< 1 Samueli 2 >
1 Ndipo Hana anapemphera nati, “Moyo wanga ukukondwera mwa Yehova; Ndiyenda mwa tukumutukumu chifukwa cha Yehova. Pakamwa panga pakula ndi kuseka adani anga mowanyogodola. Ndikukondwa chifukwa mwandipulumutsa.
Hannah pria et dit, « Mon cœur exulte en Yahvé! Ma corne est exaltée en Yahvé. Ma bouche s'élargit sur mes ennemis, car je me réjouis de ton salut.
2 “Palibe wina woyera ngati Yehova, palibe wina koma inu nokha, palibe thanthwe lofanana ndi Mulungu wathu.
Il n'y a personne d'aussi saint que Yahvé, car il n'y a personne d'autre que toi, et il n'y a aucun rocher comme notre Dieu.
3 “Musandiyankhulenso modzitama, pakamwa panu pasatuluke zonyada, pakuti Yehova ndi Mulungu wanzeru, ndipo ndiye amene amayesa ntchito za anthu onse.
« Ne continuez pas à parler avec tant d'orgueil. Ne laissez pas l'arrogance sortir de votre bouche, car Yahvé est un Dieu de la connaissance. C'est par lui que les actions sont pesées.
4 “Mauta a anthu ankhondo athyoka koma anthu ofowoka avala dzilimbe.
« Les arcs des puissants sont brisés. Ceux qui ont trébuché sont armés de force.
5 Amene kale anali okhuta tsopano akukagula chakudya, koma iwo amene anali ndi njala sakumvanso njala. Amene anali wosabereka, wabereka ana aamuna asanu ndi awiri, koma iye wobereka ana ambiri watsala yekha.
Ceux qui étaient rassasiés se sont loués pour du pain. Ceux qui avaient faim sont satisfaits. Oui, la stérile a donné naissance à sept enfants. Celle qui a beaucoup d'enfants se languit.
6 “Yehova amabweretsa imfa ndipo amaperekanso moyo, amatsitsira ku manda ndipo amawatulutsakonso. (Sheol )
« Yahvé tue et fait vivre. Il descend au Shéol et remonte. (Sheol )
7 Yehova amasaukitsa ndipo amalemeretsa, amatsitsa ndipo amakweza.
Yahvé rend pauvre et enrichit. Il abaisse, il élève aussi.
8 Iye amakweza osauka kuwachotsa pa fumbi, ndipo amachotsa anthu osowa pa dzala. Iye amawakhazika pamodzi ndi ana a mafumu, amawapatsa mpando waulemu. “Pakuti nsanamira za dziko lapansi ndi za Yehova, anakhazika dziko lapansi pa nsanamirazo.
Il fait sortir les pauvres de la poussière. Il soulève les nécessiteux du tas de fumier. pour les faire asseoir avec les princes et hériter du trône de gloire. Car les piliers de la terre appartiennent à Yahvé. Il a mis le monde sur eux.
9 Iye adzateteza moyo wa anthu okhulupirika koma anthu oyipa adzawonongedwa mu mdima. “Pakuti munthu sapambana ndi mphamvu zake.
Il gardera les pieds de ses saints, mais les méchants seront réduits au silence dans les ténèbres; car aucun homme ne prévaudra par la force.
10 Yehova adzaphwanya omutsutsa. Adzawaopsa ndi bingu kuchokera kumwamba; Yehova adzaweruza mathero a dziko lapansi. “Koma adzapereka mphamvu kwa mfumu yake, adzakuza mphamvu za odzozedwa wake.”
Ceux qui luttent contre Yahvé seront mis en pièces. Il tonnera contre eux dans le ciel. « Yahvé jugera les extrémités de la terre. Il donnera de la force à son roi, et exalte la corne de son oint. »
11 Tsono Elikana anapita ku mudzi kwawo ku Rama, koma mnyamatayo amatumikira Yehova pansi pa ulamuliro wa wansembe Eli.
Elkana se rendit à Rama, dans sa maison. L'enfant servit Yahvé devant le prêtre Eli.
12 Ana a Eli anali ana achabechabe pakuti samasamala za Yehova.
Or les fils d'Eli étaient des hommes méchants. Ils ne connaissaient pas Yahvé.
13 Ndipo chizolowezi cha ansembe pakati pa anthu chinali motere kuti pamene munthu aliyense ankapereka nsembe ndipo nyama ija ikuwira pa moto, mtumiki wa wansembe ankabwera ndi chifoloko cha mano atatu mʼdzanja lake.
