< 1 Samueli 2 >
1 Ndipo Hana anapemphera nati, “Moyo wanga ukukondwera mwa Yehova; Ndiyenda mwa tukumutukumu chifukwa cha Yehova. Pakamwa panga pakula ndi kuseka adani anga mowanyogodola. Ndikukondwa chifukwa mwandipulumutsa.
UHana wasekhuleka esithi: “Inhliziyo yami iyathokoza kuThixo; kuThixo uphondo lwami luphakeme. Umlomo wami uyaziklolodela izitha zami, ngoba ngiyathokoza ekusindiseni kwakho.
2 “Palibe wina woyera ngati Yehova, palibe wina koma inu nokha, palibe thanthwe lofanana ndi Mulungu wathu.
Kakho ongcwele njengoThixo; kakho omunye ngaphandle kwakho; akulaDwala elinjengo-Nkulunkulu wethu.
3 “Musandiyankhulenso modzitama, pakamwa panu pasatuluke zonyada, pakuti Yehova ndi Mulungu wanzeru, ndipo ndiye amene amayesa ntchito za anthu onse.
Lingabe lisakhuluma ngokuzigqaja kanje loba uyekele umlomo wakho ukhuluma ukuzikhukhumeza okunje, ngoba uThixo unguNkulunkulu owaziyo, njalo izenzo zilinganiswa nguye.
4 “Mauta a anthu ankhondo athyoka koma anthu ofowoka avala dzilimbe.
Amadandili amabutho ephukile, kodwa labo abakhubekayo bahlonyiswe ngamandla.
5 Amene kale anali okhuta tsopano akukagula chakudya, koma iwo amene anali ndi njala sakumvanso njala. Amene anali wosabereka, wabereka ana aamuna asanu ndi awiri, koma iye wobereka ana ambiri watsala yekha.
Labo ababesuthi baziqhatshisa ngokudla, kodwa labo ababelambile kabalambi futhi. Lowo owayeyinyumbakazi usezele abantwana abayisikhombisa, kodwa lowo owayelamadodana amanengi uyacikizeka.
6 “Yehova amabweretsa imfa ndipo amaperekanso moyo, amatsitsira ku manda ndipo amawatulutsakonso. (Sheol )
Uthixo uletha ukufa njalo enze ukuphila, wehlisela phansi engcwabeni njalo avuse. (Sheol )
7 Yehova amasaukitsa ndipo amalemeretsa, amatsitsa ndipo amakweza.
Uthixo uthumela ubuyanga kanye lenotho; uyathobekisa njalo uyaphakamisa.
8 Iye amakweza osauka kuwachotsa pa fumbi, ndipo amachotsa anthu osowa pa dzala. Iye amawakhazika pamodzi ndi ana a mafumu, amawapatsa mpando waulemu. “Pakuti nsanamira za dziko lapansi ndi za Yehova, anakhazika dziko lapansi pa nsanamirazo.
Uvusa abayanga ethulini aphakamise abaswelayo esilotheni; abahlalise lamakhosana. Enze bathole isihlalo sodumo sibe yilifa labo. Ngoba izisekelo zomhlaba ngezikaThixo; umise umhlaba phezu kwazo.
9 Iye adzateteza moyo wa anthu okhulupirika koma anthu oyipa adzawonongedwa mu mdima. “Pakuti munthu sapambana ndi mphamvu zake.
Uzalondoloza inyawo zabathembekileyo bakhe, kodwa ababi bazathuliselwa emnyameni. Akusikho ngamandla ukuthi umuntu ehlule;
10 Yehova adzaphwanya omutsutsa. Adzawaopsa ndi bingu kuchokera kumwamba; Yehova adzaweruza mathero a dziko lapansi. “Koma adzapereka mphamvu kwa mfumu yake, adzakuza mphamvu za odzozedwa wake.”
labo abaphikisa uThixo bazaphahlazwa. OPhezukonke uzaduma amelane labo esezulwini; uThixo uzakwahlulela imikhawulo yomhlaba. Uzayinika amandla inkosi yakhe aphakamise lophondo logcotshiweyo wakhe.”
