< 1 Samueli 2 >

1 Ndipo Hana anapemphera nati, “Moyo wanga ukukondwera mwa Yehova; Ndiyenda mwa tukumutukumu chifukwa cha Yehova. Pakamwa panga pakula ndi kuseka adani anga mowanyogodola. Ndikukondwa chifukwa mwandipulumutsa.
Mon âme a tressailli d’allégresse dans le Seigneur, et ma force a été exaltée en mon Dieu; ma bouche s’est dilatée sur mes ennemis, parce que je me suis réjouie dans votre assistance.
2 “Palibe wina woyera ngati Yehova, palibe wina koma inu nokha, palibe thanthwe lofanana ndi Mulungu wathu.
Il n’est pas de saint comme est le Seigneur; car il n’en est pas d’autre en dehors de vous, et il n’est pas de fort comme notre Dieu.
3 “Musandiyankhulenso modzitama, pakamwa panu pasatuluke zonyada, pakuti Yehova ndi Mulungu wanzeru, ndipo ndiye amene amayesa ntchito za anthu onse.
Ne multipliez point des paroles hautaines en vous glorifiant; que les anciens discours s’éloignent de votre bouche, parce que le Seigneur est le Dieu des sciences, et que c’est pour lui que sont préparées les pensées.
4 “Mauta a anthu ankhondo athyoka koma anthu ofowoka avala dzilimbe.
L’arc des forts a été vaincu, et les faibles ont été ceints de force.
5 Amene kale anali okhuta tsopano akukagula chakudya, koma iwo amene anali ndi njala sakumvanso njala. Amene anali wosabereka, wabereka ana aamuna asanu ndi awiri, koma iye wobereka ana ambiri watsala yekha.
Ceux qui auparavant regorgeaient se sont loués pour du pain; et les affamés ont été rassasiés, jusque là qu’une femme stérile a enfanté un grand nombre d’enfants, et que celle qui en avait beaucoup est tombée dans la langueur.
6 “Yehova amabweretsa imfa ndipo amaperekanso moyo, amatsitsira ku manda ndipo amawatulutsakonso. (Sheol h7585)
C’est le Seigneur qui fait mourir et qui fait vivre, qui conduit aux enfers et qui en ramène. (Sheol h7585)
7 Yehova amasaukitsa ndipo amalemeretsa, amatsitsa ndipo amakweza.
C’est le Seigneur qui fait le pauvre et qui enrichit, qui abaisse et qui relève.
8 Iye amakweza osauka kuwachotsa pa fumbi, ndipo amachotsa anthu osowa pa dzala. Iye amawakhazika pamodzi ndi ana a mafumu, amawapatsa mpando waulemu. “Pakuti nsanamira za dziko lapansi ndi za Yehova, anakhazika dziko lapansi pa nsanamirazo.
Il fait sortir de la poussière l’indigent, et du fumier il élève le pauvre, afin qu’il s’asseye avec les princes, et qu’il occupe un trône de gloire; car au Seigneur appartiennent les pôles de la terre, et il a posé sur eux l’univers.
9 Iye adzateteza moyo wa anthu okhulupirika koma anthu oyipa adzawonongedwa mu mdima. “Pakuti munthu sapambana ndi mphamvu zake.
Il gardera les pieds de ses saints, et les impies se tairont dans les ténèbres, parce que ce n’est point par sa propre force que l’homme se fortifiera.
10 Yehova adzaphwanya omutsutsa. Adzawaopsa ndi bingu kuchokera kumwamba; Yehova adzaweruza mathero a dziko lapansi. “Koma adzapereka mphamvu kwa mfumu yake, adzakuza mphamvu za odzozedwa wake.”
C’est le Seigneur que redouteront ses ennemis, et c’est sur eux-mêmes qu’il tonnera dans les cieux. Le Seigneur jugera les confins de la terre, il donnera l’empire à son roi, et il élèvera la puissance de son christ.
11 Tsono Elikana anapita ku mudzi kwawo ku Rama, koma mnyamatayo amatumikira Yehova pansi pa ulamuliro wa wansembe Eli.
Après cela, Elcana s’en alla à Ramatha dans sa maison; mais l’enfant servait en la présence du Seigneur et devant Héli, le prêtre.
12 Ana a Eli anali ana achabechabe pakuti samasamala za Yehova.
Or, les fils d’Héli étaient des fils de Bélial, ne connaissant point le Seigneur,
13 Ndipo chizolowezi cha ansembe pakati pa anthu chinali motere kuti pamene munthu aliyense ankapereka nsembe ndipo nyama ija ikuwira pa moto, mtumiki wa wansembe ankabwera ndi chifoloko cha mano atatu mʼdzanja lake.
Ni le devoir des prêtres envers le peuple; car quiconque avait immolé une victime, le serviteur du prêtre venait, tandis que les chairs cuisaient, et il avait la fourchette à trois dents en sa main,
14 Iye ankachipisa mu mʼphikamo, ndipo wansembeyo amatenga chilichonse chimene folokoyo yabaya. Umu ndi mmene ansembewo amachitira ndi Aisraeli onse amene amabwera ku Silo.
