< 1 Samueli 20 >
1 Tsono Davide anathawa ku Nayoti ku Rama ndi kupita kwa Yonatani ndipo anamufunsa kuti, “Kodi ine ndinachita chiyani? Kodi ndinalakwa chiyani? Kodi abambo ako ndinawalakwira chiyani kuti azifuna kundipha?”
David el kaingla liki acn Naioth in Ramah ac som nu yorol Jonathan. El siyuk sel Jonathan, “Ku mea nga oru? Ma koluk fuka nga orala? Ya oasr ma nga oru in lain papa tomom pwanang el suk elan uniyuwi?”
2 Yonatani anayankha kuti, “Sizitheka! Iwe sufa ayi! Taona abambo anga sachita chinthu chilichonse chachikulu kapena chachingʼono wosandiwuza ine. Tsopano abambo anga angandibisire bwanji zimenezi? Sichoncho ayi.”
Jonathan el topuk ac fahk, “Ac tia ouinge! Kom fah tia misa! Ma nukewa papa tumuk el oru el muta fahk nu sik, ma srisrik nu ke ma yohk, na pa el tia ku in okanla ma se inge likiyu. Tiana ku in ouinge!”
3 Koma Davide analumbira kuti, “Abambo ako akudziwa bwino lomwe kuti iwe umandikonda ndipo iwo amaganiza kuti, Yonatani sayenera kudziwa zimenezi mwina adzamva chisoni kwambiri. Komabe, pali Yehova ndi pali iwe, imfa sinanditalikire.”
Ac David el fahk, “Papa tomom el etu na lupan lungse lom nu sik, na pa el sulela elan tia fahk nu sum ma el akoo in oru inge, mweyen el etu lah kom ac arulana toasr kac. Nga fulahk nu sum ke Inen LEUM GOD moul lah kutu srisrik na ngan misa!”
4 Yonatani anawuza Davide kuti, “Chilichonse chimene iwe ukufuna kuti ndichite, ndidzakuchitira.”
Jonathan el fahk, “Kutena ma kom lungse nga in oru, nga ac oru.”
5 Ndipo Davide anati, “Taona mawa ndi tsiku la chikondwerero cha mwezi watsopano, ndipo ine ndiyenera kukadya ndi mfumu. Koma undilole ndipite ndikabisale mʼmunda mpaka mkuja madzulo.
Na David el fahk, “Kufwen Malem Sasu pa ac orek lutu, na ac fal nga in muta yurin tokosra ke pacl in mongo. Tusruktu fin wo sum, nga ac som wikla inimae nwe ke eku in ulela.
6 Ngati abambo ako akafunsa za ine, ukawawuze kuti, ‘Davide anandiwumiriza kuti ndimulole apite msanga kwawo ku Betelehemu, chifukwa akupereka nsembe yapachaka ya banja lonse.’
Papa tomom el fin akilen lah nga wangin ke tepu lal an, kom fah fahk nu sel mu nga tuh kwafe sum nga in sulaklak som nu acn sik uh Bethlehem, mweyen pa inge pacl se sou luk nufon elos orek kisa ke yac se inge.
7 Akanena kuti, ‘Wachita bwino,’ ndiye kuti zinthu zindiyendera bwino ine mtumiki wako. Koma ngati akapsa mtima, ndiye udziwe kuti iwo atsimikiza zondichita zoyipa.
Na el fin fahk mu ‘Wona,’ na wangin ma nga ac fosrnga kac. A el fin kasrkusrak, na kom fah etu na lah oasr ma upa el akoo in oru nu sik.
8 Koma undikomere mtima ine mtumiki wako, pakuti unapangana nane pangano pamaso pa Yehova. Ngati ndine wolakwa undiphe ndiwe, koma usandipereke kwa abambo ako.”
Nga siyuk kom in nunak munas ac sruokyana wulela mutal kom tuh oru inmasrlok kom. Tusruktu fin oasr mwetik, na kom sifacna uniyuwi. Mwe mea kom in usyula nu yurin papa tomom in tuh anwuki nga?”
9 Yonatani anati, “Sizitheka! Ndikanadziwa kuti abambo anga atsimikiza kuti akuchite choyipa, kodi sindikanakuwuza?”
Jonathan el fahk, “Nimet kom nunak ouingan! Nga funu etu na pwaye lah papa tumuk el akoo in oru ma upa nu sum, ya nga ku in tia fahk nu sum?”
