< 1 Samueli 2 >

1 Ndipo Hana anapemphera nati, “Moyo wanga ukukondwera mwa Yehova; Ndiyenda mwa tukumutukumu chifukwa cha Yehova. Pakamwa panga pakula ndi kuseka adani anga mowanyogodola. Ndikukondwa chifukwa mwandipulumutsa.
Hanna şöyle dua etti: “Yüreğim RAB'de bulduğum sevinçle coşuyor; Gücümü yükselten RAB'dir. Düşmanlarımın karşısında övünüyor, Kurtarışınla seviniyorum!
2 “Palibe wina woyera ngati Yehova, palibe wina koma inu nokha, palibe thanthwe lofanana ndi Mulungu wathu.
Kutsallıkta RAB'bin benzeri yok, Evet, senin gibisi yok, ya RAB! Tanrımız gibi dayanak yok.
3 “Musandiyankhulenso modzitama, pakamwa panu pasatuluke zonyada, pakuti Yehova ndi Mulungu wanzeru, ndipo ndiye amene amayesa ntchito za anthu onse.
Artık büyük konuşmayın, Ağzınızdan küstahça sözler çıkmasın. Çünkü RAB her şeyi bilen Tanrı'dır; O'dur davranışları tartan.
4 “Mauta a anthu ankhondo athyoka koma anthu ofowoka avala dzilimbe.
Güçlülerin yayları kırılır; Güçsüzlerse güçle donatılır.
5 Amene kale anali okhuta tsopano akukagula chakudya, koma iwo amene anali ndi njala sakumvanso njala. Amene anali wosabereka, wabereka ana aamuna asanu ndi awiri, koma iye wobereka ana ambiri watsala yekha.
Toklar yiyecek uğruna gündelikçi olur, Açlar doyurulur. Kısır kadın yedi çocuk doğururken, Çok çocuklu kadın kimsesiz kalır.
6 “Yehova amabweretsa imfa ndipo amaperekanso moyo, amatsitsira ku manda ndipo amawatulutsakonso. (Sheol h7585)
RAB öldürür de diriltir de, Ölüler diyarına indirir ve çıkarır. (Sheol h7585)
7 Yehova amasaukitsa ndipo amalemeretsa, amatsitsa ndipo amakweza.
O kimini yoksul, kimini varsıl kılar; Kimini alçaltır, kimini yükseltir.
8 Iye amakweza osauka kuwachotsa pa fumbi, ndipo amachotsa anthu osowa pa dzala. Iye amawakhazika pamodzi ndi ana a mafumu, amawapatsa mpando waulemu. “Pakuti nsanamira za dziko lapansi ndi za Yehova, anakhazika dziko lapansi pa nsanamirazo.
Düşkünü yerden kaldırır, Yoksulu çöplükten çıkarır; Soylularla oturtsun Ve kendilerine onur tahtını miras olarak bağışlasın diye. Çünkü yeryüzünün temelleri RAB'bindir, O dünyayı onların üzerine kurmuştur.
9 Iye adzateteza moyo wa anthu okhulupirika koma anthu oyipa adzawonongedwa mu mdima. “Pakuti munthu sapambana ndi mphamvu zake.
RAB sadık kullarının adımlarını korur, Ama kötüler karanlıkta susturulur. Çünkü güçle zafere ulaşamaz insan.
10 Yehova adzaphwanya omutsutsa. Adzawaopsa ndi bingu kuchokera kumwamba; Yehova adzaweruza mathero a dziko lapansi. “Koma adzapereka mphamvu kwa mfumu yake, adzakuza mphamvu za odzozedwa wake.”
RAB'be karşı gelenler paramparça olacak, RAB onlara karşı gökleri gürletecek, Bütün dünyayı yargılayacak, Kralını güçle donatacak, Meshettiği kralın gücünü yükseltecek.”
11 Tsono Elikana anapita ku mudzi kwawo ku Rama, koma mnyamatayo amatumikira Yehova pansi pa ulamuliro wa wansembe Eli.
Sonra Elkana Rama'ya, evine döndü. Küçük Samuel ise Kâhin Eli'nin gözetiminde RAB'bin hizmetinde kaldı.
12 Ana a Eli anali ana achabechabe pakuti samasamala za Yehova.
Eli'nin oğulları değersiz kişilerdi. RAB'bi ve kâhinlerin halkla ilgili kurallarını önemsemiyorlardı. Biri sunduğu kurbanın etini haşlarken, kâhinin hizmetkârı elinde üç dişli büyük bir çatalla gelir,
13 Ndipo chizolowezi cha ansembe pakati pa anthu chinali motere kuti pamene munthu aliyense ankapereka nsembe ndipo nyama ija ikuwira pa moto, mtumiki wa wansembe ankabwera ndi chifoloko cha mano atatu mʼdzanja lake.
14 Iye ankachipisa mu mʼphikamo, ndipo wansembeyo amatenga chilichonse chimene folokoyo yabaya. Umu ndi mmene ansembewo amachitira ndi Aisraeli onse amene amabwera ku Silo.
