< 1 Samueli 2 >

1 Ndipo Hana anapemphera nati, “Moyo wanga ukukondwera mwa Yehova; Ndiyenda mwa tukumutukumu chifukwa cha Yehova. Pakamwa panga pakula ndi kuseka adani anga mowanyogodola. Ndikukondwa chifukwa mwandipulumutsa.
Og Hanna bad og sa: Mitt hjerte fryder sig i Herren, høit er mitt horn i Herren, vidt oplatt min munn mot mine fiender, for jeg gleder mig over din frelse.
2 “Palibe wina woyera ngati Yehova, palibe wina koma inu nokha, palibe thanthwe lofanana ndi Mulungu wathu.
Ingen er hellig som Herren; for det er ingen foruten dig, og det er ingen klippe som vår Gud.
3 “Musandiyankhulenso modzitama, pakamwa panu pasatuluke zonyada, pakuti Yehova ndi Mulungu wanzeru, ndipo ndiye amene amayesa ntchito za anthu onse.
Tal ikke så mange høie ord, la ikke frekke ord gå ut av eders munn! For en allvitende Gud er Herren, og av ham veies gjerninger.
4 “Mauta a anthu ankhondo athyoka koma anthu ofowoka avala dzilimbe.
Kjempenes bue brytes, og de snublende omgjorder sig med kraft.
5 Amene kale anali okhuta tsopano akukagula chakudya, koma iwo amene anali ndi njala sakumvanso njala. Amene anali wosabereka, wabereka ana aamuna asanu ndi awiri, koma iye wobereka ana ambiri watsala yekha.
De mette lar sig leie for brød, og de hungrige hører op å hungre; endog den ufruktbare føder syv barn, og den som er rik på sønner, visner bort.
6 “Yehova amabweretsa imfa ndipo amaperekanso moyo, amatsitsira ku manda ndipo amawatulutsakonso. (Sheol h7585)
Herren døder og gjør levende; han fører ned i dødsriket og fører op derfra. (Sheol h7585)
7 Yehova amasaukitsa ndipo amalemeretsa, amatsitsa ndipo amakweza.
Herren gjør fattig og gjør rik; han nedtrykker, og han ophøier;
8 Iye amakweza osauka kuwachotsa pa fumbi, ndipo amachotsa anthu osowa pa dzala. Iye amawakhazika pamodzi ndi ana a mafumu, amawapatsa mpando waulemu. “Pakuti nsanamira za dziko lapansi ndi za Yehova, anakhazika dziko lapansi pa nsanamirazo.
han reiser den ringe av støvet, løfter den fattige av skarnet for å sette ham hos fyrster og gi ham et ærefullt sete; for Herren hører jordens støtter til, og på dem har han bygget jorderike.
9 Iye adzateteza moyo wa anthu okhulupirika koma anthu oyipa adzawonongedwa mu mdima. “Pakuti munthu sapambana ndi mphamvu zake.
Han verner sine frommes føtter, men ugudelige går til grunne i mørket; for ikke ved egen kraft er mannen sterk.
10 Yehova adzaphwanya omutsutsa. Adzawaopsa ndi bingu kuchokera kumwamba; Yehova adzaweruza mathero a dziko lapansi. “Koma adzapereka mphamvu kwa mfumu yake, adzakuza mphamvu za odzozedwa wake.”
Forferdes skal hver den som strider mot Herren; over ham lar han det tordne i himmelen. Herren dømmer jordens ender, og han vil gi sin konge styrke og ophøie sin salvedes horn.
11 Tsono Elikana anapita ku mudzi kwawo ku Rama, koma mnyamatayo amatumikira Yehova pansi pa ulamuliro wa wansembe Eli.
Så drog Elkana hjem igjen til Rama, men gutten tjente Herren under Elis, prestens, tilsyn.
12 Ana a Eli anali ana achabechabe pakuti samasamala za Yehova.
Men Elis sønner var ryggesløse; de brydde sig ikke om Herren.
13 Ndipo chizolowezi cha ansembe pakati pa anthu chinali motere kuti pamene munthu aliyense ankapereka nsembe ndipo nyama ija ikuwira pa moto, mtumiki wa wansembe ankabwera ndi chifoloko cha mano atatu mʼdzanja lake.
Sådan var prestenes adferd mot folket: Så ofte nogen kom med et offer, og kjøttet blev kokt, kom prestens dreng og hadde en gaffel med tre grener i sin hånd;
14 Iye ankachipisa mu mʼphikamo, ndipo wansembeyo amatenga chilichonse chimene folokoyo yabaya. Umu ndi mmene ansembewo amachitira ndi Aisraeli onse amene amabwera ku Silo.
den stakk han ned i kjelen eller i gryten eller i pannen eller i potten, og alt det som kom op med gaffelen, tok presten til sig. Således gjorde de med alle israelitter som kom der til Silo.