Et il la plongeait dans la chaudière, ou dans le chaudron, ou dans la marmite, ou dans le pot; et tout ce qu’enlevait la fourchette, le prêtre l’emportait pour lui. C’est ainsi qu’ils faisaient à tous ceux d’Israël qui venaient à Silo.
15 Ndipo ngakhale mafuta asanatenthedwe, mtumiki wansembe amabwera ndi kunena kwa munthu amene akupereka nsembeyo kuti, “Ndipatse nyama kuti ndiwotche, pakuti Yehova salandira nyama yophika koma yayiwisi.”
Même avant qu’on brûlât la graisse, le serviteur du prêtre venait, et disait à celui qui immolait: Donne-moi de la chair, afin que je la fasse cuire pour le prêtre; car je ne recevrai pas de toi de la chair cuite, mais de la crue.
16 Ngati munthuyo anena kuti, “Apseretu mafuta poyamba, ndipo kenaka mutenge mmene mufunira,” mtumikiyo amayankha kuti, “Ayi ndipatse tsopano lino. Ngati sutero, ine nditenga molanda.”
Et celui qui immolait lui disait: Que la graisse d’abord soit brûlée aujourd’hui, selon l’usage, et prenez pour vous tout autant qu’en désire votre âme. Et celui-ci, répondant, lui disait: Point du tout; car tu m’en donneras maintenant, ou bien j’en prendrai de force.
17 Tchimo la ana a Eli linali lalikulu kwambiri pamaso pa Yehova pakuti iwo amanyoza nsembe za Yehova.
Ainsi le péché des enfants d’Héli était très grand devant le Seigneur, puisqu’ils détournaient les hommes des sacrifices du Seigneur.
18 Koma Samueli amatumikira pamaso pa Yehova atavala efodi ya nsalu yofewa yosalala.
Cependant devant la face du Seigneur servait Samuel, enfant revêtu d’un éphod de lin.
19 Chaka chilichonse amayi ake ankamusokera kamkanjo ndi kukamupatsa akamapita ndi mwamuna wake kukapereka nsembe za pa chaka.
Et sa mère lui faisait une petite tunique qu’elle lui apportait aux jours prescrits, montant avec son mari, pour immoler l’hostie solennelle.
20 Tsono Eli amadalitsa Elikana ndi mkazi wake ndi mawu akuti “Yehova akupatseni ana mwa mkazi uyu kulowa mʼmalo mwa amene anapempha ndi kumupereka kwa Yehova.”
Et Héli bénit Elcana et sa femme et dit à Elcana: Que le Seigneur te rende une postérité par cette femme pour l’intérêt de ce que tu as prêté au Seigneur. Et ils s’en allèrent dans leur demeure.
21 Ndipo Yehova anamukomera mtima Hana. Anakhala ndi pathupi ndi kubereka ana aamuna atatu ndi ana aakazi awiri. Ndipo Samueli ankakula pamaso pa Yehova.
Le Seigneur visita donc Anne, et elle conçut et enfanta trois fils et deux filles, et l’enfant Samuel devint grand devant le Seigneur.
22 Tsono Eli anakalamba kwambiri. Iye ankamva zonse zimene ana ake aamuna ankachitira Aisraeli onse, ndiponso kuti ankagona ndi akazi pa chipata cha tenti ya msonkhano.
Or, Héli était fort vieux; et il apprit tout ce que faisaient ses fils à tout Israël, et comment ils dormaient avec les femmes qui veillaient à la porte du tabernacle,
23 Choncho anawafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani mukuchita zinthu zotere? Ine ndikumva kuchokera kwa anthu onse za zoyipa zanuzo.
Et il leur demanda: Pourquoi faites-vous des choses de cette nature, choses très mauvaises, que j’apprends moi-même de tout le peuple?
24 Ayi, ana anga si mbiri yabwino imene ndikumva anthu a Mulungu akufalitsa.
Cessez, mes enfants; car il n’est pas honorable le bruit qui est parvenu jusqu’à moi, que vous faites transgresser le peuple du Seigneur.
25 Ngati munthu alakwira munthu mnzake, mwina Mulungu adzamupepesera, koma ngati munthu achimwira Yehova adzamupepesera ndani?” Koma ana ake sanamvere kudzudzula kwa abambo awo, pakuti chinali cholinga cha Yehova kuti awaphe.
Si un homme pèche contre un homme, Dieu pourra être apaisé pour lui; mais si c’est contre le Seigneur qu’un homme pèche, qui priera pour lui? Et ils n’écoutèrent pas la voix de leur père, parce que le Seigneur voulut les perdre.
26 Ndipo mnyamata Samueli anapitirira kukula mu msinkhu, ndipo ankapeza kuyanja pamaso pa Yehova ndi anthu.
Cependant l’enfant Samuel avançait et croissait, et plaisait autant au Seigneur qu’aux hommes.