11 Tsono Elikana anapita ku mudzi kwawo ku Rama, koma mnyamatayo amatumikira Yehova pansi pa ulamuliro wa wansembe Eli.
Emva kwalokho u-Elikhana wabuyela ekhaya eRama, kodwa umfana wakhonza phambi kukaThixo ngaphansi kuka-Eli umphristi.
12 Ana a Eli anali ana achabechabe pakuti samasamala za Yehova.
Amadodana ka-Eli ayengabantu abaxhwalileyo, ayengamnanzi uThixo.
13 Ndipo chizolowezi cha ansembe pakati pa anthu chinali motere kuti pamene munthu aliyense ankapereka nsembe ndipo nyama ija ikuwira pa moto, mtumiki wa wansembe ankabwera ndi chifoloko cha mano atatu mʼdzanja lake.
Kwakungumkhuba wabaphristi labantu ukuthi kokuphela nxa loba ngubani enikele umhlatshelo, njalo lapho inyama isaphekwa, inceku yomphristi yayisiza iphethe ifologwe elencijo ezintathu.
14 Iye ankachipisa mu mʼphikamo, ndipo wansembeyo amatenga chilichonse chimene folokoyo yabaya. Umu ndi mmene ansembewo amachitira ndi Aisraeli onse amene amabwera ku Silo.
Yayihlaba ngayo epaneni loba egedleleni loba ebhodweni kumbe embizeni, umphristi abe esezithathela loba kuyini okuphume lefologwe. Le yiyo indlela abaphatha ngayo bonke abako-Israyeli abafika eShilo.
15 Ndipo ngakhale mafuta asanatenthedwe, mtumiki wansembe amabwera ndi kunena kwa munthu amene akupereka nsembeyo kuti, “Ndipatse nyama kuti ndiwotche, pakuti Yehova salandira nyama yophika koma yayiwisi.”
Kodwa lalapho amahwahwa engakatshi, inceku yomphristi yayisiya emuntwini onikelayo ithi, “Nika umphristi inyama yokosa; kasoze ayamukele kuwe inyama ephekiweyo, kodwa eluhlaza kuphela.”
16 Ngati munthuyo anena kuti, “Apseretu mafuta poyamba, ndipo kenaka mutenge mmene mufunira,” mtumikiyo amayankha kuti, “Ayi ndipatse tsopano lino. Ngati sutero, ine nditenga molanda.”
Lapho umuntu ethe kuyo, “Yekela amahwahwa aqale atshe, ube usuthathake lokho okufunayo,” inceku yayiphendula ithi, “Hatshi, ngiqhubela yona khathesi; nxa ungenzi njalo, ngizayihluthuna ngamandla.”
17 Tchimo la ana a Eli linali lalikulu kwambiri pamaso pa Yehova pakuti iwo amanyoza nsembe za Yehova.
Lesisono samajaha sasisikhulu kakhulu emehlweni kaThixo, ngoba babephatha umnikelo kaThixo ngokwedelela.
18 Koma Samueli amatumikira pamaso pa Yehova atavala efodi ya nsalu yofewa yosalala.
Kodwa uSamuyeli wayekhonza phambi kukaThixo engumfana egqoka isembatho samahlombe selineni.
19 Chaka chilichonse amayi ake ankamusokera kamkanjo ndi kukamupatsa akamapita ndi mwamuna wake kukapereka nsembe za pa chaka.
Minyaka yonke unina wayemenzela ingubo encane ayise kuye lapho esiya khonale lomkakhe ukuyanikela umhlatshelo weminyaka yonke.
20 Tsono Eli amadalitsa Elikana ndi mkazi wake ndi mawu akuti “Yehova akupatseni ana mwa mkazi uyu kulowa mʼmalo mwa amene anapempha ndi kumupereka kwa Yehova.”
U-Eli wayebusisa u-Elikhana lomkakhe, esithi, “Sengathi uThixo angalipha abantwana ngalo owesifazane ukuba bathathe isikhundla salowo amkhulekelayo wasemnika uThixo.” Emva kwalokho babebuyela ekhaya.
