< 1 Samueli 2 >

1 Ndipo Hana anapemphera nati, “Moyo wanga ukukondwera mwa Yehova; Ndiyenda mwa tukumutukumu chifukwa cha Yehova. Pakamwa panga pakula ndi kuseka adani anga mowanyogodola. Ndikukondwa chifukwa mwandipulumutsa.
Och Hanna bad, och sade: Mitt hjerta fröjdar sig i Herranom; mitt horn är upphöjdt i Herranom; min mun hafver vidt öppnat sig öfver mina fiendar; ty jag fröjdar mig af dine salighet.
2 “Palibe wina woyera ngati Yehova, palibe wina koma inu nokha, palibe thanthwe lofanana ndi Mulungu wathu.
Ingen är helig såsom Herren. Utan dig är ingen; och ingen tröst är såsom vår Gud.
3 “Musandiyankhulenso modzitama, pakamwa panu pasatuluke zonyada, pakuti Yehova ndi Mulungu wanzeru, ndipo ndiye amene amayesa ntchito za anthu onse.
Låter af att berömma eder och tala stor ord. Låter det gamla utur edar mun: ty Herren är en Gud, som vet det, och låter icke sådana anslag hafva framgång.
4 “Mauta a anthu ankhondo athyoka koma anthu ofowoka avala dzilimbe.
De starkas båge är sönderbruten, och de svage äro omgjordade med starkhet.
5 Amene kale anali okhuta tsopano akukagula chakudya, koma iwo amene anali ndi njala sakumvanso njala. Amene anali wosabereka, wabereka ana aamuna asanu ndi awiri, koma iye wobereka ana ambiri watsala yekha.
De som mätte voro, de vordo sålde för bröd; och de som hunger ledo, hungra intet mer; tilldess den ofruktsamma födde sju, och den som mång barn hade, vardt försvagad.
6 “Yehova amabweretsa imfa ndipo amaperekanso moyo, amatsitsira ku manda ndipo amawatulutsakonso. (Sheol h7585)
Herren dödar, och gifver lif; förer till helvete, och derut igen. (Sheol h7585)
7 Yehova amasaukitsa ndipo amalemeretsa, amatsitsa ndipo amakweza.
Herren gör fattigan; han gör ock rikan han förnedrar och upphöjer.
8 Iye amakweza osauka kuwachotsa pa fumbi, ndipo amachotsa anthu osowa pa dzala. Iye amawakhazika pamodzi ndi ana a mafumu, amawapatsa mpando waulemu. “Pakuti nsanamira za dziko lapansi ndi za Yehova, anakhazika dziko lapansi pa nsanamirazo.
Han uppreser den torftiga utu stoftet, och upphäfver den fattiga utu träcken, att han skall sätta honom ibland Förstar, och låtan ärfva ärones stol; ty verldenes ändar äro Herrans, och jordenes krets hafver han satt deruppå.
9 Iye adzateteza moyo wa anthu okhulupirika koma anthu oyipa adzawonongedwa mu mdima. “Pakuti munthu sapambana ndi mphamvu zake.
Han varder bevarandes sina heligas fötter; men de ogudaktige skola vara tyste i mörkrena; ty ingen förmår något af sin egen kraft.
10 Yehova adzaphwanya omutsutsa. Adzawaopsa ndi bingu kuchokera kumwamba; Yehova adzaweruza mathero a dziko lapansi. “Koma adzapereka mphamvu kwa mfumu yake, adzakuza mphamvu za odzozedwa wake.”
För Herranom skola förskräckas hans fiender; öfver dem skall han dundra i himmelen. Herren skall döma verldenes ändar, och skall gifva sinom Konung magt, och upphöja sins Smordas horn.
11 Tsono Elikana anapita ku mudzi kwawo ku Rama, koma mnyamatayo amatumikira Yehova pansi pa ulamuliro wa wansembe Eli.
Och ElKana gick hem igen till Hamath uti sitt hus, och pilten var Herrans tjenare inför Presten Eli.
12 Ana a Eli anali ana achabechabe pakuti samasamala za Yehova.
Men Eli söner voro Belials barn, och visste intet af Herranom;
13 Ndipo chizolowezi cha ansembe pakati pa anthu chinali motere kuti pamene munthu aliyense ankapereka nsembe ndipo nyama ija ikuwira pa moto, mtumiki wa wansembe ankabwera ndi chifoloko cha mano atatu mʼdzanja lake.
Ej heller hvad deras Prestaämbete var till folket. Då någor ville något offra, så kom Prestens dräng, medan köttet kokades, och hade en treuddad gaffel i sine hand:
14 Iye ankachipisa mu mʼphikamo, ndipo wansembeyo amatenga chilichonse chimene folokoyo yabaya. Umu ndi mmene ansembewo amachitira ndi Aisraeli onse amene amabwera ku Silo.