çatalı kap, tencere, tava ya da kazana daldırırdı. Çatalla çıkarılan her şey kâhin için ayırılırdı. Şilo'ya gelen İsrailliler'in hepsine böyle davranırlardı.
15 Ndipo ngakhale mafuta asanatenthedwe, mtumiki wansembe amabwera ndi kunena kwa munthu amene akupereka nsembeyo kuti, “Ndipatse nyama kuti ndiwotche, pakuti Yehova salandira nyama yophika koma yayiwisi.”
Üstelik kurbanın yağları yakılmadan önce, kâhinin hizmetkârı gelip kurban sunan adama, “Kâhine kızartmalık et ver. Senden haşlanmış et değil, çiğ et alacak” derdi.
16 Ngati munthuyo anena kuti, “Apseretu mafuta poyamba, ndipo kenaka mutenge mmene mufunira,” mtumikiyo amayankha kuti, “Ayi ndipatse tsopano lino. Ngati sutero, ine nditenga molanda.”
Kurban sunan, “Önce hayvanın yağları yakılmalı, sonra dilediğin kadar al” diyecek olsa, hizmetkâr, “Hayır, şimdi vereceksin, yoksa zorla alırım” diye karşılık verirdi.
17 Tchimo la ana a Eli linali lalikulu kwambiri pamaso pa Yehova pakuti iwo amanyoza nsembe za Yehova.
Gençlerin RAB'be karşı işledikleri günah çok büyüktü; çünkü RAB'be sunulan sunuları küçümsüyorlardı.
18 Koma Samueli amatumikira pamaso pa Yehova atavala efodi ya nsalu yofewa yosalala.
Bu arada genç Samuel, keten efod giymiş, RAB'bin önünde hizmet ediyordu.
19 Chaka chilichonse amayi ake ankamusokera kamkanjo ndi kukamupatsa akamapita ndi mwamuna wake kukapereka nsembe za pa chaka.
Yıllık kurbanı sunmak için annesi her yıl kocasıyla birlikte oraya gider, diktiği cüppeyi oğluna getirirdi.
20 Tsono Eli amadalitsa Elikana ndi mkazi wake ndi mawu akuti “Yehova akupatseni ana mwa mkazi uyu kulowa mʼmalo mwa amene anapempha ndi kumupereka kwa Yehova.”
Kâhin Eli de, Elkana ile karısına iyi dilekte bulunarak, “Dilediği ve RAB'be adadığı çocuğun yerine RAB sana bu kadından başka çocuklar versin” derdi. Bundan sonra evlerine dönerlerdi.
21 Ndipo Yehova anamukomera mtima Hana. Anakhala ndi pathupi ndi kubereka ana aamuna atatu ndi ana aakazi awiri. Ndipo Samueli ankakula pamaso pa Yehova.
RAB'bin lütfuna eren Hanna gebe kalıp üç erkek, iki kız daha doğurdu. Küçük Samuel ise RAB'bin hizmetinde büyüdü.
22 Tsono Eli anakalamba kwambiri. Iye ankamva zonse zimene ana ake aamuna ankachitira Aisraeli onse, ndiponso kuti ankagona ndi akazi pa chipata cha tenti ya msonkhano.
Eli artık çok yaşlanmıştı. Oğullarının İsrailliler'e bütün yaptıklarını, Buluşma Çadırı'nın girişinde görevli kadınlarla düşüp kalktıklarını duymuştu.
23 Choncho anawafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani mukuchita zinthu zotere? Ine ndikumva kuchokera kwa anthu onse za zoyipa zanuzo.
Onlara, “Neden böyle şeyler yapıyorsunuz?” dedi, “Yaptığınız kötülükleri herkesten işitiyorum.
24 Ayi, ana anga si mbiri yabwino imene ndikumva anthu a Mulungu akufalitsa.
Olmaz bu, oğullarım! RAB'bin halkı arasında yayıldığını duyduğum haber iyi değil.
25 Ngati munthu alakwira munthu mnzake, mwina Mulungu adzamupepesera, koma ngati munthu achimwira Yehova adzamupepesera ndani?” Koma ana ake sanamvere kudzudzula kwa abambo awo, pakuti chinali cholinga cha Yehova kuti awaphe.
İnsan insana karşı günah işlerse, Tanrı onun için aracılık eder. Ama RAB'be karşı günah işleyeni kim savunacak?” Ne var ki, onlar babalarının sözünü dinlemediler. Çünkü RAB onları öldürmek istiyordu.
26 Ndipo mnyamata Samueli anapitirira kukula mu msinkhu, ndipo ankapeza kuyanja pamaso pa Yehova ndi anthu.
Bu arada giderek büyüyen genç Samuel RAB'bin de halkın da beğenisini kazanmaktaydı.
27 Tsiku lina munthu wa Mulungu anabwera kwa Eli ndipo anamuwuza kuti, “Yehova akuti, ‘Kodi Ine sindinadziwulule ndekha kwa banja la kholo lako pamene iwo anali akapolo a Farao ku Igupto?
