< 1 Samueli 2 >
1 Ndipo Hana anapemphera nati, “Moyo wanga ukukondwera mwa Yehova; Ndiyenda mwa tukumutukumu chifukwa cha Yehova. Pakamwa panga pakula ndi kuseka adani anga mowanyogodola. Ndikukondwa chifukwa mwandipulumutsa.
И Ана се помоли и рече: Развесели се срце моје у Господу; подиже се рог мој у Господу; отворише се уста моја на непријатеље моје, јер сам радосна ради спасења Твог.
2 “Palibe wina woyera ngati Yehova, palibe wina koma inu nokha, palibe thanthwe lofanana ndi Mulungu wathu.
Нема светог као што је Господ; јер нема другог осим Тебе; и нема стене као што је Бог наш.
3 “Musandiyankhulenso modzitama, pakamwa panu pasatuluke zonyada, pakuti Yehova ndi Mulungu wanzeru, ndipo ndiye amene amayesa ntchito za anthu onse.
Не говорите више поносито, и нека не излазе из уста ваших речи охоле; јер је Господ Бог који све зна, и Он удешава намере.
4 “Mauta a anthu ankhondo athyoka koma anthu ofowoka avala dzilimbe.
Лук јунацима сломи се, и изнемогли опасаше се снагом.
5 Amene kale anali okhuta tsopano akukagula chakudya, koma iwo amene anali ndi njala sakumvanso njala. Amene anali wosabereka, wabereka ana aamuna asanu ndi awiri, koma iye wobereka ana ambiri watsala yekha.
Који беху сити, наимају се за хлеб; а који беху гладни, нису више; и нероткиња роди седморо, а која имаше деце, изнеможе.
6 “Yehova amabweretsa imfa ndipo amaperekanso moyo, amatsitsira ku manda ndipo amawatulutsakonso. (Sheol )
Господ убија, и оживљује; спушта у гроб, и извлачи. (Sheol )
7 Yehova amasaukitsa ndipo amalemeretsa, amatsitsa ndipo amakweza.
Господ сиромаши и богати; понижује и узвишује.
8 Iye amakweza osauka kuwachotsa pa fumbi, ndipo amachotsa anthu osowa pa dzala. Iye amawakhazika pamodzi ndi ana a mafumu, amawapatsa mpando waulemu. “Pakuti nsanamira za dziko lapansi ndi za Yehova, anakhazika dziko lapansi pa nsanamirazo.
Сиромаха подиже из праха, и из буњишта узвишује убогог да га посади с кнезовима, и даје им да наследе престо славе; јер су Господњи темељи земаљски, и на њима је основао васиљену.
9 Iye adzateteza moyo wa anthu okhulupirika koma anthu oyipa adzawonongedwa mu mdima. “Pakuti munthu sapambana ndi mphamvu zake.
Сачуваће ноге милих својих, а безбожници ће умукнути у мраку; јер својом снагом неће човек надјачати.
10 Yehova adzaphwanya omutsutsa. Adzawaopsa ndi bingu kuchokera kumwamba; Yehova adzaweruza mathero a dziko lapansi. “Koma adzapereka mphamvu kwa mfumu yake, adzakuza mphamvu za odzozedwa wake.”
Који се супроте Господу, сатрће се; на њих ће загрмети с неба; Господ ће судити крајевима земаљским, и даће снагу цару свом, и узвисиће рог помазанику свом.
11 Tsono Elikana anapita ku mudzi kwawo ku Rama, koma mnyamatayo amatumikira Yehova pansi pa ulamuliro wa wansembe Eli.
Потом отиде Елкана у Рамат кући својој, а дете служаше Господу пред Илијем свештеником.
12 Ana a Eli anali ana achabechabe pakuti samasamala za Yehova.
А синови Илијеви беху неваљали, и не знаху за Господа.
13 Ndipo chizolowezi cha ansembe pakati pa anthu chinali motere kuti pamene munthu aliyense ankapereka nsembe ndipo nyama ija ikuwira pa moto, mtumiki wa wansembe ankabwera ndi chifoloko cha mano atatu mʼdzanja lake.
Јер у тих свештеника беше обичај према народу: кад ко приношаше жртву, долажаше момак свештеников док се куваше месо с виљушкама трокраким у руци,
14 Iye ankachipisa mu mʼphikamo, ndipo wansembeyo amatenga chilichonse chimene folokoyo yabaya. Umu ndi mmene ansembewo amachitira ndi Aisraeli onse amene amabwera ku Silo.