10 Davide anafunsa kuti, “Adzandiwuza ndani ngati abambo ako akuyankhe mwaukali?”
Na David el siyuk, “Papa tomom el fin kasrkusrak topuk kom, na su ac fahkma nu sik?”
11 Yonatani anawuza Davide kuti, “Tiyeni tikayende ku mundako.” Ndipo anapita onse awiri.
Na Jonathan el fahk, “Fahsru kut som nu inimae.” Na eltal som,
12 Kenaka Yonatani anawuza Davide kuti, “Yehova Mulungu wa Israeli akhale mboni! Ine ndikadzafunsa abambo anga nthawi yonga ino mmawa kapena mkuja, ndipo ndikadzapeza kuti akukufunira zabwino, ine ndidzatuma mawu kuti udziwe.
ac Jonathan el fahk nu sel David, “Lela tuh LEUM GOD lun Israel Elan orek lou inmasrlosr. Ke pacl se inge lutu, oayapa ulela, nga fah kusen siyuk sin papa tumuk. Nunak lal fin wo keim, na nga a akkalemye nu sum.
13 Koma ngati abambo anga atsimikiza kukuchita choyipa, Yehova andilange ine Yonatani, ndipotu kwambiri ngati sindidzakudziwitsa ndi kukulola kuti upite mu mtendere. Yehova akhale nawe monga anakhalira ndi abambo anga.
Tuh el fin nunku in akkolukye kom, lela tuh LEUM GOD Elan uniyuwi nga fin tia akkalemye nu sum tuh kom in ku in kaingla. Lela LEUM GOD Elan wi kom oana ke El tuh welul papa tumuk ah.
14 Ndikakhalabe ndi moyo udzandionetse kukoma mtima monga kwa Yehova nthawi yonse ya moyo wanga, kuti ine ndisaphedwe.
Ac nga fin moul na, kom fah nunak munas sruokya wulela mutal lom nu sik, ac kom in pwayena nu sik. A nga fin misa,
15 Ndipo usadzaleke kuchitira chifundo banja langa. Pamene Yehova adzawatha adani onse a Davide pa dziko lapansi.”
na kom in akkalemye kulang lom nu sin sou luk nwe tok. Ac LEUM GOD El fin kunausla mwet lokoalok lom nukewa,
16 “Dzina la ine Yonatani lisadzafafanizidwe nawo pamodzi. Yehova alange adani onse a Davide.”
lela tuh wulela se inmasrloktal in tiana musalla. Fin musalla, LEUM GOD El ac fah kai kom.”
17 Kenaka Yonatani anamulumbiritsanso Davide kuti asaleke kumukonda, pakuti ankamukonda monga ankadzikondera yekha.
Na Jonathan el sifilpa sap David elan wulela mu el ac lungse na el, mweyen Jonathan el lungse na pwaye David oana ke el lungse el sifacna.
18 Kenaka Yonatani anawuzanso Davide kuti, “Mawa ndi tsiku la chikondwerero cha mwezi watsopano. Zidzadziwika kuti iwe palibe chifukwa mpando wako udzakhala wopanda munthu.
Ac Jonathan el fahk nu sel David, “Kalem lah kom fin wangin liki tepu in mongo lutu, ac fah akilenyuk, mweyen Kufwen Malem Sasu lutu.
19 Mkuja adzakufunafuna. Tsono udzapite pamalo pamene unabisala poyamba paja ndipo ukadikire pa mulu wa miyala uli apowo.
Ac ulela kom fin wangin pac, ac arulana akilenyuk lah kom wangin. Ke ma inge, wona kom in sifil som wikla acn se na ma kom tuh wikla we meet ah, tukun yol in eot sac.
20 Ine ndidzaponya mivi itatu pambali pake, ngati ndikulasa chinthu.
Na nga fah pusrkaot sukan pisr tolkwe nu ke yol in eot sac, in mu nga pisr in akoalel.
21 Ndipo ndidzatuma mnyamata ndi kuti, ‘Pita ukatole miviyo!’ Ngati ndidzanena kwa iye kuti, ‘Taona, mivi ili mbali yakuno, kayitole,’ iwe ukatuluke, pakuti ndikulumbira, pali Yehova Wamoyo, ndiye kuti zako zili bwino, palibe choopsa chilichonse.