La coutume des prêtres avec le peuple était que, lorsque quelqu'un offrait un sacrifice, le serviteur du prêtre venait pendant que la viande bouillait, avec une fourchette de trois dents dans la main;
14 Iye ankachipisa mu mʼphikamo, ndipo wansembeyo amatenga chilichonse chimene folokoyo yabaya. Umu ndi mmene ansembewo amachitira ndi Aisraeli onse amene amabwera ku Silo.
et il la plantait dans la casserole, ou la marmite, ou le chaudron, ou le pot. Le prêtre prenait pour lui tout ce que la fourchette faisait remonter. On faisait cela à tous les Israélites qui venaient là, à Silo.
15 Ndipo ngakhale mafuta asanatenthedwe, mtumiki wansembe amabwera ndi kunena kwa munthu amene akupereka nsembeyo kuti, “Ndipatse nyama kuti ndiwotche, pakuti Yehova salandira nyama yophika koma yayiwisi.”
Avant de brûler la graisse, le serviteur du prêtre vint et dit à l'homme qui avait sacrifié: « Donne de la viande à rôtir pour le prêtre, car il n'acceptera pas de toi de la viande bouillie, mais crue. »
16 Ngati munthuyo anena kuti, “Apseretu mafuta poyamba, ndipo kenaka mutenge mmene mufunira,” mtumikiyo amayankha kuti, “Ayi ndipatse tsopano lino. Ngati sutero, ine nditenga molanda.”
Si l'homme lui disait: « Qu'on brûle d'abord la graisse, et qu'ensuite tu prennes autant que ton âme le désire », il répondait: « Non, mais tu me la donneras maintenant; sinon, je la prendrai de force. »
17 Tchimo la ana a Eli linali lalikulu kwambiri pamaso pa Yehova pakuti iwo amanyoza nsembe za Yehova.
Le péché des jeunes gens fut très grand devant l'Éternel, car ils méprisèrent l'offrande de l'Éternel.
18 Koma Samueli amatumikira pamaso pa Yehova atavala efodi ya nsalu yofewa yosalala.
Samuel, lui, faisait le service devant l'Éternel; il était encore un enfant, vêtu d'un éphod de lin.
19 Chaka chilichonse amayi ake ankamusokera kamkanjo ndi kukamupatsa akamapita ndi mwamuna wake kukapereka nsembe za pa chaka.
Sa mère lui fit aussi une petite robe, qu'elle lui apporta d'année en année, quand elle montait avec son mari pour offrir le sacrifice annuel.
20 Tsono Eli amadalitsa Elikana ndi mkazi wake ndi mawu akuti “Yehova akupatseni ana mwa mkazi uyu kulowa mʼmalo mwa amene anapempha ndi kumupereka kwa Yehova.”
Eli bénit Elkana et sa femme et dit: « Que l'Éternel vous donne une descendance de cette femme pour la demande qui a été faite à l'Éternel. » Puis ils s'en allèrent chez eux.
21 Ndipo Yehova anamukomera mtima Hana. Anakhala ndi pathupi ndi kubereka ana aamuna atatu ndi ana aakazi awiri. Ndipo Samueli ankakula pamaso pa Yehova.
Yahvé visita Anne, qui conçut et enfanta trois fils et deux filles. L'enfant Samuel grandit devant Yahvé.
22 Tsono Eli anakalamba kwambiri. Iye ankamva zonse zimene ana ake aamuna ankachitira Aisraeli onse, ndiponso kuti ankagona ndi akazi pa chipata cha tenti ya msonkhano.
Or Éli était très vieux, et il apprit tout ce que ses fils faisaient à tout Israël, et comment ils couchaient avec les femmes qui servaient à l'entrée de la tente de la Rencontre.
23 Choncho anawafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani mukuchita zinthu zotere? Ine ndikumva kuchokera kwa anthu onse za zoyipa zanuzo.
Il leur dit: « Pourquoi faites-vous de telles choses? Car j'apprends de tous ces gens que vous agissez mal.
24 Ayi, ana anga si mbiri yabwino imene ndikumva anthu a Mulungu akufalitsa.
Non, mes fils, car ce n'est pas un bon rapport que j'entends! Vous faites désobéir le peuple de Yahvé.
25 Ngati munthu alakwira munthu mnzake, mwina Mulungu adzamupepesera, koma ngati munthu achimwira Yehova adzamupepesera ndani?” Koma ana ake sanamvere kudzudzula kwa abambo awo, pakuti chinali cholinga cha Yehova kuti awaphe.
Si un homme pèche contre un autre, Dieu le jugera; mais si un homme pèche contre Yahvé, qui intercédera pour lui? ». Malgré tout, ils n'ont pas écouté la voix de leur père, car Yahvé avait l'intention de les tuer.
26 Ndipo mnyamata Samueli anapitirira kukula mu msinkhu, ndipo ankapeza kuyanja pamaso pa Yehova ndi anthu.
L'enfant Samuel grandissait et augmentait sa popularité auprès de Yahvé et des hommes.