Och stack i grytona eller kettilen, eller pannona, eller krukona, och hvad han drog ut med gaffelen, det tog Presten till sig. Så gjorde de allom Israel, som ditkommo till Silo.
15 Ndipo ngakhale mafuta asanatenthedwe, mtumiki wansembe amabwera ndi kunena kwa munthu amene akupereka nsembeyo kuti, “Ndipatse nyama kuti ndiwotche, pakuti Yehova salandira nyama yophika koma yayiwisi.”
Sammalunda, förra än de uppbrände det feta, kom Prestens dräng, och sade till honom, som offret frambar: Få mig kött, att jag må steka det åt Prestenom; ty han vill icke taga kokadt kött af dig, utan rått.
16 Ngati munthuyo anena kuti, “Apseretu mafuta poyamba, ndipo kenaka mutenge mmene mufunira,” mtumikiyo amayankha kuti, “Ayi ndipatse tsopano lino. Ngati sutero, ine nditenga molanda.”
När då någor sade till honom: Låt upptända det feta såsom det bör sig i dag, och tag sedan hvad ditt hjerta begärar, så sade han till honom: Du skall nu gifva mig det, eljest skall jag taga det med våld.
17 Tchimo la ana a Eli linali lalikulu kwambiri pamaso pa Yehova pakuti iwo amanyoza nsembe za Yehova.
Derföre var piltarnas synd ganska stor för Herranom; förty folket förhädde Herrans spisoffer.
18 Koma Samueli amatumikira pamaso pa Yehova atavala efodi ya nsalu yofewa yosalala.
Men Samuel var en tjenare för Herranom, en dräng i en linnen lifkjortel.
19 Chaka chilichonse amayi ake ankamusokera kamkanjo ndi kukamupatsa akamapita ndi mwamuna wake kukapereka nsembe za pa chaka.
Dertill gjorde hans moder honom en liten kjortel, och förde den upp till honom i sinom tid, då hon uppgick med sin man, till att offra offer i sinom tid.
20 Tsono Eli amadalitsa Elikana ndi mkazi wake ndi mawu akuti “Yehova akupatseni ana mwa mkazi uyu kulowa mʼmalo mwa amene anapempha ndi kumupereka kwa Yehova.”
Och Eli välsignade ElKana och hans hustru, och sade: Herren gifve dig säd utaf denna qvinnone för den bön, som du hafver bedit af Herranom. Och de gingo hem till sitt igen.
21 Ndipo Yehova anamukomera mtima Hana. Anakhala ndi pathupi ndi kubereka ana aamuna atatu ndi ana aakazi awiri. Ndipo Samueli ankakula pamaso pa Yehova.
Och Herren sökte Hanna, att hon blef hafvandes, och födde tre söner och två döttrar; men pilten Samuel växte till för Herranom.
22 Tsono Eli anakalamba kwambiri. Iye ankamva zonse zimene ana ake aamuna ankachitira Aisraeli onse, ndiponso kuti ankagona ndi akazi pa chipata cha tenti ya msonkhano.
Men Eli var ganska gammal, och han förnam hvad hans söner gjorde allom Israel; och att de sofvo när de qvinnor, som tjente inför dörrene af vittnesbördsens tabernakel.
23 Choncho anawafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani mukuchita zinthu zotere? Ine ndikumva kuchokera kwa anthu onse za zoyipa zanuzo.
Och han sade till dem: Hvi gören I sådant? Ty jag hörer edart onda väsende af allt detta folket.
24 Ayi, ana anga si mbiri yabwino imene ndikumva anthu a Mulungu akufalitsa.
Icke så, mina barn, det är icke godt rykte, som jag hörer; I kommen Herrans folk till att synda.
25 Ngati munthu alakwira munthu mnzake, mwina Mulungu adzamupepesera, koma ngati munthu achimwira Yehova adzamupepesera ndani?” Koma ana ake sanamvere kudzudzula kwa abambo awo, pakuti chinali cholinga cha Yehova kuti awaphe.
Om någor syndar emot en mennisko, så kunna domarena förlika det; men om någor syndar emot Herran, ho kan förlikat? Och de hörde intet sins faders röst; ty Herren ville döda dem.
26 Ndipo mnyamata Samueli anapitirira kukula mu msinkhu, ndipo ankapeza kuyanja pamaso pa Yehova ndi anthu.
Men pilten Samuel växte till, och var både Herranom och menniskom täcker.