И забадаше у суд, или у котао, или у таву, или у лонац, и шта се год набоде на виљушке узимаше свештеник. Тако чињаху свему Израиљу који долажаше у Силом.
15 Ndipo ngakhale mafuta asanatenthedwe, mtumiki wansembe amabwera ndi kunena kwa munthu amene akupereka nsembeyo kuti, “Ndipatse nyama kuti ndiwotche, pakuti Yehova salandira nyama yophika koma yayiwisi.”
Тако и пре него би запалили сало, дошао би момак свештеников, те би рекао човеку који приношаше жртву: Дај месо да испечем свештенику, јер ти нећу примити месо кувано, него сирово.
16 Ngati munthuyo anena kuti, “Apseretu mafuta poyamba, ndipo kenaka mutenge mmene mufunira,” mtumikiyo amayankha kuti, “Ayi ndipatse tsopano lino. Ngati sutero, ine nditenga molanda.”
Ако би му тада човек одговорио: Нека се прво запали сало, па онда узми шта ти год душа жели; он би рекао: Не, него дај сада, ако ли не даш, узећу силом.
17 Tchimo la ana a Eli linali lalikulu kwambiri pamaso pa Yehova pakuti iwo amanyoza nsembe za Yehova.
И грех оних младића беше врло велик пред Господом, јер људи не мараху за принос Господњи.
18 Koma Samueli amatumikira pamaso pa Yehova atavala efodi ya nsalu yofewa yosalala.
А Самуило служаше пред Господом, још дете у оплећку ланеном.
19 Chaka chilichonse amayi ake ankamusokera kamkanjo ndi kukamupatsa akamapita ndi mwamuna wake kukapereka nsembe za pa chaka.
А мати му начини мали плашт и донесе му, и тако чињаше сваке године долазећи с мужем својим да принесе жртву годишњу.
20 Tsono Eli amadalitsa Elikana ndi mkazi wake ndi mawu akuti “Yehova akupatseni ana mwa mkazi uyu kulowa mʼmalo mwa amene anapempha ndi kumupereka kwa Yehova.”
А Илије благослови Елкану и жену његову говорећи: Господ да ти да порода од те жене за овог ког је дала Господу! И отидоше у своје место.
21 Ndipo Yehova anamukomera mtima Hana. Anakhala ndi pathupi ndi kubereka ana aamuna atatu ndi ana aakazi awiri. Ndipo Samueli ankakula pamaso pa Yehova.
И Господ походи Ану, и она затрудне и роди три сина и две кћери. А дете Самуило растијаше пред Господом.
22 Tsono Eli anakalamba kwambiri. Iye ankamva zonse zimene ana ake aamuna ankachitira Aisraeli onse, ndiponso kuti ankagona ndi akazi pa chipata cha tenti ya msonkhano.
А Илије беше врло стар, и чу све што чињаху синови његови свему Израиљу, и како спаваху са женама које долажаху гомилама на врата шатора од састанка.
23 Choncho anawafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani mukuchita zinthu zotere? Ine ndikumva kuchokera kwa anthu onse za zoyipa zanuzo.
И говораше им: Зашто то радите? Јер чујем зле речи о вама од свега народа.
24 Ayi, ana anga si mbiri yabwino imene ndikumva anthu a Mulungu akufalitsa.
Немојте, децо моја; јер није добро шта чујем; отпађујете народ Господњи.
25 Ngati munthu alakwira munthu mnzake, mwina Mulungu adzamupepesera, koma ngati munthu achimwira Yehova adzamupepesera ndani?” Koma ana ake sanamvere kudzudzula kwa abambo awo, pakuti chinali cholinga cha Yehova kuti awaphe.
Кад човек згреши човеку, судиће му судија; али кад ко згреши Господу, ко ће молити за њ? Али не послушаше оца свог, јер Господ хтеде да их убије.
26 Ndipo mnyamata Samueli anapitirira kukula mu msinkhu, ndipo ankapeza kuyanja pamaso pa Yehova ndi anthu.
А дете Самуило растијаше и беше мио Господу и људима.