15 Ndipo ngakhale mafuta asanatenthedwe, mtumiki wansembe amabwera ndi kunena kwa munthu amene akupereka nsembeyo kuti, “Ndipatse nyama kuti ndiwotche, pakuti Yehova salandira nyama yophika koma yayiwisi.”
Endog før de brente fettet, kom prestens dreng og sa til den mann som ofret: Kom hit med kjøtt til å steke for presten! Han tar ikke imot kokt kjøtt av dig, bare rått.
16 Ngati munthuyo anena kuti, “Apseretu mafuta poyamba, ndipo kenaka mutenge mmene mufunira,” mtumikiyo amayankha kuti, “Ayi ndipatse tsopano lino. Ngati sutero, ine nditenga molanda.”
Så sa mannen til ham: Først må fettet brennes; siden kan du ta for dig efter som du har lyst til. Da svarte han: Nei, nu straks skal du komme med det; ellers tar jeg det med makt.
17 Tchimo la ana a Eli linali lalikulu kwambiri pamaso pa Yehova pakuti iwo amanyoza nsembe za Yehova.
Og de unge menns synd var meget stor for Herrens åsyn; for mennene ringeaktet Herrens offer.
18 Koma Samueli amatumikira pamaso pa Yehova atavala efodi ya nsalu yofewa yosalala.
Men Samuel tjente for Herrens åsyn - en ung gutt klædd i en livkjortel av lerret.
19 Chaka chilichonse amayi ake ankamusokera kamkanjo ndi kukamupatsa akamapita ndi mwamuna wake kukapereka nsembe za pa chaka.
Og hans mor gjorde hvert år en liten kappe til ham; den hadde hun med til ham, når hun drog op med sin mann for å bære frem det årlige offer.
20 Tsono Eli amadalitsa Elikana ndi mkazi wake ndi mawu akuti “Yehova akupatseni ana mwa mkazi uyu kulowa mʼmalo mwa amene anapempha ndi kumupereka kwa Yehova.”
Da velsignet Eli Elkana og hans hustru og sa: Herren gi dig barn igjen med denne kvinne istedenfor ham som hun bad om for Herren! Så drog de hjem igjen.
21 Ndipo Yehova anamukomera mtima Hana. Anakhala ndi pathupi ndi kubereka ana aamuna atatu ndi ana aakazi awiri. Ndipo Samueli ankakula pamaso pa Yehova.
Og Herren så til Hanna, og hun blev fruktsommelig og fødte tre sønner og to døtre; men gutten Samuel vokste op hos Herren.
22 Tsono Eli anakalamba kwambiri. Iye ankamva zonse zimene ana ake aamuna ankachitira Aisraeli onse, ndiponso kuti ankagona ndi akazi pa chipata cha tenti ya msonkhano.
Eli var meget gammel, og når han hørte om alt det hans sønner gjorde mot hele Israel, og at de lå hos de kvinner som gjorde tjeneste ved inngangen til sammenkomstens telt,
23 Choncho anawafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani mukuchita zinthu zotere? Ine ndikumva kuchokera kwa anthu onse za zoyipa zanuzo.
sa han til dem: Hvorfor gjør I således? Jeg hører av hele folket her at eders adferd er ond.
24 Ayi, ana anga si mbiri yabwino imene ndikumva anthu a Mulungu akufalitsa.
Ikke så, mine sønner! Det rykte jeg hører, er ikke godt; I forfører Herrens folk.
25 Ngati munthu alakwira munthu mnzake, mwina Mulungu adzamupepesera, koma ngati munthu achimwira Yehova adzamupepesera ndani?” Koma ana ake sanamvere kudzudzula kwa abambo awo, pakuti chinali cholinga cha Yehova kuti awaphe.
Når en mann synder mot en annen mann, skal Gud dømme ham; men når en mann synder mot Herren, hvem skal da bede for ham? Men de hørte ikke på det deres far sa; for det var Herrens vilje å la dem dø.
26 Ndipo mnyamata Samueli anapitirira kukula mu msinkhu, ndipo ankapeza kuyanja pamaso pa Yehova ndi anthu.
Men gutten Samuel gikk frem i alder og i yndest både hos Herren og hos mennesker.
27 Tsiku lina munthu wa Mulungu anabwera kwa Eli ndipo anamuwuza kuti, “Yehova akuti, ‘Kodi Ine sindinadziwulule ndekha kwa banja la kholo lako pamene iwo anali akapolo a Farao ku Igupto?
