< 1 Samueli 18 >
1 Davide atatha kuyankhula ndi Sauli, mtima wa Yonatani unagwirizana ndi mtima wa Davide, ndipo iye ankamukonda Davide monga momwe ankadzikondera yekha.
[And it came to pass when he had finished speaking to Saul, that the soul of Jonathan was knit to the soul of David and David loved him ] [as his own soul. ]
2 Choncho Sauli anamusunga Davideyo kuyambira tsiku limenelo ndipo sanamulole kuti abwerere ku nyumba ya abambo ake.
[And Saul took him in that day, and did not suffer him to return to his father's house. ]
3 Ndipo Yonatani anapanga pangano ndi Davide chifukwa ankamukonda monga momwe ankadzikondera.
[And Jonathan and David made a covenant because he loved him as his own soul. ]
4 Yonatani anavula mkanjo umene anavala ndipo anamupatsa Davide pamodzi ndi zovala za nkhondo, lupanga, uta ndi lamba.
[And Jonathan stripped himself of his ] [upper garment, and gave it to David, and his mantle and all he had upon him, even to his sword and to his bow, and to his girdle. ]
5 Davide ankapita kulikonse kumene Sauli ankamutuma kuti apite kukamenya nkhondo, ndipo ankapambana. Choncho Sauli anamupatsa udindo woyangʼanira gulu lankhondo. Ichi chinakondweretsa anthu onse ngakhalenso atsogoleri a nkhondo a Sauli.
[And David went out withersoever Saul sent him, and ] [acted wisely, and Saul set him over the men of war, and he was pleasing in the eyes of all the people, and also in the eyes of the servants of Saul. ]
6 Anthu akubwerera kwawo Davide atapha Mfilisiti uja, amayi anatuluka mʼmizinda yonse ya Israeli, akuyimba ndi kuvina kukachingamira mfumu Sauli. Ankayimba ndi kuvina mokondwa, kwinaku ngʼoma ndi zitoliro zikulira.
And there came out women in dances to meet David out of all the cities of Israel, with timbrels, and with rejoicing, and with cymbals.
7 Amayiwo ankalandizana nyimbo mokondwera namati: “Sauli wapha 1,000, Koma Davide wapha miyandamiyanda.”
And the women began [the strain], and said, Saul has struck his thousands, and David his ten thousands.
8 Koma Sauli anapsa mtima kwambiri ndipo mawu amenewa anamuyipira. Iye anati, “Iwo amuwerengera Davide miyandamiyanda, koma ine 1,000 okha. Nanga chatsalanso nʼchiyani kuti atenge? Si ufumu basi?”
And it seemed evil in the eyes of Saul concerning this matter, and he said, To David they have given ten thousands, and to me they have given thousands. [And what more can he have but the kingdom? ]
9 Ndipo kuyambira tsiku limeneli Sauli ankamuchitira nsanje Davide.
[And Saul eyed David from that day and onward. ]
10 Mmawa mwake mzimu woyipa uja unabwera mwamphamvu pa Sauli. Sauli anayamba kubwebweta mʼnyumba mwake. Davide ankamuyimbira zeze monga nthawi zonse. Sauli anali ndi mkondo mʼdzanja lake.
[And it came to pass on the morrow that an evil spirit from God fell upon Saul, and he prophesied in the midst of his house. And David was playing on the harp with his hand, according to his daily custom. And Saul’s spear was in his hand. ]
11 Tsono anawuponya mkondowo, namati mu mtima mwake, “Ndimubaya Davide ndi kumukhomera ku khoma.” Koma Davide anawulewa kawiri konse.
[And Saul took his spear and said, I will strike David even to the wall. But David escaped twice from his presence. ]
12 Pambuyo pake Sauli amamuopa Davide chifukwa Yehova anali ndi Davideyo, nʼkumusiya Sauli.
And Saul was alarmed on account of David.
13 Kotero Sauli anamuchotsa Davide pamaso pake ndi kumuyika kukhala mtsogoleri wa ankhondo 1,000. Choncho Davide ankapita ndi kubwera akutsogolera ankhondowa.
And he removed him from him, and made him a captain of a thousand for himself; and he went out and came in before the people.
14 Davide ankapambana kwambiri pa chilichonse chimene amachita chifukwa Yehova anali naye.
And David was prudent in all his ways, and the Lord was with him.
15 Sauli ataona momwe Davide ankapambanira, iye anamuopa kwambiri.
And Saul saw that he was very wise, and he was afraid of him.
16 Koma Aisraeli onse ndi anthu a Yuda ankamukonda Davide chifukwa ankawatsogolera pa nkhondo zawo.
And all Israel and Juda loved David, because he came in and went out before the people.