27 Tsiku lina munthu wa Mulungu anabwera kwa Eli ndipo anamuwuza kuti, “Yehova akuti, ‘Kodi Ine sindinadziwulule ndekha kwa banja la kholo lako pamene iwo anali akapolo a Farao ku Igupto?
Тада дође човек Божји к Илију, и рече му: Овако вели Господ: Не јавих ли се дому оца твог, кад беху у Мисиру у кући Фараоновој?
28 Ndipo ndinamusankha pakati pa mafuko a Israeli kuti akhale wansembe wanga ndi kuti azipita pa guwa langa la nsembe, kufukiza Lubani ndi kuvala efodi pamaso panga. Ndinapatsa banja la abambo ako gawo la nsembe zonse zopsereza zimene Aisraeli amapereka.
И изабрах га између свих племена Израиљевих себи за свештеника да приноси жртве на олтару мом и да кади кадом и носи оплећак преда мном, и дадох дому оца твог све жртве огњене синова Израиљевих?
29 Nʼchifukwa chiyani ukunyoza nsembe ndi zopereka zanga zimene ndinalamula? Nʼchifukwa chiyani ukupereka ulemu kwa ana ako kuposa Ine podzinenepetsa nokha ndi zopereka zabwino kwambiri za nsembe zimene Aisraeli amapereka?’”
Зашто газите жртву моју и принос мој, које сам заповедио да се приносе у шатору? И пазиш синове своје већма него мене, да се гојите првинама свих приноса Израиља, народа мог?
30 “Paja Ine Yehova Mulungu wa Israeli ‘Ndinalonjeza kuti anthu a pa banja lako ndi a pa banja la abambo ako azidzanditumikira nthawi zonse.’ Koma tsopano ndikuti, ‘Zonsezi zithe!’ Tsopano anthu amene amandilemekeza Inenso ndidzawalemekeza koma iwo amene amandinyoza Ine ndidzawanyoza.
Зато Господ Бог Израиљев каже: Рекао сам доиста: Дом твој и дом оца твог служиће преда мном до века; али каже Господ: Неће бити тако, јер оне ћу поштовати који мене поштују, а који мене презиру, биће презрени.
31 Nthawi ikubwera imene ndidzachotsa anyamata ako ndi anyamata a pa banja la abambo ako, kotero kuti sipadzakhala munthu wokalamba pa banja lako.
Гле, иду дани кад ћу одсећи теби руку и руку дому оца твог, да не буде старца у дому твом.
32 Pa mavuto ako udzayangʼana ndi maso ansanje zabwino zimene ndidzachitira Aisraeli ena. Mʼbanja lako simudzapezeka munthu wokalamba.
И видећеш невољу у шатору место свега добра што је Господ чинио Израиљу; неће бити старца у дому твом довека.
33 Komabe pa banja lako mmodzi yekha ndidzamuleka wosamuchotsa kuti azidzanditumikira. Iyeyu azidzakuliritsa ndi kukumvetsa chisoni. Koma ena onse pa banja lako adzafa akanali aangʼono.”
А кога од твојих не истребим испред олтара свог, онај ће остати да ти чиле очи и да ти се цвели душа; и сав подмладак дома твог умираће у најбољим годинама.
34 “‘Ndipo chimene chidzachitike kwa ana ako awiriwa, Hofini ndi Finehasi, chidzakhala chizindikiro kwa iwe. Onse awiri adzafa pa tsiku limodzi.
И ово да ти је знак шта ће доћи на оба сина твоја, на Офнија и Финеса: у један дан погинуће обојица.
35 Pambuyo pake ndidzasankha wansembe wokhulupirika, amene adzachita zimene zili mu mtima ndi mʼmaganizo mwanga. Ndidzakhazikitsa banja lako kolimba ndipo adzatumikira pamaso pa wodzozedwa wanga nthawi zonse.
А себи ћу подигнути свештеника верног, он ће радити по срцу мом и по души мојој; и сазидаћу му тврд дом, и он ће ходити пред помазаником мојим вазда.
36 Ndipo aliyense wotsala wa banja lako adzabwera ndi kugwada pamaso pake kupempha ndalama kapena chakudya.’ Adzati, ‘Chonde ndiloleni kuti ndizithandizako pa ntchito iliyonse ya unsembe kuti ndipeze chakudya.’”
И ко остане од дома твог, доћи ће да му се поклони за сребрн новац и за комад хлеба, и говориће: Прими ме у какву службу свештеничку да имам комад хлеба.