27 Tsiku lina munthu wa Mulungu anabwera kwa Eli ndipo anamuwuza kuti, “Yehova akuti, ‘Kodi Ine sindinadziwulule ndekha kwa banja la kholo lako pamene iwo anali akapolo a Farao ku Igupto?
Un homme de Dieu s'approcha d'Eli et lui dit: « Yahvé dit: « Ne me suis-je pas révélé à la maison de ton père lorsqu'ils étaient en Égypte, en servitude chez Pharaon?
28 Ndipo ndinamusankha pakati pa mafuko a Israeli kuti akhale wansembe wanga ndi kuti azipita pa guwa langa la nsembe, kufukiza Lubani ndi kuvala efodi pamaso panga. Ndinapatsa banja la abambo ako gawo la nsembe zonse zopsereza zimene Aisraeli amapereka.
Ne l'ai-je pas choisi parmi toutes les tribus d'Israël pour être mon prêtre, pour monter à mon autel, pour brûler les parfums, pour porter l'éphod devant moi? N'ai-je pas donné à la maison de ton père toutes les offrandes consumées par le feu des enfants d'Israël?
29 Nʼchifukwa chiyani ukunyoza nsembe ndi zopereka zanga zimene ndinalamula? Nʼchifukwa chiyani ukupereka ulemu kwa ana ako kuposa Ine podzinenepetsa nokha ndi zopereka zabwino kwambiri za nsembe zimene Aisraeli amapereka?’”
Pourquoi donnez-vous des coups de pied à mon sacrifice et à mon offrande, que j'ai ordonnés dans ma demeure, et honorez-vous vos fils au-dessus de moi, pour vous engraisser avec les meilleures de toutes les offrandes d'Israël, mon peuple?
30 “Paja Ine Yehova Mulungu wa Israeli ‘Ndinalonjeza kuti anthu a pa banja lako ndi a pa banja la abambo ako azidzanditumikira nthawi zonse.’ Koma tsopano ndikuti, ‘Zonsezi zithe!’ Tsopano anthu amene amandilemekeza Inenso ndidzawalemekeza koma iwo amene amandinyoza Ine ndidzawanyoza.
C'est pourquoi Yahvé, le Dieu d'Israël, dit: « J'ai dit que ta maison et la maison de ton père marcheraient devant moi pour toujours. Mais maintenant, Yahvé dit: 'Loin de moi cette idée, car j'honorerai ceux qui m'honorent, et je maudirai ceux qui me méprisent'.
31 Nthawi ikubwera imene ndidzachotsa anyamata ako ndi anyamata a pa banja la abambo ako, kotero kuti sipadzakhala munthu wokalamba pa banja lako.
Voici que les jours viennent où je couperai ton bras et le bras de la maison de ton père, et où il n'y aura plus de vieillard dans ta maison.
32 Pa mavuto ako udzayangʼana ndi maso ansanje zabwino zimene ndidzachitira Aisraeli ena. Mʼbanja lako simudzapezeka munthu wokalamba.
Tu verras l'affliction de ma demeure, dans toutes les richesses que je donnerai à Israël. Il n'y aura pas à jamais de vieillard dans ta maison.
33 Komabe pa banja lako mmodzi yekha ndidzamuleka wosamuchotsa kuti azidzanditumikira. Iyeyu azidzakuliritsa ndi kukumvetsa chisoni. Koma ena onse pa banja lako adzafa akanali aangʼono.”
L'homme de ta maison que je ne retrancherai pas de mon autel consumera tes yeux et affligera ton cœur. Tout l'accroissement de ta maison mourra dans la fleur de l'âge.
34 “‘Ndipo chimene chidzachitike kwa ana ako awiriwa, Hofini ndi Finehasi, chidzakhala chizindikiro kwa iwe. Onse awiri adzafa pa tsiku limodzi.
Tel sera pour toi le signe qui viendra sur tes deux fils, Hophni et Phinées: en un seul jour, ils mourront tous les deux.
35 Pambuyo pake ndidzasankha wansembe wokhulupirika, amene adzachita zimene zili mu mtima ndi mʼmaganizo mwanga. Ndidzakhazikitsa banja lako kolimba ndipo adzatumikira pamaso pa wodzozedwa wanga nthawi zonse.
Je me susciterai un prêtre fidèle qui agira selon ce qui est dans mon cœur et dans mon esprit. Je lui bâtirai une maison sûre. Il marchera devant mon oint pour toujours.
36 Ndipo aliyense wotsala wa banja lako adzabwera ndi kugwada pamaso pake kupempha ndalama kapena chakudya.’ Adzati, ‘Chonde ndiloleni kuti ndizithandizako pa ntchito iliyonse ya unsembe kuti ndipeze chakudya.’”
Tous ceux qui resteront dans ta maison viendront se prosterner devant lui pour une pièce d'argent et une miche de pain, et diront: « Mets-moi dans l'une des fonctions sacerdotales, je te prie, pour que je mange un morceau de pain. »"