21 Ndipo Yehova anamukomera mtima Hana. Anakhala ndi pathupi ndi kubereka ana aamuna atatu ndi ana aakazi awiri. Ndipo Samueli ankakula pamaso pa Yehova.
Uthixo waba lomusa kuHana; wakhulelwa wazala amadodana amathathu lamadodakazi amabili. Kusenjalo, umfana uSamuyeli wakhula phambi kukaThixo.
22 Tsono Eli anakalamba kwambiri. Iye ankamva zonse zimene ana ake aamuna ankachitira Aisraeli onse, ndiponso kuti ankagona ndi akazi pa chipata cha tenti ya msonkhano.
Ngalesosikhathi u-Eli, owayesemdala kakhulu, wezwa ngakho konke okwakusenziwa ngamadodana akhe ku-Israyeli wonke kanye lokuthi ayelala njani labesifazane ababesebenza esangweni lethente lokuhlangana.
23 Choncho anawafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani mukuchita zinthu zotere? Ine ndikumva kuchokera kwa anthu onse za zoyipa zanuzo.
Ngakho wathi kuwo, “Kungani lisenza izinto ezinje na? Ngizizwa ngabantu bonke lezizenzo zenu ezimbi.
24 Ayi, ana anga si mbiri yabwino imene ndikumva anthu a Mulungu akufalitsa.
Hatshi, madodana ami; akusimbiko omuhle engiwuzwa usanda phakathi kwabantu bakaThixo.
25 Ngati munthu alakwira munthu mnzake, mwina Mulungu adzamupepesera, koma ngati munthu achimwira Yehova adzamupepesera ndani?” Koma ana ake sanamvere kudzudzula kwa abambo awo, pakuti chinali cholinga cha Yehova kuti awaphe.
Nxa umuntu esona komunye umuntu, uNkulunkulu angaba ngumeli wakhe kodwa nxa umuntu esona kuThixo, ngubani ongamkhulumela na?” Kodwa amadodana akhe kawakulalelanga ukukhuza kukayise, ngoba kwakuyisifiso sikaThixo ukuba awabulale.
26 Ndipo mnyamata Samueli anapitirira kukula mu msinkhu, ndipo ankapeza kuyanja pamaso pa Yehova ndi anthu.
Umfana uSamuyeli waqhubeka ekhula ngomzimba langokuthandeka kuThixo lasebantwini.
27 Tsiku lina munthu wa Mulungu anabwera kwa Eli ndipo anamuwuza kuti, “Yehova akuti, ‘Kodi Ine sindinadziwulule ndekha kwa banja la kholo lako pamene iwo anali akapolo a Farao ku Igupto?
Ngalesosikhathi umuntu kaNkulunkulu wafika ku-Eli wathi kuye, “Nanku okutshiwo nguThixo ukuthi: ‘Kangizibonakalisanga ngokubalulekileyo endlini kayihlo lapho babeseGibhithe ngaphansi kukaFaro na?
28 Ndipo ndinamusankha pakati pa mafuko a Israeli kuti akhale wansembe wanga ndi kuti azipita pa guwa langa la nsembe, kufukiza Lubani ndi kuvala efodi pamaso panga. Ndinapatsa banja la abambo ako gawo la nsembe zonse zopsereza zimene Aisraeli amapereka.
Ngakhetha uyihlo phakathi kwezizwana zonke zako-Israyeli ukuba abe ngumphristi wami, ukuba aye e-alithareni lami, ukuba atshise impepha, lokuba agqoke isembatho samahlombe phambi kwami. Njalo nganika indlu kayihlo yonke iminikelo eyenziwa ngomlilo ngabako-Israyeli.
29 Nʼchifukwa chiyani ukunyoza nsembe ndi zopereka zanga zimene ndinalamula? Nʼchifukwa chiyani ukupereka ulemu kwa ana ako kuposa Ine podzinenepetsa nokha ndi zopereka zabwino kwambiri za nsembe zimene Aisraeli amapereka?’”