17 Tsiku lina Sauli anawuza Davide kuti, “Nayu Merabi mwana wanga wamkazi wamkulu. Ine ndakupatsa kuti umukwatire. Koma unditumikire molimba mtima pomenya nkhondo za Yehova.” Poteropo Sauli ankanena kuti, “Ndisamuphe ndi manja angawa koma aphedwe ndi Afilisti!”
[And Saul said to David, Behold my elder daughter Merob, I will give her to you to Wife, only be you to me a mighty man and fight the wars of the Lord. And Saul said, Let not my hand be upon him, but the hand of the Philistines shall be upon him. ]
18 Ndipo Davide anati kwa Sauli, “Ine ndine yani, ndipo abale anga kapena banja la abambo anga ndife yani mʼdziko la Israeli kuti ndikhale mpongozi wa mfumu?”
[And David said to Saul, Who am I, and What is the life of my father’s family in Israel, that I should be the king’s son—in-law? ]
19 Koma pa nthawi yoti Merabi mwana wa Sauli akwatiwe ndi Davide, Sauli anamupereka kwa Adrieli wa ku Mehola kuti amukwatire.
[But it came to pass at the time when Merob Saul’s daughter should have been given to David, that she was given to Israel the Mothulathite to wife. ]
20 Koma Mikala mwana wamkazi wa Sauli anamukonda Davide ndipo Sauli atamva za zimenezi, anakondwera.
And Melchol the daughter of Saul loved David; and it was told Saul, and the thing was pleasing in his eyes.
21 Sauli ankaganiza kuti, “Ndimupatse amukwatire kuti akhale ngati msampha kwa Davideyo, ndipo adzaphedwe ndi Afilisti.” Choncho Sauli anawuza Davide kachiwiri, “Tsopano udzakhala mkamwini wanga.”
And Saul said, I will give her to him, and she shall be a stumbling block to him. Now the hand of the Philistines was against Saul.
22 Sauli analamulanso nduna zake kuti, “Muyankhuleni Davide mwamseri ndi kumuwuza kuti, ‘Taona, mfumu imakondwera nawe, ndipo nduna zake zonse zimakukonda. Tsono ukhale mkamwini wa mfumu.’”
And Saul charged his servants, saying, Speak you privately to David, saying, Behold, the king delights in you, and all his servants love you, and do you becomes the king's son-in-law.
23 Iwo anakamuwuza Davide mawu amenewa, koma Davide anati, “Kodi inu mukuganiza kuti ndi chinthu chapafupi kukhala mpongozi wa mfumu? Ine ndine wosauka ndiponso wosatchuka.”
And the servants of Saul spoke these words in the ears of David; and David said, [Is it] a light thing in your eyes to become son-in-law to the king? Whereas I [am] an humble man, an not honorable?
24 Nduna za Sauli zinamuwuza zonse zimene anayankha Davide.
And the servants of Saul reported to him according to these words, which David spoke.
25 Sauli anayankha kuti, “Kamuwuzeni Davide kuti, ‘Mfumu sikufuna malowolo a mtundu wina uliwonse koma timakungu ta msonga za mavalo a Afilisti 100 kuti ilipsire adani ake.’” Maganizo a Sauli anali akuti Davide aphedwe ndi Afilisti.
And Saul said, Thus shall you speak to David, The king wants no gift but a hundred foreskins of the Philistines, to avenge himself on the kings enemies. Now Saul thought to cast him into the hands of the Philistines.
26 Nduna za Saulizo zitamuwuza Davide zimenezi, anakondwera kuti akhale mpongozi wa mfumu. Koma nthawi imene anapatsidwa isanathe,
And the servants of Saul report these words to David, and David was well pleased to become the son-in-law to the king.
27 Davide ndi anyamata ake anapita ndi kukapha Afilisti 200. Iye anabwera ndi timakungu tija natipereka tonse kwa mfumu kuti akhale mpongozi wa mfumu. Kotero Sauli anapereka mwana wake wamkazi, Mikala, kwa Davide kuti amukwatire.
And David arose, and went, he and his men, and struck among the Philistines a hundred men: and he brought their foreskins, and he becomes the king's son-in-law, and [Saul] gives him Melchol his daughter to wife.
28 Sauli atazindikira kuti Yehova anali ndi Davide ndiponso kuti mwana wake Mikala amamukonda Davide,
And Saul saw that the Lord [was] with David, and [that] all Israel loved him.
29 iye anapitirirabe kumuopa Davide ndi kumadana naye moyo wake wonse.
And he was yet more afraid of David.
30 Nthawi zonse pamene atsogoleri a Afilisti ankatuluka kukamenya nkhondo, Davide ankapambana kuposa nduna zonse za Sauli. Choncho dzina lake linatchuka kwambiri.
[And the chief of the Philistines went forth; and it came to pass that from the suficiency of their expedition David acted Wisely above all the servants of Saul; and his name was honored exceedingly. ]