O sıralarda bir Tanrı adamı Eli'ye gelip şöyle dedi: “RAB diyor ki, ‘Atan ve soyu Mısır'da firavunun halkına kölelik ederken kendimi onlara açıkça göstermedim mi?
28 Ndipo ndinamusankha pakati pa mafuko a Israeli kuti akhale wansembe wanga ndi kuti azipita pa guwa langa la nsembe, kufukiza Lubani ndi kuvala efodi pamaso panga. Ndinapatsa banja la abambo ako gawo la nsembe zonse zopsereza zimene Aisraeli amapereka.
Sunağıma çıkması, buhur yakıp önümde efod giymesi için bütün İsrail oymakları arasından yalnız atanı kendime kâhin seçtim. Üstelik İsrailliler'in yakılan bütün sunularını da atanın soyuna verdim.
29 Nʼchifukwa chiyani ukunyoza nsembe ndi zopereka zanga zimene ndinalamula? Nʼchifukwa chiyani ukupereka ulemu kwa ana ako kuposa Ine podzinenepetsa nokha ndi zopereka zabwino kwambiri za nsembe zimene Aisraeli amapereka?’”
Öyleyse neden konutum için buyurduğum kurbanı ve sunuyu küçümsüyorsunuz? Halkım İsrail'in sunduğu bütün sunuların en iyi kısımlarıyla kendinizi semirterek neden oğullarını benden daha çok önemsiyorsun?’
30 “Paja Ine Yehova Mulungu wa Israeli ‘Ndinalonjeza kuti anthu a pa banja lako ndi a pa banja la abambo ako azidzanditumikira nthawi zonse.’ Koma tsopano ndikuti, ‘Zonsezi zithe!’ Tsopano anthu amene amandilemekeza Inenso ndidzawalemekeza koma iwo amene amandinyoza Ine ndidzawanyoza.
“Bu nedenle İsrail'in Tanrısı RAB şöyle diyor: ‘Gerçekten, ailen ve atanın soyu sonsuza dek bana hizmet edecekler demiştim.’ Ama şimdi RAB şöyle buyuruyor: ‘Bu benden uzak olsun! Beni onurlandıranı ben de onurlandırırım. Ama beni saymayan küçük düşürülecek.
31 Nthawi ikubwera imene ndidzachotsa anyamata ako ndi anyamata a pa banja la abambo ako, kotero kuti sipadzakhala munthu wokalamba pa banja lako.
Soyundan hiç kimsenin yaşlanacak kadar yaşamaması için senin ve atanın soyunun gücünü kıracağım günler yaklaşıyor.
32 Pa mavuto ako udzayangʼana ndi maso ansanje zabwino zimene ndidzachitira Aisraeli ena. Mʼbanja lako simudzapezeka munthu wokalamba.
İsrail'e yapılacak bütün iyiliğe karşın, sen konutumda sıkıntı göreceksin. Artık soyundan hiç kimse yaşlanacak kadar yaşamayacak.
33 Komabe pa banja lako mmodzi yekha ndidzamuleka wosamuchotsa kuti azidzanditumikira. Iyeyu azidzakuliritsa ndi kukumvetsa chisoni. Koma ena onse pa banja lako adzafa akanali aangʼono.”
Sunağımdan bütün soyunu yok edeceğim, yalnız bir kişiyi esirgeyeceğim. Gözleri ağlamaktan kör olacak, yüreği yanacak. Ama soyundan gelenlerin hepsi kılıçla ölecekler.
34 “‘Ndipo chimene chidzachitike kwa ana ako awiriwa, Hofini ndi Finehasi, chidzakhala chizindikiro kwa iwe. Onse awiri adzafa pa tsiku limodzi.
İki oğlun Hofni ile Pinehas'ın başına gelecek olay senin için bir belirti olacak: İkisi de aynı gün ölecek.
35 Pambuyo pake ndidzasankha wansembe wokhulupirika, amene adzachita zimene zili mu mtima ndi mʼmaganizo mwanga. Ndidzakhazikitsa banja lako kolimba ndipo adzatumikira pamaso pa wodzozedwa wanga nthawi zonse.
İsteklerimi ve amaçlarımı yerine getirecek güvenilir bir kâhin çıkaracağım kendime. Onun soyunu sürdüreceğim; o da meshettiğim kişinin önünde sürekli hizmet edecek.
36 Ndipo aliyense wotsala wa banja lako adzabwera ndi kugwada pamaso pake kupempha ndalama kapena chakudya.’ Adzati, ‘Chonde ndiloleni kuti ndizithandizako pa ntchito iliyonse ya unsembe kuti ndipeze chakudya.’”
Ailenden sağ kalan herkes bir parça gümüş ve bir somun ekmek için gelip ona boyun eğecek ve, Ne olur, karın tokluğuna beni herhangi bir kâhinlik görevine ata! diye yalvaracak.’”

< 1 Samueli 2 >