Pho kungani useyisa imihlatshelo yami kanye leminikelo engayiphawulela indlu yami yokuhlala na? Kungani uhlonipha amadodana akho okudlula mina ngokuzikhuluphalisa lina ngokwenu ngezingxenye zekhethelo zeminikelo yonke eyenziwa ngabantu bako-Israyeli na?’
30 “Paja Ine Yehova Mulungu wa Israeli ‘Ndinalonjeza kuti anthu a pa banja lako ndi a pa banja la abambo ako azidzanditumikira nthawi zonse.’ Koma tsopano ndikuti, ‘Zonsezi zithe!’ Tsopano anthu amene amandilemekeza Inenso ndidzawalemekeza koma iwo amene amandinyoza Ine ndidzawanyoza.
Ngakho-ke uThixo, uNkulunkulu ka-Israyeli, uthi, ‘Ngathembisa ukuthi indlu yakho lendlu kayihlo zizakhonza phambi kwami nini lanini.’ Kodwa khathesi uThixo uthi, ‘Akusenjalo kimi!’ Labo abangihloniphayo ngizabahlonipha, kodwa labo abangeyisayo bazakweyiswa.
31 Nthawi ikubwera imene ndidzachotsa anyamata ako ndi anyamata a pa banja la abambo ako, kotero kuti sipadzakhala munthu wokalamba pa banja lako.
Isikhathi siyeza lapho engizaphungula khona amandla akho lamandla endlu kayihlo, ukuze kungabi lomuntu omdala kusendo lwakwenu
32 Pa mavuto ako udzayangʼana ndi maso ansanje zabwino zimene ndidzachitira Aisraeli ena. Mʼbanja lako simudzapezeka munthu wokalamba.
njalo uzabona usizi lapho engihlala khona. Lanxa okuhle kuzakwenziwa ku-Israyeli, kwabosendo lwakho akuyikuba lomuntu omdala.
33 Komabe pa banja lako mmodzi yekha ndidzamuleka wosamuchotsa kuti azidzanditumikira. Iyeyu azidzakuliritsa ndi kukumvetsa chisoni. Koma ena onse pa banja lako adzafa akanali aangʼono.”
Lowo lalowo wakini engingayikumsusa e-alithareni lami uzayekelwa nje ukuba amehlo akhe afiphale lokuba azwise inhliziyo yakho ubuhlungu, njalo yonke inzalo yakho izakufa kuyikhona isephakathi kwempilo.
34 “‘Ndipo chimene chidzachitike kwa ana ako awiriwa, Hofini ndi Finehasi, chidzakhala chizindikiro kwa iwe. Onse awiri adzafa pa tsiku limodzi.
‘Njalo okwenzakala emadodaneni akho amabili, uHofini loFinehasi, kuzakuba yisiboniso kuwe, bobabili bazakufa langa linye.
35 Pambuyo pake ndidzasankha wansembe wokhulupirika, amene adzachita zimene zili mu mtima ndi mʼmaganizo mwanga. Ndidzakhazikitsa banja lako kolimba ndipo adzatumikira pamaso pa wodzozedwa wanga nthawi zonse.
Ngizakuzimisela umphristi othembekileyo ozakwenza mayelana lokusenhliziyweni yami lengqondweni yami. Ngizamisa indlu yakhe iqine, njalo uzakhonza phambi kogcotshiweyo wami kokuphela.
36 Ndipo aliyense wotsala wa banja lako adzabwera ndi kugwada pamaso pake kupempha ndalama kapena chakudya.’ Adzati, ‘Chonde ndiloleni kuti ndizithandizako pa ntchito iliyonse ya unsembe kuti ndipeze chakudya.’”
Lapho-ke bonke abosendo lwakho abaseleyo bazakuza bakhothame kuye becela uhlamvu lwesiliva loqweqwe lwesinkwa njalo bakhalaze besithi, “Ake ungibeke kwesinye isikhundla sobuphristi ukuze ngithole ukudla ngidle.”’”