Og det kom en Guds mann til Eli, og sa til ham: Så sier Herren: Har jeg ikke åpenbaret mig for din fars hus, da de var i Egypten og måtte tjene Faraos hus?
28 Ndipo ndinamusankha pakati pa mafuko a Israeli kuti akhale wansembe wanga ndi kuti azipita pa guwa langa la nsembe, kufukiza Lubani ndi kuvala efodi pamaso panga. Ndinapatsa banja la abambo ako gawo la nsembe zonse zopsereza zimene Aisraeli amapereka.
Og jeg valgte ham blandt alle Israels stammer til prest for mig, til å ofre på mitt alter, brenne røkelse, bære livkjortel for mitt åsyn, og jeg gav din fars hus alle Israels barns ildoffer.
29 Nʼchifukwa chiyani ukunyoza nsembe ndi zopereka zanga zimene ndinalamula? Nʼchifukwa chiyani ukupereka ulemu kwa ana ako kuposa Ine podzinenepetsa nokha ndi zopereka zabwino kwambiri za nsembe zimene Aisraeli amapereka?’”
Hvorfor treder I mitt slaktoffer og mitt matoffer under føtter, de offer som jeg har påbudt i min bolig? Og du ærer dine sønner mere enn mig, idet I mesker eder med det beste av hver offergave som mitt folk, Israel, bærer frem.
30 “Paja Ine Yehova Mulungu wa Israeli ‘Ndinalonjeza kuti anthu a pa banja lako ndi a pa banja la abambo ako azidzanditumikira nthawi zonse.’ Koma tsopano ndikuti, ‘Zonsezi zithe!’ Tsopano anthu amene amandilemekeza Inenso ndidzawalemekeza koma iwo amene amandinyoza Ine ndidzawanyoza.
Derfor lyder ordet fra Herren, Israels Gud: Vel har jeg sagt: Ditt hus og din fars hus skal ferdes for mitt åsyn til evig tid. Men nu lyder Herrens ord: Det være langt fra mig! Dem som ærer mig, vil jeg ære, og de som ringeakter mig, skal bli til skamme.
31 Nthawi ikubwera imene ndidzachotsa anyamata ako ndi anyamata a pa banja la abambo ako, kotero kuti sipadzakhala munthu wokalamba pa banja lako.
Se, dager skal komme da jeg avhugger din arm og din fars ætts arm, så ingen i din ætt skal bli gammel.
32 Pa mavuto ako udzayangʼana ndi maso ansanje zabwino zimene ndidzachitira Aisraeli ena. Mʼbanja lako simudzapezeka munthu wokalamba.
Og du skal skue trengsel for Guds bolig tross alt det gode han gjør mot Israel, og det skal aldri finnes nogen gammel i ditt hus.
33 Komabe pa banja lako mmodzi yekha ndidzamuleka wosamuchotsa kuti azidzanditumikira. Iyeyu azidzakuliritsa ndi kukumvetsa chisoni. Koma ena onse pa banja lako adzafa akanali aangʼono.”
Dog vil jeg ikke utrydde hver mann av din ætt fra mitt alter, så jeg lar dine øine slukne og din sjel vansmekte; men alle som vokser op i ditt hus, skal dø i sine manndomsår.
34 “‘Ndipo chimene chidzachitike kwa ana ako awiriwa, Hofini ndi Finehasi, chidzakhala chizindikiro kwa iwe. Onse awiri adzafa pa tsiku limodzi.
Og til tegn på dette skal du ha det som skal ramme begge dine sønner, Hofni og Pinehas: De skal begge dø på en dag.
35 Pambuyo pake ndidzasankha wansembe wokhulupirika, amene adzachita zimene zili mu mtima ndi mʼmaganizo mwanga. Ndidzakhazikitsa banja lako kolimba ndipo adzatumikira pamaso pa wodzozedwa wanga nthawi zonse.
Og jeg vil opreise for mig en trofast prest: han skal gjøre efter min hu og min vilje, og jeg vil bygge ham et hus som blir stående, og han skal ferdes for min salvedes åsyn alle dager.
36 Ndipo aliyense wotsala wa banja lako adzabwera ndi kugwada pamaso pake kupempha ndalama kapena chakudya.’ Adzati, ‘Chonde ndiloleni kuti ndizithandizako pa ntchito iliyonse ya unsembe kuti ndipeze chakudya.’”
Og enhver som er igjen av ditt hus, skal komme og bøie sig for ham for å få en sølvskilling og et brød og si: Kjære, sett mig i et av presteembedene, sa jeg kan få et stykke brød å ete!

< 1 Samueli 2 >