
5 Davide anayankha kuti, “Kunena zoona sitinakhudzane ndi mkazi monga timachitira nthawi zonse tikakhala pa ulendo. Anthu anga salola kudziyipitsa ndi mkazi ngakhale pa ulendo wamba. Nanji lero tili pa ulendo woterewu!”
Et David répondit au sacrificateur, et lui dit: Certes, les femmes ont été éloignées de nous, depuis hier et avant-hier que je suis parti; et les vases de mes gens sont purs; et si c'est là un usage profane, certes il sera, aujourd'hui, purifié par le vase.
6 Choncho wansembe uja anamupatsa buledi wachipembedzo popeza kunalibeko buledi wina aliyense koma yekhayo amene amaperekedwa kwa Yehova. Uyu ndi amene anachotsedwa tsiku limenelo kuti ayikepo wina wotentha.
Le sacrificateur lui donna donc le pain sacré; car il n'y avait point là d'autre pain que les pains de proposition, qui avaient été ôtés de devant l'Éternel, pour y remettre du pain chaud, au jour qu'on avait ôté l'autre.
7 Koma tsiku limenelo mmodzi wa antchito a Sauli anali pomwepo kudikirira kuti achite mwambo wa chipembedzo mʼnyumba ya Mulungu. Munthuyu dzina lake anali Doegi Mwedomu, munthu wamphamvu pakati pa abusa a Sauli.
Or, en ce jour, un homme d'entre les serviteurs de Saül se tenait là, devant l'Éternel; il se nommait Doëg, l'Iduméen, chef des bergers de Saül.
8 Davide anafunsa Ahimeleki kuti, “Kodi muli ndi mkondo kapena lupanga pano? Ine sindinatenge lupanga langa kapena chida china chilichonse chifukwa zimene andituma amfumu ndi zamsangamsanga.”
Et David dit à Achimélec: N'as-tu donc pas sous la main quelque lance ou quelque épée? car je n'ai point pris mon épée ni mes armes avec moi, parce que l'affaire du roi était pressée.
9 Wansembeyo anayankha kuti, “Kuno kuli lupanga la Goliati Mfilisiti uja amene unamupha mʼchigwa cha Ela, lakulungidwa mʼnsalu paseli pa Efodi. Ngati mufuna kulitenga, tengani popeza kuno kulibe lina koma lokhalo.” Davide anati, “Palibe lina lofanana nalo. Ndipatseni lomwelo.”
Et le sacrificateur dit: Voici l'épée de Goliath, le Philistin, que tu tuas dans la vallée du chêne; elle est enveloppée dans un drap, derrière l'éphod; si tu veux la prendre pour toi, prends-la; car il n'y en a point ici d'autre que celle-là. Et David dit: il n'y en a point de pareille; donne-la-moi.
10 Tsiku lomwelo Davide ananyamuka kuthawa Sauli ndipo anapita kwa Akisi, mfumu wa ku Gati.
Alors David se leva, et s'enfuit ce jour-là de devant Saül, et s'en alla vers Akish, roi de Gath.
11 Koma nduna za Akisi zinafunsa mfumuyo kuti, “Kodi uyu si Davide mfumu ya dzikoli? Kodi iyeyu si uja pomuvinira ankayimba kuti, “Sauli wapha 1,000, koma Davide wapha miyandamiyanda?”
Or les serviteurs d'Akish lui dirent: N'est-ce pas là David, le roi du pays? N'est-ce pas celui dont on disait, en chantant dans les danses: Saül a tué ses mille, et David ses dix mille?
12 Mawu amenewa anamulowa kwambiri Davide mu mtima ndipo anayamba kuopa kwambiri Akisi mfumu ya ku Gati.
Et David fut frappé de ces paroles, et il eut une fort grande peur d'Akish, roi de Gath.
13 Choncho anasintha makhalidwe ake pamaso pawo, nʼkudzisandutsa ngati wamisala. Iye ankangolembalemba pa zitseko za chipata ndi kumangotuluka dovi, nʼkumayenderera mʼndevu zake.
Et il dissimula sa raison à leurs yeux, et fit l'insensé entre leurs mains; il faisait des marques sur les portes, et laissait couler sa salive sur sa barbe.
14 Akisi anawuza nduna zake kuti, “Mukumuona munthu uyu kuti ndi wamisala! Nʼchifukwa chiyani mukubwera naye kwa ine?
Alors Akish dit à ses serviteurs: Vous voyez bien que cet homme est fou? Pourquoi me l'avez-vous amené?
15 Kodi ine ndikusowa anthu amisala kuti muzibwera naye munthuyu kwa ine kuti azidzachita zamisala zake pamaso panga? Kodi munthu ameneyu nʼkulowa mʼnyumba mwanga?”
Manquais-je de gens insensés, que vous m'ayez amené celui-ci, pour faire l'insensé devant moi? Cet homme entrerait-il dans ma maison?