27 Tsiku lina munthu wa Mulungu anabwera kwa Eli ndipo anamuwuza kuti, “Yehova akuti, ‘Kodi Ine sindinadziwulule ndekha kwa banja la kholo lako pamene iwo anali akapolo a Farao ku Igupto?
Och en Guds man kom till Eli, och sade till honom: Så säger Herren: Jag hafver uppenbarat mig dins faders huse, då de ännu voro uti Egypten i Pharaos hus;
28 Ndipo ndinamusankha pakati pa mafuko a Israeli kuti akhale wansembe wanga ndi kuti azipita pa guwa langa la nsembe, kufukiza Lubani ndi kuvala efodi pamaso panga. Ndinapatsa banja la abambo ako gawo la nsembe zonse zopsereza zimene Aisraeli amapereka.
Och utvalde honom der mig, för all Israels slägter till Presterskap, att han skulle offra på mitt altare, och upptända rökverk, och bära lifkjortel för mig: och gaf dins faders huse all Israels barnas offer.
29 Nʼchifukwa chiyani ukunyoza nsembe ndi zopereka zanga zimene ndinalamula? Nʼchifukwa chiyani ukupereka ulemu kwa ana ako kuposa Ine podzinenepetsa nokha ndi zopereka zabwino kwambiri za nsembe zimene Aisraeli amapereka?’”
Hvi spjernar du då emot mitt offer och spisoffer, som jag budit hafver i tabernaklet, och du ärar dina söner mer än mig, så att I göden eder utaf allt mitt folks Israels spisoffers förstling?
30 “Paja Ine Yehova Mulungu wa Israeli ‘Ndinalonjeza kuti anthu a pa banja lako ndi a pa banja la abambo ako azidzanditumikira nthawi zonse.’ Koma tsopano ndikuti, ‘Zonsezi zithe!’ Tsopano anthu amene amandilemekeza Inenso ndidzawalemekeza koma iwo amene amandinyoza Ine ndidzawanyoza.
Derföre säger Herren Israels Gud: Jag hafver sagt, att ditt hus och dins faders hus skulle vandra för mig evinnerliga. Men nu säger Herren: Det vare långt ifrå mig; utan den mig ärar, honom vill jag ock ära: men den mig föraktar, han skall komma på skam.
31 Nthawi ikubwera imene ndidzachotsa anyamata ako ndi anyamata a pa banja la abambo ako, kotero kuti sipadzakhala munthu wokalamba pa banja lako.
Si, den tid skall komma, att jag skall bryta din arm sönder, och dins faders hus arm, så att ingen gammal skall vara i dino huse.
32 Pa mavuto ako udzayangʼana ndi maso ansanje zabwino zimene ndidzachitira Aisraeli ena. Mʼbanja lako simudzapezeka munthu wokalamba.
Och du skall se din motståndare uti tabernaklet i allo Israels godo; och ingen gammal skall vara i dins faders hus evinnerliga.
33 Komabe pa banja lako mmodzi yekha ndidzamuleka wosamuchotsa kuti azidzanditumikira. Iyeyu azidzakuliritsa ndi kukumvetsa chisoni. Koma ena onse pa banja lako adzafa akanali aangʼono.”
Dock vill jag icke utrota af dig allan man ifrå mitt altare, på det din ögon skola försmäkta, och din själ gräma sig; och hela hopen i dino huse skola dö, då de till manna komne äro.
34 “‘Ndipo chimene chidzachitike kwa ana ako awiriwa, Hofini ndi Finehasi, chidzakhala chizindikiro kwa iwe. Onse awiri adzafa pa tsiku limodzi.
Och detta skall vara dig ett tecken, som båda dina söner Hophni och Pinehas öfvergå skall: På en dag skola de både dö.
35 Pambuyo pake ndidzasankha wansembe wokhulupirika, amene adzachita zimene zili mu mtima ndi mʼmaganizo mwanga. Ndidzakhazikitsa banja lako kolimba ndipo adzatumikira pamaso pa wodzozedwa wanga nthawi zonse.
Och jag skall uppväcka mig en trogen Prest, och han skall göra såsom det i mino hjerta och mine själ är; honom skall jag bygga ett säkert hus, så att han skall vandra inför minom Smorda i alla dagar.
36 Ndipo aliyense wotsala wa banja lako adzabwera ndi kugwada pamaso pake kupempha ndalama kapena chakudya.’ Adzati, ‘Chonde ndiloleni kuti ndizithandizako pa ntchito iliyonse ya unsembe kuti ndipeze chakudya.’”
Och den qvar blifver af ditt hus, han skall komma och falla neder för honom, om en silfpenning och ett stycke bröd, och skall säga: Käre, låt mig komma till en Prestadel, att jag må äta en beta bröd.

< 1 Samueli 2 >