Na nga ac supwaot sie mwet kulansap luk in fahsrot suk. Nga fin fahk nu sel, ‘Liye, sukan pisr uh oan layenu liki kom. Fahla use,’ kalmac pa ma nukewa wo, ac kom ku in ilme. Nga fulahk ke LEUM GOD moul lah wangin mwe fosrnga nu sum.
22 Koma ndikadzati, ‘Taona mivi ili patsogolo pako,’ iwe udzachoke chifukwa Yehova ndiye walola kuti uchokepo.
A nga fin fahk nu sin mwet kulansap luk mu, ‘Sukan pisr uh oan layeno liki kom,’ na kom fah kaing, mweyen LEUM GOD pa supwekom inge.
23 Tsono zimene tapanganazi Yehova ndiye mboni pakati pa iwe ndi ine mpaka muyaya.”
Ac nu ke wulela se kital orala inmasrloktal uh, LEUM GOD El ac fah oru tuh in oan ma pahtpat.”
24 Choncho Davide anakabisala mʼmunda ndipo nthawi ya chikondwerero cha mwezi watsopano itakwana mfumu Sauli anadzakhala pansi kuti adye.
Na David el som wikla inimae. Ke pacl in Kufwen Malem Sasu, Tokosra Saul el tuku nu ke tepu uh
25 Iye anakhala pa malo ake a nthawi zonse pafupi ndi khoma moyangʼanana ndi Yonatani, ndipo Abineri anakhala moyandikana ndi Sauli, koma pa malo a Davide panalibe munthu.
ac el muta ke nien muta lal sisken pesinka uh. Abner el muta siskal, ac Jonathan el muta ke la tepu uh ngetang nu yoroltal. Acn in muta lal David uh oalalla.
26 Sauli sananene chilichonse tsiku limenelo pakuti ankaganiza kuti “Chilipo chimene chachitika ndi Davide. Mwina mwake ngosayenera za chipembedzo.”
Wangin ma Saul el fahk kac ke len sac, mweyen el nunku mu sahp oasr sripa se sikyak ac David el tia nasnas fal nu ke alu lalos.
27 Koma pa tsiku lachiwiri la chikondwerero cha mwezi watsopano pamalo pa Davide panalibenso munthu. Kenaka Sauli anafunsa Yonatani kuti, “Nʼchifukwa chiyani mwana wa Yese sanabwere kudzadya, dzulo ngakhale lero?”
Ke len se akluo ah, len se tukun Kufwen Malem Sasu, nien muta lal David ke tepu uh srakna oalal, ac Saul el siyuk sel Jonathan, “Efu ku David el tia tuku nu ke tepu uh ekea, sifilpa misenge?”
28 Yonatani anayankha kuti, “Davide anandiwumiriza kuti ndimulole kuti apite ku Betelehemu.
Jonathan el topuk ac fahk, “El tuh kwafe sik ngan fuhlella elan som nu Bethlehem.
29 Anati, ‘Undilole ndipite, chifukwa banja lathu likupereka nsembe mu mzindamo ndipo mʼbale wanga wandiwumiriza kuti ndikakhale nawo. Ngati wandikomera mtima, chonde ndilole ndipite ndikaone abale anga.’ Nʼchifukwa chake sanabwere kudzadya ndi mfumu.”
El fahk ouinge nu sik, ‘Nunak munas filiyula ngan som, tuh sou luk elos orek kisa ke acn sesr uh, ac tamulel luk el sap nga in som welulos. Na pa kom fin mwet kawuk luk, filiyula nga in som nu yurin sou luk.’ Pa inge sripa se sis el wangin liki nien mutal lal ke tepu lun tokosra.”
30 Sauli anamupsera mtima Yonatani ndipo namuwuza kuti, “Iwe mwana wobadwa mwa mkazi wamakhalidwe oyipa ndi wowukira! Kodi ukuyesa kuti ine sindikudziwa kuti umagwirizana ndi mwana wa Yese, amene akufuna kukuchititsa manyazi iwe ndi amayi ako?
Saul el foloyak sel Jonathan ac fahk nu sel, “Kom wen nutin sie mutan likkeke ac seakos! Inge nga etu na lah kom welul David lac, ac kom sifacna akmwekinye kom ac nina kiom ah!
31 Mwana wa Yese akakhala ndi moyo pa dziko lapansi lino, iwe sudzakhala mfumu. Tsopano tumiza munthu akamutenge kubwera naye kwa ine, pakuti Davide ayenera kufa basi!”