27 Tsiku lina munthu wa Mulungu anabwera kwa Eli ndipo anamuwuza kuti, “Yehova akuti, ‘Kodi Ine sindinadziwulule ndekha kwa banja la kholo lako pamene iwo anali akapolo a Farao ku Igupto?
Or, il vint un homme de Dieu vers Héli, et il lui dit: Voici ce que dit le Seigneur: Ne me suis-je pas ouvertement révélé à la maison de ton père, lorsqu’ils étaient en Égypte, dans la maison de Pharaon?
28 Ndipo ndinamusankha pakati pa mafuko a Israeli kuti akhale wansembe wanga ndi kuti azipita pa guwa langa la nsembe, kufukiza Lubani ndi kuvala efodi pamaso panga. Ndinapatsa banja la abambo ako gawo la nsembe zonse zopsereza zimene Aisraeli amapereka.
Je l’ai choisi entre toutes les tribus d’Israël pour mon prêtre, afin qu’il montât à mon autel, qu’il brûlât pour moi de l’encens, et qu’il portât un éphod devant moi; et j’ai donné à la maison de ton père de tous les sacrifices des enfants d’Israël.
29 Nʼchifukwa chiyani ukunyoza nsembe ndi zopereka zanga zimene ndinalamula? Nʼchifukwa chiyani ukupereka ulemu kwa ana ako kuposa Ine podzinenepetsa nokha ndi zopereka zabwino kwambiri za nsembe zimene Aisraeli amapereka?’”
Pourquoi avez-vous jeté sous vos pieds ma victime et mes présents que j’ai ordonné d’offrir dans le temple, et as-tu plus honoré tes fils que moi, pour que vous mangeassiez les prémices de tous les sacrifices d’Israël mon peuple?
30 “Paja Ine Yehova Mulungu wa Israeli ‘Ndinalonjeza kuti anthu a pa banja lako ndi a pa banja la abambo ako azidzanditumikira nthawi zonse.’ Koma tsopano ndikuti, ‘Zonsezi zithe!’ Tsopano anthu amene amandilemekeza Inenso ndidzawalemekeza koma iwo amene amandinyoza Ine ndidzawanyoza.
C’est pour cela que le Seigneur Dieu d’Israël dit: Parlant, j’ai parlé, afin que ta maison et la maison de ton père servit en ma présence pour toujours. Or, le Seigneur dit maintenant: Loin de moi cela! mais quiconque m’aura glorifié, je le glorifierai; ceux au contraire qui me méprisent, seront avilis.
31 Nthawi ikubwera imene ndidzachotsa anyamata ako ndi anyamata a pa banja la abambo ako, kotero kuti sipadzakhala munthu wokalamba pa banja lako.
Voici que des jours viendront, et je couperai ton bras, et le bras de la maison de ton père, en sorte qu’il n’y ait point de vieillard dans ta maison.
32 Pa mavuto ako udzayangʼana ndi maso ansanje zabwino zimene ndidzachitira Aisraeli ena. Mʼbanja lako simudzapezeka munthu wokalamba.
Et tu verras ton rival dans le temple, au milieu de toutes les prospérités d’Israël; et il n’y aura de vieillard dans ta maison en aucun jour.
33 Komabe pa banja lako mmodzi yekha ndidzamuleka wosamuchotsa kuti azidzanditumikira. Iyeyu azidzakuliritsa ndi kukumvetsa chisoni. Koma ena onse pa banja lako adzafa akanali aangʼono.”
Cependant je n’enlèverai pas entièrement de mon autel tout homme issu de toi; mais je ferai que tes yeux s’éteindront, et que ton âme se desséchera: et une grande partie de ta maison mourra, lorsqu’elle sera parvenue à l’âge viril.
34 “‘Ndipo chimene chidzachitike kwa ana ako awiriwa, Hofini ndi Finehasi, chidzakhala chizindikiro kwa iwe. Onse awiri adzafa pa tsiku limodzi.
Or, ce qui en sera pour toi le signe, est ce qui doit arriver à tes deux fils, Ophni et Phinéès: en un seul jour ils mourront tous les deux.
35 Pambuyo pake ndidzasankha wansembe wokhulupirika, amene adzachita zimene zili mu mtima ndi mʼmaganizo mwanga. Ndidzakhazikitsa banja lako kolimba ndipo adzatumikira pamaso pa wodzozedwa wanga nthawi zonse.
Et je me susciterai un prêtre fidèle qui agira selon mon cœur et mon âme; et je lui édifierai une maison fidèle, et il marchera devant mon christ, tous les jours.
36 Ndipo aliyense wotsala wa banja lako adzabwera ndi kugwada pamaso pake kupempha ndalama kapena chakudya.’ Adzati, ‘Chonde ndiloleni kuti ndizithandizako pa ntchito iliyonse ya unsembe kuti ndipeze chakudya.’”
Or, il arriva, que quiconque sera resté dans ta maison, viendra, afin qu’on prie pour lui et qu’il offre une pièce d’argent, et une miche de pain, et qu’il dise: Admettez-moi, je vous conjure, à une fonction sacerdotale, afin que je mange une bouchée de pain.

< 1 Samueli 2 >