Mea, kom nikin lah ke lusenna moul lal David, kom ac tia ku in tokosra fin facl se inge? Fahla ingena ac usalu. El enenu na elan misa!”
32 Yonatani anafunsa abambo ake kuti, “Nʼchifukwa chiyani mufuna kuti Davide aphedwe? Iye walakwa chiyani?”
Ac Jonathan el siyuk, “Ku efu ku elan misa? Mea el orala?”
33 Apo Sauli anamuponyera mkondo wake kuti amuphe. Tsono Yonatani anadziwa kuti abambo ake atsimikiza mtima kuti aphe Davide.
Na Saul el kipakin osra natul ah nu kacl Jonathan in unilya, ac Jonathan el fah kalem lah Saul el nunku na pwaye elan unilya David.
34 Yonatani anachoka pa tebulopo ali wopsa mtima kwambiri. Tsiku lachiwiri la chikondwererocho Yonatani sanadye chakudya. Iye anawawidwa mtima chifukwa abambo ake anatsimikiza zakupha Davide.
Ac Jonathan el kasrkusrak ac tuyak liki tepu ah, ac el tia mongo in len sac nufon — len se akluo ke Kufwen Malem Sasu. El arulana asor kacl David ke sripen Saul el fahk kas na upa kacl.
35 Tsono mmawa Yonatani anapita ku munda kumene anapangana ndi Davide. Anali ndi mnyamata wake.
Lotutang in len tok ah, Jonathan el som nu inimae in sonol David, in oana ma eltal tuh aetuila kac. El us tulik mukul fusr se welul,
36 Tsono anawuza mnyamatayo kuti, “Thamanga ukatole muvi umene nditi ndiponye.” Mnyamatayo akuthamanga Yonatani anaponya muvi patsogolo pa mnyamatayo.
na el fahk nu sel, “Yuwot ac suk sukan pisr nga ac pusrkaot inge.” Tulik sac kasrusr yula, ac Jonathan el pusrkala pisr soko ah alukela tulik sac.
37 Mnyamatayo atafika pamene muvi wa Yonatani unagwera,
Ke tulik sac sun acn se ma sukan pisr soko ah putati we ah, Jonathan el wowo nu sin tulik sac ac fahk, “Sukan pisr soko ah pa oemeeto!
38 Yonatani anayitananso mnyamatayo kuti, “Fulumira, pita msanga usayime.” Choncho mnyamatayo anatola muvi uja ndi kubwera nayo kwa mbuye wake.
Nimet tu na insacn! Sulaklak!” Tulik sac el srukak sukan pisr soko ah, ac el use nu yurin mwet kacto lal.
39 (Mnyamatayo sanadziwe chimene chimachitika koma Yonatani ndi Davide ndiwo ankadziwa).
Tulik sac tiana etu lah mea kalmen ma inge. Jonathan ac David mukena pa kalem kac uh.
40 Pambuyo pake Yonatani anapereka zida zake za nkhondo kwa mnyamatayo ndipo anati, “Pita, nyamula ubwerere nazo ku mzinda.”
Na Jonathan el sang kufwen mwe pisr natul nu sin tulik sac, ac sap elan us som nu in siti uh.
41 Mnyamatayo anapita. Kenaka Davide anatuluka ku mbali ina ya mulu wa miyala uja, nadzigwetsa pansi ndi kugunditsa nkhope yake pansi katatu. Anapsompsona nayamba kulira onse awiri, koma Davide analira kwambiri.
Tukun tulik sac som, David el tuyak liki yol in eot se el wikwik we, ac el sikukmutunte ac faksufi pacl tolu. Na el Jonathan tukeni tung ac angokmwet sie sin sie, ac asor lal David tuh yohk liki asor lal Jonathan.
42 Yonatani anawuza Davide kuti, “Pita mu mtendere pakuti ife awiri tinalumbira mʼdzina la Yehova kuti, ‘Yehova ndiye akhale mboni pakati pa iwe ndi ine ndiponso pakati pa zidzukulu zako ndi zidzukulu zanga kwa nthawi yonse.’” Kenaka Davide anachoka, ndipo Yonatani anabwerera ku mzinda kuja.
Ac Jonathan el fahk nu sel David, “God Elan wi kom. LEUM GOD El ac fah oru tuh kom ac fwil nutum, oayapa nga ac fwil nutik, in sruokyana wulela mutal se su nga kom orala inmasrloktal tuh in oan ma pahtpat.” Na David el som, ac Jonathan el folok nu in siti uh.